Add parallel Print Page Options

Ana Aakazi a Zelofehadi

27 Kenaka ana aakazi a Zelofehadi mwana wa Heferi, mwana wa Giliyadi, mwana wa Makiri, mwana wamwamuna wa Manase, a mʼmabanja a Manase, mwana wa Yosefe anabwera. Mayina a ana aakaziwo anali awa: Mala, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza. Iwo anakayima pa chipata cha tenti ya msonkhano pamaso pa Mose, wansembe Eliezara, atsogoleri ndi anthu onse, ndipo anati, “Abambo athu anafera mʼchipululu koma sanali nawo mʼgulu la anthu otsatira Kora, omwe anasonkhana pamodzi kutsutsana ndi Yehova. Abambo athuwo anafa chifukwa cha tchimo lawo ndipo sanasiye ana aamuna. Nʼchifukwa chiyani dzina la abambo athu lasowa pakati pa fuko lawo, kodi popeza analibe mwana wamwamuna? Tipatseni cholowa chathu pakati pa abale a abambo athu.”

Tsono Mose anabweretsa nkhani yawo pamaso pa Yehova ndipo Yehova anati kwa iye, “Zimene ana aakazi a Zelofehadi akunena ndi zoona. Uyenera kuwapatsadi cholowa chawo pakati pa abale a abambo awo ndipo uwapatse cholowa cha abambo awowo.

“Uza Aisraeli kuti, ‘Ngati munthu afa wosasiya mwana wamwamuna, muzipereka cholowa chake kwa mwana wake wamkazi. Ngati alibe mwana wamkazi, muzipereka cholowa chakecho kwa abale ake. 10 Ngati alibe abale muzipereka cholowa chake kwa abale a abambo ake. 11 Ngati abambo ake analibe mʼbale, muzipereka cholowa chakecho kwa mnansi wake wa mʼbanja lake kuti chikhale chake. Ili likhale lamulo kwa Aisraeli, monga momwe Yehova analamulira Mose.’ ”

Yoswa Alowa Mʼmalo mwa Mose

12 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Kwera phiri la Abarimu kuti ukaone dziko limene ndalipereka kwa Aisraeli. 13 Ukakaliona udzamwalira ngati Aaroni mʼbale wako, 14 chifukwa pamene anthu anawukira ku madzi a Meriba mʼchipululu cha Zini, inu nonse simunamvere lamulo londilemekeza Ine ngati Woyera pamaso pawo.” (Awa anali madzi a ku Meriba ku Kadesi mʼchipululu cha Zini).

15 Mose anati kwa Yehova, 16 “Ngati nʼkotheka Yehova, Mulungu wa mizimu ya anthu onse, sankhani munthu woti ayangʼanire gulu ili kuti 17 alitsogolere potuluka ndi polowa, kuti anthu a Yehova asakhale ngati nkhosa zopanda mʼbusa.”

18 Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti, “Tenga Yoswa mwana wa Nuni, munthu amene ali ndi mzimu wa utsogoleri, ndipo umusanjike dzanja lako. 19 Umuyimiritse pamaso pa wansembe Eliezara ndi pamaso pa gulu lonse ndipo umupatse mphamvu zolamulira, anthuwo akuona. 20 Umupatse gawo lina la ulemerero wako kuti Aisraeli onse azimumvera. 21 Ayime pamaso pa wansembe Eliezara, amene adzamudziwitse zimene Yehova akufuna pogwiritsa ntchito Urimu. Iye akalamula, Aisraeli onse azituluka ndipo akalamulanso, Aisraeliwo azibwereranso.”

22 Mose anachita monga Yehova anamulamulira. Anatenga Yoswa ndi kumuyimiritsa pamaso pa Eliezara wansembe ndi pamaso pa gulu lonse. 23 Ndipo anamusanjika manja ndi kumupatsa mphamvu, monga Yehova ananenera kudzera mwa Mose.

Zelophehad’s Daughters(A)

27 The daughters of Zelophehad(B) son of Hepher,(C) the son of Gilead,(D) the son of Makir,(E) the son of Manasseh, belonged to the clans of Manasseh son of Joseph. The names of the daughters were Mahlah, Noah, Hoglah, Milkah and Tirzah. They came forward and stood before Moses,(F) Eleazar the priest, the leaders(G) and the whole assembly at the entrance to the tent of meeting(H) and said, “Our father died in the wilderness.(I) He was not among Korah’s followers, who banded together against the Lord,(J) but he died for his own sin and left no sons.(K) Why should our father’s name disappear from his clan because he had no son? Give us property among our father’s relatives.”

So Moses brought their case(L) before the Lord,(M) and the Lord said to him, “What Zelophehad’s daughters are saying is right. You must certainly give them property as an inheritance(N) among their father’s relatives and give their father’s inheritance to them.(O)

“Say to the Israelites, ‘If a man dies and leaves no son, give his inheritance to his daughter. If he has no daughter, give his inheritance to his brothers. 10 If he has no brothers, give his inheritance to his father’s brothers. 11 If his father had no brothers, give his inheritance to the nearest relative in his clan, that he may possess it. This is to have the force of law(P) for the Israelites, as the Lord commanded Moses.’”

Joshua to Succeed Moses

12 Then the Lord said to Moses, “Go up this mountain(Q) in the Abarim Range(R) and see the land(S) I have given the Israelites.(T) 13 After you have seen it, you too will be gathered to your people,(U) as your brother Aaron(V) was, 14 for when the community rebelled at the waters in the Desert of Zin,(W) both of you disobeyed my command to honor me as holy(X) before their eyes.” (These were the waters of Meribah(Y) Kadesh, in the Desert of Zin.)

15 Moses said to the Lord, 16 “May the Lord, the God who gives breath to all living things,(Z) appoint someone over this community 17 to go out and come in before them, one who will lead them out and bring them in, so the Lord’s people will not be like sheep without a shepherd.”(AA)

18 So the Lord said to Moses, “Take Joshua son of Nun, a man in whom is the spirit of leadership,[a](AB) and lay your hand on him.(AC) 19 Have him stand before Eleazar the priest and the entire assembly and commission him(AD) in their presence.(AE) 20 Give him some of your authority so the whole Israelite community will obey him.(AF) 21 He is to stand before Eleazar the priest, who will obtain decisions for him by inquiring(AG) of the Urim(AH) before the Lord. At his command he and the entire community of the Israelites will go out, and at his command they will come in.”

22 Moses did as the Lord commanded him. He took Joshua and had him stand before Eleazar the priest and the whole assembly. 23 Then he laid his hands on him and commissioned him,(AI) as the Lord instructed through Moses.

Footnotes

  1. Numbers 27:18 Or the Spirit