Add parallel Print Page Options

42 Atsogoleri onse a ankhondo pamodzi ndi Yohanani mwana wa Kareya ndi Azariya mwana wa Hosayia, ndiponso anthu onse, ana ndi akuluakulu omwe, anapita kwa mneneri Yeremiya ndipo anamuwuza kuti, “Chonde imvani dandawulo lathu ndipo mutipempherere anthu otsalafe kwa Yehova Mulungu wanu. Pakuti monga tsopano mukuona, ngakhale kuti kale tinalipo ambiri, koma tsopano ochepa okha ndiye amene atsala. Mupemphere kuti Yehova Mulungu wanu atiwuze kumene tiyenera kupita ndi chimene tiyenera kuchita.”

Mneneri Yeremiya anawayankha kuti, “Ndamva zimene mwanenazi. Ndithu ndidzapemphera kwa Yehova Mulungu wanu monga momwe mwandipemphera. Ndidzakuwuzani chilichonse chimene Yehova anene ndipo sindidzakubisirani kanthu kalikonse.”

Ndipo iwo anawuza Yeremiya kuti, “Yehova akhale mboni yoona ndi yokhulupirika yodzatitsutsa ife ngati sitichita mogwirizana ndi chilichonse chimene Yehova Mulungu adzakutumani kuti mutiwuze. Kaya ndi zotikomera kapena zosatikomera, ife tidzamvera Yehova Mulungu wathu, amene takutumaniko. Tidzamvera Yehova Mulungu wathu kuti zinthu zidzatiyendere bwino.”

Patapita masiku khumi, Yehova anayankhula ndi Yeremiya. Choncho Yeremiya anayitana Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi atsogoleri onse a ankhondo amene anali naye ndiponso anthu onse, ana ndi akulu omwe. Yehova, Mulungu wa Israeli amene munanditumako kuti ndikapereke madandawulo mʼdzina lanu akuti, 10 “Ngati mukhala mʼdziko muno, ndiye kuti ndidzakukhazikitsani, osakuchotsani. Inde ndidzakudzalani osakuchotsani pakuti ndi kumva chisoni kwambiri chifukwa cha mavuto amene ndabweretsa pa inu. 11 Musayiope mfumu ya ku Babuloni, imene mukuyiopa tsopano. Musachite nayo mantha, akutero Yehova, pakuti Ine ndili nanu ndipo ndidzakupulumutsani ndi kukulanditsani mʼmanja mwake. 12 Ndidzakuchitirani chifundo, ndipo mfumuyonso idzakuchitirani chifundo ndi kukulolani kuti mukhale mʼdziko mwanumwanu.

13 “Koma mwina simudzamvera Yehova Mulungu wanu nʼkumanena kuti, ‘Ayi ife sitidzakhala mʼdziko muno, 14 ndipo ngati mukunena kuti, ‘Ayi, koma tidzapita ku Igupto kumene sitidzaonako nkhondo kapena kumva kulira kwa lipenga kapenanso kusowa chakudya.’ 15 Tsono, inu otsala a ku Yuda, imvani mawu a Yehova. Iye akuti, ngati mutsimikiza zopita ku Igupto, nʼkupitadi kukakhala kumeneko, 16 ndiye nkhondo imene mukuyiopayo idzakugonjetsani ku Igupto komweko. Njala imene mukuyiopayo idzakupezani ku Igupto komweko ndipo mudzafera kumeneko. 17 Kunena zoona, onse amene atsimikiza zopita ku Igupto kuti akakhale kumeneko adzafa ndi nkhondo njala ndi mliri. Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzapulumuke kapena kuthawa mavuto amene ndidzawagwetsera.’ 18 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Momwe ndinawakwiyira mwaukali anthu okhala mu Yerusalemu, koteronso ndidzakukwiyirani mukapita ku Igupto. Mudzasanduka chinthu chotembereredwa ndi chochititsa mantha, choseketsa ndi chonyozeka. Malo ano simudzawaonanso.’

19 “Inu otsala a ku Yuda, Yehova wakuwuzani kuti, ‘Musapite ku Igupto.’ Dziwani chinthu ichi: Ine lero ndikukuchenjezani 20 kuti munalakwitsa kwambiri. Inu munandituma kwa Yehova Mulungu wanu nʼkumati ‘Mukatipempherere kwa Yehova Mulungu wathu, nʼkudzatiwuza chimene afuna kuti tichite, ndipo ife tidzachita.’ 21 Ine lero ndakuwuzani, koma inu simukumverabe zonse zimene Yehova Mulungu anandituma kuti ndikuwuzeni. 22 Tsono dziwani ichi: mudzafadi ndi nkhondo, njala ndi mliri kumalo kumene mukufuna mukakhaleko.”

42 Then all the army officers, including Johanan(A) son of Kareah and Jezaniah[a] son of Hoshaiah,(B) and all the people from the least to the greatest(C) approached Jeremiah the prophet and said to him, “Please hear our petition and pray(D) to the Lord your God for this entire remnant.(E) For as you now see, though we were once many, now only a few(F) are left. Pray that the Lord your God will tell us where we should go and what we should do.”(G)

“I have heard you,” replied Jeremiah the prophet. “I will certainly pray(H) to the Lord your God as you have requested; I will tell(I) you everything the Lord says and will keep nothing back from you.”(J)

Then they said to Jeremiah, “May the Lord be a true(K) and faithful(L) witness(M) against us if we do not act in accordance with everything the Lord your God sends you to tell us. Whether it is favorable or unfavorable, we will obey the Lord our God, to whom we are sending you, so that it will go well(N) with us, for we will obey(O) the Lord our God.”

Ten days later the word of the Lord came to Jeremiah. So he called together Johanan son of Kareah and all the army officers(P) who were with him and all the people from the least to the greatest.(Q) He said to them, “This is what the Lord, the God of Israel, to whom you sent me to present your petition,(R) says:(S) 10 ‘If you stay in this land,(T) I will build(U) you up and not tear you down; I will plant(V) you and not uproot you,(W) for I have relented concerning the disaster I have inflicted on you.(X) 11 Do not be afraid of the king of Babylon,(Y) whom you now fear.(Z) Do not be afraid of him, declares the Lord, for I am with you and will save(AA) you and deliver you from his hands.(AB) 12 I will show you compassion(AC) so that he will have compassion on you and restore you to your land.’(AD)

13 “However, if you say, ‘We will not stay in this land,’ and so disobey(AE) the Lord your God, 14 and if you say, ‘No, we will go and live in Egypt,(AF) where we will not see war or hear the trumpet(AG) or be hungry for bread,’(AH) 15 then hear the word of the Lord,(AI) you remnant of Judah. This is what the Lord Almighty, the God of Israel, says: ‘If you are determined to go to Egypt and you do go to settle there, 16 then the sword(AJ) you fear(AK) will overtake you there, and the famine(AL) you dread will follow you into Egypt, and there you will die.(AM) 17 Indeed, all who are determined to go to Egypt to settle there will die by the sword, famine and plague;(AN) not one of them will survive or escape the disaster I will bring on them.’ 18 This is what the Lord Almighty, the God of Israel, says: ‘As my anger and wrath(AO) have been poured out on those who lived in Jerusalem,(AP) so will my wrath be poured out on you when you go to Egypt. You will be a curse[b](AQ) and an object of horror,(AR) a curse[c] and an object of reproach;(AS) you will never see this place again.’(AT)

19 “Remnant(AU) of Judah, the Lord has told you, ‘Do not go to Egypt.’(AV) Be sure of this: I warn you today 20 that you made a fatal mistake when you sent me to the Lord your God and said, ‘Pray to the Lord our God for us; tell us everything he says and we will do it.’(AW) 21 I have told you today, but you still have not obeyed the Lord your God in all he sent me to tell you.(AX) 22 So now, be sure of this: You will die by the sword, famine(AY) and plague(AZ) in the place where you want to go to settle.”(BA)

Footnotes

  1. Jeremiah 42:1 Hebrew; Septuagint (see also 43:2) Azariah
  2. Jeremiah 42:18 That is, your name will be used in cursing (see 29:22); or, others will see that you are cursed.
  3. Jeremiah 42:18 That is, your name will be used in cursing (see 29:22); or, others will see that you are cursed.