Add parallel Print Page Options

Kuchita Ntchito Zabwino

Uwakumbutse anthu kuti azigonjera oweruza ndi olamulira, aziwamvera ndi kukhala okonzeka kuchita chilichonse chabwino. Asamachitire chipongwe aliyense, asamakangane, akhale ofatsa ndipo oganizira ena, ndipo nthawi zonse akhale aulemu kwa anthu onse.

Nthawi ina tinali opusa, osamvera, onamizidwa ndi omangidwa ndi zilakolako ndi zokondweretsa zamitundumitundu. Tinkakhala moyo wadumbo ndi wakaduka, odedwa ndiponso odana wina ndi mnzake. Koma kukoma mtima ndi chikondi cha Mulungu Mpulumutsi wathu chitaonekera, Iye anatipulumutsa, osati chifukwa cha ntchito zathu zolungama zimene tinachita koma chifukwa cha chifundo chake. Anatipulumutsa potisambitsa, kutibadwitsa kwatsopano ndi kutikonzanso mwa Mzimu Woyera amene anatipatsa mowolowamanja kudzera mwa Yesu Khristu Mpulumutsi wathu, kuti titalungamitsidwa mwachisomo chake, tikhale olowamʼmalo okhala ndi chiyembekezo cha moyo wosatha. Mawuwa ndi okhulupirika ndipo ine ndikufuna kuti iwe utsindike zinthu izi, kuti amene akhulupirira Mulungu adzipereke kuchita ntchito zabwino. Zinthu izi ndi zabwino kwambiri ndi zopindulitsa kwa aliyense.

Koma upewe kufufuzafufuza zopusa, kuwerengawerenga mndandanda wa mibado ya makolo, mikangano ndi mitsutso pa za Malamulo, chifukwa zimenezi ndi zosapindulitsa ndi zopanda pake. 10 Munthu woyambitsa mipatuko umuchenjeze koyamba, ndiponso umuchenjeze kachiwiri. Kenaka umupewe. 11 Iwe udziwe kuti munthu wotero ngosokoneza ndi wochimwa, ndipo akudzitsutsa yekha.

Mawu Otsiriza

12 Ndikadzamutuma Artema kapena Tukiko kwanuko, udzayesetse kundipeza ku Nikapoli, chifukwa ndatsimikiza kukhala kumeneko pa nthawi yozizira. 13 Uyesetse chilichonse ungathe kuthandiza Zena katswiri wa malamulo ndi Apolo, kuti apitirize ulendo wawo, ndipo uwonetsetse asasowe kanthu. 14 Anthu athu aphunzire kudzipereka pogwira ntchito zabwino, nʼcholinga chakuti athandize zinthu zimene zikufunika msangamsanga. Ndipo asakhale moyo osapindulitsa.

15 Onse amene ali ndi ine akupereka moni. Upereke moni kwa amene amatikonda ife mʼchikhulupiriro.

Chisomo chikhale ndi inu nonse.

Saved in Order to Do Good

Remind the people to be subject to rulers and authorities,(A) to be obedient, to be ready to do whatever is good,(B) to slander no one,(C) to be peaceable and considerate, and always to be gentle toward everyone.

At one time(D) we too were foolish, disobedient, deceived and enslaved by all kinds of passions and pleasures. We lived in malice and envy, being hated and hating one another. But when the kindness(E) and love of God our Savior(F) appeared,(G) he saved us,(H) not because of righteous things we had done,(I) but because of his mercy.(J) He saved us through the washing(K) of rebirth and renewal(L) by the Holy Spirit, whom he poured out on us(M) generously through Jesus Christ our Savior, so that, having been justified by his grace,(N) we might become heirs(O) having the hope(P) of eternal life.(Q) This is a trustworthy saying.(R) And I want you to stress these things, so that those who have trusted in God may be careful to devote themselves to doing what is good.(S) These things are excellent and profitable for everyone.

But avoid(T) foolish controversies and genealogies and arguments and quarrels(U) about the law,(V) because these are unprofitable and useless.(W) 10 Warn a divisive person once, and then warn them a second time. After that, have nothing to do with them.(X) 11 You may be sure that such people are warped and sinful; they are self-condemned.

Final Remarks

12 As soon as I send Artemas or Tychicus(Y) to you, do your best to come to me at Nicopolis, because I have decided to winter there.(Z) 13 Do everything you can to help Zenas the lawyer and Apollos(AA) on their way and see that they have everything they need. 14 Our people must learn to devote themselves to doing what is good,(AB) in order to provide for urgent needs and not live unproductive lives.

15 Everyone with me sends you greetings. Greet those who love us in the faith.(AC)

Grace be with you all.(AD)