Add parallel Print Page Options

“Ngati munthu asudzula mkazi wake
    ndipo mkaziyo nʼkuchoka nakakwatiwa ndi mwamuna wina,
kodi mwamuna woyambayo angathe kumutenganso mkaziyo?
    Kodi atatero sindiye kuti dzikolo layipitsidwa kwambiri?
Koma iwe Israeli wachita zadama ndi zibwenzi zambiri.
    Komabe bwerera kwa ine,”
            akutero Yehova.
“Tayangʼana ku zitunda zowuma.
    Kodi aliponso malo ena amene iwe sunachitepo zadama?
Iwe unkakhala mʼmbali mwa njira kumadikira zibwenzi zako,
    ngati Mluya wobisalira anthu mʼchipululu.
Inu mwayipitsa dziko ndi zadama zanu
    ndi ntchito zanu zoyipa.
Nʼchifukwa chake Yehova wayimitsa mvula,
    ndipo mvula ya nthawi ya masika sinagwe.
Komabe uli ndi maonekedwe a mkazi wachiwerewere;
    ndipo sukuchita manyazi ndi pangʼono pomwe.
Kodi iwe siposachedwa pomwepa pamene wanena
    kuti, ‘Abambo anga, Inu bwenzi langa la unyamata wanga,
kodi mudzandikwiyira nthawi zonse?
    Kodi ukali wanu udzakhalabe mpaka muyaya?’
Umu ndimo mmene umayankhulira,
    koma umapitirizabe kuchita zoyipa monga momwe umathera.”

Kusakhulupirika kwa Israeli

Pa nthawi ya Mfumu Yosiya Yehova anandiwuza kuti, “Kodi waona zomwe Israeli wosakhulupirika uja wachita? Anakwera pa phiri lililonse lalitali ndi kupita pa tsinde pa mtengo uliwonse wogudira kukapembedza. Choncho anachita za chiwerewere kumeneko. Ndinaganiza kuti atachita zonsezi, adzabwerera kwa Ine, koma sanabwerere, ndipo mlongo wake wosakhulupirika uja, Yuda, anaziona zimenezi. Anaona kuti ndinasudzula Israeli wosakhulupirikayo ndi kumupirikitsa chifukwa cha zigololo zake. Komabe Yuda mʼbale wake wosakhulupirika uja sanaope, nayenso anapita kukachita chigololo. Chiwerewere cha Israeli chinali chochititsa manyazi kotero kuti chinayipitsa dziko lonse. Anachita chigololo popembedza mafano a miyala ndi mitengo. 10 Israeli atachita zonsezi, Yuda mʼbale wake wosakhulupirika uja sanabwerere kwa Ine ndi mtima wake wonse, koma mwachiphamaso chabe,” akutero Yehova.

11 Yehova anandiwuza kuti, “Kusakhulupirika kwa Israeli nʼkochepa kuyerekeza ndi kusakhulupirika kwa Yuda. 12 Pita ukalalikire kumpoto uthenga wakuti,

“ ‘Israeli wosakhulupirikawe, bwerera,’ akutero Yehova.
    ‘Sindidzakukalipira mpaka kalekale,
pakuti ndine wachifundo,’ akutero Yehova.
    ‘Sindidzakukwiyira mpaka kalekale.
13 Ungovomera kulakwa kwako
    kuti unawukira Yehova Mulungu wako.
Vomera kuti unayendayenda kukapembedza milungu yachilendo
    pansi pa mtengo uliwonse wogudira,
    ndiponso kuti sunandimvere,’ ”
            akutero Yehova.

14 “Bwererani, ana osakhulupirika, pakuti ndine mbuye wanu,” akutero Yehova. “Ndinakusankhani, mmodzimmodzi kuchokera ku mudzi uliwonse ndiponso awiriawiri kuchokera ku banja lililonse. 15 Ndipo ndidzakupatsani abusa a pamtima panga amene adzakutsogolerani mwanzeru ndi mwaluntha. 16 Masiku amenewo mukadzachulukana kwambiri mʼdzikomo, anthu sadzanenanso za ‘Bokosi la Chipangano la Yehova’ kapena kuliganizira. Sadzalikumbukiranso kapena kulifuna, ndipo sadzapanganso lina,”

            akutero Yehova.

17 Nthawi imeneyo adzatcha Yerusalemu Mpando Waufumu wa Yehova, ndipo mitundu yonse ya anthu idzasonkhana mu Yerusalemu pamaso pa Yehova. Sadzawumiriranso kutsata mitima yawo yoyipa. 18 Masiku amenewo fuko la Yuda lidzaphatikizana ndi fuko la Israeli, onse pamodzi adzachokera ku dziko la kumpoto kupita ku dziko limene ndinapatsa makolo awo, kuti likhale cholowa.

19 “Ine mwini ndinati,

“ ‘Ndikanakonda bwanji kukukhazikani pakati pa ana anga
    ndikukupatsani dziko labwino kwambiri,
    cholowa chokongola kwambiri kuposa cha mitundu ina ya anthu.’
Ndinaganiza kuti mudzanditcha Ine ‘Atate’
    ndi kuti simudzaleka kunditsata.
20 Koma monga mkazi wosakhulupirika amasiya mwamuna wake,
    momwemonso inu mwakhala osakhulupirika kwa Ine, inu fuko la Israeli,”
            akutero Yehova.

21 Mawu akumveka pa magomo,
    Aisraeli akulira ndi kupempha chifundo
chifukwa anatsata njira zoyipa
    ndi kuyiwala Yehova Mulungu wawo.

22 Inu mukuti, “Bwererani, anthu osakhulupirika;
    ndidzachiritsa kubwerera mʼmbuyo kwanu.”

“Inde, tidzabwerera kwa Inu
    pakuti ndinu Yehova Mulungu wathu.
23 Ndithu kupembedza pa magomo
    komanso kuchita maphwando pa mapiri zilibe phindu.
Zoonadi chipulumutso cha Israeli
    chili mwa Yehova Mulungu wathu basi.
24 Kuyambira pa ubwana wathu milungu yochititsa manyazi ija yakhala ikutiwonongetsa phindu
    la ntchito za makolo athu,
nkhosa ndi ngʼombe zawo,
    ana awo aamuna ndi aakazi.
25 Tilekeni tigone pansi mwa manyazi,
    ndipo kunyozeka kwathu kutiphimbe.
Paja tachimwira Yehova Mulungu wathu,
    ife pamodzi ndi makolo athu
kuyambira nthawi ya ubwana wathu mpaka lero lino
    sitinamvere Yehova Mulungu wathu.”

“If a man divorces(A) his wife
    and she leaves him and marries another man,
should he return to her again?
    Would not the land be completely defiled?(B)
But you have lived as a prostitute with many lovers(C)
    would you now return to me?”(D)
declares the Lord.
“Look up to the barren heights(E) and see.
    Is there any place where you have not been ravished?
By the roadside(F) you sat waiting for lovers,
    sat like a nomad in the desert.
You have defiled the land(G)
    with your prostitution(H) and wickedness.
Therefore the showers have been withheld,(I)
    and no spring rains(J) have fallen.
Yet you have the brazen(K) look of a prostitute;
    you refuse to blush with shame.(L)
Have you not just called to me:
    ‘My Father,(M) my friend from my youth,(N)
will you always be angry?(O)
    Will your wrath continue forever?’
This is how you talk,
    but you do all the evil you can.”

Unfaithful Israel

During the reign of King Josiah,(P) the Lord said to me, “Have you seen what faithless(Q) Israel has done? She has gone up on every high hill and under every spreading tree(R) and has committed adultery(S) there. I thought that after she had done all this she would return to me but she did not, and her unfaithful sister(T) Judah saw it.(U) I gave faithless Israel(V) her certificate of divorce(W) and sent her away because of all her adulteries. Yet I saw that her unfaithful sister Judah had no fear;(X) she also went out and committed adultery. Because Israel’s immorality mattered so little to her, she defiled the land(Y) and committed adultery(Z) with stone(AA) and wood.(AB) 10 In spite of all this, her unfaithful sister Judah did not return(AC) to me with all her heart, but only in pretense,(AD)” declares the Lord.(AE)

11 The Lord said to me, “Faithless Israel is more righteous(AF) than unfaithful(AG) Judah.(AH) 12 Go, proclaim this message toward the north:(AI)

“‘Return,(AJ) faithless(AK) Israel,’ declares the Lord,
    ‘I will frown on you no longer,
for I am faithful,’(AL) declares the Lord,
    ‘I will not be angry(AM) forever.
13 Only acknowledge(AN) your guilt—
    you have rebelled against the Lord your God,
you have scattered your favors to foreign gods(AO)
    under every spreading tree,(AP)
    and have not obeyed(AQ) me,’”
declares the Lord.

14 “Return,(AR) faithless people,” declares the Lord, “for I am your husband.(AS) I will choose you—one from a town and two from a clan—and bring you to Zion. 15 Then I will give you shepherds(AT) after my own heart,(AU) who will lead you with knowledge and understanding. 16 In those days, when your numbers have increased greatly in the land,” declares the Lord, “people will no longer say, ‘The ark(AV) of the covenant of the Lord.’ It will never enter their minds or be remembered;(AW) it will not be missed, nor will another one be made. 17 At that time they will call Jerusalem The Throne(AX) of the Lord, and all nations(AY) will gather in Jerusalem to honor(AZ) the name of the Lord. No longer will they follow the stubbornness of their evil hearts.(BA) 18 In those days the people of Judah will join the people of Israel,(BB) and together(BC) they will come from a northern(BD) land to the land(BE) I gave your ancestors as an inheritance.

19 “I myself said,

“‘How gladly would I treat you like my children
    and give you a pleasant land,(BF)
    the most beautiful inheritance(BG) of any nation.’
I thought you would call me ‘Father’(BH)
    and not turn away from following me.
20 But like a woman unfaithful to her husband,
    so you, Israel, have been unfaithful(BI) to me,”
declares the Lord.

21 A cry is heard on the barren heights,(BJ)
    the weeping(BK) and pleading of the people of Israel,
because they have perverted their ways
    and have forgotten(BL) the Lord their God.

22 “Return,(BM) faithless people;
    I will cure(BN) you of backsliding.”(BO)

“Yes, we will come to you,
    for you are the Lord our God.
23 Surely the idolatrous commotion on the hills(BP)
    and mountains is a deception;
surely in the Lord our God
    is the salvation(BQ) of Israel.
24 From our youth shameful(BR) gods have consumed
    the fruits of our ancestors’ labor—
their flocks and herds,
    their sons and daughters.
25 Let us lie down in our shame,(BS)
    and let our disgrace cover us.
We have sinned(BT) against the Lord our God,
    both we and our ancestors;(BU)
from our youth(BV) till this day
    we have not obeyed(BW) the Lord our God.”