Add parallel Print Page Options

Miriamu ndi Aaroni Atsutsana ndi Mose

12 Miriamu ndi Aaroni anayamba kuyankhula motsutsana ndi Mose chifukwa cha mkazi wa ku Kusi, popeza Moseyo anakwatira Mkusi. Iwowo anafunsa kuti, “Kodi Yehova anayankhula kudzera mwa Mose yekha? Kodi sanayankhule kudzeranso mwa ife?” Ndipo Yehova anamva zimenezi.

(Koma Mose anali munthu wodzichepetsa kwambiri kuposa munthu aliyense pa dziko lapansi).

Nthawi yomweyo Yehova anati kwa Mose, Aaroni ndi Miriamu, “Bwerani ku tenti ya msonkhano nonse atatu.” Ndipo atatuwo anapitadi kumeneko. Tsono Yehova anatsika mu mtambo, nayima pa khomo la chihema. Kenaka anayitana Aaroni ndi Miriamu. Ndipo onse awiri atapita patsogolo, Mulungu anati, “Mverani mawu anga:

“Pakakhala mneneri wa Yehova pakati panu,
    ndimadzionetsera kwa iyeyo mʼmasomphenya,
    ndimayankhula naye mʼmaloto.
Koma sinditero ndi Mose mtumiki wanga;
    Iyeyu ndi wokhulupirika mʼnyumba yanga yonse.
Ndimayankhula naye maso ndi maso,
    momveka bwino osati mophiphiritsa;
    ndipo amaona maonekedwe a Yehova.
Nʼchifukwa chiyani simunaope
    kuyankhula motsutsana ndi Mose mtumiki wanga?”

Ndipo Yehova anawakwiyira, nachoka.

10 Pamene mtambo unachoka pamwamba pa Chihema, taonani, Miriamu anagwidwa ndi khate. Aaroni atachewuka anaona Miriamu ali ndi khate; 11 ndipo Aaroni anawuza Mose kuti, “Pepani mbuye wanga, musatilange chifukwa cha tchimo limene tachita mopusa. 12 Musalole kuti Miriamu akhale ngati mwana wobadwa wakufa kuchoka mʼmimba mwa amayi ake, thupi lake litawonongeka.”

13 Tsono Mose anafuwulira Yehova kuti, “Chonde Inu Mulungu, muchiritseni!”

14 Yehova anayankha Mose kuti, “Abambo ake akanamulavulira malovu mʼmaso, kodi sakanakhala wonyozeka masiku asanu ndi awiri? Mutsekereni kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri, kenaka mumulowetsenso.” 15 Choncho anamutsekera Miriamu kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri ndipo anthu sanayende ulendo wawo mpaka Miriamu atamulowetsanso.

16 Pambuyo pake anthu ananyamuka ku Heziroti ndi kukamanga mʼchipululu cha Parani.

Miriam and Aaron Oppose Moses

12 Miriam(A) and Aaron began to talk against Moses because of his Cushite wife,(B) for he had married a Cushite. “Has the Lord spoken only through Moses?” they asked. “Hasn’t he also spoken through us?”(C) And the Lord heard this.(D)

(Now Moses was a very humble man,(E) more humble than anyone else on the face of the earth.)

At once the Lord said to Moses, Aaron and Miriam, “Come out to the tent of meeting, all three of you.” So the three of them went out. Then the Lord came down in a pillar of cloud;(F) he stood at the entrance to the tent and summoned Aaron and Miriam. When the two of them stepped forward, he said, “Listen to my words:

“When there is a prophet among you,
    I, the Lord, reveal(G) myself to them in visions,(H)
    I speak to them in dreams.(I)
But this is not true of my servant Moses;(J)
    he is faithful in all my house.(K)
With him I speak face to face,
    clearly and not in riddles;(L)
    he sees the form of the Lord.(M)
Why then were you not afraid
    to speak against my servant Moses?”(N)

The anger of the Lord burned against them,(O) and he left them.(P)

10 When the cloud lifted from above the tent,(Q) Miriam’s skin was leprous[a]—it became as white as snow.(R) Aaron turned toward her and saw that she had a defiling skin disease,(S) 11 and he said to Moses, “Please, my lord, I ask you not to hold against us the sin we have so foolishly committed.(T) 12 Do not let her be like a stillborn infant coming from its mother’s womb with its flesh half eaten away.”

13 So Moses cried out to the Lord, “Please, God, heal her!(U)

14 The Lord replied to Moses, “If her father had spit in her face,(V) would she not have been in disgrace for seven days? Confine her outside the camp(W) for seven days; after that she can be brought back.” 15 So Miriam was confined outside the camp(X) for seven days,(Y) and the people did not move on till she was brought back.

16 After that, the people left Hazeroth(Z) and encamped in the Desert of Paran.(AA)

Footnotes

  1. Numbers 12:10 The Hebrew for leprous was used for various diseases affecting the skin.