Add parallel Print Page Options

Kugwa kwa Ninive

Wodzathira nkhondo akubwera
    kudzalimbana nawe, Ninive.
    Tetezani malinga anu,
    dziyangʼanani ku msewu,
    konzekerani nkhondo,
    valani dzilimbe.
Yehova adzabwezeretsa ulemerero wa Yakobo
    ngati ulemerero wa Israeli,
ngakhale anthu owononga anawawononga kotheratu
    ndipo anawononganso mpesa wawo.

Zishango za ankhondo ake ndi zofiira;
    asilikali ake avala zovala zofiirira.
Zitsulo za pa magaleta zikunyezimira
    tsiku la kukonzekera kwake.
    Akuonetsa mikondo ya mkungudza yonoledwa.
Magaleta akuthamanga mʼmisewu
    akungothamangathamanga pa mabwalo.
Akuoneka ngati miyuni yoyaka;
    akuthamanga ngati chingʼaningʼani.

Iye akuyitanitsa asilikali ake wolemekezeka,
    koma iwo akubwera napunthwa.
Akuthamangira ku linga la mzinda;
    akuyimika chodzitchinjirizira pamalo pake.
Atsekula zipata zotchinga madzi a mu mtsinje
    ndipo nyumba yaufumu yagwa.
Zatsimikizika kuti mzinda
    utengedwa ndi kupita ku ukapolo.
Akapolo aakazi akulira ngati nkhunda
    ndipo akudziguguda pachifuwa.
Ninive ali ngati dziwe,
    ndipo madzi ake akutayika.
Iwo akufuwula kuti, “Imani! Imani!”
    Koma palibe amene akubwerera.
Funkhani siliva!
    Funkhani golide!
Katundu wake ndi wochuluka kwambiri,
    chuma chochokera pa zinthu zake zamtengowapatali!
10 Iye wawonongedwa, wafunkhidwa ndipo wavulidwa!
    Mitima yasweka, mawondo akuwombana,
    anthu akunjenjemera ndipo
    nkhope zasandulika ndi mantha.

11 Kodi tsopano dzenje la mikango lili kuti,
    malo amene mikango inkadyetserako ana ake,
kumene mkango waumuna ndi waukazi unkapitako,
    ndipo ana a mkango sankaopa kanthu kalikonse?
12 Mkango waumuna unkapha nyama yokwanira ana ake
    ndiponso kuphera nyama mkango waukazi,
kudzaza phanga lake ndi zimene wapha
    ndiponso dzenje lake ndi nyama imene waphayo.

13 Yehova Wamphamvuzonse akuti,
    “Ine ndikutsutsana nawe.
Ndidzatentha magaleta ako mpaka utsi tolotolo,
    ndipo lupanga lidzapha mikango yako yayingʼono;
sindidzakusiyira chilichonse choti udye pa dziko lapansi.
Mawu a amithenga anu sadzamvekanso.”

Nineveh to Fall

[a]An attacker(A) advances against you, Nineveh.
    Guard the fortress,
    watch the road,
    brace yourselves,
    marshal all your strength!

The Lord will restore(B) the splendor(C) of Jacob
    like the splendor of Israel,
though destroyers have laid them waste
    and have ruined their vines.

The shields of the soldiers are red;
    the warriors are clad in scarlet.(D)
The metal on the chariots flashes
    on the day they are made ready;
    the spears of juniper are brandished.[b]
The chariots(E) storm through the streets,
    rushing back and forth through the squares.
They look like flaming torches;
    they dart about like lightning.

Nineveh summons her picked troops,
    yet they stumble(F) on their way.
They dash to the city wall;
    the protective shield is put in place.
The river gates(G) are thrown open
    and the palace collapses.
It is decreed[c] that Nineveh
    be exiled and carried away.
Her female slaves moan(H) like doves
    and beat on their breasts.(I)
Nineveh is like a pool
    whose water is draining away.
“Stop! Stop!” they cry,
    but no one turns back.
Plunder the silver!
    Plunder the gold!
The supply is endless,
    the wealth from all its treasures!
10 She is pillaged, plundered, stripped!
    Hearts melt,(J) knees give way,
    bodies tremble, every face grows pale.(K)

11 Where now is the lions’ den,(L)
    the place where they fed their young,
where the lion and lioness went,
    and the cubs, with nothing to fear?
12 The lion killed(M) enough for his cubs
    and strangled the prey for his mate,
filling his lairs(N) with the kill
    and his dens with the prey.(O)

13 “I am against(P) you,”
    declares the Lord Almighty.
“I will burn up your chariots in smoke,(Q)
    and the sword(R) will devour your young lions.
    I will leave you no prey on the earth.
The voices of your messengers
    will no longer be heard.”(S)

Footnotes

  1. Nahum 2:1 In Hebrew texts 2:1-13 is numbered 2:2-14.
  2. Nahum 2:3 Hebrew; Septuagint and Syriac ready; / the horsemen rush to and fro.
  3. Nahum 2:7 The meaning of the Hebrew for this word is uncertain.