Add parallel Print Page Options

Yeremiya Aponyedwa Mʼchitsime cha Matope

38 Sefatiya mwana wa Matani, Gedaliya mwana wa Pasi-Huri, Yukali mwana wa Selemiya, ndi Pasi-Huri mwana wa Malikiya anamva zimene Yeremiya ankawuza anthu onse kuti, “Yehova akuti, ‘Aliyense amene akhale mu mzinda muno adzafa ndi nkhondo njala kapena mliri. Koma aliyense amene atatuluke kukadzipereka kwa Ababuloni adzapulumutsa moyo wake; iyeyo adzakhala ndi moyo. Mzinda uno udzaperekedwa ndithu kwa gulu lankhondo la mfumu ya ku Babuloni, amene adzawulande.’ ”

Tsono akuluakuluwo anawuza mfumu kuti, “Munthu uyu ayenera kuphedwa. Iye akutayitsa mtima asilikali pamodzi ndi anthu onse amene atsala mu mzinda muno, chifukwa cha zimene akuwawuza. Munthu ameneyu sakufunira zabwino anthuwa koma chiwonongeko chawo.”

Mfumu Zedekiya anayankha kuti, “Munthuyu ali mʼmanja mwanu. Ine sindingakuletseni chimene mukufuna kumuchitira.”

Choncho iwo anatenga Yeremiya nakamuponya mʼchitsime cha Malikiya, mwana wa mfumu, chimene chinali mʼbwalo la alonda. Iwo anamutsitsira mʼdzenjemo ndi chingwe. Munalibe madzi koma matope okhaokha, ndipo Yeremiya anamira mʼmatopewo.

Koma Ebedi-Meleki, Mkusi, mmodzi mwa anthu ofulidwa ogwira ntchito mʼnyumba ya mfumu, anamva kuti Yeremiya anamuponya mʼchitsime. Nthawi imeneyo nʼkuti mfumu ili ku chipata cha Benjamini. Ebedi-Meleki anatuluka ku nyumba ya mfumu kukayiwuza kuti, “Mbuye wanga mfumu, zimene anthu awa amuchitira mneneri Yeremiya ndi zoyipa kwambiri. Iwo amuponya mʼchitsime, ndipo adzafa ndi njala chifukwa buledi watha mu mzinda muno.”

10 Tsono mfumu inalamula Ebedi-Meleki, Mkusi, kuti, “Tenga anthu makumi atatu, ndipo mukamutulutse mʼchitsimemo mneneri Yeremiya asanafe.”

11 Pamenepo Ebedi-Meleki anatenga anthuwo, napita nawo ku nyumba ya mfumu ya pansi pa chipinda chosungiramo chuma. Kumeneko anakatengako sanza ndipo anatsitsira sanzazo ndi chingwe mʼchitsime mʼmene munali Yeremiya. 12 Ebedi-Meleki, Mkusi, anawuza Yeremiya kuti, “Ika sanzazo mkwapa mwako kuti zingwe zingakupweteke.” Yeremiya anachitadi zimenezi, 13 ndipo anamukoka ndi zingwe ndi kumutulutsa mʼchitsimecho. Ndipo Yeremiya anakhalabe ku bwalo la alonda.

Zedekiya Afunsanso Yeremiya

14 Tsiku lina Mfumu Zedekiya anayitana mneneri Yeremiya ndipo anabwera naye ku chipata chachitatu cha Nyumba ya Yehova. Mfumu inawuza Yeremiya kuti, “Ndikufuna kukufunsa kanthu kena, ndipo usandibisire chilichonse.”

15 Yeremiya anati kwa Zedekiya, “Ndikakuyankhani, kodi simundipha? Ngakhaletu ine nditakulangizani, inu simudzandimvera.”

16 Koma Mfumu Zedekiya mwachinsinsi inalumbira kwa Yeremiya kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene amatipatsa moyo, sindidzakupha ngakhalenso kukupereka kwa amene akufuna kukuphawa.”

17 Pamenepo Yeremiya anati kwa Zedekiya, “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ngati mutuluka kukadzipereka kwa ankhondo a mfumu ya ku Babuloni, mudzakhala ndi moyo ndipo mzinda uno sadzawutentha, inu pamodzi ndi banja lanu mudzakhala ndi moyo. 18 Koma ngati simutuluka kukadzipereka kwa ankhondo a mfumu ya ku Babuloni, mzinda uno udzaperekedwa kwa Ababuloni ndipo adzawutentha; inuyo simudzapulumuka mʼdzanja mwawo.’ ”

19 Mfumu Zedekiya inati kwa Yeremiya, “Ine ndikuopa Ayuda amene anathawira kale kwa Ababuloni, pakuti mwina Ababuloniwo adzandipereka kwa Ayudawo ndipo iwowo adzandizunza.”

20 Yeremiya anayankha kuti, “Ngati mumvera Yehova ndi kuchita zimene ndakuwuzani, ndiye kuti zinthu zidzakuyenderani bwino. Inu simudzaphedwa. 21 Koma mukakana kudzipereka, chimene Yehova wandiwululira ndi ichi: 22 Akazi onse amene atsala mʼnyumba ya mfumu ya Yuda adzaperekedwa kwa akuluakulu a mfumu ya ku Babuloni. Akazi amenewo adzakuwuzani kuti,

“ ‘Abwenzi ako okhulupirika aja anakusokeretsa,
    ndipo anakugonjetsa.
Poti tsopano miyendo yako yazama mʼmatope;
    abwenzi ako aja akusiya.’

23 “Akazi pamodzi ndi ana anu adzaperekedwa kwa Ababuloni. Inuyo simudzapulumuka mʼmanja mwawo koma mfumu ya ku Babuloni idzakugwirani; mzinda uno adzawutentha.”

24 Pamenepo Zedekiya anati kwa Yeremiya, “Usawuze munthu wina aliyense zimene takambiranazi, ukatero udzaphedwa. 25 Akuluakulu akamva kuti ndinayankhula nawe ndipo akabwera kwa iwe nʼkudzakufunsa kuti, ‘Tiwuze zimene unanena kwa mfumu ndi zimene mfumu inanena kwa iwe; usatibisire, ukatero tidzakupha,’ 26 udzawawuze kuti, ‘Ine ndimapempha mfumu kuti isandibwezerenso ku nyumba ya Yonatani kuti ndikafere kumeneko.’ ”

27 Akuluakulu onse anabweradi kwa Yeremiya kudzamufunsa. Iye anawayankha monga momwe mfumu inamulamula. Choncho palibe amene ananenanso kanthu, pakuti palibe amene anamva zomwe anakambirana ndi mfumu.

28 Ndipo Yeremiya anakhalabe mʼbwalo la alonda mpaka tsiku limene mzinda wa Yerusalemu unalandidwa.

Jeremiah Thrown Into a Cistern

38 Shephatiah son of Mattan, Gedaliah son of Pashhur(A), Jehukal[a](B) son of Shelemiah, and Pashhur son of Malkijah heard what Jeremiah was telling all the people when he said, “This is what the Lord says: ‘Whoever stays in this city will die by the sword, famine or plague,(C) but whoever goes over to the Babylonians[b] will live. They will escape with their lives; they will live.’(D) And this is what the Lord says: ‘This city will certainly be given into the hands of the army of the king of Babylon, who will capture it.’”(E)

Then the officials(F) said to the king, “This man should be put to death.(G) He is discouraging(H) the soldiers who are left in this city, as well as all the people, by the things he is saying to them. This man is not seeking the good of these people but their ruin.”

“He is in your hands,”(I) King Zedekiah answered. “The king can do nothing(J) to oppose you.”

So they took Jeremiah and put him into the cistern of Malkijah, the king’s son, which was in the courtyard of the guard.(K) They lowered Jeremiah by ropes(L) into the cistern; it had no water in it,(M) only mud, and Jeremiah sank down into the mud.(N)

But Ebed-Melek,(O) a Cushite,[c] an official[d](P) in the royal palace, heard that they had put Jeremiah into the cistern. While the king was sitting in the Benjamin Gate,(Q) Ebed-Melek went out of the palace and said to him, “My lord the king, these men have acted wickedly in all they have done to Jeremiah the prophet. They have thrown him into a cistern,(R) where he will starve to death when there is no longer any bread(S) in the city.”

10 Then the king commanded Ebed-Melek the Cushite, “Take thirty men from here with you and lift Jeremiah the prophet out of the cistern before he dies.”

11 So Ebed-Melek took the men with him and went to a room under the treasury in the palace. He took some old rags and worn-out clothes from there and let them down with ropes(T) to Jeremiah in the cistern. 12 Ebed-Melek the Cushite said to Jeremiah, “Put these old rags and worn-out clothes under your arms to pad the ropes.” Jeremiah did so, 13 and they pulled him up with the ropes and lifted him out of the cistern. And Jeremiah remained in the courtyard of the guard.(U)

Zedekiah Questions Jeremiah Again

14 Then King Zedekiah sent(V) for Jeremiah the prophet and had him brought to the third entrance to the temple of the Lord. “I am going to ask you something,” the king said to Jeremiah. “Do not hide(W) anything from me.”

15 Jeremiah said to Zedekiah, “If I give you an answer, will you not kill me? Even if I did give you counsel, you would not listen to me.”

16 But King Zedekiah swore this oath secretly(X) to Jeremiah: “As surely as the Lord lives, who has given us breath,(Y) I will neither kill you nor hand you over to those who want to kill you.”(Z)

17 Then Jeremiah said to Zedekiah, “This is what the Lord God Almighty, the God of Israel, says: ‘If you surrender(AA) to the officers of the king of Babylon, your life will be spared and this city will not be burned down; you and your family will live.(AB) 18 But if you will not surrender to the officers of the king of Babylon, this city will be given into the hands(AC) of the Babylonians and they will burn(AD) it down; you yourself will not escape(AE) from them.’”

19 King Zedekiah said to Jeremiah, “I am afraid(AF) of the Jews who have gone over(AG) to the Babylonians, for the Babylonians may hand me over to them and they will mistreat me.”

20 “They will not hand you over,” Jeremiah replied. “Obey(AH) the Lord by doing what I tell you. Then it will go well(AI) with you, and your life(AJ) will be spared. 21 But if you refuse to surrender, this is what the Lord has revealed to me: 22 All the women(AK) left in the palace of the king of Judah will be brought out to the officials of the king of Babylon. Those women will say to you:

“‘They misled you and overcame you—
    those trusted friends(AL) of yours.
Your feet are sunk in the mud;(AM)
    your friends have deserted you.’

23 “All your wives and children(AN) will be brought out to the Babylonians. You yourself will not escape(AO) from their hands but will be captured(AP) by the king of Babylon; and this city will[e] be burned down.”(AQ)

24 Then Zedekiah said to Jeremiah, “Do not let anyone know(AR) about this conversation, or you may die. 25 If the officials hear that I talked with you, and they come to you and say, ‘Tell us what you said to the king and what the king said to you; do not hide it from us or we will kill you,’ 26 then tell(AS) them, ‘I was pleading with the king not to send me back to Jonathan’s house(AT) to die there.’”

27 All the officials did come to Jeremiah and question him, and he told them everything the king had ordered him to say. So they said no more to him, for no one had heard his conversation with the king.

28 And Jeremiah remained in the courtyard of the guard(AU) until the day Jerusalem was captured.

The Fall of Jerusalem(AV)

This is how Jerusalem(AW) was taken:

Footnotes

  1. Jeremiah 38:1 Hebrew Jukal, a variant of Jehukal
  2. Jeremiah 38:2 Or Chaldeans; also in verses 18, 19 and 23
  3. Jeremiah 38:7 Probably from the upper Nile region
  4. Jeremiah 38:7 Or a eunuch
  5. Jeremiah 38:23 Or and you will cause this city to