Add parallel Print Page Options

15 Kuyankha kofatsa kumathetsa mkwiyo,
    koma mawu ozaza amautsa ukali.

Munthu wanzeru amayankhula zinthu za nzeru,
    koma pakamwa pa zitsiru pamatulutsa za uchitsiru.

Maso a Yehova ali ponseponse,
    amayangʼana pa oyipa ndi abwino omwe.

Kuyankhula kodekha kuli ngati mtengo wopatsa moyo,
    koma kuyankhula kopotoka kumapweteka mtima.

Chitsiru chimanyoza mwambo wa abambo ake,
    koma wochenjera amasamala chidzudzulo.

Munthu wolungama amakhala ndi chuma chambiri,
    zimene woyipa amapindula nazo zimamugwetsa mʼmavuto.

Pakamwa pa anthu anzeru pamafalitsa nzeru;
    koma mitima ya zitsiru sitero.

Nsembe za anthu oyipa zimamunyansa Yehova,
    koma amakondwera ndi pemphero la anthu owona mtima.

Ntchito za anthu oyipa zimamunyansa Yehova
    koma amakonda amene amafunafuna chilungamo.

10 Amene amasiya njira yabwino adzalangidwa koopsa.
    Odana ndi chidzudzulo adzafa.

11 Manda ndi chiwonongeko ndi zosabisika pamaso pa Yehova,
    nanji mitima ya anthu!

12 Wonyoza sakonda kudzudzulidwa;
    iye sapita kwa anthu anzeru.

13 Mtima wokondwa umachititsa nkhope kukhala yachimwemwe,
    koma mtima wosweka umawawitsa moyo.

14 Mtima wa munthu wozindikira zinthu umafunafuna nzeru,
    koma pakamwa pa zitsiru pamadya uchitsiru wawo.

15 Munthu woponderezedwa masiku ake onse amakhala oyipa,
    koma mtima wachimwemwe umakhala pa chisangalalo nthawi zonse.

16 Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono nʼkumaopa Yehova,
    kusiyana ndi kukhala ndi chuma chambiri uli pamavuto.

17 Kuli bwino kudyera ndiwo zamasamba pamene pali chikondi,
    kusiyana ndi kudyera nyama yangʼombe yonenepa pamene pali udani.

18 Munthu wopsa mtima msanga amayambitsa mikangano,
    koma munthu woleza mtima amathetsa ndewu.

19 Njira ya munthu waulesi ndi yowirira ndi mtengo waminga,
    koma njira ya munthu wolungama ili ngati msewu waukulu.

20 Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake,
    koma mwana wopusa amanyoza amayi ake.

21 Uchitsiru umakondweretsa munthu wopanda nzeru,
    koma munthu womvetsa zinthu amayenda mowongoka.

22 Popanda uphungu zolinga zako munthu zimalephereka,
    koma pakakhala aphungu ambiri zolinga zimatheka.

23 Munthu amakondwera ndi kuyankha koyenera,
    ndipo mawu onena pa nthawi yake ndi okoma.

24 Munthu wanzeru amatsata njira yopita ku moyo
    kuti apewe malo okhala anthu akufa.

25 Yehova amapasula nyumba ya munthu wonyada
    koma amasamalira malo a mkazi wamasiye.

26 Maganizo a anthu oyipa amamunyansa Yehova,
    koma mawu a anthu oyera mtima amamusangalatsa.

27 Munthu wofuna phindu mwachinyengo amavutitsa banja lake,
    koma wodana ndi ziphuphu adzakhala ndi moyo.

28 Munthu wolungama amaganizira za mmene ayankhire,
    koma pakamwa pa munthu woyipa pamatulutsa mawu oyipa.

29 Yehova amakhala kutali ndi anthu oyipa,
    koma amamva pemphero la anthu olungama.

30 Kuwala kwa maso kumasangalatsa mtima
    ndipo uthenga wabwino umalimbitsa munthu.

31 Womvera mawu a chidzudzulo amene apatsa moyo
    adzakhala pakati pa anthu anzeru.

32 Amene amanyoza mwambo amadzinyoza yekha,
    koma womvera mawu a chidzudzulo amapeza nzeru zomvetsa zinthu.

33 Kuopa Yehova kumaphunzitsa munthu nzeru,
    ndipo kudzichepetsa ndi ulemu chili patsogolo ndi kudzichepetsa.