Add parallel Print Page Options

Zapansipano Nʼzopandapake

Mawu a Mlaliki, mwana wa Davide, mfumu ya ku Yerusalemu:

“Zopandapake! Zopandapake!”
    atero Mlaliki.
“Zopandapake kotheratu!
    Zopandapake.”

Kodi munthu amapindulanji pa ntchito zake zonse
    zimene amasautsidwa nazo pansi pano?
Mibado imabwera ndipo mibado imapita,
    koma dziko lapansi limakhalapobe nthawi zonse.
Dzuwa limatuluka ndipo dzuwa limalowa
    ndipo limapita mwamsanga kumene limatulukira.
Mphepo imawombera cha kummwera
    ndi kukhotera cha kumpoto;
imawomba mozungulirazungulira,
    kumangobwererabwerera komwe yachokera.
Mitsinje yonse imakathira ku nyanja,
    koma nyanjayo sidzaza;
kumene madziwo amachokera,
    amabwereranso komweko.
Zinthu zonse ndi zotopetsa,
    kutopetsa kwake ndi kosaneneka.
Maso satopa ndi kuona
    kapena khutu kukwaniritsidwa ndi kumva.
Zomwe zinalipo kale zidzakhalaponso,
    zomwe zinachitika kale zidzachitikanso.
    Ndiye kuti chatsopano palibiretu pansi pano.
10 Kodi chilipo chinthu chimene wina anganene kuti,
    “Taona! Ichi ndiye chatsopano?”
Chinalipo kale, kalekale;
    chinalipo ife kulibe.
11 Anthu akale sakumbukiridwa,
    ngakhale amene adzabwera mʼtsogolomu
sadzakumbukiridwa ndi iwo
    amene adzabwere pambuyo pawo.

Nzeru Nʼzopandapake

12 Ine, Mlalikine, ndinali mfumu ya Israeli mu Yerusalemu. 13 Ndinayika mtima wanga pophunzira ndi kufunafuna mwa nzeru zinthu zonse zimene zimachitika pansi pa thambo. Ndi ntchito yolemetsa ndithu imene Mulungu anayipereka kwa anthu! 14 Ine ndaona zinthu zonse zochitika pansi pano; zinthu zonsezo ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.

15 Chinthu chokhota sichingathe kuwongoledwa;
    chimene palibe sichingathe kuwerengedwa.

16 Ine ndinaganiza mu mtima mwanga, “Taona, ine ndakula ndi kukhala wa nzeru zochuluka kupambana aliyense amene analamulirapo Yerusalemu ndisanabadwe; ndaphunzira nzeru zochuluka ndi luntha.” 17 Ndipo ndinadzipereka kuti ndithe kumvetsa kuti nzeru nʼchiyani, misala nʼchiyani, uchitsiru nʼchiyani, koma ndinazindikira ichi, kuti kuteronso nʼkungodzivuta chabe.

18 Pakuti nzeru zochuluka zimabweretsa chisoni chochulukanso:
    chidziwitso chochuluka, zowawa zochulukanso.

Everything Is Meaningless

The words of the Teacher,[a](A) son of David, king in Jerusalem:(B)

“Meaningless! Meaningless!”
    says the Teacher.
“Utterly meaningless!
    Everything is meaningless.”(C)

What do people gain from all their labors
    at which they toil under the sun?(D)
Generations come and generations go,
    but the earth remains forever.(E)
The sun rises and the sun sets,
    and hurries back to where it rises.(F)
The wind blows to the south
    and turns to the north;
round and round it goes,
    ever returning on its course.
All streams flow into the sea,
    yet the sea is never full.
To the place the streams come from,
    there they return again.(G)
All things are wearisome,
    more than one can say.
The eye never has enough of seeing,(H)
    nor the ear its fill of hearing.
What has been will be again,
    what has been done will be done again;(I)
    there is nothing new under the sun.
10 Is there anything of which one can say,
    “Look! This is something new”?
It was here already, long ago;
    it was here before our time.
11 No one remembers the former generations,(J)
    and even those yet to come
will not be remembered
    by those who follow them.(K)

Wisdom Is Meaningless

12 I, the Teacher,(L) was king over Israel in Jerusalem.(M) 13 I applied my mind to study and to explore by wisdom all that is done under the heavens.(N) What a heavy burden God has laid on mankind!(O) 14 I have seen all the things that are done under the sun; all of them are meaningless, a chasing after the wind.(P)

15 What is crooked cannot be straightened;(Q)
    what is lacking cannot be counted.

16 I said to myself, “Look, I have increased in wisdom more than anyone who has ruled over Jerusalem before me;(R) I have experienced much of wisdom and knowledge.” 17 Then I applied myself to the understanding of wisdom,(S) and also of madness and folly,(T) but I learned that this, too, is a chasing after the wind.

18 For with much wisdom comes much sorrow;(U)
    the more knowledge, the more grief.(V)

Footnotes

  1. Ecclesiastes 1:1 Or the leader of the assembly; also in verses 2 and 12