Add parallel Print Page Options

Kalembera Wachiwiri

26 Utatha mliri Yehova anati kwa Mose ndi Eliezara mwana wa Aaroni, “Werengani Aisraeli onse mwa mabanja awo, onse a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli.” Kotero mu zigwa za Mowabu pafupi ndi mtsinje wa Yorodani ku Yeriko, Mose ndi wansembe Eliezara anayankhula nawo kuti, “Werengani amuna a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo, monga momwe Yehova walamulira Mose.”

Aisraeli omwe anachokera ku Igupto ndi awa:

Zidzukulu za Rubeni, mwana woyamba wamwamuna wa Israeli, zinali izi:

kuchokera mwa Hanoki, fuko la Ahanoki;

kuchokera mwa Palu, fuko la Apalu;

kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi;

kuchokera mwa Karimi, fuko la Akarimi.

Awa anali mafuko a Rubeni: onse amene anawerengedwa analipo 43,730.

Mwana wa Palu anali Eliabu, ndipo ana a Eliabu anali Nemueli, Datani ndi Abiramu. Datani ndi Abiramu anali gulu la akuluakulu aja amene anawukira Mose ndi Aaroni ndipo analinso mʼgulu la otsatira Kora pamene anawukira Yehova. 10 Nthaka inangʼambika ndi kuwameza pamodzi ndi Kora, kotero kuti gulu lawo linafa pamene moto unapsereza anthu 250 aja, nasanduka chenjezo. 11 Koma ana a Kora sanafe nawo.

12 Zidzukulu za Simeoni mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Nemueli, fuko la Anemuele;

kuchokera mwa Yamini, fuko la Ayamini;

kuchokera mwa Yakini fuko la Ayakini;

13 kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera;

kuchokera mwa Sauli, fuko la Asauli.

14 Awa anali mafuko a Simeoni. Iwowa analipo amuna 22,200.

15 Zidzukulu za Gadi mwa mafuko awo ndi izi:

kuchokera mwa Zefoni, fuko la Azefoni;

kuchokera mwa Hagi, fuko la Ahagi;

kuchokera mwa Suni, fuko la Asuni;

16 kuchokera mwa Ozini, fuko la Aozini;

kuchokera mwa Eri, fuko la Aeri;

17 kuchokera mwa Arodi, fuko la Aarodi;

kuchokera mwa Arieli, fuko la a Areli.

18 Awa ndiwo anali mafuko a Gadi. Onse amene anawerengedwa analipo 40,500.

19 Eri ndi Onani anali ana aamuna a Yuda, koma anafera mu Kanaani.

20 Zidzukulu za Yuda monga mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Sela, fuko la Asera;

kuchokera mwa Perezi, fuko la Aperezi;

kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera.

21 Zidzukulu za Perezi zinali izi:

kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi;

kuchokera mwa Hamuli, fuko la Ahamuli.

22 Awa ndiwo anali mafuko a Yuda. Amene anawerenga analipo 76,500.

23 Zidzukulu za Isakara monga mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Tola, fuko la Atola;

kuchokera mwa Puwa, fuko la Apuwa;

24 kuchokera mwa Yasubu, fuko la Ayasubu.

Kuchokera mwa Simironi, fuko la Asimironi.

25 Awa ndi amene anali a fuko la Isakara. Amene anawerengedwa analipo 64,300.

26 Zidzukulu za Zebuloni mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Seredi, fuko la Aseredi;

kuchokera mwa Eloni, fuko la Aeloni;

kuchokera mwa Yahaleeli, fuko la Ayahaleeli.

27 Awa ndiwo anali mafuko a Zebuloni. Amene anawerengedwa analipo 60,500.

28 Zidzukulu za Yosefe mwa mafuko awo kupyolera mwa Manase ndi Efereimu zinali izi:

29 Zidzukulu za Manase:

kuchokera mwa Makiri, fuko la Amakiri (Makiri anali abambo ake a Giliyadi);

kuchokera mwa Giliyadi, fuko la Agiliyadi.

30 Izi ndizo zinali zidzukulu za Giliyadi;

kuchokera mwa Iyezeri, fuko la Aiyezeri;

kuchokera mwa Heleki, fuko la Aheleki;

31 kuchokera mwa Asirieli, fuko la Aasirieli;

kuchokera mwa Sekemu, fuko la Asekemu;

32 kuchokera mwa Semida, fuko la Asemida;

kuchokera mwa Heferi, fuko la Aheferi.

33 (Zelofehadi mwana wa Heferi analibe ana aamuna koma ana aakazi okha, amene mayina awo anali: Mala, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza.)

34 Awa ndiwo anali mafuko a Manase. Amene anawerengedwa analipo 52,700.

35 Zidzukulu za Efereimu monga mwa mafuko awo zinali izi;

kuchokera mwa Sutela, fuko la Asutela;

kuchokera mwa Bekeri, fuko la Abekeri;

kuchokera mwa Tahani, fuko la Atahani.

36 Zidzukulu za Sutela zinali izi:

kuchokera mwa Erani, fuko la Aerani.

37 Awa ndiwo anali mafuko a Efereimu. Amene anawerengedwa analipo 32,500.

Zimenezi zinali zidzukulu za Yosefe monga mwa mafuko awo.

38 Zidzukulu za Benjamini monga mwa mabanja awo zinali izi:

kuchokera mwa Bela, fuko la Abela;

kuchokera mwa Asibeli, fuko la Aasibeli;

kuchokera mwa Ahiramu, fuko la Ahiramu;

39 kuchokera mwa Sufamu, fuko la Asufamu;

kuchokera mwa Hufamu, fuko la Ahufamu;

40 Zidzukulu za Bela kupyolera mwa Aridi ndi Naamani zinali izi:

kuchokera mwa Aridi, fuko la Aaridi;

kuchokera mwa Naamani, fuko la Anaamani;

41 Awa ndiwo anali mabanja a Benjamini. Amene nawerengedwa analipo 45,600.

42 Zidzukulu za Dani mwa mabanja awo zinali izi:

kuchokera mwa Suhamu fuko la Asuhamu.

Izi zinali zidzukulu za Dani. 43 Onse a fuko la Asuhamu amene anawerengedwa analipo 64,400.

44 Zidzukulu za Aseri monga mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Imina, fuko la Aimuna;

kuchokera mwa Isivi, fuko la Ayisivi;

kuchokera mwa Beriya, fuko la Aberiya;

45 ndipo kupyolera mwa zidzukulu za Beriya:

kuchokera mwa Heberi, fuko la Aheberi;

kuchokera mwa Malikieli, fuko la Amalikieli;

46 (Aseri anali ndi mwana wamkazi dzina lake Sera)

47 Awa ndiwo anali mafuko a Aseri. Onse amene anawerengedwa analipo 53,400.

48 Zidzukulu za Nafutali mwa mafuko awo zinali izi:

kuchokera mwa Yahazeeli, fuko la Ayahazeeli;

kuchokera mwa Guni, fuko la Aguni;

49 kuchokera mwa Yezeri, fuko la Ayezeri;

kuchokera mwa Silemu, fuko la Asilemu.

50 Awa ndiwo anali mafuko a Nafutali. Onse amene anawerengedwa analipo 45,400.

51 Chiwerengero chonse cha amuna mu Israeli chinalipo 601,730.

52 Yehova anawuza Mose kuti, 53 “Uwagawire dziko anthu awa kuti likhale cholowa chawo molingana ndi chiwerengero cha mayina awo. 54 Gulu lalikulu ulipatse cholowa chachikulu, ndipo lochepa cholowa chocheperapo. Gulu lililonse lilandire cholowa chake molingana ndi chiwerengero cha amene anawerengedwa. 55 Dzikolo uligawe pochita maere. Alandire cholowa chawocho potsata mayina a mafuko a makolo awo. 56 Cholowa chawo uchigawe pakati pa fuko lalikulu ndi lalingʼono mwa maere.”

57 Alevi omwe anawerengedwa monga mwa mafuko awo ndi awa:

kuchokera mwa Geresoni, fuko la Ageresoni;

kuchokera mwa Kohati, fuko la Akohati;

kuchokera mwa Merari, fuko la Amerari.

58 Awanso anali mabanja a Alevi:

banja la Alibini,

banja la Ahebroni,

banja la Amali,

banja la Amusi, fuko la Kora

banja la Akohati,

(Kohati anali abambo a Amramu. 59 Dzina la mkazi wa Amramu linali Yokobedi, mdzukulu wa Levi, yemwe anabadwa mwa Alevi mu Igupto. Yokobedi anaberekera Amramu Aaroni, Mose ndi Miriamu mlongo wawo. 60 Aaroni anali abambo a Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara. 61 Koma Nadabu ndi Abihu anafa pamene anapereka nsembe pamaso pa Yehova ndi moto wachilendo).

62 Alevi onse aamuna a mwezi umodzi kapena kuposera pamenepa analipo 23,000. Iwowo sanawerengedwe pamodzi ndi Aisraeli ena chifukwa sanalandire cholowa pakati pawo.

63 Awa ndi amene anawerengedwa ndi Mose ndi Eliezara wansembe pamene ankawerenga Aisraeli pa zigwa za ku Mowabu mʼmbali mwa Yorodani ku Yeriko. 64 Mwa anthu amenewa panalibe ndi mmodzi yemwe amene anali mʼgulu la Aisraeli omwe Mose ndi wansembe Aaroni anawawerenga mʼchipululu cha Sinai; 65 Chifukwa Yehova anali atawuza Aisraeliwo kuti adzafera ndithu mʼchipululu, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala kupatula Kalebe mwana wa Yefune ndi Yoswa mwana wa Nuni.

The Second Census

26 After the plague(A) the Lord said to Moses and Eleazar son of Aaron, the priest, “Take a census(B) of the whole Israelite community by families—all those twenty years old or more who are able to serve in the army(C) of Israel.” So on the plains of Moab(D) by the Jordan across from Jericho,(E) Moses and Eleazar the priest spoke with them and said, “Take a census of the men twenty years old or more, as the Lord commanded Moses.”

These were the Israelites who came out of Egypt:(F)

The descendants of Reuben,(G) the firstborn son of Israel, were:

through Hanok,(H) the Hanokite clan;

through Pallu,(I) the Palluite clan;

through Hezron,(J) the Hezronite clan;

through Karmi,(K) the Karmite clan.

These were the clans of Reuben; those numbered were 43,730.

The son of Pallu was Eliab, and the sons of Eliab(L) were Nemuel, Dathan and Abiram. The same Dathan and Abiram were the community(M) officials who rebelled against Moses and Aaron and were among Korah’s followers when they rebelled against the Lord.(N) 10 The earth opened its mouth and swallowed them(O) along with Korah, whose followers died when the fire devoured the 250 men.(P) And they served as a warning sign.(Q) 11 The line of Korah,(R) however, did not die out.(S)

12 The descendants of Simeon by their clans were:

through Nemuel,(T) the Nemuelite clan;

through Jamin,(U) the Jaminite clan;

through Jakin, the Jakinite clan;

13 through Zerah,(V) the Zerahite clan;

through Shaul, the Shaulite clan.

14 These were the clans of Simeon;(W) those numbered were 22,200.(X)

15 The descendants of Gad by their clans were:

through Zephon,(Y) the Zephonite clan;

through Haggi, the Haggite clan;

through Shuni, the Shunite clan;

16 through Ozni, the Oznite clan;

through Eri, the Erite clan;

17 through Arodi,[a] the Arodite clan;

through Areli, the Arelite clan.

18 These were the clans of Gad;(Z) those numbered were 40,500.

19 Er(AA) and Onan(AB) were sons of Judah, but they died(AC) in Canaan.

20 The descendants of Judah by their clans were:

through Shelah,(AD) the Shelanite clan;

through Perez,(AE) the Perezite clan;

through Zerah, the Zerahite clan.(AF)

21 The descendants of Perez(AG) were:

through Hezron,(AH) the Hezronite clan;

through Hamul, the Hamulite clan.

22 These were the clans of Judah;(AI) those numbered were 76,500.

23 The descendants of Issachar by their clans were:

through Tola,(AJ) the Tolaite clan;

through Puah, the Puite[b] clan;

24 through Jashub,(AK) the Jashubite clan;

through Shimron, the Shimronite clan.

25 These were the clans of Issachar;(AL) those numbered were 64,300.

26 The descendants of Zebulun(AM) by their clans were:

through Sered, the Seredite clan;

through Elon, the Elonite clan;

through Jahleel, the Jahleelite clan.

27 These were the clans of Zebulun;(AN) those numbered were 60,500.

28 The descendants of Joseph(AO) by their clans through Manasseh and Ephraim(AP) were:

29 The descendants of Manasseh:(AQ)

through Makir,(AR) the Makirite clan (Makir was the father of Gilead(AS));

through Gilead, the Gileadite clan.

30 These were the descendants of Gilead:(AT)

through Iezer,(AU) the Iezerite clan;

through Helek, the Helekite clan;

31 through Asriel, the Asrielite clan;

through Shechem, the Shechemite clan;

32 through Shemida, the Shemidaite clan;

through Hepher, the Hepherite clan.

33 (Zelophehad(AV) son of Hepher had no sons;(AW) he had only daughters, whose names were Mahlah, Noah, Hoglah, Milkah and Tirzah.)(AX)

34 These were the clans of Manasseh; those numbered were 52,700.(AY)

35 These were the descendants of Ephraim(AZ) by their clans:

through Shuthelah, the Shuthelahite clan;

through Beker, the Bekerite clan;

through Tahan, the Tahanite clan.

36 These were the descendants of Shuthelah:

through Eran, the Eranite clan.

37 These were the clans of Ephraim;(BA) those numbered were 32,500.

These were the descendants of Joseph by their clans.

38 The descendants of Benjamin(BB) by their clans were:

through Bela, the Belaite clan;

through Ashbel, the Ashbelite clan;

through Ahiram, the Ahiramite clan;

39 through Shupham,[c] the Shuphamite clan;

through Hupham, the Huphamite clan.

40 The descendants of Bela through Ard(BC) and Naaman were:

through Ard,[d] the Ardite clan;

through Naaman, the Naamite clan.

41 These were the clans of Benjamin;(BD) those numbered were 45,600.

42 These were the descendants of Dan(BE) by their clans:(BF)

through Shuham,(BG) the Shuhamite clan.

These were the clans of Dan: 43 All of them were Shuhamite clans; and those numbered were 64,400.

44 The descendants of Asher(BH) by their clans were:

through Imnah, the Imnite clan;

through Ishvi, the Ishvite clan;

through Beriah, the Beriite clan;

45 and through the descendants of Beriah:

through Heber, the Heberite clan;

through Malkiel, the Malkielite clan.

46 (Asher had a daughter named Serah.)

47 These were the clans of Asher;(BI) those numbered were 53,400.

48 The descendants of Naphtali(BJ) by their clans were:

through Jahzeel, the Jahzeelite clan;

through Guni, the Gunite clan;

49 through Jezer, the Jezerite clan;

through Shillem, the Shillemite clan.

50 These were the clans of Naphtali;(BK) those numbered were 45,400.(BL)

51 The total number of the men of Israel was 601,730.(BM)

52 The Lord said to Moses, 53 “The land is to be allotted to them as an inheritance based on the number of names.(BN) 54 To a larger group give a larger inheritance, and to a smaller group a smaller one; each is to receive its inheritance according to the number(BO) of those listed.(BP) 55 Be sure that the land is distributed by lot.(BQ) What each group inherits will be according to the names for its ancestral tribe. 56 Each inheritance is to be distributed by lot among the larger and smaller groups.”

57 These were the Levites(BR) who were counted by their clans:

through Gershon, the Gershonite clan;

through Kohath, the Kohathite clan;

through Merari, the Merarite clan.

58 These also were Levite clans:

the Libnite clan,

the Hebronite clan,

the Mahlite clan,

the Mushite clan,

the Korahite clan.

(Kohath was the forefather of Amram;(BS) 59 the name of Amram’s wife was Jochebed,(BT) a descendant of Levi, who was born to the Levites[e] in Egypt. To Amram she bore Aaron, Moses(BU) and their sister(BV) Miriam.(BW) 60 Aaron was the father of Nadab and Abihu, Eleazar and Ithamar.(BX) 61 But Nadab and Abihu(BY) died when they made an offering before the Lord with unauthorized fire.)(BZ)

62 All the male Levites a month old or more numbered 23,000.(CA) They were not counted(CB) along with the other Israelites because they received no inheritance(CC) among them.(CD)

63 These are the ones counted(CE) by Moses and Eleazar the priest when they counted the Israelites on the plains of Moab(CF) by the Jordan across from Jericho.(CG) 64 Not one of them was among those counted(CH) by Moses and Aaron(CI) the priest when they counted the Israelites in the Desert of Sinai. 65 For the Lord had told those Israelites they would surely die in the wilderness,(CJ) and not one of them was left except Caleb(CK) son of Jephunneh and Joshua son of Nun.(CL)

Footnotes

  1. Numbers 26:17 Samaritan Pentateuch and Syriac (see also Gen. 46:16); Masoretic Text Arod
  2. Numbers 26:23 Samaritan Pentateuch, Septuagint, Vulgate and Syriac (see also 1 Chron. 7:1); Masoretic Text through Puvah, the Punite
  3. Numbers 26:39 A few manuscripts of the Masoretic Text, Samaritan Pentateuch, Vulgate and Syriac (see also Septuagint); most manuscripts of the Masoretic Text Shephupham
  4. Numbers 26:40 Samaritan Pentateuch and Vulgate (see also Septuagint); Masoretic Text does not have through Ard.
  5. Numbers 26:59 Or Jochebed, a daughter of Levi, who was born to Levi