Add parallel Print Page Options

Kugwa kwa Ninive

Wodzathira nkhondo akubwera
    kudzalimbana nawe, Ninive.
    Tetezani malinga anu,
    dziyangʼanani ku msewu,
    konzekerani nkhondo,
    valani dzilimbe.
Yehova adzabwezeretsa ulemerero wa Yakobo
    ngati ulemerero wa Israeli,
ngakhale anthu owononga anawawononga kotheratu
    ndipo anawononganso mpesa wawo.

Zishango za ankhondo ake ndi zofiira;
    asilikali ake avala zovala zofiirira.
Zitsulo za pa magaleta zikunyezimira
    tsiku la kukonzekera kwake.
    Akuonetsa mikondo ya mkungudza yonoledwa.
Magaleta akuthamanga mʼmisewu
    akungothamangathamanga pa mabwalo.
Akuoneka ngati miyuni yoyaka;
    akuthamanga ngati chingʼaningʼani.

Iye akuyitanitsa asilikali ake wolemekezeka,
    koma iwo akubwera napunthwa.
Akuthamangira ku linga la mzinda;
    akuyimika chodzitchinjirizira pamalo pake.
Atsekula zipata zotchinga madzi a mu mtsinje
    ndipo nyumba yaufumu yagwa.
Zatsimikizika kuti mzinda
    utengedwa ndi kupita ku ukapolo.
Akapolo aakazi akulira ngati nkhunda
    ndipo akudziguguda pachifuwa.
Ninive ali ngati dziwe,
    ndipo madzi ake akutayika.
Iwo akufuwula kuti, “Imani! Imani!”
    Koma palibe amene akubwerera.
Funkhani siliva!
    Funkhani golide!
Katundu wake ndi wochuluka kwambiri,
    chuma chochokera pa zinthu zake zamtengowapatali!
10 Iye wawonongedwa, wafunkhidwa ndipo wavulidwa!
    Mitima yasweka, mawondo akuwombana,
    anthu akunjenjemera ndipo
    nkhope zasandulika ndi mantha.

11 Kodi tsopano dzenje la mikango lili kuti,
    malo amene mikango inkadyetserako ana ake,
kumene mkango waumuna ndi waukazi unkapitako,
    ndipo ana a mkango sankaopa kanthu kalikonse?
12 Mkango waumuna unkapha nyama yokwanira ana ake
    ndiponso kuphera nyama mkango waukazi,
kudzaza phanga lake ndi zimene wapha
    ndiponso dzenje lake ndi nyama imene waphayo.

13 Yehova Wamphamvuzonse akuti,
    “Ine ndikutsutsana nawe.
Ndidzatentha magaleta ako mpaka utsi tolotolo,
    ndipo lupanga lidzapha mikango yako yayingʼono;
sindidzakusiyira chilichonse choti udye pa dziko lapansi.
Mawu a amithenga anu sadzamvekanso.”