Add parallel Print Page Options

Moto Wochokera kwa Yehova

11 Anthu atadandaula kwa Yehova chifukwa cha mavuto awo, Yehovayo anamva ndipo anakwiya kwambiri. Kenaka moto wa Yehova unayaka pakati pawo ndi kutentha zigawo zina za kunja kwa msasa. Anthuwo analira kwa Mose ndipo Moseyo atapemphera kwa Yehova, motowo unazima. Motero malowo anawatcha Tabera, chifukwa moto wa Yehova unayaka pakati pawo.

Zinziri Zochokera kwa Yehova

Anthu ena osokoneza amene anali pakati pa Aisraeli anayamba kukhumba chakudya cha ku Igupto ndipo Aisraeli nawonso anayamba kufuwula kwambiri nʼkumati, “Tikanangopeza nyama yoti nʼkudya! Tikukumbukira nsomba zaulere zimene tinkadya ku Igupto komanso nkhaka, mavwende, anyezi wamitundumitundu ndi adyo. Koma tsopano chilakolako chathu chatha. Sitikuona kanthu kena kakudya koma mana basi!”

Mana ankafanana ndi mbewu zamapira ndipo maonekedwe ake anali ngati ulimbo wowuma. Anthu ankapita kukatola manawo, nʼkumasinja mu mtondo kapena kupera. Ankawaphika mu mʼphika kapena kupanga makeke. Ndipo ankakoma ngati makeke ophikira mafuta a olivi. Mame akamagwa pa msasawo usiku ankagwera kumodzi ndi manawo.

10 Mose anamva anthu a banja lililonse akufuwula, banja lililonse pa khomo la tenti yake. Yehova anakwiya kwambiri ndipo Mose anavutikanso mu mtima. 11 Mose anafunsa Yehova kuti, “Chifukwa chiyani mwabweretsa mavuto otere pa mtumiki wanune? Nʼchiyani chimene ndachita choti sichinakusangalatseni mpaka kundisenzetsa katundu wa anthu onsewa? 12 Kodi Ndine amene ndinatenga pathupi pa anthu onsewa? Kodi ndinawabala ndine? Bwanji mukundiwuza kuti ndiwanyamule mʼmanja mwanga, monga momwe mlezi amanyamulira kamwana, kupita nawo ku malo omwe munalonjeza ndi lumbiro kwa makolo awo? 13 Ndingayipeze kuti nyama yoti anthu onsewa adye? Iwowa akulirira ine kuti, ‘Tipatse nyama tidye!’ 14 Sindingathe kusamala anthu onsewa ndekha. Katundu ameneyu ndi wolemera kwambiri kwa ine. 15 Ngati umu ndi mmene muzichitira nane, chonde ingondiphani pompano. Koma ngati mwandikomera mtima ndiye ndisaonenso mavutowa.”

16 Yehova anawuza Mose kuti, “Undibweretsere anthu 70 ochokera pakati pa akuluakulu a Aisraeli, amene umawadziwa kuti ndiwo atsogoleri komanso akuluakulu a mabanja. Abwere ku tenti ya msonkhano kuti ayime kumeneko pamodzi ndi iwe. 17 Ndidzatsika ndi kuyankhula nawe kumeneko, ndipo ndidzatenga mzimu umene uli pa iwe ndi kuyika pa iwowo. Adzakuthandiza kusenza nkhawa za anthuwa ndipo sudzasenzanso wekha.”

18 “Uwawuze anthuwo kuti, ‘Mudziyeretse, kukonzekera mawa, pamene mudzadya nyama.’ Yehova anakumvani pamene munkalira kuti, ‘Zikanakhala bwino tikanapeza nyama yoti tidye! Tinkakhala bwino ku Igupto!’ Tsopano Yehova adzakupatsani nyama ndipo mudzayidyadi. 19 Simudzadya tsiku limodzi lokha, kapena masiku awiri, kapena asanu, khumi kapena masiku makumi awiri, 20 koma mwezi wonse, mpaka itakukolani ndi kutopa nayo chifukwa mwakana Yehova yemwe ali pakati panu ndipo mwalira pamaso pake kuti, ‘Bwanji tinachoka ku Igupto?’ ”

21 Koma Mose anati, “Taonani pano ndili pakati pa anthu 600,000 amene ndi kuyenda nawo ndipo Inuyo mukuti, ‘Ndidzawapatsa nyama kuti adye mwezi wathunthu!’ 22 Kodi ngakhale titapha nkhosa ndi ngʼombe, zingawakwanire? Ngakhale titagwira nsomba zonse za mʼnyanja, kodi zingawakwanire iwowa?”

23 Yehova anayankha Mose kuti, “Kodi dzanja langa ndi lalifupi? Uwona tsopano ngati zimene ndanenazo zichitike kapena ayi.”

24 Choncho Mose anatuluka nakawuza anthu zomwe Yehova ananena. Anasonkhanitsa pamodzi akuluakulu makumi asanu ndi awiri aja ndi kuwayimiritsa mozungulira Chihema. 25 Ndipo Yehova anatsika mʼmitambo ndi kuyankhula naye ndipo anatengako mzimu womwe unali pa Mose ndi kuwuyika pa akuluakulu makumi asanu ndi awiri aja. Pamene mzimuwo unakhazikika pa akuluakuluwo, anayamba kunenera koma sanapitirize.

26 Koma anthu ena awiri omwe mayina awo anali Elidadi ndi Medadi, anatsalira mu msasa. Anali nawo mʼgulu la olembedwa aja, koma sanapite nawo ku Chihema. Komabe mzimu unakhala pa iwo ndipo ananenera ali mu msasa. 27 Mnyamata wina anathamanga kudzawuza Mose kuti, “Elidadi ndi Medadi akunenera mu msasa.”

28 Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Mose kuyambira ubwana wake, anayankha kuti, “Mbuye wanga Mose, aletseni!”

29 Koma Mose anati, “Kodi ukuchita nsanje chifukwa cha ine? Ndikanakonda kuti anthu onse a Yehova akhale aneneri ndi kuti Yehova ayike mzimu wake pa iwo!” 30 Mose ndi akuluakulu a Israeli aja anabwerera ku msasa.

31 Pamenepo Yehova anawutsa mphepo yochokera ku nyanja imene inabweretsa zinziri. Zinzirizo zinagwera pansi kuzungulira msasa, mtunda wa kilomita imodzi mbali zonse ndipo msinkhu wake unali mita imodzi. 32 Tsiku limenelo masana onse mpaka usiku ndiponso tsiku lotsatiralo, anthu anatuluka kunja kukatola zinziri. Palibe amene anasonkhanitsa zochepera makilogalamu 1,000 ndipo anaziyanika kuzungulira msasa wonse. 33 Koma pamene anthuwo ankadya nyamayo, asanayimeze nʼkomwe, ukali wa Yehova unafika pa iwo ndipo Iye anawakantha ndi mliri woopsa. 34 Nʼchifukwa chake malowo anawatcha Kibiroti Hatava chifukwa pamenepo anakwirirapo anthu osusuka aja.

35 Kuchoka pa Kibiroti Hatava anthuwo anayenda kupita ku Heziroti ndipo anakhala kumeneko kwa kanthawi.

Fire From the Lord

11 Now the people complained(A) about their hardships in the hearing of the Lord,(B) and when he heard them his anger was aroused.(C) Then fire from the Lord burned among them(D) and consumed(E) some of the outskirts of the camp. When the people cried out to Moses, he prayed(F) to the Lord(G) and the fire died down. So that place was called Taberah,[a](H) because fire from the Lord had burned among them.(I)

Quail From the Lord

The rabble with them began to crave other food,(J) and again the Israelites started wailing(K) and said, “If only we had meat to eat! We remember the fish we ate in Egypt at no cost—also the cucumbers, melons, leeks, onions and garlic.(L) But now we have lost our appetite; we never see anything but this manna!(M)

The manna was like coriander seed(N) and looked like resin.(O) The people went around gathering it,(P) and then ground it in a hand mill or crushed it in a mortar. They cooked it in a pot or made it into loaves. And it tasted like something made with olive oil. When the dew(Q) settled on the camp at night, the manna also came down.

10 Moses heard the people of every family wailing(R) at the entrance to their tents. The Lord became exceedingly angry, and Moses was troubled. 11 He asked the Lord, “Why have you brought this trouble(S) on your servant? What have I done to displease you that you put the burden of all these people on me?(T) 12 Did I conceive all these people? Did I give them birth? Why do you tell me to carry them in my arms, as a nurse carries an infant,(U) to the land you promised on oath(V) to their ancestors?(W) 13 Where can I get meat for all these people?(X) They keep wailing to me, ‘Give us meat to eat!’ 14 I cannot carry all these people by myself; the burden is too heavy for me.(Y) 15 If this is how you are going to treat me, please go ahead and kill me(Z)—if I have found favor in your eyes—and do not let me face my own ruin.”

16 The Lord said to Moses: “Bring me seventy of Israel’s elders(AA) who are known to you as leaders and officials among the people.(AB) Have them come to the tent of meeting,(AC) that they may stand there with you. 17 I will come down and speak with you(AD) there, and I will take some of the power of the Spirit that is on you and put it on them.(AE) They will share the burden of the people with you so that you will not have to carry it alone.(AF)

18 “Tell the people: ‘Consecrate yourselves(AG) in preparation for tomorrow, when you will eat meat. The Lord heard you when you wailed,(AH) “If only we had meat to eat! We were better off in Egypt!”(AI) Now the Lord will give you meat,(AJ) and you will eat it. 19 You will not eat it for just one day, or two days, or five, ten or twenty days, 20 but for a whole month—until it comes out of your nostrils and you loathe it(AK)—because you have rejected the Lord,(AL) who is among you, and have wailed before him, saying, “Why did we ever leave Egypt?”’”(AM)

21 But Moses said, “Here I am among six hundred thousand men(AN) on foot, and you say, ‘I will give them meat to eat for a whole month!’ 22 Would they have enough if flocks and herds were slaughtered for them? Would they have enough if all the fish in the sea were caught for them?”(AO)

23 The Lord answered Moses, “Is the Lord’s arm too short?(AP) Now you will see whether or not what I say will come true for you.(AQ)

24 So Moses went out and told the people what the Lord had said. He brought together seventy of their elders and had them stand around the tent. 25 Then the Lord came down in the cloud(AR) and spoke with him,(AS) and he took some of the power of the Spirit(AT) that was on him and put it on the seventy elders.(AU) When the Spirit rested on them, they prophesied(AV)—but did not do so again.

26 However, two men, whose names were Eldad and Medad, had remained in the camp. They were listed among the elders, but did not go out to the tent. Yet the Spirit also rested on them,(AW) and they prophesied in the camp. 27 A young man ran and told Moses, “Eldad and Medad are prophesying in the camp.”

28 Joshua son of Nun,(AX) who had been Moses’ aide(AY) since youth, spoke up and said, “Moses, my lord, stop them!”(AZ)

29 But Moses replied, “Are you jealous for my sake? I wish that all the Lord’s people were prophets(BA) and that the Lord would put his Spirit(BB) on them!”(BC) 30 Then Moses and the elders of Israel returned to the camp.

31 Now a wind went out from the Lord and drove quail(BD) in from the sea. It scattered them up to two cubits[b] deep all around the camp, as far as a day’s walk in any direction. 32 All that day and night and all the next day the people went out and gathered quail. No one gathered less than ten homers.[c] Then they spread them out all around the camp. 33 But while the meat was still between their teeth(BE) and before it could be consumed, the anger(BF) of the Lord burned against the people, and he struck them with a severe plague.(BG) 34 Therefore the place was named Kibroth Hattaavah,[d](BH) because there they buried the people who had craved other food.

35 From Kibroth Hattaavah the people traveled to Hazeroth(BI) and stayed there.

Footnotes

  1. Numbers 11:3 Taberah means burning.
  2. Numbers 11:31 That is, about 3 feet or about 90 centimeters
  3. Numbers 11:32 That is, possibly about 1 3/4 tons or about 1.6 metric tons
  4. Numbers 11:34 Kibroth Hattaavah means graves of craving.