Add parallel Print Page Options

Malo omwe Aisraeli Anayima pa Ulendo Wawo

33 Malo otsatirawa ndi omwe Aisraeli anayima pa maulendo awo atatuluka mʼdziko la Igupto mʼmagulu awo motsogozedwa ndi Mose ndi Aaroni. Mose analemba malo amene anayambira maulendo awo molamulidwa ndi Yehova. Maulendo awo ndi malo omwe anayambira ndi awa:

Aisraeli ananyamuka kuchokera ku Ramesesi pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, itangotha Paska. Iwo anatuluka nayenda molimba mtima Aigupto onse akuona, pamene ankayika maliro a ana awo oyamba kubadwa, omwe Yehova anawakantha pakati pawo chifukwa Yehova anaweruza milungu yawo.

Aisraeli atachoka ku Ramesesi, anamanga misasa yawo ku Sukoti.

Atachoka ku Sukoti anakamanga misasa yawo ku Etamu, mʼmbali mwa chipululu.

Ndipo atachoka ku Etamu, anabwerera ku Pihahiroti, kummawa kwa Baala-Zefoni, ndipo anamanga misasa yawo pafupi ndi Migidoli.

Atachoka ku Pihahiroti anadutsa mʼkati mwa nyanja kupita ku chipululu ndipo atayenda masiku atatu mʼchipululu cha Etamu, anamanga misasa yawo ku Mara.

Atachoka ku Mara anafika ku Elimu, kumene kunali akasupe a madzi khumi ndi awiri ndi mitengo ya migwalangwa 70 ndipo anamanga misasa yawo kumeneko.

10 Atachoka ku Elimu anakamanga misasa yawo mʼmbali mwa Nyanja Yofiira.

11 Atachoka ku Nyanja Yofiira anakamanga misasa yawo mʼchipululu cha Sini.

12 Atachoka ku chipululu cha Sini anakamanga ku Dofika.

13 Atachoka ku Dofika anakamanga misasa yawo ku Alusi.

14 Atachoka ku Alusi anakamanga misasa yawo ku Refidimu, kumene kunalibe madzi woti anthu ndi kumwa.

15 Atachoka ku Refidimu anakamanga ku chipululu cha Sinai

16 Atachoka ku chipululu cha Sinai anakamanga misasa yawo ku Kiburoti-Hataava.

17 Atachoka ku Kiburoti-Hataava anakamanga misasa yawo ku Heziroti.

18 Atachoka ku Heziroti anakamanga ku Ritima.

19 Atachoka ku Ritima anakamanga ku Rimoni-Perezi.

20 Atachoka ku Rimoni-Perezi anakamanga ku Libina.

21 Atachoka ku Libina anakamanga ku Risa.

22 Atachoka ku Risa anakamanga ku Kehelata.

23 Atachoka ku Kehelata anakamanga ku phiri la Seferi.

24 Atachoka ku phiri la Seferi anakamanga ku Harada.

25 Atachoka ku Harada anakamanga ku Mekheloti.

26 Atachoka ku Mekheloti anakamanga ku Tahati.

27 Atachoka ku Tahati anakamanga ku Tera.

28 Atachoka ku Tera anakamanga ku Mitika.

29 Atachoka ku Mitika anakamanga ku Hasimona.

30 Atachoka ku Hasimona anakamanga ku Moseroti.

31 Atachoka ku Moseroti anakamanga ku Beni Yaakani.

32 Atachoka ku Beni Yaakani anakamanga ku Hori-Hagidigadi.

33 Atachoka ku Hori-Hagidigadi anakamanga ku Yotibata.

34 Atachoka ku Yotibata anakamanga ku Abirona.

35 Atachoka ku Abirona anakamanga ku Ezioni-Geberi.

36 Atachoka ku Ezioni-Geberi anakamanga ku Kadesi, mʼchipululu cha Zini chimene ndi Kadesi.

37 Anachoka ku Kadesi ndi kukamanga ku phiri la Hori, mʼmalire mwa dziko la Edomu. 38 Molamulidwa ndi Yehova, wansembe Aaroni anakwera ku phiri la Hori kumene anakamwalirira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu, mʼchaka cha makumi anayi, Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto. 39 Aaroni anamwalira pa phiri la Hori ali ndi zaka 123.

40 Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi yomwe inkakhala ku Negevi kummwera kwa Kanaani, inamva kuti Aisraeli akubwera.

41 Atachoka ku phiri la Hori anakamanga ku Zalimoni.

42 Atachoka ku Zalimoni anakamanga ku Punoni.

43 Atachoka ku Punoni anakamanga ku Oboti.

44 Atachoka ku Oboti anakamanga ku Iye-Abarimu.

45 Atachoka ku Iye-Abarimu anakamanga ku Diboni Gadi.

46 Atachoka ku Diboni Gadi anakamanga ku Alimoni-Dibulataimu.

47 Atachoka ku Alimoni-Dibulataimu anakamanga mʼmapiri a Abarimu, pafupi ndi Nebo.

48 Atachoka ku mapiri a Abarimu anakamanga ku zigwa za Mowabu mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi Yeriko. 49 Ali ku zigwa za Mowabu anamanga mʼmbali mwa Yorodani kuchokera ku Beti-Yesimoti mpaka ku Abeli-Sitimu.

50 Pa zigwa za Mowabu, mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi ku Yeriko, Yehova anawuza Mose kuti, 51 “Nena kwa Aisraeli kuti, ‘Pamene muwoloka Yorodani kulowa mʼdziko la Kanaani, 52 mukathamangitse nzika zonse za mʼdzikomo pamaso panu. Mukawononge mafano awo onse a miyala ndi osula ndi malo awo achipembedzo. 53 Mukalande dzikolo ndi kukhalamo chifukwa ndakupatsani dziko limenelo kuti mukhalemo. 54 Mukagawane dzikolo pochita maere monga mwa mafuko anu. Kwa omwe ali ambiri, cholowa chambiri, ndipo amene ali ocheperapo, chocheperanso. Chilichonse chimene chidzawagwere iwo mwa maere chidzakhala chawo. Mukaligawane monga mwa mafuko a makolo anu.

55 “ ‘Koma ngati simukathamangitsa nzika zimene zili mʼdzikomo, amene mukawalole kukhalamo adzakhala ngati zisonga mʼmaso mwanu ndi ngati minga mʼmbali mwanu. Adzakubweretserani mavuto mʼdziko limene mudzakhalemolo. 56 Ndipo pamenepo ndidzachitira inu zomwe ndinaganiza kuwachitira iwowo.’ ”

Stages in Israel’s Journey

33 Here are the stages in the journey(A) of the Israelites when they came out of Egypt(B) by divisions under the leadership of Moses and Aaron.(C) At the Lord’s command Moses recorded(D) the stages in their journey(E). This is their journey by stages:

The Israelites set out(F) from Rameses(G) on the fifteenth day of the first month, the day after the Passover.(H) They marched out defiantly(I) in full view of all the Egyptians, who were burying all their firstborn,(J) whom the Lord had struck down among them; for the Lord had brought judgment(K) on their gods.(L)

The Israelites left Rameses and camped at Sukkoth.(M)

They left Sukkoth and camped at Etham, on the edge of the desert.(N)

They left Etham, turned back to Pi Hahiroth, to the east of Baal Zephon,(O) and camped near Migdol.(P)

They left Pi Hahiroth[a](Q) and passed through the sea(R) into the desert, and when they had traveled for three days in the Desert of Etham, they camped at Marah.(S)

They left Marah and went to Elim, where there were twelve springs and seventy palm trees, and they camped(T) there.

10 They left Elim(U) and camped by the Red Sea.[b]

11 They left the Red Sea and camped in the Desert of Sin.(V)

12 They left the Desert of Sin and camped at Dophkah.

13 They left Dophkah and camped at Alush.

14 They left Alush and camped at Rephidim, where there was no water for the people to drink.(W)

15 They left Rephidim(X) and camped in the Desert of Sinai.(Y)

16 They left the Desert of Sinai and camped at Kibroth Hattaavah.(Z)

17 They left Kibroth Hattaavah and camped at Hazeroth.(AA)

18 They left Hazeroth and camped at Rithmah.

19 They left Rithmah and camped at Rimmon Perez.

20 They left Rimmon Perez and camped at Libnah.(AB)

21 They left Libnah and camped at Rissah.

22 They left Rissah and camped at Kehelathah.

23 They left Kehelathah and camped at Mount Shepher.

24 They left Mount Shepher and camped at Haradah.

25 They left Haradah and camped at Makheloth.

26 They left Makheloth and camped at Tahath.

27 They left Tahath and camped at Terah.

28 They left Terah and camped at Mithkah.

29 They left Mithkah and camped at Hashmonah.

30 They left Hashmonah and camped at Moseroth.(AC)

31 They left Moseroth and camped at Bene Jaakan.(AD)

32 They left Bene Jaakan and camped at Hor Haggidgad.

33 They left Hor Haggidgad and camped at Jotbathah.(AE)

34 They left Jotbathah and camped at Abronah.

35 They left Abronah and camped at Ezion Geber.(AF)

36 They left Ezion Geber and camped at Kadesh, in the Desert of Zin.(AG)

37 They left Kadesh and camped at Mount Hor,(AH) on the border of Edom.(AI) 38 At the Lord’s command Aaron the priest went up Mount Hor, where he died(AJ) on the first day of the fifth month of the fortieth year(AK) after the Israelites came out of Egypt.(AL) 39 Aaron was a hundred and twenty-three years old when he died on Mount Hor.

40 The Canaanite king(AM) of Arad,(AN) who lived in the Negev(AO) of Canaan, heard that the Israelites were coming.

41 They left Mount Hor and camped at Zalmonah.

42 They left Zalmonah and camped at Punon.

43 They left Punon and camped at Oboth.(AP)

44 They left Oboth and camped at Iye Abarim, on the border of Moab.(AQ)

45 They left Iye Abarim and camped at Dibon Gad.

46 They left Dibon Gad and camped at Almon Diblathaim.

47 They left Almon Diblathaim and camped in the mountains of Abarim,(AR) near Nebo.(AS)

48 They left the mountains of Abarim(AT) and camped on the plains of Moab(AU) by the Jordan(AV) across from Jericho.(AW) 49 There on the plains of Moab they camped along the Jordan from Beth Jeshimoth(AX) to Abel Shittim.(AY)

50 On the plains of Moab by the Jordan across from Jericho(AZ) the Lord said to Moses, 51 “Speak to the Israelites and say to them: ‘When you cross the Jordan into Canaan,(BA) 52 drive out all the inhabitants of the land before you. Destroy all their carved images and their cast idols, and demolish all their high places.(BB) 53 Take possession of the land and settle in it, for I have given you the land to possess.(BC) 54 Distribute the land by lot,(BD) according to your clans.(BE) To a larger group give a larger inheritance, and to a smaller group a smaller one.(BF) Whatever falls to them by lot will be theirs. Distribute it according to your ancestral tribes.(BG)

55 “‘But if you do not drive out the inhabitants of the land, those you allow to remain will become barbs in your eyes and thorns(BH) in your sides. They will give you trouble in the land where you will live. 56 And then I will do to you what I plan to do to them.(BI)’”

Footnotes

  1. Numbers 33:8 Many manuscripts of the Masoretic Text, Samaritan Pentateuch and Vulgate; most manuscripts of the Masoretic Text left from before Hahiroth
  2. Numbers 33:10 Or the Sea of Reeds; also in verse 11