Add parallel Print Page Options

Arekabu

35 Yehova anayankhula ndi Yeremiya nthawi ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, kuti: “Pita ku banja la Arekabu ndipo ukawayitane kuti abwere mʼchipinda chimodzi cha Nyumba ya Yehova ndipo akafika uwapatse vinyo kuti amwe.”

Choncho ndinakatenga Yaazaniya (mwana wa Yeremiya winanso amene anali mwana wa Habaziniya), abale ake, ana ake onse aamuna ndi banja lonse la Arekabu. Ndinabwera nawo ku Nyumba ya Yehova, ku chipinda cha ophunzira a mneneri Hanani mwana wa Igidaliya, munthu wa Mulungu. Chipinda chimenechi chinali pafupi ndi chipinda cha akuluakulu, chimene chinali pamwamba pa chipinda cha Maaseya mwana wa Salumu, mlonda wa pa khomo. Kenaka ndinayika mabotolo odzaza ndi vinyo ndi zikho zake pamaso pa Arekabu ndipo ndinawawuza kuti, “Imwani vinyoyu.”

Koma iwo anayankha kuti, “Ife sitimwa vinyo, chifukwa kholo lathu Yehonadabu mwana wa Rekabu anatilamula kuti, ‘Inuyo ngakhale zidzukulu zanu, musadzamwe vinyo mpaka kalekale. Musadzamange nyumba kapena kufesa mbewu, kapena kulima minda ya mpesa; musadzakhale ndi zinthu zimenezi. Mʼmalo mwake muzidzakhale mʼmatenti. Mukadzatero mudzakhala nthawi yayitali mʼdziko limene mukukhalamo.’ Ife takhala tikumvera zonse zimene kholo lathu Yehonadabu mwana wa Rekabu anatilamula. Ife ngakhale akazi athu kapena ana athu aamuna ndi aakazi sitinamwepo vinyo kapena kumanga nyumba kuti tizikhalamo kapenanso kukhala ndi minda ya mpesa, minda ina iliyonse kapena mbewu. 10 Koma takhala mʼmatenti ndipo tamvera kwathunthu chilichonse chimene kholo lathu Yehonadabu anatilamula. 11 Koma pamene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anathira nkhondo dziko lino, ife tinati, ‘Tiyeni tichoke, tipite ku Yerusalemu kuti tithawe magulu ankhondo a Akasidi ndi Aaramu.’ Kotero ife takhala tikukhala mu Yerusalemu.”

12 Yehova anayankhulanso ndi Yeremiya kuti, 13 “Iyeyu, Yehova Mulungu wa Israeli anawuza Yeremiya kuti: Pita ukawawuze anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, ‘Kodi simungatengeko phunziro ndi kumvera mawu anga?’ akutero Yehova. 14 ‘Yehonadabu mwana wa Rekabu analamula ana ake kuti asamwe vinyo ndipo lamulo limeneli alisunga. Mpaka lero lino iwo samwa vinyo, chifukwa akumvera lamulo la kholo lawo. Koma Ine ndakhala ndikuyankhula nanu kawirikawiri kukuchenjezani, koma inu simunandimvere Ine. 15 Kawirikawiri ndakhala ndikutumiza atumiki anga, aneneri, kwa inu. Iwo akhala akukuwuzani kuti, ‘Aliyense wa inu asiye ntchito zake zoyipa ndi kukonza makhalidwe ake; musatsatire milungu ina ndi kumayitumikira. Pamenepo mudzakhala mʼdziko limene ndinakupatsani ndi makolo anu.’ Komabe inu simunasamale zimenezi kapena kundimvera Ine. 16 Zidzukulu za Yehonadabu mwana wa Rekabu zakhala zikumvera lamulo limene kholo lawo anazilamula, koma inuyo simunandimvere Ine.

17 “Nʼchifukwa chake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndidzagwetsera pa Yuda ndi pa onse okhala mu Yerusalemu masautso onse amene ndinakonza chifukwa sanandimvere. Ndinawayitana koma iwo sanayankhe.’ ”

18 Yeremiya anawuza banja la Arekabu mawu onse a Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, kuti, “Munamvera lamulo la kholo lanu Yehonadabu ndipo mwatsatira malangizo ake onse ndi kuchita chilichonse chimene anakulamulani.” 19 Tsono Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Yehonadabu mwana wa Rekabu sadzasowa munthu wonditumikira Ine nthawi zonse.”

The Rekabites

35 This is the word that came to Jeremiah from the Lord during the reign of Jehoiakim(A) son of Josiah king of Judah: “Go to the Rekabite(B) family and invite them to come to one of the side rooms(C) of the house of the Lord and give them wine to drink.”

So I went to get Jaazaniah son of Jeremiah, the son of Habazziniah, and his brothers and all his sons—the whole family of the Rekabites. I brought them into the house of the Lord, into the room of the sons of Hanan son of Igdaliah the man of God.(D) It was next to the room of the officials, which was over that of Maaseiah son of Shallum(E) the doorkeeper.(F) Then I set bowls full of wine and some cups before the Rekabites and said to them, “Drink some wine.”

But they replied, “We do not drink wine, because our forefather Jehonadab[a](G) son of Rekab gave us this command: ‘Neither you nor your descendants must ever drink wine.(H) Also you must never build houses, sow seed or plant vineyards; you must never have any of these things, but must always live in tents.(I) Then you will live a long time in the land(J) where you are nomads.’ We have obeyed everything our forefather(K) Jehonadab son of Rekab commanded us. Neither we nor our wives nor our sons and daughters have ever drunk wine or built houses to live in or had vineyards, fields or crops.(L) 10 We have lived in tents and have fully obeyed everything our forefather Jehonadab commanded us. 11 But when Nebuchadnezzar king of Babylon invaded(M) this land, we said, ‘Come, we must go to Jerusalem(N) to escape the Babylonian[b] and Aramean armies.’ So we have remained in Jerusalem.”

12 Then the word of the Lord came to Jeremiah, saying: 13 “This is what the Lord Almighty, the God of Israel, says: Go and tell(O) the people of Judah and those living in Jerusalem, ‘Will you not learn a lesson(P) and obey my words?’ declares the Lord. 14 ‘Jehonadab son of Rekab ordered his descendants not to drink wine and this command has been kept. To this day they do not drink wine, because they obey their forefather’s command.(Q) But I have spoken to you again and again,(R) yet you have not obeyed(S) me. 15 Again and again I sent all my servants the prophets(T) to you. They said, “Each of you must turn(U) from your wicked ways and reform(V) your actions; do not follow other gods(W) to serve them. Then you will live in the land(X) I have given to you and your ancestors.” But you have not paid attention or listened(Y) to me. 16 The descendants of Jehonadab son of Rekab have carried out the command their forefather(Z) gave them, but these people have not obeyed me.’

17 “Therefore this is what the Lord God Almighty, the God of Israel, says: ‘Listen! I am going to bring on Judah and on everyone living in Jerusalem every disaster(AA) I pronounced against them. I spoke to them, but they did not listen;(AB) I called to them, but they did not answer.’”(AC)

18 Then Jeremiah said to the family of the Rekabites, “This is what the Lord Almighty, the God of Israel, says: ‘You have obeyed the command of your forefather(AD) Jehonadab and have followed all his instructions and have done everything he ordered.’ 19 Therefore this is what the Lord Almighty, the God of Israel, says: ‘Jehonadab son of Rekab will never fail(AE) to have a descendant to serve(AF) me.’”

Footnotes

  1. Jeremiah 35:6 Hebrew Jonadab, a variant of Jehonadab; here and often in this chapter
  2. Jeremiah 35:11 Or Chaldean