Add parallel Print Page Options

Chikondwerero cha Malipenga

29 “ ‘Pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Ili ndi tsiku limene muziliza malipenga. Muzipereka mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi wopanda chilema monga nsembe zopsereza, fungo lokoma kwa Yehova. Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzipereka chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa yayimuna iliyonse muzipereka makilogalamu awiri. Pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja muzipereka kilogalamu imodzi. Muziperekanso mbuzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu. Izi ndi zowonjezera pa nsembe zopsereza za mwezi ndi mwezi komanso za tsiku ndi tsiku pamodzi ndi zopereka za chakudya ndi zopereka za chakumwa potsata malamulo ake. Izi ndi zopereka zotentha pa moto, zoperekedwa kwa Yehova, fungo lokoma.

Tsiku la Mwambo Wopepesera Machimo

“ ‘Pa tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiriwu, muzichita msonkhano wopatulika. Muzisala zakudya ndipo musamagwire ntchito. Muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza, yotulutsa fungo lokoma lokondweretsa Yehovayo; ngʼombe yayimuna imodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi. Zimenezi zizikhala zopanda chilema. Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri; 10 kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiriwo. 11 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe yopepesera machimo ya pa tsiku la mwambo ija, kuwonjezanso pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija, pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi cha chakumwa.

Chikondwerero cha Misasa

12 “ ‘Pa tsiku la mwezi wachisanu ndi chiwiri, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Muzichita madyerero a Yehova masiku asanu ndi awiri. 13 Muzipereka nsembe yotentha pa moto, kuti izikhala fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu, nkhosa zazimuna ziwiri, ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema. 14 Pa mwana wangʼombe aliyense mwa ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu aja, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa iliyonse mwa nkhosa ziwiri zija, mukonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri. 15 Pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa aamuna khumi ndi anayiwo, muzipereka chakudya cha kilogalamu imodzi. 16 Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhale nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.

17 “ ‘Pa tsiku lachiwiri muzipereka ana angʼombe aamuna khumi ndi awiri aja, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi aja, zonse zopanda chilema. 18 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo. 19 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.

20 “ ‘Pa tsiku lachitatu muzipereka ngʼombe zazimuna khumi ndi imodzi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema. 21 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo. 22 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.

23 “ ‘Pa tsiku lachinayi muzipereka ngʼombe zazimuna khumi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema. 24 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo. 25 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.

26 “ ‘Pa tsiku lachisanu muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zinayi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema. 27 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo. 28 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.

29 “ ‘Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zitatu, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema. 30 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo. 31 Muziperekenso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.

32 “ ‘Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa amuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema. 33 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo. 34 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.

35 “ ‘Pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzichita msonkhano ndipo musamagwire ntchito iliyonse. 36 Muzipereka chopereka chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ngʼombe imodzi yayimuna, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa amuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema. 37 Pamodzi ndi ngʼombe yayimunayo, nkhosa yayimunayo ndi ana ankhosawo, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo. 38 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.

39 “ ‘Kuwonjezera pa zopereka zimene munalumbirira ndi pa zopereka zanu zaufulu, muzipereka zimenezi kwa Yehova pa masiku osankhika a chikondwerero chanu. Nsembe zanu zachakumwa ndi nsembe zanu zachiyanjano.’ ”

40 Mose anawuza Aisraeli zonse zimene Yehova anamulamulira.

The Festival of Trumpets(A)

29 “‘On the first day of the seventh month hold a sacred assembly and do no regular work.(B) It is a day for you to sound the trumpets. As an aroma pleasing to the Lord,(C) offer a burnt offering(D) of one young bull, one ram and seven male lambs a year old,(E) all without defect.(F) With the bull offer a grain offering(G) of three-tenths of an ephah[a] of the finest flour mixed with olive oil; with the ram, two-tenths[b]; and with each of the seven lambs, one-tenth.[c](H) Include one male goat(I) as a sin offering[d] to make atonement for you. These are in addition to the monthly(J) and daily burnt offerings(K) with their grain offerings(L) and drink offerings(M) as specified. They are food offerings presented to the Lord, a pleasing aroma.(N)

The Day of Atonement(O)

“‘On the tenth day of this seventh month hold a sacred assembly. You must deny yourselves[e](P) and do no work.(Q) Present as an aroma pleasing to the Lord a burnt offering of one young bull, one ram and seven male lambs a year old, all without defect.(R) With the bull offer a grain offering(S) of three-tenths of an ephah of the finest flour mixed with oil; with the ram, two-tenths;(T) 10 and with each of the seven lambs, one-tenth.(U) 11 Include one male goat(V) as a sin offering, in addition to the sin offering for atonement and the regular burnt offering(W) with its grain offering, and their drink offerings.(X)

The Festival of Tabernacles(Y)

12 “‘On the fifteenth day of the seventh(Z) month,(AA) hold a sacred assembly and do no regular work. Celebrate a festival to the Lord for seven days. 13 Present as an aroma pleasing to the Lord(AB) a food offering consisting of a burnt offering of thirteen young bulls, two rams and fourteen male lambs a year old, all without defect.(AC) 14 With each of the thirteen bulls offer a grain offering(AD) of three-tenths of an ephah of the finest flour mixed with oil; with each of the two rams, two-tenths; 15 and with each of the fourteen lambs, one-tenth.(AE) 16 Include one male goat as a sin offering,(AF) in addition to the regular burnt offering with its grain offering and drink offering.(AG)

17 “‘On the second day(AH) offer twelve young bulls, two rams and fourteen male lambs a year old, all without defect.(AI) 18 With the bulls, rams and lambs, offer their grain offerings(AJ) and drink offerings(AK) according to the number specified.(AL) 19 Include one male goat as a sin offering,(AM) in addition to the regular burnt offering(AN) with its grain offering, and their drink offerings.(AO)

20 “‘On the third day offer eleven bulls, two rams and fourteen male lambs a year old, all without defect.(AP) 21 With the bulls, rams and lambs, offer their grain offerings and drink offerings according to the number specified.(AQ) 22 Include one male goat as a sin offering, in addition to the regular burnt offering with its grain offering and drink offering.

23 “‘On the fourth day offer ten bulls, two rams and fourteen male lambs a year old, all without defect. 24 With the bulls, rams and lambs, offer their grain offerings and drink offerings according to the number specified. 25 Include one male goat as a sin offering, in addition to the regular burnt offering with its grain offering and drink offering.

26 “‘On the fifth day offer nine bulls, two rams and fourteen male lambs a year old, all without defect. 27 With the bulls, rams and lambs, offer their grain offerings and drink offerings according to the number specified. 28 Include one male goat as a sin offering, in addition to the regular burnt offering with its grain offering and drink offering.

29 “‘On the sixth day offer eight bulls, two rams and fourteen male lambs a year old, all without defect. 30 With the bulls, rams and lambs, offer their grain offerings and drink offerings according to the number specified. 31 Include one male goat as a sin offering, in addition to the regular burnt offering with its grain offering and drink offering.

32 “‘On the seventh day offer seven bulls, two rams and fourteen male lambs a year old, all without defect. 33 With the bulls, rams and lambs, offer their grain offerings and drink offerings according to the number specified. 34 Include one male goat as a sin offering, in addition to the regular burnt offering with its grain offering and drink offering.

35 “‘On the eighth day hold a closing special assembly(AR) and do no regular work. 36 Present as an aroma pleasing to the Lord(AS) a food offering consisting of a burnt offering of one bull, one ram and seven male lambs a year old,(AT) all without defect. 37 With the bull, the ram and the lambs, offer their grain offerings and drink offerings according to the number specified. 38 Include one male goat as a sin offering, in addition to the regular burnt offering with its grain offering and drink offering.

39 “‘In addition to what you vow(AU) and your freewill offerings,(AV) offer these to the Lord at your appointed festivals:(AW) your burnt offerings,(AX) grain offerings, drink offerings and fellowship offerings.(AY)’”

40 Moses told the Israelites all that the Lord commanded him.[f]

Footnotes

  1. Numbers 29:3 That is, probably about 11 pounds or about 5 kilograms; also in verses 9 and 14
  2. Numbers 29:3 That is, probably about 7 pounds or about 3.2 kilograms; also in verses 9 and 14
  3. Numbers 29:4 That is, probably about 3 1/2 pounds or about 1.6 kilograms; also in verses 10 and 15
  4. Numbers 29:5 Or purification offering; also elsewhere in this chapter
  5. Numbers 29:7 Or must fast
  6. Numbers 29:40 In Hebrew texts this verse (29:40) is numbered 30:1.