Add parallel Print Page Options

Malo a Misasa ya Mafuko Onse a Aisraeli

Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni: “Aisraeli azimanga misasa yawo mozungulira tenti ya msonkhano motalikira pangʼono. Munthu aliyense amange pamene pali mbendera ya fuko lake.”

Kummawa, kotulukira dzuwa, magulu a msasa wa Yuda amange pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa Ayudawo ndi Naasoni mwana wa Aminadabu. Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 74,600.

Fuko la Isakara lidzamanga pafupi ndi Yuda. Mtsogoleri wa gulu la Isakara ndi Netanieli mwana wa Zuwara. Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 54,400.

Lotsatira lidzakhala fuko la Zebuloni. Mtsogoleri wa gulu la Zebuloni ndi Eliabu mwana wa Heloni. Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 57,400.

Anthu onse aamuna mʼmisasa ya Yuda, chiwerengero chawo ndi 186,400 monga mwa magulu awo. Iwowo ndiwo aziyamba kusamuka.

10 Kummwera kudzakhala magulu a msasa wa Rubeni pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa gulu la Rubeni ndi Elizuri mwana wa Sedeuri. 11 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 46,500.

12 Fuko la Simeoni lidzamanga pafupi ndi Rubeni. Mtsogoleri wa gulu la Simeoni ndi Selumieli mwana wa Zurisadai. 13 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 59,300.

14 Lotsatira lidzakhala fuko la Gadi. Mtsogoleri wa gulu la Gadi ndi Eliyasafu mwana wa Deuweli. 15 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 45,650.

16 Anthu onse aamuna mu msasa wa Rubeni, chiwerengero chawo monga mwa magulu awo, ndi 151,450. Iwowo azikhala achiwiri posamuka.

17 Tsono tenti ya msonkhano ndi msasa wa Alevi zidzakhala pakati pa misasayo. Iwo adzasamuka monga momwe anamangira misasa yawo, aliyense pa malo ake pamene pali mbendera yake.

18 Kumadzulo kudzakhala magulu a msasa wa Efereimu pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa Aefereimuwo ndi Elisama mwana wa Amihudi. 19 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 40,500.

20 Fuko la Manase lidzakhala pafupi ndi Efereimu. Mtsogoleri wa Amanase ndi Gamalieli mwana wa Pedazuri. 21 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 32,200.

22 Lotsatira lidzakhala fuko la Benjamini. Mtsogoleri wa Abenjamini ndi Abidani mwana wa Gideoni. 23 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 35,400.

24 Anthu onse aamuna mu msasa wa Efereimu, chiwerengero chawo ndi 108,100 monga mwa magulu awo. Iwowo azikhala achitatu posamuka.

25 Kumpoto kudzakhala msasa wa magulu a Dani pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa Adani ndi Ahiyezeri mwana wa Amisadai. 26 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 62,700.

27 Fuko la Aseri lidzamanga pafupi ndi iwowo. Mtsogoleri wa Aaseri ndi Pagieli mwana wa Okirani. 28 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 41,500.

29 Lotsatira lidzakhala fuko la Nafutali. Mtsogoleri wa Anafutali ndi Ahira mwana wa Enani. 30 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 53,400.

31 Anthu onse aamuna mu msasa wa Dani chiwerengero chawo ndi 157,600. Iwo azidzanyamuka pomaliza, ndi mbendera zawo.

32 Amenewa ndi Aisraeli monga mwa mabanja a makolo awo. Chiwerengero cha Aisraeli onse mʼmisasa chinali 603,550, mwa magulu awo. 33 Koma Alevi sanawawerenge pamodzi ndi Aisraeli enawo monga momwe Yehova analamulira Mose.

34 Choncho Aisraeli anachita zonse zomwe Yehova analamulira Mose. Umo ndi momwe amamangira misasa yawo pamene panali mbendera zawo, ndipo ankasamuka monga mwa mafuko a makolo awo.

The Arrangement of the Tribal Camps

The Lord said to Moses and Aaron: “The Israelites are to camp around the tent of meeting some distance from it, each of them under their standard(A) and holding the banners of their family.”

On the east, toward the sunrise, the divisions of the camp of Judah are to encamp under their standard. The leader of the people of Judah is Nahshon son of Amminadab.(B) His division numbers 74,600.

The tribe of Issachar(C) will camp next to them. The leader of the people of Issachar is Nethanel son of Zuar.(D) His division numbers 54,400.

The tribe of Zebulun will be next. The leader of the people of Zebulun is Eliab son of Helon.(E) His division numbers 57,400.

All the men assigned to the camp of Judah, according to their divisions, number 186,400. They will set out first.(F)

10 On the south(G) will be the divisions of the camp of Reuben under their standard. The leader of the people of Reuben is Elizur son of Shedeur.(H) 11 His division numbers 46,500.

12 The tribe of Simeon(I) will camp next to them. The leader of the people of Simeon is Shelumiel son of Zurishaddai.(J) 13 His division numbers 59,300.

14 The tribe of Gad(K) will be next. The leader of the people of Gad is Eliasaph son of Deuel.[a](L) 15 His division numbers 45,650.

16 All the men assigned to the camp of Reuben,(M) according to their divisions, number 151,450. They will set out second.

17 Then the tent of meeting and the camp of the Levites(N) will set out in the middle of the camps. They will set out in the same order as they encamp, each in their own place under their standard.

18 On the west(O) will be the divisions of the camp of Ephraim(P) under their standard. The leader of the people of Ephraim is Elishama son of Ammihud.(Q) 19 His division numbers 40,500.

20 The tribe of Manasseh(R) will be next to them. The leader of the people of Manasseh is Gamaliel son of Pedahzur.(S) 21 His division numbers 32,200.

22 The tribe of Benjamin(T) will be next. The leader of the people of Benjamin is Abidan son of Gideoni.(U) 23 His division numbers 35,400.

24 All the men assigned to the camp of Ephraim,(V) according to their divisions, number 108,100. They will set out third.(W)

25 On the north(X) will be the divisions of the camp of Dan under their standard.(Y) The leader of the people of Dan is Ahiezer son of Ammishaddai.(Z) 26 His division numbers 62,700.

27 The tribe of Asher will camp next to them. The leader of the people of Asher is Pagiel son of Okran.(AA) 28 His division numbers 41,500.

29 The tribe of Naphtali(AB) will be next. The leader of the people of Naphtali is Ahira son of Enan.(AC) 30 His division numbers 53,400.

31 All the men assigned to the camp of Dan number 157,600. They will set out last,(AD) under their standards.

32 These are the Israelites, counted according to their families.(AE) All the men in the camps, by their divisions, number 603,550.(AF) 33 The Levites, however, were not counted(AG) along with the other Israelites, as the Lord commanded Moses.

34 So the Israelites did everything the Lord commanded Moses; that is the way they encamped under their standards, and that is the way they set out, each of them with their clan and family.

Footnotes

  1. Numbers 2:14 Many manuscripts of the Masoretic Text, Samaritan Pentateuch and Vulgate (see also 1:14); most manuscripts of the Masoretic Text Reuel