Add parallel Print Page Options

“Ngati mukufuna kubwerera, inu Aisraeli,
    bwererani kwa Ine,”
            akutero Yehova.
“Chotsani mafano anu onyansa pamaso panga
    ndipo musasocherenso.
Muzilumbira mokhulupirika ndiponso mwa chilungamo
    kuti, ‘Pali Yehova wamoyo.’
Mukatero anthu a mitundu ina yonse adzandipempha kuti ndiwadalitse
    ndipo adzanditamanda.”

Zimene Yehova akunena kwa anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu ndi izi:

“Limani masala anu
    musadzale pakati pa minga.
Dziperekeni nokha kwa Ine
    kuti munditumikire ndi mtima wanu wonse,
    inu anthu a ku Yuda ndi ku Yerusalemu.
Muzichita zimenezi kuopa kuti mkwiyo wanga ungabuke ngati moto ndi kukutenthani,
    chifukwa cha ntchito zanu zoyipazo
    popanda wina wowuzimitsa.

Adani Ochokera Kumpoto kwa Yuda

“Lengeza ku Yuda ndi kulalikira mu Yerusalemu kuti,
    ‘Lizani lipenga mʼdziko lonse!’
Ndipo fuwulani kuti,
    ‘Sonkhanani!
    Tiyeni tithawire ku mizinda yotetezedwa!’
Kwezani mbendera kuyangʼana ku Ziyoni!
    Musachedwe, thawani kuti mupulumuke!
Pakuti Ine ndikubweretsa chilango kuchokera kumpoto,
    kudzakhala chiwonongeko choopsa.”

Monga mkango umatulukira mʼngaka yake
    momwemonso wowononga mayiko
wanyamuka ndi kutuluka ku mbuto yake.
    Watero kuti awononge dziko lanu.
Mizinda yanu idzakhala mabwinja
    popanda wokhalamo.
Choncho valani ziguduli,
    lirani ndi kubuwula,
pakuti mkwiyo waukulu wa Yehova
    sunatichokere.

“Pa tsiku limenelo, mfumu ndi nduna zake adzataya mtima,
    ansembe adzachita mantha kwambiri,
ndipo aneneri adzathedwa nzeru,”
    akutero Yehova.

10 Ndipo ine ndinati, “Haa, Ambuye Yehova, ndithu munawanyenga anthu awa pamodzi ndi Yerusalemu pamene munanena kuti, ‘Mudzakhala pa mtendere,’ chonsecho lupanga lili pakhosi pathu.”

11 Nthawi imeneyo anthu awa ndi Yerusalemu adzawawuza kuti, “Mphepo yotentha yochokera ku magomo a mʼchipululu ikuwomba pa anthu anga, osati mphepo yopeta kapena yoyeretsa; 12 koma mphepo yamphamvu kwambiri yochokera kwa Ine. Tsono ndi Ineyo amene ndikuwaweruza.”

13 Taonani, adani akubwera ngati mitambo,
    magaleta awo akubwera ngati kamvuluvulu,
akavalo awo ndi aliwiro kupambana chiwombankhanga.
    Tsoka ilo! Tawonongeka!
14 Iwe Yerusalemu, tsuka mtima wako kuchotsa zoyipa kuti upulumuke.
    Kodi maganizo ako oyipawo udzakhala nawo mpaka liti?
15 Pakuti amithenga akulalika mawu mʼdziko la Dani;
    akulengeza za masautso kuchokera ku mapiri a Efereimu.
16 Iwo akuti, “Fotokozani zimenezi kwa anthu a mitundu ina,
    lengezani zimenezi mu Yerusalemu kuti,
‘Ankhondo akubwera kuchokera ku dziko lakutali,
    akufuwula ndi kudzazinga mizinda ya Yuda.
17 Azinga Yerusalemu ngati anthu olondera munda,
    chifukwa Yerusalemu wandiwukira,’ ”
            akutero Yehova.
18 “Makhalidwe anu ndi zochita zanu
    zakubweretserani zimenezi.
Chimenechi ndiye chilango chanu.
    Nʼchowawa kwambiri!
    Nʼcholasa mpaka mu mtima!”

19 Mayo, mayo,
    ndikumva kupweteka!
Aa, mtima wanga ukupweteka,
    ukugunda kuti thi, thi, thi.
    Sindingathe kukhala chete.
Pakuti ndamva kulira kwa lipenga;
    ndamva mfuwu wankhondo.
20 Tsoka limatsata tsoka linzake;
    dziko lonse lasanduka bwinja.
Mwadzidzidzi matenti athu awonongedwa,
    mwa kanthawi kochepa nsalu zake zotchinga zagwetsedwa.
21 Kodi ndikhale ndikuona mbendera ya nkhondo,
    ndi kumva kulira kwa lipenga mpaka liti?

22 Yehova akuti, “Anthu anga ndi zitsiru;
    iwo sandidziwa.
Iwo ndi ana opanda nzeru;
    samvetsa chilichonse.
Ali ndi luso lochita zoyipa,
    koma sadziwa kuchita zabwino.”

23 Ndinayangʼana dziko lapansi,
    ndipo linali lopanda anthu ndi lopanda kanthu;
ndinayangʼana thambo,
    koma linalibe kuwala kulikonse.
24 Ndinayangʼana mapiri,
    ndipo ankagwedezeka;
    magomo onse ankangosunthira uku ndi uku.
25 Ndinayangʼana, ndipo sindinaone anthu;
    mbalame iliyonse ya mlengalenga inali itathawa.
26 Ndinayangʼana, dziko lachonde linali litasanduka chipululu;
    mizinda yake yonse inali itasanduka bwinja
    pamaso pa Yehova, chifukwa cha mkwiyo wake.

27 Yehova akuti,

“Dziko lonse lidzasanduka chipululu
    komabe sindidzaliwononga kotheratu.
28 Chifukwa chake dziko lapansi lidzalira
    ndipo thambo lidzachita mdima,
pakuti ndayankhula ndipo sindidzafewa mtima,
    ndatsimikiza ndipo sindidzabwerera mʼmbuyo.”

29 Pakumva phokoso la okwera pa akavalo ndi la anthu oponya mivi,
    anthu a mʼmizinda adzathawa.
Ena adzabisala ku nkhalango;
    ena adzakwera mʼmatanthwe
mizinda yonse nʼkuyisiya;
    popanda munthu wokhalamo.

30 Iwe Yerusalemu, ndiwe bwinja!
    Ukutanthauza chiyani kuvala zovala zofiira
    ndi kuvalanso zokometsera zagolide?
Ngakhale udzikonze maso ako powapaka zokometsera,
    ukungodzivuta chabe.
Zibwenzi zako zikukunyoza;
    zikufuna kuchotsa moyo wako.

31 Ndikumva kulira ngati kwa mayi pa nthawi yake yobereka,
    kubuwula ngati kwa mayi amene akubereka mwana wake woyamba.
Kuliraku ndi kwa anthu a mu Ziyoni, wefuwefu.
    Atambalitsa manja awo nʼkumati,
“Kalanga ife! Tikukomoka.
    Moyo wathu waperekedwa kwa anthu otipha.”

“If you, Israel, will return,(A)
    then return to me,”
declares the Lord.
“If you put your detestable idols(B) out of my sight
    and no longer go astray,
and if in a truthful, just and righteous way
    you swear,(C) ‘As surely as the Lord lives,’(D)
then the nations will invoke blessings(E) by him
    and in him they will boast.(F)

This is what the Lord says to the people of Judah and to Jerusalem:

“Break up your unplowed ground(G)
    and do not sow among thorns.(H)
Circumcise yourselves to the Lord,
    circumcise your hearts,(I)
    you people of Judah and inhabitants of Jerusalem,
or my wrath(J) will flare up and burn like fire(K)
    because of the evil(L) you have done—
    burn with no one to quench(M) it.

Disaster From the North

“Announce in Judah and proclaim(N) in Jerusalem and say:
    ‘Sound the trumpet(O) throughout the land!’
Cry aloud and say:
    ‘Gather together!
    Let us flee to the fortified cities!’(P)
Raise the signal(Q) to go to Zion!
    Flee for safety without delay!
For I am bringing disaster(R) from the north,(S)
    even terrible destruction.”

A lion(T) has come out of his lair;(U)
    a destroyer(V) of nations has set out.
He has left his place
    to lay waste(W) your land.
Your towns will lie in ruins(X)
    without inhabitant.
So put on sackcloth,(Y)
    lament(Z) and wail,
for the fierce anger(AA) of the Lord
    has not turned away from us.

“In that day,” declares the Lord,
    “the king and the officials will lose heart,(AB)
the priests will be horrified,
    and the prophets will be appalled.”(AC)

10 Then I said, “Alas, Sovereign Lord! How completely you have deceived(AD) this people and Jerusalem by saying, ‘You will have peace,’(AE) when the sword is at our throats!”

11 At that time this people and Jerusalem will be told, “A scorching wind(AF) from the barren heights in the desert blows toward my people, but not to winnow or cleanse; 12 a wind(AG) too strong for that comes from me. Now I pronounce my judgments(AH) against them.”

13 Look! He advances like the clouds,(AI)
    his chariots(AJ) come like a whirlwind,(AK)
his horses(AL) are swifter than eagles.(AM)
    Woe to us! We are ruined!(AN)
14 Jerusalem, wash(AO) the evil from your heart and be saved.(AP)
    How long(AQ) will you harbor wicked thoughts?
15 A voice is announcing from Dan,(AR)
    proclaiming disaster from the hills of Ephraim.(AS)
16 “Tell this to the nations,
    proclaim concerning Jerusalem:
‘A besieging army is coming from a distant land,(AT)
    raising a war cry(AU) against the cities of Judah.(AV)
17 They surround(AW) her like men guarding a field,
    because she has rebelled(AX) against me,’”
declares the Lord.
18 “Your own conduct and actions(AY)
    have brought this on you.(AZ)
This is your punishment.
    How bitter(BA) it is!
    How it pierces to the heart!”

19 Oh, my anguish, my anguish!(BB)
    I writhe in pain.(BC)
Oh, the agony of my heart!
    My heart pounds(BD) within me,
    I cannot keep silent.(BE)
For I have heard the sound of the trumpet;(BF)
    I have heard the battle cry.(BG)
20 Disaster follows disaster;(BH)
    the whole land lies in ruins.(BI)
In an instant my tents(BJ) are destroyed,
    my shelter in a moment.
21 How long must I see the battle standard(BK)
    and hear the sound of the trumpet?(BL)

22 “My people are fools;(BM)
    they do not know me.(BN)
They are senseless children;
    they have no understanding.(BO)
They are skilled in doing evil;(BP)
    they know not how to do good.”(BQ)

23 I looked at the earth,
    and it was formless and empty;(BR)
and at the heavens,
    and their light(BS) was gone.
24 I looked at the mountains,
    and they were quaking;(BT)
    all the hills were swaying.
25 I looked, and there were no people;
    every bird in the sky had flown away.(BU)
26 I looked, and the fruitful land was a desert;(BV)
    all its towns lay in ruins(BW)
    before the Lord, before his fierce anger.(BX)

27 This is what the Lord says:

“The whole land will be ruined,(BY)
    though I will not destroy(BZ) it completely.
28 Therefore the earth will mourn(CA)
    and the heavens above grow dark,(CB)
because I have spoken and will not relent,(CC)
    I have decided and will not turn back.(CD)

29 At the sound of horsemen and archers(CE)
    every town takes to flight.(CF)
Some go into the thickets;
    some climb up among the rocks.(CG)
All the towns are deserted;(CH)
    no one lives in them.

30 What are you doing,(CI) you devastated one?
    Why dress yourself in scarlet
    and put on jewels(CJ) of gold?
Why highlight your eyes with makeup?(CK)
    You adorn yourself in vain.
Your lovers(CL) despise you;
    they want to kill you.(CM)

31 I hear a cry as of a woman in labor,(CN)
    a groan as of one bearing her first child—
the cry of Daughter Zion(CO) gasping for breath,(CP)
    stretching out her hands(CQ) and saying,
“Alas! I am fainting;
    my life is given over to murderers.”(CR)