Add parallel Print Page Options

Kugonjetsedwa kwa Yerusalemu

39 Mzinda wa Yerusalemu anawulanda motere: Mʼchaka chachisanu ndi chinayi cha Zedekiya mfumu ya Yuda, mwezi wakhumi, Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni anabwera ndi gulu lake lonse kudzathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu ndipo anawuzinga mzindawo. Ndipo pa tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi wachinayi wa chaka cha khumi ndi chimodzi cha Zedekiya, malinga a mzindawo anabowoledwa. Pamenepo akuluakulu onse a mfumu ya ku Babuloni anabwera nakakhala pa Chipata Chapakati. Akuluwo ndi awa: Nerigali-Sarezeri, Samugara Nebo, Sarisekimu mkulu wa nduna, Nerigali-Sarezeri winanso mlangizi wa mfumu ndi akuluakulu onse a mfumu ya ku Babuloni. Zedekiya mfumu ya Yuda pamodzi ndi ankhondo ake atawaona, anathawa mu mzindawo usiku podzera ku munda wa mfumu, kudutsa chipata cha pakati pa makoma awiri. Anathawira ku Araba.

Koma gulu la ankhondo la ku Babuloni linalondola ndi kumupeza Zedekiyayo mʼchigwa cha ku Yeriko. Anamugwira napita naye kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni ku Ribula mʼdziko la Hamati kumene anagamula mlandu wake. Ku Ribulako, mfumu ya ku Babuloni inapha ana aamuna a Zedekiya iyeyo akuona. Inaphanso anthu olemekezeka onse a ku Yuda. Kenaka inakolowola maso a Zedekiya ndi kumumanga ndi maunyolo a mkuwa nʼkupita naye ku Babuloni.

Ababuloni anatentha nyumba ya mfumu ndi nyumba za anthu, ndiponso anagwetsa malinga a Yerusalemu. Nebuzaradani, mtsogoleri wa alonda ankhondo a mfumu, anatenga ukapolo anthu onse otsala mu mzindamo kupita nawo ku Babuloni, pamodzi ndi amene anadzipereka kale kwa iye. 10 Koma Nebuzaradani, mtsogoleri wa alonda ankhondo anasiya mʼdziko la Yuda anthu ena osauka, amene analibe chilichonse; ndipo anawapatsa minda ya mpesa ndi minda inanso.

11 Tsono Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni inatuma mawu kwa Nebuzaradani mtsogoleri wa alonda ankhondo a mfumu za Yeremiya. Iye anati: 12 “Mutenge, umusamale bwino, ndipo usamuvute koma umuchitire zimene afuna.” 13 Choncho Nebuzaradani mtsogoleri wa alonda, Nebusazibani mkulu wa nduna, Nerigali-Sarezeri mlangizi wamkulu wa mfumu ndi akuluakulu onse a mfumu ya ku Babuloni 14 anatuma anthu nakamutulutsa Yeremiya mʼbwalo la alonda. Anakamupereka kwa Gedaliya mwana wa Ahikamu, mwana wa Safani, kuti amutumize ku nyumba yake. Ndipo Yeremiya anakhala pakati pa abale ake.

15 Yeremiya ali mʼndende ku bwalo la alonda, Yehova anayankhula naye: 16 “Pita ukamuwuze Ebedi-Meleki, Mkusi, kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Zidzachitikadi zimene ndinanena zokhudza mzinda uno; ndipo zidzakhala zoyipa osati zabwino ayi. Zimenezi zidzachitika pa nthawi yake iwe ukuona. 17 Koma ndidzakupulumutsa pa tsiku limenelo, akutero Yehova; sudzaperekedwa kwa anthu amene umawaopa. 18 Ndithu ndidzakupulumutsa; sudzaphedwa pa nkhondo koma udzapulumuka, chifukwa wadalira Ine, akutero Yehova.’ ”

39 In the ninth year of Zedekiah(A) king of Judah, in the tenth month, Nebuchadnezzar(B) king of Babylon marched against Jerusalem with his whole army and laid siege(C) to it. And on the ninth day of the fourth(D) month of Zedekiah’s eleventh year, the city wall(E) was broken through.(F) Then all the officials(G) of the king of Babylon came and took seats in the Middle Gate: Nergal-Sharezer of Samgar, Nebo-Sarsekim a chief officer, Nergal-Sharezer a high official and all the other officials of the king of Babylon. When Zedekiah king of Judah and all the soldiers saw them, they fled; they left the city at night by way of the king’s garden, through the gate between the two walls,(H) and headed toward the Arabah.[a](I)

But the Babylonian[b] army pursued them and overtook Zedekiah(J) in the plains of Jericho. They captured(K) him and took him to Nebuchadnezzar king of Babylon at Riblah(L) in the land of Hamath, where he pronounced sentence on him. There at Riblah the king of Babylon slaughtered the sons of Zedekiah before his eyes and also killed all the nobles(M) of Judah. Then he put out Zedekiah’s eyes(N) and bound him with bronze shackles to take him to Babylon.(O)

The Babylonians[c] set fire(P) to the royal palace and the houses of the people and broke down the walls(Q) of Jerusalem. Nebuzaradan commander of the imperial guard carried into exile to Babylon the people who remained in the city, along with those who had gone over to him,(R) and the rest of the people.(S) 10 But Nebuzaradan the commander of the guard left behind in the land of Judah some of the poor people, who owned nothing; and at that time he gave them vineyards and fields.

11 Now Nebuchadnezzar king of Babylon had given these orders about Jeremiah through Nebuzaradan commander of the imperial guard: 12 “Take him and look after him; don’t harm(T) him but do for him whatever he asks.” 13 So Nebuzaradan the commander of the guard, Nebushazban a chief officer, Nergal-Sharezer a high official and all the other officers(U) of the king of Babylon 14 sent and had Jeremiah taken out of the courtyard of the guard.(V) They turned him over to Gedaliah(W) son of Ahikam,(X) the son of Shaphan,(Y) to take him back to his home. So he remained among his own people.(Z)

15 While Jeremiah had been confined in the courtyard of the guard, the word of the Lord came to him: 16 “Go and tell Ebed-Melek(AA) the Cushite, ‘This is what the Lord Almighty, the God of Israel, says: I am about to fulfill my words(AB) against this city—words concerning disaster,(AC) not prosperity. At that time they will be fulfilled before your eyes. 17 But I will rescue(AD) you on that day, declares the Lord; you will not be given into the hands of those you fear. 18 I will save(AE) you; you will not fall by the sword(AF) but will escape with your life,(AG) because you trust(AH) in me, declares the Lord.’”

Footnotes

  1. Jeremiah 39:4 Or the Jordan Valley
  2. Jeremiah 39:5 Or Chaldean
  3. Jeremiah 39:8 Or Chaldeans