Add parallel Print Page Options

31 “Pa nthawi imeneyo,” akutero Yehova, “Ndidzakhala Mulungu wa mafuko onse a Israeli, ndipo iwo adzakhala anthu anga.”

Yehova akuti,

“Anthu amene anapulumuka ku nkhondo
    ndinawakomera mtima mʼchipululu;
    pamene Aisraeli ankafuna kupumula.”

Ine ndinawaonekera ndili chapatali ndipo ndinati,

“Ine ndakukondani ndi chikondi chopanda malire.
    Nʼchifukwa chake ndipitiriza kukukondani.
Ndidzakusamaliraninso, inu anthu a Israeli;
    mudzasangalala poyimba tizitoliro tanu,
ndipo mudzapita kukavina nawo
    anthu ovina mwachimwemwe.
Mudzalimanso minda ya mpesa
    pa mapiri a Samariya;
alimi adzadzala mphesa
    ndipo adzadya zipatso zake.
Lidzafika tsiku pamene alonda adzafuwula
    pa mapiri a Efereimu nati,
‘Tiyeni tipite ku Ziyoni,
    kwa Yehova Mulungu wathu.’ ”

Yehova akuti,

“Imbani mosangalala chifukwa cha Yakobo,
    fuwulani chifukwa cha mtundu wopambana mitundu yonse.
Matamando anu amveke, ndipo munene kuti,
    ‘Yehova wapulumutsa anthu ake
    otsala a Israeli.’
Taonani, ndidzabwera nawo kuchokera ku dziko la kumpoto,
    ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku malekezero a dziko lapansi.
Anthu osaona, olumala, amayi oyembekezera
    ndi amene ali pa nthawi yawo yochira adzabwera nawo pamodzi.
    Chidzakhala chikhamu cha anthu obwerera kuno.
Adzabwera akulira;
    koma Ine ndikuwatonthoza mtima, ndidzawaperekeza.
Ndidzawatsogolera ku mitsinje yamadzi
    mʼnjira yosalala mmene sadzapunthwamo.
Chifukwa ndine abambo ake a Israeli,
    ndipo Efereimu ndi mwana wanga woyamba.

10 “Imvani mawu a Yehova inu anthu a mitundu ina;
    lalikirani mawuwa kwa anthu a mayiko akutali a mʼmbali mwa nyanja;
‘Iye amene anabalalitsa Israeli adzawasonkhanitsanso
    ndipo adzayangʼanira nkhosa zake ngati mʼbusa.’
11 Pakuti Yehova wawombola fuko la Yakobo
    anawapulumutsa mʼdzanja la anthu owaposa mphamvu.
12 Anthuwo adzabwera akuyimba mofuwula pa mapiri a Ziyoni;
    adzasangalala ndi zinthu zabwino zochokera kwa Yehova.
Zinthu zabwinozo ndi izi: tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta,
    ana ankhosa ndi ana angʼombe.
Iwo adzakhala ngati munda wothiriridwa bwino,
    ndipo sadzamvanso chisoni.
13 Pamenepo anamwali adzavina ndi kusangalala.
    Anyamata ndi okalamba nawonso adzasangalala.
Kulira kwawo ndidzakusandutsa chisangalalo;
    ndidzawasangalatsa nʼkuchotsa chisoni chawo.
14 Ansembe ndidzawadyetsa chakudya chabwino,
    ndipo anthu anga adzakhuta ndi zabwino zanga,”
            akutero Yehova.

15 Yehova akuti,

“Kulira kukumveka ku Rama,
    kulira kwakukulu,
Rakele akulirira ana ake.
    Sakutonthozeka
    chifukwa ana akewo palibe.”

16 Yehova akuti,

“Leka kulira
    ndi kukhetsa misozi
pakuti udzalandira mphotho ya ntchito yako,”
            akutero Yehova.
    “Iwo adzabwerako ku dziko la adani.
17 Tsono chiyembekezo chilipo pa zamʼtsogolo,”
            akutero Yehova.
    “Ana ako adzabwerera ku dziko lawo.

18 “Ndithu ndamva Efereimu akubuwula kuti,
    ‘Ife tinali ngati ana angʼombe osamva.
    Koma inu mwatiphunzitsa kumvera.
Mutibweze kuti tithe kubwerera,
    chifukwa ndinu Yehova Mulungu wanga.
19 Popeza tatembenuka mtima,
    ndiye tikumva chisoni;
popeza tazindikira
    ndiye tikudziguguda pachifukwa.
Tachita manyazi ndipo tanyazitsidwa
    chifukwa tinachimwa paubwana wathu.’
20 Kodi Efereimu si mwana wanga wokondedwa,
    mwana amene Ine ndimakondwera naye?
Ngakhale nthawi zambiri ndimamudzudzula,
    ndimamukumbukirabe.
Kotero mtima wanga ukumufunabe;
    ndimamumvera chifundo chachikulu kwambiri,”
            akutero Yehova.

21 “Muyike zizindikiro za mu msewu;
    muyimike zikwangwani.
Yangʼanitsitsani msewuwo,
    njira imene mukuyendamo.
Bwerera, iwe namwali wa Israeli,
    bwerera ku mizinda yako ija.
22 Udzakhala jenkha mpaka liti,
    iwe mwana wa mkazi wosakhulupirika?
Yehova walenga chinthu chatsopano pa dziko lapansi; mkazi ndiye tsopano aziteteza mwamuna.”

23 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Ndikadzabwera nawo anthuwa kuchokera ku ukapolo, anthu a mʼdziko la Yuda ndi amene akukhala mʼmizinda yake adzayankhulanso mawu akuti, ‘Yehova akudalitse, iwe malo achilungamo, iwe phiri lopatulika.’ 24 Anthu adzakhala ku Yuda ndi ku mizinda yake pamodzi ndi alimi ndi oweta nkhosa. 25 Ndidzatsitsimutsa anthu otopa ndipo ndidzadyetsa anthu anjala.”

26 Pamenepo ndinadzuka nʼkuyangʼana uku ndi uku. Tulo tanga tinali tokoma.

27 “Masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzachulukitsa anthu pamodzi ndi ziweto mʼdziko la Israeli ndi la Yuda. 28 Monga momwe ndinasamalira powazula, powagwetsa, powagumula, powawononga ndi powachita zoyipa, momwemonso ndidzasamala powamanga ndi powadzala” akutero Yehova. 29 “Mʼmasiku amenewo anthu sadzanenanso kuti,

“Makolo adya mphesa zosapsa,
    koma mano a ana ndiye achita dziru.

30 Mʼmalo wake, munthu aliyense adzafa chifukwa cha tchimo lake. Iye amene adzadye mphesa zosapsazo ndiye amene mano ake adzachite dziru.”

31 “Masiku akubwera,” akutero Yehova,
    “pamene ndidzachita pangano latsopano
ndi Aisraeli
    ndiponso nyumba ya Yuda.
32 Silidzakhala ngati pangano
    limene ndinachita ndi makolo awo
pamene ndinawagwira padzanja
    nʼkuwatulutsa ku Igupto;
chifukwa anaphwanya pangano langa,
    ngakhale ndinali mwamuna wawo,”
            akutero Yehova.
33 “Ili ndi pangano limene ndidzachita ndi Aisraeli
    atapita masiku amenewo,” akutero Yehova.
“Ndidzayika lamulo langa mʼmitima mwawo
    ndi kulilemba mʼmaganizo mwawo.
Ine ndidzakhala Mulungu wawo
    ndipo iwo adzakhala anthu anga.
34 Sipadzafunikanso kuti wina aphunzitse mnzake,
    kapena munthu wina kuphunzitsa mʼbale wake, kunena kuti, ‘Mudziwe Yehova,’
chifukwa onse adzandidziwa Ine,
    kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu,”
            akutero Yehova.
“Ndidzawakhululukira zoyipa zawo
    ndipo sindidzakumbukiranso machimo awo.”

35 Yehova akuti,

Iye amene amakhazikitsa dzuwa
    kuti liziwala masana,
amene amalamula kuti mwezi ndi nyenyezi
    ziziwala usiku,
amene amavundula nyanja
    kuti mafunde akokome,
    dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse:
36 Ngati zimenezi zilekeka pamaso panga, akutero Yehova, pamenepo padzakhala pamathero a fuko la Israeli pamaso panga.

37 Yehova akuti,

“Ndidzataya fuko la Israeli chifukwa cha machimo awo.
    Ngati patapezeka munthu
amene angathe kupima zakuthambo
    nʼkufufuza maziko a dziko lapansi.”

38 “Taonani masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene mzinda wa Yehova udzamangidwanso kuyambira ku Nsanja ya Hananeli mpaka ku Chipata cha Ngodya. 39 Malire ake adzayambira pamenepo kupita ku phiri la Garebu, nʼkudzakhota kuloza ku Gowa. 40 Chigwa chonse mʼmene amatayiramo mitembo ndi phulusa, ndiponso minda yonse kuyambira ku Chigwa cha Kidroni mpaka ku ngodya ya Chipata cha Akavalo mbali ya kummawa, adzakhala malo opatulika a Yehova. Mzindawu sadzawuzulanso kapena kuwuwononga.”

31 “At that time,” declares the Lord, “I will be the God(A) of all the families of Israel, and they will be my people.”

This is what the Lord says:

“The people who survive the sword
    will find favor(B) in the wilderness;
    I will come to give rest(C) to Israel.”

The Lord appeared to us in the past,[a] saying:

“I have loved(D) you with an everlasting love;
    I have drawn(E) you with unfailing kindness.
I will build you up again,
    and you, Virgin(F) Israel, will be rebuilt.(G)
Again you will take up your timbrels(H)
    and go out to dance(I) with the joyful.(J)
Again you will plant(K) vineyards
    on the hills of Samaria;(L)
the farmers will plant them
    and enjoy their fruit.(M)
There will be a day when watchmen(N) cry out
    on the hills of Ephraim,
‘Come, let us go up to Zion,
    to the Lord our God.’”(O)

This is what the Lord says:

“Sing(P) with joy for Jacob;
    shout for the foremost(Q) of the nations.
Make your praises heard, and say,
    Lord, save(R) your people,
    the remnant(S) of Israel.’
See, I will bring them from the land of the north(T)
    and gather(U) them from the ends of the earth.
Among them will be the blind(V) and the lame,(W)
    expectant mothers and women in labor;
    a great throng will return.
They will come with weeping;(X)
    they will pray as I bring them back.
I will lead(Y) them beside streams of water(Z)
    on a level(AA) path where they will not stumble,
because I am Israel’s father,(AB)
    and Ephraim is my firstborn son.

10 “Hear the word of the Lord, you nations;
    proclaim it in distant coastlands:(AC)
‘He who scattered(AD) Israel will gather(AE) them
    and will watch over his flock like a shepherd.’(AF)
11 For the Lord will deliver Jacob
    and redeem(AG) them from the hand of those stronger(AH) than they.
12 They will come and shout for joy(AI) on the heights(AJ) of Zion;
    they will rejoice in the bounty(AK) of the Lord
the grain, the new wine and the olive oil,(AL)
    the young of the flocks(AM) and herds.
They will be like a well-watered garden,(AN)
    and they will sorrow(AO) no more.
13 Then young women will dance and be glad,
    young men and old as well.
I will turn their mourning(AP) into gladness;
    I will give them comfort(AQ) and joy(AR) instead of sorrow.
14 I will satisfy(AS) the priests(AT) with abundance,
    and my people will be filled with my bounty,(AU)
declares the Lord.

15 This is what the Lord says:

“A voice is heard in Ramah,(AV)
    mourning and great weeping,
Rachel weeping for her children
    and refusing to be comforted,(AW)
    because they are no more.”(AX)

16 This is what the Lord says:

“Restrain your voice from weeping
    and your eyes from tears,(AY)
for your work will be rewarded,(AZ)
declares the Lord.
    “They will return(BA) from the land of the enemy.
17 So there is hope(BB) for your descendants,”
declares the Lord.
    “Your children(BC) will return to their own land.

18 “I have surely heard Ephraim’s moaning:
    ‘You disciplined(BD) me like an unruly calf,(BE)
    and I have been disciplined.
Restore(BF) me, and I will return,
    because you are the Lord my God.
19 After I strayed,(BG)
    I repented;
after I came to understand,
    I beat(BH) my breast.
I was ashamed(BI) and humiliated
    because I bore the disgrace of my youth.’(BJ)
20 Is not Ephraim my dear son,
    the child(BK) in whom I delight?
Though I often speak against him,
    I still remember(BL) him.
Therefore my heart yearns for him;
    I have great compassion(BM) for him,”
declares the Lord.

21 “Set up road signs;
    put up guideposts.(BN)
Take note of the highway,(BO)
    the road that you take.
Return,(BP) Virgin(BQ) Israel,
    return to your towns.
22 How long will you wander,(BR)
    unfaithful(BS) Daughter Israel?
The Lord will create a new thing(BT) on earth—
    the woman will return to[b](BU) the man.”

23 This is what the Lord Almighty, the God of Israel, says: “When I bring them back from captivity,[c](BV) the people in the land of Judah and in its towns will once again use these words: ‘The Lord bless(BW) you, you prosperous city,(BX) you sacred mountain.’(BY) 24 People will live(BZ) together in Judah and all its towns—farmers and those who move about with their flocks.(CA) 25 I will refresh the weary(CB) and satisfy the faint.”(CC)

26 At this I awoke(CD) and looked around. My sleep had been pleasant to me.

27 “The days are coming,”(CE) declares the Lord, “when I will plant(CF) the kingdoms of Israel and Judah with the offspring of people and of animals. 28 Just as I watched(CG) over them to uproot(CH) and tear down, and to overthrow, destroy and bring disaster,(CI) so I will watch over them to build and to plant,”(CJ) declares the Lord. 29 “In those days people will no longer say,

‘The parents(CK) have eaten sour grapes,
    and the children’s teeth are set on edge.’(CL)

30 Instead, everyone will die for their own sin;(CM) whoever eats sour grapes—their own teeth will be set on edge.

31 “The days are coming,” declares the Lord,
    “when I will make a new covenant(CN)
with the people of Israel
    and with the people of Judah.
32 It will not be like the covenant(CO)
    I made with their ancestors(CP)
when I took them by the hand
    to lead them out of Egypt,(CQ)
because they broke my covenant,
    though I was a husband(CR) to[d] them,[e]
declares the Lord.
33 “This is the covenant I will make with the people of Israel
    after that time,” declares the Lord.
“I will put my law in their minds(CS)
    and write it on their hearts.(CT)
I will be their God,
    and they will be my people.(CU)
34 No longer will they teach(CV) their neighbor,
    or say to one another, ‘Know the Lord,’
because they will all know(CW) me,
    from the least of them to the greatest,”
declares the Lord.
“For I will forgive(CX) their wickedness
    and will remember their sins(CY) no more.”

35 This is what the Lord says,

he who appoints(CZ) the sun
    to shine by day,
who decrees the moon and stars
    to shine by night,(DA)
who stirs up the sea(DB)
    so that its waves roar(DC)
    the Lord Almighty is his name:(DD)
36 “Only if these decrees(DE) vanish from my sight,”
    declares the Lord,
“will Israel(DF) ever cease
    being a nation before me.”

37 This is what the Lord says:

“Only if the heavens above can be measured(DG)
    and the foundations of the earth below be searched out
will I reject(DH) all the descendants of Israel
    because of all they have done,”
declares the Lord.

38 “The days are coming,” declares the Lord, “when this city will be rebuilt(DI) for me from the Tower of Hananel(DJ) to the Corner Gate.(DK) 39 The measuring line(DL) will stretch from there straight to the hill of Gareb and then turn to Goah. 40 The whole valley(DM) where dead bodies(DN) and ashes are thrown, and all the terraces out to the Kidron Valley(DO) on the east as far as the corner of the Horse Gate,(DP) will be holy(DQ) to the Lord. The city will never again be uprooted or demolished.”

Footnotes

  1. Jeremiah 31:3 Or Lord has appeared to us from afar
  2. Jeremiah 31:22 Or will protect
  3. Jeremiah 31:23 Or I restore their fortunes
  4. Jeremiah 31:32 Hebrew; Septuagint and Syriac / and I turned away from
  5. Jeremiah 31:32 Or was their master