Add parallel Print Page Options

Naomi ndi Rute

Mu nthawi imene oweruza ankalamulira Israeli, munali njala mʼdziko, ndipo munthu wina wa ku Betelehemu mʼdziko la Yuda anapita pamodzi ndi mkazi wake ndi ana ake aamuna awiri, kukakhala ku Mowabu kwa nthawi yochepa. Dzina la munthuyo linali Elimeleki, dzina la mkazi wake linali Naomi, ndipo mayina a ana awo aamuna anali Maaloni ndi Kiliyoni. Iwo anali Aefurati ochokera ku Betelehemu ku Yuda. Ndipo anapita kukakhala ku Mowabu.

Kenaka Elimeleki, mwamuna wake wa Naomi anamwalira ndipo Naomiyo anatsala ndi ana ake aamuna awiri aja.

Iwo anakwatira akazi a Chimowabu; wina dzina lake Oripa ndi wina Rute. Atakhala kumeneko pafupifupi zaka khumi, Maloni ndi Kiliyoni anamwaliranso kotero kuti Naomi anatsala yekha wopanda ana ake awiri aja ndi mwamuna wake.

Naomi ndi apongozi ake awiri aja ananyamuka kubwerera kwawo kuchokera ku Mowabu popeza anali atamva ali ku Mowabuko kuti Yehova anakomera mtima anthu ake ndi kuwapatsa chakudya.

Naomi pamodzi ndi apongozi ake awiri aja anachoka kumene ankakhala ndi kuyamba ulendo obwerera kwawo ku Yuda.

Kenaka Naomi anati kwa apongozi ake awiri aja, “Bwererani, aliyense kwa amayi ake. Yehova akukomereni mtima, monga munachita ndi malemu aja ndi ine ndemwe.

“Yehova akuthandizeni kuti aliyense wa inu apeze pokhala pabwino komanso mwamuna.” Kenaka anawapsompsona koma awiriwo analira mokweza.

10 Ndipo anati kwa Naomi, “Ife tipita nawo kwa anthu akwanu.”

11 Koma Naomi anati, “Bwererani kwanu ana anga. Chifukwa chiyani mukufuna kupita ndi ine? Kodi ine ndingaberekenso ana ena kuti akhale amuna anu? 12 Bwererani kwanu ana anga muzipita kwanu. Ine ndakalamba kwambiri kotero kuti sindingakwatiwenso. Ngakhale ndikananena kuti ndili nacho chikhulupiriro, ngakhale ndikanakhala ndi mwamuna usiku uno, ndipo nʼkubala ana aamuna, 13 kodi inu mukanadikira kuti akule? Kodi mukanakhalabe osakwatiwa kudikira iwowo? Ayi ana anga. Zimenezi zikundiwawa kwambiri kuposa inu, chifukwa ndi ineyo amene Yehova wafuna kuti ndizunzike.”

14 Atamva zimenezi analiranso kwambiri, ndipo Oripa anapsompsona apongozi ake nawatsanzika, koma Rute anakakamirabe.

15 Naomi anati “Taona, mʼbale wako wabwerera kwawo kwa anthu ake ndi kwa milungu yake. Bwerera nawenso umulondole mʼbale wako.”

16 Koma Rute anayankha kuti, “Musandikakamize kuti ndikusiyeni kapena kuti ndibwerere osakutsatani. Kumene inu mupite ine ndipita komweko, ndipo kumene mukakhale inenso ndikakhala komweko. Abale anu adzakhala abale anga ndipo Mulungu wanu adzakhala Mulungu wanga. 17 Kumene mukafere inenso ndidzafera komweko ndipo komweko ndikayikidwa mʼmanda. Yehova andichite choyipa chingakule motani, ngati china chingatirekanitse ife kupatula imfa.”

18 Naomi atazindikira kuti Rute watsimikiza kupita naye, analeka kumukakamiza.

19 Choncho amayi awiriwo anapitiriza ulendo wawo mpaka anakafika ku Betelehemu. Pamene ankafika mu Betelehemu, anthu onse a mʼmudzimo anatekeseka chifukwa cha iwowo ndipo amayi ambiri ankanena kuti, “Kodi uyu nʼkukhala Naomi?”

20 Iye anawawuza kuti, “Musanditchenso Naomi. Muzinditchula ine kuti Mara, chifukwa Wamphamvuzonse wandizunza kwambiri. 21 Ine ndinapita wolemera, koma Yehova wabwera nane wopanda kanthu. Nanga munditchulirenji Naomi pamene Yehova wandisautsa. Wamphamvuzonse uja wandigwetsera mavuto owawa.”

22 Naomi anabwerera kuchoka ku dziko la Mowabu pamodzi ndi Rute mpongozi wake. Ndipo anafika ku Betelehemu nthawi yoyamba kukolola barele.

Naomi Loses Her Husband and Sons

In the days when the judges ruled,[a](A) there was a famine in the land.(B) So a man from Bethlehem in Judah,(C) together with his wife and two sons, went to live for a while(D) in the country of Moab.(E) The man’s name was Elimelek,(F) his wife’s name was Naomi, and the names of his two sons were Mahlon and Kilion.(G) They were Ephrathites(H) from Bethlehem,(I) Judah. And they went to Moab and lived there.

Now Elimelek, Naomi’s husband, died, and she was left with her two sons. They married Moabite women,(J) one named Orpah and the other Ruth.(K) After they had lived there about ten years, both Mahlon and Kilion(L) also died,(M) and Naomi was left without her two sons and her husband.

Naomi and Ruth Return to Bethlehem

When Naomi heard in Moab(N) that the Lord had come to the aid of his people(O) by providing food(P) for them, she and her daughters-in-law(Q) prepared to return home from there. With her two daughters-in-law she left the place where she had been living and set out on the road that would take them back to the land of Judah.

Then Naomi said to her two daughters-in-law, “Go back, each of you, to your mother’s home.(R) May the Lord show you kindness,(S) as you have shown kindness to your dead husbands(T) and to me. May the Lord grant that each of you will find rest(U) in the home of another husband.”

Then she kissed(V) them goodbye and they wept aloud(W) 10 and said to her, “We will go back with you to your people.”

11 But Naomi said, “Return home, my daughters. Why would you come with me? Am I going to have any more sons, who could become your husbands?(X) 12 Return home, my daughters; I am too old to have another husband. Even if I thought there was still hope for me—even if I had a husband tonight and then gave birth to sons— 13 would you wait until they grew up?(Y) Would you remain unmarried for them? No, my daughters. It is more bitter(Z) for me than for you, because the Lord’s hand has turned against me!(AA)

14 At this they wept(AB) aloud again. Then Orpah kissed her mother-in-law(AC) goodbye,(AD) but Ruth clung to her.(AE)

15 “Look,” said Naomi, “your sister-in-law(AF) is going back to her people and her gods.(AG) Go back with her.”

16 But Ruth replied, “Don’t urge me to leave you(AH) or to turn back from you. Where you go I will go,(AI) and where you stay I will stay. Your people will be my people(AJ) and your God my God.(AK) 17 Where you die I will die, and there I will be buried. May the Lord deal with me, be it ever so severely,(AL) if even death separates you and me.”(AM) 18 When Naomi realized that Ruth was determined to go with her, she stopped urging her.(AN)

19 So the two women went on until they came to Bethlehem.(AO) When they arrived in Bethlehem, the whole town was stirred(AP) because of them, and the women exclaimed, “Can this be Naomi?”

20 “Don’t call me Naomi,[b]” she told them. “Call me Mara,[c] because the Almighty[d](AQ) has made my life very bitter.(AR) 21 I went away full, but the Lord has brought me back empty.(AS) Why call me Naomi? The Lord has afflicted[e] me;(AT) the Almighty has brought misfortune upon me.”

22 So Naomi returned from Moab accompanied by Ruth the Moabite,(AU) her daughter-in-law,(AV) arriving in Bethlehem as the barley harvest(AW) was beginning.(AX)

Footnotes

  1. Ruth 1:1 Traditionally judged
  2. Ruth 1:20 Naomi means pleasant.
  3. Ruth 1:20 Mara means bitter.
  4. Ruth 1:20 Hebrew Shaddai; also in verse 21
  5. Ruth 1:21 Or has testified against