Nahumu 2
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Kugwa kwa Ninive
2 Wodzathira nkhondo akubwera
kudzalimbana nawe, Ninive.
Tetezani malinga anu,
dziyangʼanani ku msewu,
konzekerani nkhondo,
valani dzilimbe.
2 Yehova adzabwezeretsa ulemerero wa Yakobo
ngati ulemerero wa Israeli,
ngakhale anthu owononga anawawononga kotheratu
ndipo anawononganso mpesa wawo.
3 Zishango za ankhondo ake ndi zofiira;
asilikali ake avala zovala zofiirira.
Zitsulo za pa magaleta zikunyezimira
tsiku la kukonzekera kwake.
Akuonetsa mikondo ya mkungudza yonoledwa.
4 Magaleta akuthamanga mʼmisewu
akungothamangathamanga pa mabwalo.
Akuoneka ngati miyuni yoyaka;
akuthamanga ngati chingʼaningʼani.
5 Iye akuyitanitsa asilikali ake wolemekezeka,
koma iwo akubwera napunthwa.
Akuthamangira ku linga la mzinda;
akuyimika chodzitchinjirizira pamalo pake.
6 Atsekula zipata zotchinga madzi a mu mtsinje
ndipo nyumba yaufumu yagwa.
7 Zatsimikizika kuti mzinda
utengedwa ndi kupita ku ukapolo.
Akapolo aakazi akulira ngati nkhunda
ndipo akudziguguda pachifuwa.
8 Ninive ali ngati dziwe,
ndipo madzi ake akutayika.
Iwo akufuwula kuti, “Imani! Imani!”
Koma palibe amene akubwerera.
9 Funkhani siliva!
Funkhani golide!
Katundu wake ndi wochuluka kwambiri,
chuma chochokera pa zinthu zake zamtengowapatali!
10 Iye wawonongedwa, wafunkhidwa ndipo wavulidwa!
Mitima yasweka, mawondo akuwombana,
anthu akunjenjemera ndipo
nkhope zasandulika ndi mantha.
11 Kodi tsopano dzenje la mikango lili kuti,
malo amene mikango inkadyetserako ana ake,
kumene mkango waumuna ndi waukazi unkapitako,
ndipo ana a mkango sankaopa kanthu kalikonse?
12 Mkango waumuna unkapha nyama yokwanira ana ake
ndiponso kuphera nyama mkango waukazi,
kudzaza phanga lake ndi zimene wapha
ndiponso dzenje lake ndi nyama imene waphayo.
13 Yehova Wamphamvuzonse akuti,
“Ine ndikutsutsana nawe.
Ndidzatentha magaleta ako mpaka utsi tolotolo,
ndipo lupanga lidzapha mikango yako yayingʼono;
sindidzakusiyira chilichonse choti udye pa dziko lapansi.
Mawu a amithenga anu sadzamvekanso.”
Nahum 2
New International Version
Nineveh to Fall
2 [a]An attacker(A) advances against you, Nineveh.
Guard the fortress,
watch the road,
brace yourselves,
marshal all your strength!
2 The Lord will restore(B) the splendor(C) of Jacob
like the splendor of Israel,
though destroyers have laid them waste
and have ruined their vines.
3 The shields of the soldiers are red;
the warriors are clad in scarlet.(D)
The metal on the chariots flashes
on the day they are made ready;
the spears of juniper are brandished.[b]
4 The chariots(E) storm through the streets,
rushing back and forth through the squares.
They look like flaming torches;
they dart about like lightning.
5 Nineveh summons her picked troops,
yet they stumble(F) on their way.
They dash to the city wall;
the protective shield is put in place.
6 The river gates(G) are thrown open
and the palace collapses.
7 It is decreed[c] that Nineveh
be exiled and carried away.
Her female slaves moan(H) like doves
and beat on their breasts.(I)
8 Nineveh is like a pool
whose water is draining away.
“Stop! Stop!” they cry,
but no one turns back.
9 Plunder the silver!
Plunder the gold!
The supply is endless,
the wealth from all its treasures!
10 She is pillaged, plundered, stripped!
Hearts melt,(J) knees give way,
bodies tremble, every face grows pale.(K)
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.