Add parallel Print Page Options

Aisraeli Achita Chigololo

25 Aisraeli akukhala ku Sitimu, anayamba kuchita chigololo ndi akazi a ku Mowabu, amene ankawayitana ku nsembe za milungu yawo. Anthuwo anadya chakudya chopereka kwa milungu ndi kupembedza milunguyo. Motero Aisraeli anapembedza nawo Baala-Peori ndipo Yehova anawapsera mtima kwambiri.

Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti, “Tenga atsogoleri onse a anthu awa, uwaphe poyera, pamaso pa Yehova kuti mkwiyo waukulu wa Yehova uchoke pa Israeli.”

Choncho Mose anawuza oweruza a Israeli kuti, “Aliyense wa inu ayenera kupha anthu ake amene anapembedza nawo Baala-Peori.”

Kenaka mwamuna wina wa ku Israeli anabweretsa ku banja lake mkazi wa Chimidiyani pamaso pa Mose ndi anthu onse a Israeli pamene ankalira pa khomo la tenti ya msonkhano. Finehasi mwana wa Eliezara, mwana wa wansembe Aaroni ataona izi, anachoka pa msonkhanowo, natenga mkondo mʼdzanja lake. Ndipo anatsatira Mwisraeliyu mpaka mʼtenti yake. Anasolola mkondowo ndi kubaya awiriwo kupyola Mwisraeliyo mpaka mʼthupi la mkaziyo. Pamenepo mliri unaleka pakati pa Aisraeli. Pa mliriwo, anthu okwana 24,000 anafa.

10 Yehova anawuza Mose kuti, 11 “Finehasi mwana wa Eliezara, mwana wa wansembe Aaroni wabweza mkwiyo wanga pa Aisraeli chifukwa sanalole kuti wina aliyense apembedze mulungu wina koma Ine ndekha. Nʼchifukwa chake sindinawawononge mu mkwiyo wanga. 12 Tsono muwuze kuti ndikhazikitsa pangano langa la mtendere ndi iye. 13 Ndikupangana naye pangano la unsembe wosatha, iyeyo pamodzi ndi zidzukulu zake zonse, chifukwa sanalole kuti anthu awukire Ine Mulungu, ndipo anachita ntchito yopepesera machimo Aisraeli.”

14 Dzina la Mwisraeli yemwe anaphedwa ndi mkazi wa Chimidiyani anali Zimuri mwana wa Salu, mtsogoleri wa banja la Simeoni. 15 Ndipo dzina la mkazi wa Chimidiyani, yemwe anaphedwayo, linali Kozibi mwana wa Zuri, mtsogoleri wa fuko la ku Midiyaniko.

16 Yehova anawuza Mose kuti, 17 “Amidiyani ndi adani anu ndipo uwaphe, 18 chifukwa ankakuonani inu ngati adani awo pamene anakupusitsani pa nkhani ya ku Peori, ndiponso za mlongo wawo Kozibi, mwana wamkazi wa mtsogoleri wa Amidiyani, mkazi yemwe anaphedwa pamene mliri unabwera chifukwa cha zimene zinachitika ku Peori.”

Moab Seduces Israel

25 While Israel was staying in Shittim,(A) the men began to indulge in sexual immorality(B) with Moabite(C) women,(D) who invited them to the sacrifices(E) to their gods.(F) The people ate the sacrificial meal and bowed down before these gods. So Israel yoked themselves to(G) the Baal of Peor.(H) And the Lord’s anger burned against them.

The Lord said to Moses, “Take all the leaders(I) of these people, kill them and expose(J) them in broad daylight before the Lord,(K) so that the Lord’s fierce anger(L) may turn away from Israel.”

So Moses said to Israel’s judges, “Each of you must put to death(M) those of your people who have yoked themselves to the Baal of Peor.”(N)

Then an Israelite man brought into the camp a Midianite(O) woman right before the eyes of Moses and the whole assembly of Israel while they were weeping(P) at the entrance to the tent of meeting. When Phinehas(Q) son of Eleazar, the son of Aaron, the priest, saw this, he left the assembly, took a spear(R) in his hand and followed the Israelite into the tent. He drove the spear into both of them, right through the Israelite man and into the woman’s stomach. Then the plague against the Israelites was stopped;(S) but those who died in the plague(T) numbered 24,000.(U)

10 The Lord said to Moses, 11 “Phinehas son of Eleazar, the son of Aaron, the priest, has turned my anger away from the Israelites.(V) Since he was as zealous for my honor(W) among them as I am, I did not put an end to them in my zeal. 12 Therefore tell him I am making my covenant of peace(X) with him. 13 He and his descendants will have a covenant of a lasting priesthood,(Y) because he was zealous(Z) for the honor(AA) of his God and made atonement(AB) for the Israelites.”(AC)

14 The name of the Israelite who was killed with the Midianite woman(AD) was Zimri son of Salu, the leader of a Simeonite family.(AE) 15 And the name of the Midianite woman who was put to death was Kozbi(AF) daughter of Zur, a tribal chief of a Midianite family.(AG)

16 The Lord said to Moses,(AH) 17 “Treat the Midianites(AI) as enemies(AJ) and kill them.(AK) 18 They treated you as enemies when they deceived you in the Peor incident(AL) involving their sister Kozbi, the daughter of a Midianite leader, the woman who was killed when the plague came as a result of that incident.”