Add parallel Print Page Options

Kubadwa kwa Samsoni

13 Aisraeli anachitanso zinthu zoyipira Yehova, kotero Yehova anawapereka mʼmanja mwa Afilisti kwa zaka makumi anayi.

Ku Zora kunali munthu wina dzina lake Manowa, wochokera ku fuko la Dani. Mkazi wake analibe ana popeza anali wosabereka. Mngelo wa Yehova anaonekera mkaziyo ndipo anati, “Ndinu wosabereka ndipo mulibedi mwana, komabe mudzakhala ndi pakati ndipo mudzabereka mwana wamwamuna. Tsono mudzisamale bwino, osamwa vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa ndiponso musamadye chakudya chilichonse chodetsedwa, chifukwa mudzakhala ndi pakati ndipo mudzabereka mwana wamwamuna. Mwanayo akadzabadwa lumo lisadzapite pa mutu chifukwa mnyamatayo adzakhala Mnaziri, ndiye kuti wopatulika kwa Mulungu kuyambira pa nthawi imene adzakhale ali mʼchiberekero. Ndipo adzayamba ntchito yopulumutsa Israeli mʼmanja mwa Afilisti.”

Kenaka mayiyo anapita kukawuza mwamuna wake kuti, “Munthu wa Mulungu anabwera kwa ine, ndipo maonekedwe ake anali ngati mngelo wa Mulungu, maonekedwe woopsa kwambiri. Ine sindinamufunse kumene amachokera, ndipo iyeyo sanandiwuzenso dzina lake. Koma anandiwuza kuti, ‘Mudzakhala ndi pakati ndipo mudzabereka mwana wamwamuna. Choncho musamamwe vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa, musamadye chakudya chilichonse choyipitsidwa chifukwa mwanayo adzakhala Mnaziri, wopatulika kwa Mulungu kuyambira pa nthawi imene adzakhale ali mʼchiberekero mpaka tsiku la kufa kwake.’ ”

Kenaka Manowa anapemphera kwa Yehova kuti, “Chonde Ambuye, lolani munthu wa Mulungu amene munamutuma abwerenso kwa ife kuti adzatiphunzitse zochita ndi mwanayo akadzabadwa.”

Mulungu anamva pemphero la Manowa, ndipo mngelo wa Mulungu anabweranso kwa mkaziyo nthawi imene anali ku munda, koma Manowa mwamuna wake sanali naye. 10 Tsono mkaziyo anathamanga kukawuza mwamuna wake kuti, “Wandionekeranso munthu uja amene anabwera kwa ine tsiku lija.”

11 Choncho Manowa ananyamuka namutsatira mkazi wake. Atafika kwa munthuyo anamufunsa kuti, “Kodi ndinu munayankhula ndi mkazi wanga?”

Iye anayankha kuti, “Ndine.”

12 Kenaka Manowa anafunsa kuti, “Tiyerekeze kuti mawu anuwa akwaniritsidwadi, ndiye mwanayu azidzakhala bwanji ndipo azidzachita chiyani?”

13 Ndipo mngelo wa Yehova uja anamuyankha kuti, “Zonse zimene ndinawawuza akazi anuwa asamale ndipo adzazichitedi. 14 Asadzadye chilichonse chochokera ku mphesa. Asadzamwe vinyo kapena choledzeretsa chilichonse, ngakhale kudya chakudya chilichonse chodetsedwa. Zonse zimene ndinawalamula azisunge bwino.”

15 Manowa anamuwuza mngelo wa Yehova uja kuti, “Chonde dikirani pangʼono, timati tikukonzereni mwana wambuzi.”

16 Mngelo wa Yehova anayankha kuti, “Ngakhale mukundidikiritsa, ine sindidya chakudya chanu. Koma ngati mukonze nsembe yopsereza iperekeni kwa Yehova.” (Manowa nʼkuti asakudziwa kuti munthuyo anali mngelo wa Mulungu).

17 Tsono Manowa anapempha mngelo wa Yehova kuti, “Chonde tidziwitseni dzina lanu kuti zikadzachitika zimene mwanenazi ife tidzakulemekezeni?”

18 Iye anayankha kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukufunsa dzina langa? Dzina laketu ndi lodabwitsa.” 19 Ndipo Manowa anatenga mwana wambuzi pamodzi ndi chopereka cha chakudya nakapereka nsembe pa thanthwe kwa Yehova ndipo Yehova anachita zodabwitsa kwa Manowa ndi mkazi wake akuona. 20 Pamene malawi a moto amakwera kumwamba kuchoka pa guwa, mngelo wa Yehova uja anakwera kumwamba mʼmalawi a motowo Manowa ndi mkazi wake akuona. Tsono anadzigwetsa pansi naweramitsa mitu yawo pansi. 21 Mngelo wa Yehova uja sanaonekerenso kwa Manowa ndi mkazi wake. Choncho Manowa anazindikira kuti anali mngelo wa Yehova.

22 Iye anawuza mkazi wake kuti, “Ife tifa basi pakuti taona Mulungu!”

23 Koma mkazi wake anamuyankha kuti, “Yehova akanafuna kutipha sakanayilandira nsembe yathu yopsereza ndi chopereka chathu chachakudya chija, ndipo sakanationetsanso zinthu zonsezi kapena kutiwuza zinthu ngati zimenezi nthawi ino.”

24 Motero mkaziyo anabereka mwana wa mwamuna, namutcha dzina lake Samsoni. Iye anakula ndipo Yehova anamudalitsa. 25 Mzimu wa Yehova unayamba kumulimbikitsa pamene ankakhala ku misasa ya anthu a fuko la Dani, malo amene anali pakati pa Zora ndi Esitaoli.

The Birth of Samson

13 Again the Israelites did evil in the eyes of the Lord, so the Lord delivered them into the hands of the Philistines(A) for forty years.(B)

A certain man of Zorah,(C) named Manoah,(D) from the clan of the Danites,(E) had a wife who was childless,(F) unable to give birth. The angel of the Lord(G) appeared to her(H) and said, “You are barren and childless, but you are going to become pregnant and give birth to a son.(I) Now see to it that you drink no wine or other fermented drink(J) and that you do not eat anything unclean.(K) You will become pregnant and have a son(L) whose head is never to be touched by a razor(M) because the boy is to be a Nazirite,(N) dedicated to God from the womb. He will take the lead(O) in delivering Israel from the hands of the Philistines.”

Then the woman went to her husband and told him, “A man of God(P) came to me. He looked like an angel of God,(Q) very awesome.(R) I didn’t ask him where he came from, and he didn’t tell me his name. But he said to me, ‘You will become pregnant and have a son. Now then, drink no wine(S) or other fermented drink(T) and do not eat anything unclean, because the boy will be a Nazirite of God from the womb until the day of his death.(U)’”

Then Manoah(V) prayed to the Lord: “Pardon your servant, Lord. I beg you to let the man of God(W) you sent to us come again to teach us how to bring up the boy who is to be born.”

God heard Manoah, and the angel of God came again to the woman while she was out in the field; but her husband Manoah was not with her. 10 The woman hurried to tell her husband, “He’s here! The man who appeared to me(X) the other day!”

11 Manoah got up and followed his wife. When he came to the man, he said, “Are you the man who talked to my wife?”

“I am,” he said.

12 So Manoah asked him, “When your words are fulfilled, what is to be the rule that governs the boy’s life and work?”

13 The angel of the Lord answered, “Your wife must do all that I have told her. 14 She must not eat anything that comes from the grapevine, nor drink any wine or other fermented drink(Y) nor eat anything unclean.(Z) She must do everything I have commanded her.”

15 Manoah said to the angel of the Lord, “We would like you to stay until we prepare a young goat(AA) for you.”

16 The angel of the Lord replied, “Even though you detain me, I will not eat any of your food. But if you prepare a burnt offering,(AB) offer it to the Lord.” (Manoah did not realize(AC) that it was the angel of the Lord.)

17 Then Manoah inquired of the angel of the Lord, “What is your name,(AD) so that we may honor you when your word comes true?”

18 He replied, “Why do you ask my name?(AE) It is beyond understanding.[a] 19 Then Manoah took a young goat, together with the grain offering, and sacrificed it on a rock(AF) to the Lord. And the Lord did an amazing thing while Manoah and his wife watched: 20 As the flame(AG) blazed up from the altar toward heaven, the angel of the Lord ascended in the flame. Seeing this, Manoah and his wife fell with their faces to the ground.(AH) 21 When the angel of the Lord did not show himself again to Manoah and his wife, Manoah realized(AI) that it was the angel of the Lord.

22 “We are doomed(AJ) to die!” he said to his wife. “We have seen(AK) God!”

23 But his wife answered, “If the Lord had meant to kill us, he would not have accepted a burnt offering and grain offering from our hands, nor shown us all these things or now told us this.”(AL)

24 The woman gave birth to a boy and named him Samson.(AM) He grew(AN) and the Lord blessed him,(AO) 25 and the Spirit of the Lord began to stir(AP) him while he was in Mahaneh Dan,(AQ) between Zorah and Eshtaol.

Footnotes

  1. Judges 13:18 Or is wonderful