Add parallel Print Page Options

Zopereka Zapadera

15 Yehova anawuza Mose kuti, “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukupatsanilo, ndipo mukamadzapereka kwa Yehova, nsembe yotentha pa moto ya ngʼombe kapena nkhosa monga fungo lokoma kwa Yehova, kaya ndi nsembe yopsereza kapena nsembe zina, nsembe yapadera chifukwa cha lumbiro kapena nsembe yoperekedwa mwaufulu kapenanso yoperekedwa pa chikondwerero, munthu amene akubweretsa zopereka zake, azikapereka kwa Yehova chopereka chachakudya cholemera kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta wokwana lita imodzi. Pamodzi ndi mwana wankhosa aliyense wa nsembe yopsereza kapena nsembe ina, muzikakonzanso lita imodzi la vinyo ngati chopereka cha chakumwa.’ ”

“Pamodzi ndi nkhosa yayimuna, muzikakonzanso chopereka cha chakudya cholemera makilogalamu awiri a ufa wosalala, wosakaniza ndi mafuta okwanira lita imodzi ndi theka, ndi vinyo wokwanira lita imodzi ndi theka ngati chopereka cha chakumwa. Muzikapereka monga nsembe yopereka fungo lokoma kwa Yehova.

“ ‘Pamene mukukonza mwana wangʼombe wamwamuna kuti akhale nsembe yopsereza kapena nsembe ina iliyonse: ya lumbiro lapadera kapena nsembe yachiyanjano kwa Yehova, pamodzi ndi mwana wangʼombe wamwamunayo muzibweretsa nsembe yachakudya yolemera makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta okwana malita awiri. 10 Komanso muzibweretsa vinyo wokwanira malita awiri monga chopereka chachakumwa. Imeneyi idzakhala chopereka chotentha pa moto kuti likhale fungo lokoma kwa Yehova. 11 Ngʼombe yayimuna iliyonse kapena nkhosa yayimuna iliyonse, mwana wankhosa aliyense kapena mbuzi yayingʼono, zizikonzedwa motere. 12 Ngakhale zingachuluke chotani, chitani izi kwa iliyonse ya nyamazo.

13 “ ‘Mbadwa iliyonse ya mu Israeli izichita zimenezi pamene ibweretsa nsembe yotentha pa moto kuti ikhale fungo lokoma kwa Yehova. 14 Ku mibado yanu yonse ya mʼtsogolo, pamene mlendo kapena wina aliyense wokhala pakati panu apereka chopereka chotentha pa moto kuti chikhale fungo lokoma kwa Yehova, azichita mofanana ndi momwe inu mumachitira. 15 Gulu lonse likhale ndi malamulo ofanana a inu kapena mlendo wokhala pakati panu. Limeneli ndi lamulo lamuyaya kwa mibado imene ikubwera. Inuyo ndi mlendo mudzakhala wofanana pamaso pa Yehova. 16 Mudzakhale ndi malamulo ndi miyambo yofanana, inuyo ndi mlendo wokhala pakati panu.’ ”

17 Yehova anawuza Mose kuti, 18 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo unene kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukutengeraniko 19 ndipo mukakadya chakudya cha mʼdzikolo, mukapereke gawo lina kwa Yehova monga chopereka. 20 Pa buledi wanu woyamba, mukapereke mmodzi monga nsembe, ngati chopereka chochokera ku malo wopunthira tirigu. 21 Pa mibado yanu yonse muzidzapereka chopereka ichi kwa Yehova kuchokera ku zakudya zanu zoyamba za mʼnthaka.

Chopereka Chopepesera Machimo Ochita Mosadziwa

22 “ ‘Ndipo ngati muchimwa mosadziwa posasunga ena mwa malamulo awa amene Yehova wapereka kwa Mose, 23 lina lililonse mwa malamulo a Yehova amene wapereka kwa inu kudzera mwa Mose, kuyambira tsiku limene Yehova anawapereka mpaka mibado ya mʼtsogolo, 24 ndipo ngati zimenezi zachitika osati mwadala ndipo gulu lonse silinadziwe, zikatero gulu lonselo lipereke mwana wangʼombe wamwamuna monga nsembe yopsereza kuti likhale fungo lokoma kwa Yehova pamodzinso ndi chopereka chachakudya ndi chopereka cha chakumwa ndi mbuzi yayimuna ngati nsembe yopepesera machimo potsata zimene zinalamulidwa. 25 Wansembe apereke nsembe yopepesera machimo a gulu lonse la Aisraeli, ndipo adzakhululukidwa, pakuti linali tchimo lochita mosadziwa. Ndipo chifukwa cha tchimo lawolo, abweretse kwa Yehova nsembe yotentha pa moto ndi nsembe yopepesera machimo. 26 Gulu lonse la Aisraeli ndi alendo okhala pakati pawo adzakhululukidwa chifukwa anthu onsewo anachimwa mosadziwa.

27 “ ‘Koma ngati munthu mmodzi achimwa mosadziwa, ayenera kubweretsa mbuzi yayikazi ya chaka chimodzi kuti ikhale nsembe yopepesera machimo. 28 Wansembe apereke nsembe yopepesera machimowo pamaso pa Yehova chifukwa cha munthu yemwe anachimwa mosadziwayo. Nsembe yopepesera tchimo lakelo ikaperekedwa, munthuyo adzakhululukidwa. 29 Lamulo lomweli ligwiritsidwe ntchito kwa aliyense wochimwa mosadziwa, kaya ndi mbadwa ya mu Israeli kapena mlendo.

30 “ ‘Koma aliyense amene achimwa mwadala, kaya ndi mbadwa kapena mlendo, nachitira chipongwe Yehova, ameneyo achotsedwe ndithu pakati pa anthu ake. 31 Popeza wanyoza mawu a Yehova ndi kuphwanya malamulo ake. Munthu ameneyo achotsedwe ndithu, kuchimwa kwake kudzakhala pa iyeyo.’ ”

Wosasunga Sabata Aphedwa

32 Aisraeli ali mʼchipululu, munthu wina anapezeka akutola nkhuni tsiku la Sabata. 33 Amene anamupeza akutola nkhunizo anabwera naye kwa Mose ndi Aaroni ndi kwa gulu lonse 34 ndipo anamutsekera mʼndende chifukwa sankadziwa choti achite naye. 35 Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti, “Munthu ameneyu ayenera kuphedwa. Gulu lonse liyenera kumugenda ndi miyala kunja kwa msasa.” 36 Choncho gululo linamutengera kunja kwa msasa ndi kumupha pomugenda ndi miyala, monga momwe Yehova analamulira Mose.

Mphonje pa Zovala

37 Yehova anawuza Mose kuti, 38 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pa mibado yanu yonse muzisokerera mphonje pa ngodya za zovala zanu ndipo pa ngodya ya mphonje iliyonse azisokererapo chingwe chobiriwira. 39 Mudzakhala ndi mphonje zimenezi kuti mukaziona muzikakumbukira malamulo onse a Yehova ndi kuwamvera kuti musamatsatenso zilakolako za mʼmitima mwanu ndi za maso anu. 40 Motero mudzakumbukira kumvera malamulo anga ndipo mudzakhala opatulikira a Mulungu wanu. 41 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto kuti ndikhale Mulungu wanu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’ ”

Supplementary Offerings

15 The Lord said to Moses, “Speak to the Israelites and say to them: ‘After you enter the land I am giving you(A) as a home and you present to the Lord food offerings from the herd or the flock,(B) as an aroma pleasing to the Lord(C)—whether burnt offerings(D) or sacrifices, for special vows or freewill offerings(E) or festival offerings(F) then the person who brings an offering shall present to the Lord a grain offering(G) of a tenth of an ephah[a] of the finest flour(H) mixed with a quarter of a hin[b] of olive oil. With each lamb(I) for the burnt offering or the sacrifice, prepare a quarter of a hin of wine(J) as a drink offering.(K)

“‘With a ram(L) prepare a grain offering(M) of two-tenths of an ephah[c](N) of the finest flour mixed with a third of a hin[d] of olive oil,(O) and a third of a hin of wine(P) as a drink offering.(Q) Offer it as an aroma pleasing to the Lord.(R)

“‘When you prepare a young bull(S) as a burnt offering or sacrifice, for a special vow(T) or a fellowship offering(U) to the Lord, bring with the bull a grain offering(V) of three-tenths of an ephah[e](W) of the finest flour mixed with half a hin[f] of olive oil, 10 and also bring half a hin of wine(X) as a drink offering.(Y) This will be a food offering, an aroma pleasing to the Lord.(Z) 11 Each bull or ram, each lamb or young goat, is to be prepared in this manner. 12 Do this for each one, for as many as you prepare.(AA)

13 “‘Everyone who is native-born(AB) must do these things in this way when they present a food offering as an aroma pleasing to the Lord.(AC) 14 For the generations to come,(AD) whenever a foreigner(AE) or anyone else living among you presents a food(AF) offering(AG) as an aroma pleasing to the Lord, they must do exactly as you do. 15 The community is to have the same rules for you and for the foreigner residing among you; this is a lasting ordinance for the generations to come.(AH) You and the foreigner shall be the same before the Lord: 16 The same laws and regulations will apply both to you and to the foreigner residing among you.(AI)’”

17 The Lord said to Moses, 18 “Speak to the Israelites and say to them: ‘When you enter the land to which I am taking you(AJ) 19 and you eat the food of the land,(AK) present a portion as an offering to the Lord.(AL) 20 Present a loaf from the first of your ground meal(AM) and present it as an offering from the threshing floor.(AN) 21 Throughout the generations to come(AO) you are to give this offering to the Lord from the first of your ground meal.(AP)

Offerings for Unintentional Sins

22 “‘Now if you as a community unintentionally fail to keep any of these commands the Lord gave Moses(AQ) 23 any of the Lord’s commands to you through him, from the day the Lord gave them and continuing through the generations to come(AR) 24 and if this is done unintentionally(AS) without the community being aware of it,(AT) then the whole community is to offer a young bull for a burnt offering(AU) as an aroma pleasing to the Lord,(AV) along with its prescribed grain offering(AW) and drink offering,(AX) and a male goat for a sin offering.[g](AY) 25 The priest is to make atonement for the whole Israelite community, and they will be forgiven,(AZ) for it was not intentional(BA) and they have presented to the Lord for their wrong a food offering(BB) and a sin offering.(BC) 26 The whole Israelite community and the foreigners residing among them will be forgiven, because all the people were involved in the unintentional wrong.(BD)

27 “‘But if just one person sins unintentionally,(BE) that person must bring a year-old female goat for a sin offering.(BF) 28 The priest is to make atonement(BG) before the Lord for the one who erred by sinning unintentionally, and when atonement has been made, that person will be forgiven.(BH) 29 One and the same law applies to everyone who sins unintentionally, whether a native-born Israelite or a foreigner residing among you.(BI)

30 “‘But anyone who sins defiantly,(BJ) whether native-born or foreigner,(BK) blasphemes the Lord(BL) and must be cut off from the people of Israel.(BM) 31 Because they have despised(BN) the Lord’s word and broken his commands,(BO) they must surely be cut off; their guilt remains on them.(BP)’”

The Sabbath-Breaker Put to Death

32 While the Israelites were in the wilderness,(BQ) a man was found gathering wood on the Sabbath day.(BR) 33 Those who found him gathering wood brought him to Moses and Aaron and the whole assembly, 34 and they kept him in custody, because it was not clear what should be done to him.(BS) 35 Then the Lord said to Moses, “The man must die.(BT) The whole assembly must stone him outside the camp.(BU) 36 So the assembly took him outside the camp and stoned him(BV) to death,(BW) as the Lord commanded Moses.(BX)

Tassels on Garments

37 The Lord said to Moses, 38 “Speak to the Israelites and say to them: ‘Throughout the generations to come(BY) you are to make tassels on the corners of your garments,(BZ) with a blue cord on each tassel. 39 You will have these tassels to look at and so you will remember(CA) all the commands of the Lord, that you may obey them and not prostitute yourselves(CB) by chasing after the lusts of your own hearts(CC) and eyes. 40 Then you will remember to obey all my commands(CD) and will be consecrated to your God.(CE) 41 I am the Lord your God, who brought you out of Egypt to be your God.(CF) I am the Lord your God.(CG)’”

Footnotes

  1. Numbers 15:4 That is, probably about 3 1/2 pounds or about 1.6 kilograms
  2. Numbers 15:4 That is, about 1 quart or about 1 liter; also in verse 5
  3. Numbers 15:6 That is, probably about 7 pounds or about 3.2 kilograms
  4. Numbers 15:6 That is, about 1 1/3 quarts or about 1.3 liters; also in verse 7
  5. Numbers 15:9 That is, probably about 11 pounds or about 5 kilograms
  6. Numbers 15:9 That is, about 2 quarts or about 1.9 liters; also in verse 10
  7. Numbers 15:24 Or purification offering; also in verses 25 and 27