Add parallel Print Page Options

Kuwonongedwa kwa Aradi

21 Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi, imene inkakhala ku Negevi, itamva kuti Aisraeli akubwera kudzera msewu wopita ku Atarimu, inachita nkhondo ndi Aisraeli nigwira ena mwa iwo. Ndipo Israeli anachita lonjezo ili kwa Yehova: “Mukapereka anthu awa mʼdzanja lathu ife tidzawonongeratu mizinda yawo.” Yehova anamva pempho la Aisraeli ndipo anapereka Akanaaniwo kwa iwo. Anawawononga pamodzi ndi mizinda yawo. Kotero malowo anatchedwa Horima.

Njoka Yamkuwa

Aisraeli anayenda kuchokera ku phiri la Hori kudzera njira ya ku Nyanja Yofiira kuzungulira dziko la Edomu. Koma anthu anataya mtima mʼnjiramo ndipo anayankhula motsutsana ndi Mulungu ndi Mose, nati, “Chifukwa chiyani munatitulutsa kuchoka mʼdziko la Igupto kuti tidzafere mʼchipululu muno? Kuno kulibe chakudya, kulibe madzi ndipo chakudya cha chabechabechi tatopa nacho.”

Choncho Yehova anatumiza njoka zaululu pakati pawo. Zinaluma anthu ndipo Aisraeli ambiri anafa. Anthuwo anabwera kwa Mose ndi kunena kuti, “Tachimwa chifukwa tayankhula motsutsana ndi Yehova komanso inu. Pempherani kwa Yehova kuti atichotsere njokazi.” Tsono Mose anapempherera anthuwo.

Yehova anati kwa Mose, “Upange njoka yaululu ndipo uyipachike pa mtengo. Aliyense amene walumidwa akangoyangʼana njokayo adzakhala ndi moyo.” Pamenepo Mose anapanga njoka yamkuwa ndi kuyipachika pa mtengo. Ndipo aliyense wolumidwa akayangʼana njoka yamkuwayo ankakhala ndi moyo.

Ulendo wa ku Mowabu

10 Aisraeli anayendabe nakamanga misasa yawo ku Oboti. 11 Kenaka anasamuka ku Oboti nakamanga misasa yawo ku Iye-Abarimu, mʼchipululu chimene chili kummawa kwa Mowabu, kotulukira dzuwa. 12 Kuchoka kumeneko anayendabe nakamanga misasa yawo mʼchigwa cha Zeredi. 13 Anasamukanso kumeneko nakamanga moyandikana ndi Arinoni mʼdera limene lili mʼchipululu chimene chimafika mʼdziko la Aamori. Arinoni ndiwo malire a Mowabu ndi Aamori. 14 Nʼchifukwa chake Buku la Nkhondo za Yehova limati,

“Mzinda wa Wahebu uli mu Sufa,
mu zigwa za Arinoni, 15     ku matsitso a zigwa
amene afika mpaka ku Ari
    nakhudza malire a dziko la Mowabu.”

16 Kuchokera kumeneko anapitirira mpaka ku Beeri, pa chitsime chomwe Yehova anawuza Mose kuti, “Sonkhanitsa anthu pamodzi ndipo ndidzawapatsa madzi.”

17 Pamenepo Aisraeli anayimba nyimbo iyi:

“Tulutsa madzi, chitsime iwe!
    Chiyimbireni nyimbo,
18 chitsime chomwe anakumba mafumu,
    chomwe anakumba anthu omveka,
    ndi ndodo zawo zaufumu ndi ndodo zawo zoyendera.”

Kenaka anachoka ku chipululu ndi kupita ku Matana. 19 Kuchoka ku Matana anapita ku Nahalieli, kuchoka ku Nahalieli anapita ku Bamoti, 20 ndipo atachoka ku Bamoti anapita ku chigwa cha dziko la Mowabu kudzera njira ya pamwamba pa phiri la Pisiga, moyangʼanana ndi Yesimoni.

Kugonjetsedwa kwa Sihoni ndi Ogi

21 Aisraeli anatumiza amithenga kwa Sihoni mfumu ya Aamori, kuti,

22 “Tiloleni kuti tidutse mʼdziko mwanu. Sitidzapatukira mʼminda mwanu kapena mu mpesa wanu kapena kumwa madzi mʼchitsime chili chonse. Tidzayenda mu msewu waukulu wa mfumu mpaka titadutsa malire a dziko lanu.”

23 Koma Sihoni sanalole kuti Aisraeli adutse mʼdziko mwake. Iye anasonkhanitsa pamodzi ankhondo ake onse kuti akamenyane ndi Aisraeli mʼchipululu. Atafika pa Yahazi anamenyana ndi Aisraeli. 24 Koma Aisraeli anamupha ndi kulanda dziko lake kuchokera ku Arinoni mpaka ku Yaboki, kulekezera mʼmalire a dziko la Aamoni, chifukwa malire a dziko la Aamoni anali otetezedwa. 25 Ndipo Aisraeli analanda mizinda yonse ya Aamori, nakhalamo kuphatikizapo Hesiboni ndi midzi yake yozungulira. 26 Hesiboni unali mzinda wa Sihoni mfumu ya Aamori, yemwe anamenyana ndi mfumu yakale ya dziko la Mowabu. Lonselo linakhala dziko lake mpaka ku Arinoni.

27 Nʼchifukwa chake alakatuli amati:

“Bwerani ku Hesiboni, mzindawo umangidwenso;
    mzinda wa Sihoni ukhazikike.

28 “Moto unabuka ku Hesiboni,
    malawi a moto kuchokera mu mzinda wa Sihoni.
Unanyeketsa Ari mzinda wa ku Mowabu,
    nzika za ku malo okwera a Arinoni.
29 Tsoka kwa iwe Mowabu!
    Mwawonongedwa inu anthu a ku Kemosi!
Ana ake aamuna wawasandutsa ngati anthu othawathawa
    ndipo ana ake aakazi ngati akapolo,
    akapolo a Sihoni, mfumu ya Aamori.

30 “Koma ife tawagonjetsa;
    Hesiboni wawonongedwa mʼnjira monse mpaka kufika ku Diboni.
Tawaphwasula mpaka ku mzinda wa Nofa,
    mzinda womwe umafika ku Medeba.

31 “Choncho Aisraeli anakhala mʼdziko la Aamori.”

32 Mose atatumiza azondi ku Yazeri, Aisraeliwo analanda midzi yozungulira ndi kuthamangitsa Aamori omwe ankakhala kumeneko. 33 Kenaka anabwerera, nadzera njira ya ku Basani. Choncho Ogi mfumu ya ku Basani ndi gulu lake lonse lankhondo anatuluka kukakumana nawo ndipo anamenyana nawo ku Ederi.

34 Yehova anati kwa Mose, “Usachite naye mantha pakuti ndamupereka mʼmanja mwako pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo ndi dziko lake lomwe. Ndipo uchite kwa iye zimene unachita Sihoni mfumu ya Aamori, amene ankalamulira ku Hesiboni.”

35 Choncho Aisraeli anapha Ogi pamodzi ndi ana ake aamuna ndi gulu lake lonse la nkhondo. Palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala wamoyo, ndipo analanda dziko lakelo.

Arad Destroyed

21 When the Canaanite king of Arad,(A) who lived in the Negev,(B) heard that Israel was coming along the road to Atharim, he attacked the Israelites and captured some of them. Then Israel made this vow(C) to the Lord: “If you will deliver these people into our hands, we will totally destroy[a](D) their cities.” The Lord listened to Israel’s plea and gave the Canaanites(E) over to them. They completely destroyed them(F) and their towns; so the place was named Hormah.[b](G)

The Bronze Snake

They traveled from Mount Hor(H) along the route to the Red Sea,[c](I) to go around Edom.(J) But the people grew impatient on the way;(K) they spoke against God(L) and against Moses, and said, “Why have you brought us up out of Egypt(M) to die in the wilderness?(N) There is no bread! There is no water!(O) And we detest this miserable food!”(P)

Then the Lord sent venomous snakes(Q) among them; they bit the people and many Israelites died.(R) The people came to Moses(S) and said, “We sinned(T) when we spoke against the Lord and against you. Pray that the Lord(U) will take the snakes away from us.” So Moses prayed(V) for the people.

The Lord said to Moses, “Make a snake and put it up on a pole;(W) anyone who is bitten can look at it and live.” So Moses made a bronze snake(X) and put it up on a pole. Then when anyone was bitten by a snake and looked at the bronze snake, they lived.(Y)

The Journey to Moab

10 The Israelites moved on and camped at Oboth.(Z) 11 Then they set out from Oboth and camped in Iye Abarim, in the wilderness that faces Moab(AA) toward the sunrise. 12 From there they moved on and camped in the Zered Valley.(AB) 13 They set out from there and camped alongside the Arnon(AC), which is in the wilderness extending into Amorite territory. The Arnon is the border of Moab, between Moab and the Amorites.(AD) 14 That is why the Book of the Wars(AE) of the Lord says:

“. . . Zahab[d] in Suphah and the ravines,
    the Arnon 15 and[e] the slopes of the ravines
that lead to the settlement of Ar(AF)
    and lie along the border of Moab.”

16 From there they continued on to Beer,(AG) the well where the Lord said to Moses, “Gather the people together and I will give them water.”

17 Then Israel sang this song:(AH)

“Spring up, O well!
    Sing about it,
18 about the well that the princes dug,
    that the nobles of the people sank—
    the nobles with scepters and staffs.”

Then they went from the wilderness to Mattanah, 19 from Mattanah to Nahaliel, from Nahaliel to Bamoth, 20 and from Bamoth to the valley in Moab where the top of Pisgah(AI) overlooks the wasteland.

Defeat of Sihon and Og

21 Israel sent messengers(AJ) to say to Sihon(AK) king of the Amorites:(AL)

22 “Let us pass through your country. We will not turn aside into any field or vineyard, or drink water from any well. We will travel along the King’s Highway until we have passed through your territory.(AM)

23 But Sihon would not let Israel pass through his territory.(AN) He mustered his entire army and marched out into the wilderness against Israel. When he reached Jahaz,(AO) he fought with Israel.(AP) 24 Israel, however, put him to the sword(AQ) and took over his land(AR) from the Arnon to the Jabbok,(AS) but only as far as the Ammonites,(AT) because their border was fortified. 25 Israel captured all the cities of the Amorites(AU) and occupied them,(AV) including Heshbon(AW) and all its surrounding settlements. 26 Heshbon was the city of Sihon(AX) king of the Amorites,(AY) who had fought against the former king of Moab(AZ) and had taken from him all his land as far as the Arnon.(BA)

27 That is why the poets say:

“Come to Heshbon and let it be rebuilt;
    let Sihon’s city be restored.

28 “Fire went out from Heshbon,
    a blaze from the city of Sihon.(BB)
It consumed(BC) Ar(BD) of Moab,
    the citizens of Arnon’s heights.(BE)
29 Woe to you, Moab!(BF)
    You are destroyed, people of Chemosh!(BG)
He has given up his sons as fugitives(BH)
    and his daughters as captives(BI)
    to Sihon king of the Amorites.

30 “But we have overthrown them;
    Heshbon’s dominion has been destroyed all the way to Dibon.(BJ)
We have demolished them as far as Nophah,
    which extends to Medeba.(BK)

31 So Israel settled in the land of the Amorites.(BL)

32 After Moses had sent spies(BM) to Jazer,(BN) the Israelites captured its surrounding settlements and drove out the Amorites who were there. 33 Then they turned and went up along the road toward Bashan(BO),(BP) and Og king of Bashan and his whole army marched out to meet them in battle at Edrei.(BQ)

34 The Lord said to Moses, “Do not be afraid of him, for I have delivered him into your hands, along with his whole army and his land. Do to him what you did to Sihon king of the Amorites, who reigned in Heshbon.(BR)

35 So they struck him down, together with his sons and his whole army, leaving them no survivors.(BS) And they took possession of his land.(BT)

Footnotes

  1. Numbers 21:2 The Hebrew term refers to the irrevocable giving over of things or persons to the Lord, often by totally destroying them; also in verse 3.
  2. Numbers 21:3 Hormah means destruction.
  3. Numbers 21:4 Or the Sea of Reeds
  4. Numbers 21:14 Septuagint; Hebrew Waheb
  5. Numbers 21:15 Or “I have been given from Suphah and the ravines / of the Arnon 15 to