Add parallel Print Page Options

12 Munthu amene amakonda mwambo amakonda kudziwa zinthu,
    koma amene amadana ndi chidzudzulo ndi wopusa.

Munthu wabwino amapeza kuyanja pamaso pa Yehova,
    koma Yehova amatsutsa munthu wochita chinyengo.

Munthu sangakhazikike bwino pochita zoyipa,
    koma maziko a anthu olungama sadzatekeseka.

Mkazi wakhalidwe labwino ali ngati chipewa chaufumu kwa mwamuna wake,
    koma mkazi wochititsa manyazi ali ngati chilonda cha mafinya kwa mwamuna wake.

Maganizo a anthu olungama ndi owongoka,
    koma malangizo a anthu oyipa ndi achinyengo.

Mawu a anthu oyipa ndi ophetsa,
    koma mawu a anthu olungama amapulumutsa.

Anthu oyipa amagonjetsedwa ndipo amayiwalika,
    koma nyumba ya anthu olungama idzakhalabe.

Munthu amatamandidwa malinga ndi nzeru zake,
    koma anthu amitima yokhota amanyozedwa.

Nʼkwabwino kukhala munthu wonyozeka koma wodzigwirira ntchito nʼkukhala ndi zonse zofunika,
    kuposa kukhala wodzikuza koma ulibe ndi chakudya chomwe.

10 Munthu wolungama amasamalira moyo wa ziweto zake,
    koma chifundo cha munthu woyipa ndi chakhanza.

11 Wolima mʼmunda mwake mwakhama adzakhala ndi chakudya chochuluka,
    koma wotsata zopanda pake alibe nzeru.

12 Munthu woyipa amalakalaka zofunkha za anthu oyipa,
    koma mizu ya anthu olungama imabereka zipatso.

13 Munthu woyipa amakodwa mu msampha wa mayankhulidwe ake oyipa;
    koma munthu wolungama amatuluka mʼmavuto.

14 Munthu amakhala ndi zabwino zambiri chifukwa cha mawu ake
    ndipo ntchito zimene munthu agwira ndi manja ake zimamupindulira.

15 Zochita za chitsiru mwini wakeyo amaziona ngati zabwino,
    koma munthu wanzeru amamvera malangizo.

16 Mkwiyo wa chitsiru umadziwika nthawi yomweyo,
    koma munthu wanzeru sasamala kunyozedwa.

17 Woyankhula zoona amapereka umboni woona,
    koma mboni yabodza imafotokoza zonama.

18 Munthu woyankhula mosasamala mawu ake amalasa ngati lupanga,
    koma mawu a munthu wanzeru amachiritsa.

19 Mawu woona amakhala mpaka muyaya
    koma mawu abodza sakhalitsa.

20 Mʼmitima ya anthu amene amakonza zoyipa muli chinyengo;
    koma anthu olimbikitsa za mtendere amakhala ndi chimwemwe.

21 Palibe choyipa chimene chimagwera munthu wolungama,
    koma munthu woyipa mavuto samuthera.

22 Pakamwa pa bodza pamamunyansa Yehova,
    koma amakondwera ndi anthu oyankhula zoona.

23 Munthu wochenjera amabisa nzeru zake,
    koma munthu wopusa amaonetsa uchitsiru wake poyera.

24 Ogwira ntchito mwakhama adzalamulira,
    koma aulesi adzakhala ngati kapolo.

25 Nkhawa imakhala ngati katundu wolemera mu mtima mwa munthu,
    koma mawu abwino amamusangalatsa.

26 Munthu wolungama amatsogolera mnansi wake,
    koma ntchito za anthu oyipa zimawasocheretsa.

27 Munthu waulesi sapeza chimene akufuna,
    koma munthu wakhama amapeza chuma chamtengo wapatali.

28 Mʼnjira yachilungamo muli moyo;
    koma njira ya munthu woyipa imafikitsa ku imfa.