Add parallel Print Page Options

Chenjezo kwa Achuma Opondereza Anzawo

Tsono tamverani, inu anthu achuma, lirani ndi kufuwula chifukwa cha zovuta zimene zidzakugwereni. Chuma chanu chawola ndipo njenjete zadya zovala zanu. Golide ndi siliva wanu zachita dzimbiri. Dzimbirilo lidzakhala umboni wokutsutsani ndi kuwononga mnofu wanu ngati moto. Mwadziwunjikira chuma pa masiku ano otsiriza. Taonani, ndalama za malipiro zimene munakanika kulipira aganyu aja ankasenga mʼmunda mwanu zikulira mokutsutsani. Kulira kwa okololawo kwamveka mʼmakutu mwa Ambuye Wamphamvuzonse. Mwakhala pa dziko lapansi pano moyo ofewa ndipo mwalidyera dziko lapansi. Mwadzinenepetsa pa tsiku lokaphedwa. Mwaweruza kuti ndi wolakwa ndipo mwapha munthu wosalakwa, amene sakutsutsana nanu.

Kupirira Mʼmasautso

Tsono abale, pirirani mpaka kubwera kwa Ambuye. Onani mmene amachitira mlimi. Amadikirira kuti zipatso zabwino zioneke mʼmunda mwake. Amayembekezera mokhazikika mtima kuyambira nthawi ya mvula yoyamba mpaka yotsiriza. Inunso mukhale owugwira mtima ndi osasinthika chifukwa Ambuye ali pafupi kubwera. Abale, musamanenezane zoyipa kuopa kuti mungadzaweruzidwe. Woweruza ali pa khomo!

10 Abale, tengerani chitsanzo cha aneneri amene anayankhula mʼdzina la Ambuye. Iwowo anakumana ndi zovuta koma anapirira. 11 Monga mukudziwa, tinawatenga ngati odalitsika anthu amene anapirira. Munamva za kupirira kwa Yobu ndipo mwaona zimene Ambuye anamuchitira potsiriza pake. Ambuye ndi wodzaza ndi chisoni ndi chifundo.

12 Koposa zonse, abale anga, musamalumbire. Polumbira osamatchula kumwamba kapena dziko lapansi, kapena china chilichonse. “Inde” wanu azikhala “Inde,” ndipo “Ayi” wanu azikhala “Ayi,” kuopa kuti mungadzapezeke olakwa.

Pemphero la Chikhulupiriro

13 Kodi alipo wina mwa inu amene ali pa mavuto? Apemphere. Kodi wina wakondwa? Ayimbe nyimbo zolemekeza. 14 Kodi alipo wina mwa inu akudwala? Ayitane akulu ampingo kuti adzamupempherere ndi kumudzoza mafuta mʼdzina la Ambuye. 15 Ndipo pemphero lachikhulupiriro lidzachiritsa munthu wodwalayo ndipo Ambuye adzamuutsa. Ngati wachimwa adzakhululukidwa. 16 Choncho, ululiranani machimo anu ndi kupemphererana wina ndi mnzake kuti muchiritsidwe. Pemphero la munthu wolungama ndi lamphamvu ndipo limagwira ntchito.

17 Eliya anali munthu ngati ife. Iye anapemphera mwamphamvu kuti mvula isagwe ndipo sinagwedi kwa zaka zitatu ndi theka. 18 Kenaka anapempheranso, ndipo kumwamba kunagwetsa mvula, ndipo dziko lapansi linatulutsa zomera zake. 19 Abale anga, ngati mmodzi wa inu apatuka pa choonadi ndipo wina wake ndi kumubweza, 20 kumbukirani izi: Aliyense wobweza wochimwa kuchoka ku cholakwa chake, adzamupulumutsa ku imfa ndi kukwirira machimo ambiri.

Warning to Rich Oppressors

Now listen,(A) you rich people,(B) weep and wail(C) because of the misery that is coming on you. Your wealth has rotted, and moths have eaten your clothes.(D) Your gold and silver are corroded. Their corrosion will testify against you and eat your flesh like fire. You have hoarded wealth in the last days.(E) Look! The wages you failed to pay the workers(F) who mowed your fields are crying out against you. The cries(G) of the harvesters have reached the ears of the Lord Almighty.(H) You have lived on earth in luxury and self-indulgence. You have fattened yourselves(I) in the day of slaughter.[a](J) You have condemned and murdered(K) the innocent one,(L) who was not opposing you.

Patience in Suffering

Be patient, then, brothers and sisters, until the Lord’s coming.(M) See how the farmer waits for the land to yield its valuable crop, patiently waiting(N) for the autumn and spring rains.(O) You too, be patient and stand firm, because the Lord’s coming(P) is near.(Q) Don’t grumble against one another, brothers and sisters,(R) or you will be judged. The Judge(S) is standing at the door!(T)

10 Brothers and sisters, as an example of patience in the face of suffering, take the prophets(U) who spoke in the name of the Lord. 11 As you know, we count as blessed(V) those who have persevered. You have heard of Job’s perseverance(W) and have seen what the Lord finally brought about.(X) The Lord is full of compassion and mercy.(Y)

12 Above all, my brothers and sisters, do not swear—not by heaven or by earth or by anything else. All you need to say is a simple “Yes” or “No.” Otherwise you will be condemned.(Z)

The Prayer of Faith

13 Is anyone among you in trouble? Let them pray.(AA) Is anyone happy? Let them sing songs of praise.(AB) 14 Is anyone among you sick? Let them call the elders(AC) of the church to pray over them and anoint them with oil(AD) in the name of the Lord. 15 And the prayer offered in faith(AE) will make the sick person well; the Lord will raise them up. If they have sinned, they will be forgiven. 16 Therefore confess your sins(AF) to each other and pray for each other so that you may be healed.(AG) The prayer of a righteous person is powerful and effective.(AH)

17 Elijah was a human being, even as we are.(AI) He prayed earnestly that it would not rain, and it did not rain on the land for three and a half years.(AJ) 18 Again he prayed, and the heavens gave rain, and the earth produced its crops.(AK)

19 My brothers and sisters, if one of you should wander from the truth(AL) and someone should bring that person back,(AM) 20 remember this: Whoever turns a sinner from the error of their way will save(AN) them from death and cover over a multitude of sins.(AO)

Footnotes

  1. James 5:5 Or yourselves as in a day of feasting