Add parallel Print Page Options

Kubwezeretsedwa kwa Israeli

30 Yehova anawuza Yeremiya kuti, “Ine Yehova, Mulungu wa Israeli ndikuti, ‘Lemba mʼbuku mawu onse amene ndakuwuza. Nthawi ikubwera pamene ndidzachotse anthu anga, Israeli ndi Yuda kuchokera ku ukapolo ndi kuwabwezera dziko limene ndinapatsa makolo awo,’ akutero Yehova.”

Nawa mawu amene Yehova anayankhula ndi anthu a ku Israeli ndi Yuda: “Yehova akuti:

“Ndamva kulira chifukwa cha nkhawa,
    ndamva kulira kwa mantha popeza palibe mtendere.
Tsono khalani pansi ndi kudzifunsa kuti:
    Kodi munthu wamwamuna angathe kubereka mwana?
Nanga nʼchifukwa chiyani ndikuona munthu aliyense wamwamuna
    atagwira manja ake pa mimba pake ngati mayi pa nthawi yake yochira?
    Chifukwa chiyani nkhope iliyonse ili yakugwa?
Mayo ine! Tsiku limeneli ndi lalikulu kwambiri!
    Sipadzakhala lina lofanana nalo.
Idzakhala nthawi ya masautso kwa Yakobo,
    koma adzapulumuka ku masautsowo.”

Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Pa tsiku limenelo,
    ndidzathyola goli la ukapolo mʼkhosi mwawo
ndipo ndidzadula zingwe zowamanga;
    Aisraeli sadzakhalanso akapolo a alendo.
Mʼmalo mwake, adzatumikira Yehova Mulungu wawo
    ndiponso Davide mfumu yawo,
    amene ndidzawasankhira.

10 “ ‘Tsono usachite mantha, iwe mtumiki wanga Yakobo;
    usade nkhawa, iwe Israeli,’
            akutero Yehova.
‘Ndithu ndidzakupulumutsa kuchokera ku dziko lakutali,
    zidzukulu zako kuchokera ku dziko la ukapolo wawo.
Yakobo adzabwerera ndipo adzakhala modekha pa mtendere,
    ndipo palibe amene adzamuchititsa mantha.
11 Ine ndili nanu ndipo ndidzakupulumutsani,’
    akutero Yehova.
‘Ngakhale ndidzawononga kotheratu mitundu yonse ya anthu
    kumene ndinakubalalitsirani,
    koma inu sindidzakuwonongani kotheratu.
Sindidzakulekani kuti mukhale osalangidwa.
    Koma ndidzakulangani mwachilungamo.’ ”

12 Yehova akuti,

“Chilonda chanu nʼchosachizika,
    bala lanu ndi lonyeka.
13 Palibe amene angathe kukutetezani pa mlandu wanu,
    palibe chiyembekezo choti inu nʼkuchira,
    palibe mankhwala ochiritsa inu.
14 Abwenzi anu onse akuyiwalani;
    sasamalanso za inu.
Ndakukanthani ngati mmene mdani akanachitira.
    Ndipo ndakulangani mwa nkhanza,
chifukwa machimo anu ndi ambiri,
    ndipo kulakwa kwanu ndi kwakukulu.
15 Chifukwa chiyani mukulira nacho chilonda chanu?
    Bala lanu silingapole ayi.
Ine ndakuchitani zimenezi chifukwa machimo anu ndi ambiri
    ndipo kulakwa kwanu nʼkwakukulu.

16 “Tsono onse amene anakuwonongani, nawonso adzawonongedwa;
    adani anu onse adzapita ku ukapolo.
Iwo amene anafunkha zinthu zanu, zinthu zawo zidzafunkhidwanso;
    onse amene anakusakazani nawonso adzasakazidwa.
17 Ndidzachiza matenda anu
    ndi kupoletsa zilonda zanu,
            akutero Yehova,
‘chifukwa mukutchedwa anthu otayika.
    Amati, ndi anthu a ku Ziyoni awa amene alibe wowasamala.’ ”

18 Yehova akuti,

“Ndidzabwera nalo banja la Yakobo ku dziko lawo
    ndipo ndidzachitira chifundo malo ake okhalamo;
mzinda wa Yerusalemu udzamangidwanso pa bwinja pake,
    nyumba yaufumu idzamangidwanso pa malo pake penipeni.
19 Anthuwo adzayimba nyimbo zoyamika Yehova
    ndipo kudzamveka phokoso lachisangalalo.
Ndidzawachulukitsa,
    ndipo chiwerengero chawo sichidzatsika;
ndidzawapatsa ulemerero,
    ndipo sadzanyozedwanso.
20 Ana awo adzakhalanso monga mmene analili kale,
    ndipo gulu lawo ndidzalikhazikitsa pamaso panga;
    ndidzalanga onse owazunza.
21 Mtsogoleri wawo adzakhala mmodzi mwa iwo.
    Wodzawalamulira adzachokera pakati pawo.
Choncho ndidzawakokera kufupi ndi Ine ndipo iye adzandiyandikira.
    Ndani angalimbe mtima payekha kuyandikana nane
    popanda kuyitanidwa?”
            akutero Yehova.
22 “Choncho inu mudzakhala anthu anga,
    ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wanu.”

23 Taonani ukali wa Yehova wowomba
    ngati mphepo ya mkuntho.
Mphepo ya namondwe
    ikuwomba pa mitu ya anthu oyipa.
24 Mkwiyo woopsa wa Yehova sudzachoka
    mpaka atakwaniritsa zolinga
    za mu mtima mwake.
Mudzamvetsa zimenezi
    masiku akubwerawo.

Restoration of Israel

30 This is the word that came to Jeremiah from the Lord: “This is what the Lord, the God of Israel, says: ‘Write(A) in a book all the words I have spoken to you. The days(B) are coming,’ declares the Lord, ‘when I will bring(C) my people Israel and Judah back from captivity[a] and restore(D) them to the land I gave their ancestors to possess,’ says the Lord.”

These are the words the Lord spoke concerning Israel and Judah: “This is what the Lord says:

“‘Cries of fear(E) are heard—
    terror, not peace.
Ask and see:
    Can a man bear children?
Then why do I see every strong man
    with his hands on his stomach like a woman in labor,(F)
    every face turned deathly pale?(G)
How awful that day(H) will be!
    No other will be like it.
It will be a time of trouble(I) for Jacob,
    but he will be saved(J) out of it.

“‘In that day,’ declares the Lord Almighty,
    ‘I will break the yoke(K) off their necks
and will tear off their bonds;(L)
    no longer will foreigners enslave them.(M)
Instead, they will serve the Lord their God
    and David(N) their king,(O)
    whom I will raise up for them.

10 “‘So do not be afraid,(P) Jacob my servant;(Q)
    do not be dismayed, Israel,’
declares the Lord.
‘I will surely save(R) you out of a distant place,
    your descendants from the land of their exile.
Jacob will again have peace and security,(S)
    and no one will make him afraid.(T)
11 I am with you(U) and will save you,’
    declares the Lord.
‘Though I completely destroy all the nations
    among which I scatter you,
    I will not completely destroy(V) you.
I will discipline(W) you but only in due measure;
    I will not let you go entirely unpunished.’(X)

12 “This is what the Lord says:

“‘Your wound(Y) is incurable,
    your injury beyond healing.(Z)
13 There is no one to plead your cause,(AA)
    no remedy for your sore,
    no healing(AB) for you.
14 All your allies(AC) have forgotten you;
    they care nothing for you.
I have struck you as an enemy(AD) would
    and punished you as would the cruel,(AE)
because your guilt is so great
    and your sins(AF) so many.
15 Why do you cry out over your wound,
    your pain that has no cure?(AG)
Because of your great guilt and many sins
    I have done these things to you.(AH)

16 “‘But all who devour(AI) you will be devoured;
    all your enemies will go into exile.(AJ)
Those who plunder(AK) you will be plundered;
    all who make spoil of you I will despoil.
17 But I will restore you to health
    and heal(AL) your wounds,’
declares the Lord,
‘because you are called an outcast,(AM)
    Zion for whom no one cares.’(AN)

18 “This is what the Lord says:

“‘I will restore the fortunes(AO) of Jacob’s tents(AP)
    and have compassion(AQ) on his dwellings;
the city will be rebuilt(AR) on her ruins,
    and the palace will stand in its proper place.
19 From them will come songs(AS) of thanksgiving(AT)
    and the sound of rejoicing.(AU)
I will add to their numbers,(AV)
    and they will not be decreased;
I will bring them honor,(AW)
    and they will not be disdained.
20 Their children(AX) will be as in days of old,
    and their community will be established(AY) before me;
    I will punish(AZ) all who oppress them.
21 Their leader(BA) will be one of their own;
    their ruler will arise from among them.(BB)
I will bring him near(BC) and he will come close to me—
    for who is he who will devote himself
    to be close to me?’
declares the Lord.
22 “‘So you will be my people,(BD)
    and I will be your God.(BE)’”

23 See, the storm(BF) of the Lord
    will burst out in wrath,
a driving wind swirling down
    on the heads of the wicked.
24 The fierce anger(BG) of the Lord will not turn back(BH)
    until he fully accomplishes
    the purposes of his heart.
In days to come
    you will understand(BI) this.

Footnotes

  1. Jeremiah 30:3 Or will restore the fortunes of my people Israel and Judah