Add parallel Print Page Options

Tola

10 Atafa Abimeleki panabwera Tola mwana wa Puwa, mdzukulu wa Dodo kudzapulumutsa Aisraeli. Iyeyu anali wa fuko la Isakara ndipo ankakhala ku Samiri mʼdziko la mapiri la Efereimu. Iye anatsogolera Aisraeli kwa zaka 23, ndipo anamwalira ndi kuyikidwa ku Samiri.

Yairo

Atafa Tola panabwera Yairi wa ku Giliyadi, amene anatsogolera Israeli kwa zaka 22. Iyeyu anali ndi ana aamuna makumi atatu, amene ankakwera pa abulu makumi atatu. Iwo anali ndi mizinda makumi atatu mʼdziko la Giliyadi, imene mpaka lero ikutchedwa kuti Havoti Yairi. Atamwalira Yairi anayikidwa mʼmanda ku Kamoni.

Yefita

Aisraeli anachitanso zoyipira Yehova. Iwo anatumikira Abaala ndi Asitoreti, milungu ya ku Aramu, Sidoni, Mowabu, Aamoni ndi Afilisti. Choncho analeka osatumikiranso Yehova. Tsono Yehova anapsera mtima Aisraeli ndipo anawapereka mʼmanja mwa Afilisti ndi Aamoni. Iwowa anawagonjetseratu Aisraeli mʼchaka chimenechi, ndipo kwa zaka 18 anakhala akusautsa Aisraeli onse amene anali pa tsidya la Yorodani, mʼdziko la Aamori ku Giliyadi. Aamori anawoloka mtsinje wa Yorodani kukathira nkhondo mafuko a Yuda, Benjamini ndi Efereimu kotero kuti Israeli anavutika kwambiri. 10 Kenaka Aisraeli analira kwa Yehova kuti, “Ife takuchimwirani popeza tasiya Inu Mulungu wathu ndi kutumikira Abaala.”

11 Yehova anawafunsa kuti, “Suja ine ndinakupulumutsani kwa Aigupto, Aamori, Aamoni ndi Afilisti? 12 Ndiponso pamene Asidoni, Aamaleki ndi Amoni anakuzunzani, inu nʼkulirira kwa ine suja ndinakupulumutsani kwa anthu amenewa? 13 Komabe inu mwandikana ndipo mukutumikira milungu ina. Choncho sindidzakupulumutsaninso. 14 Pitani kalireni kwa milungu imene mwayisankha. Iyoyo ikupulumutseni ku mavuto anuwo.”

15 Koma Aisraeli anayankha Yehova kuti, “Ife tachimwa. Tichitireni chimene mukuona kuti ndi chabwino, koma chonde tipulumutseni lero lokha.” 16 Ndipo anachotsa milungu ya chilendo pakati pawo ndi kuyamba kutumikira Yehova. Ndipo Yehova anamva chisoni poona mmene Aisraeli ankazunzikira.

17 Tsono Aamoni anasonkhana ndi kumanga zithando za nkhondo ku Giliyadi. Nawonso Aisraeli anasonkhana ndi kumanga zithando zawo za nkhondo ku Mizipa. 18 Kenaka anthuwo ndi atsogoleri a Agiliyadi anayamba kufunsana kuti, “Kodi ndi munthu wotani amene atayambe kuthira nkhondo Aamoni? Iyeyu adzakhala mtsogoleri wolamulira anthu onse a ku Giliyadi.”

Tola

10 After the time of Abimelek,(A) a man of Issachar(B) named Tola son of Puah,(C) the son of Dodo, rose to save(D) Israel. He lived in Shamir,(E) in the hill country of Ephraim. He led[a] Israel twenty-three years; then he died, and was buried in Shamir.

Jair

He was followed by Jair(F) of Gilead, who led Israel twenty-two years. He had thirty sons, who rode thirty donkeys.(G) They controlled thirty towns in Gilead, which to this day are called Havvoth Jair.[b](H) When Jair(I) died, he was buried in Kamon.

Jephthah

Again the Israelites did evil in the eyes of the Lord.(J) They served the Baals and the Ashtoreths,(K) and the gods of Aram,(L) the gods of Sidon,(M) the gods of Moab, the gods of the Ammonites(N) and the gods of the Philistines.(O) And because the Israelites forsook the Lord(P) and no longer served him, he became angry(Q) with them. He sold them(R) into the hands of the Philistines and the Ammonites, who that year shattered and crushed them. For eighteen years they oppressed all the Israelites on the east side of the Jordan in Gilead,(S) the land of the Amorites. The Ammonites also crossed the Jordan to fight against Judah,(T) Benjamin and Ephraim;(U) Israel was in great distress. 10 Then the Israelites cried(V) out to the Lord, “We have sinned(W) against you, forsaking our God and serving the Baals.”(X)

11 The Lord replied, “When the Egyptians,(Y) the Amorites,(Z) the Ammonites,(AA) the Philistines,(AB) 12 the Sidonians, the Amalekites(AC) and the Maonites[c](AD) oppressed you(AE) and you cried to me for help, did I not save you from their hands? 13 But you have forsaken(AF) me and served other gods,(AG) so I will no longer save you. 14 Go and cry out to the gods you have chosen. Let them save(AH) you when you are in trouble!(AI)

15 But the Israelites said to the Lord, “We have sinned. Do with us whatever you think best,(AJ) but please rescue us now.” 16 Then they got rid of the foreign gods among them and served the Lord.(AK) And he could bear Israel’s misery(AL) no longer.(AM)

17 When the Ammonites were called to arms and camped in Gilead, the Israelites assembled and camped at Mizpah.(AN) 18 The leaders of the people of Gilead said to each other, “Whoever will take the lead in attacking the Ammonites will be head(AO) over all who live in Gilead.”

Footnotes

  1. Judges 10:2 Traditionally judged; also in verse 3
  2. Judges 10:4 Or called the settlements of Jair
  3. Judges 10:12 Hebrew; some Septuagint manuscripts Midianites