Add parallel Print Page Options

Uthenga Wonena za Mowabu

48 Ponena za Mowabu:

Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti,

“Tsoka kwa mzinda wa Nebo, chifukwa wawonongedwa.
    Mzinda wa Kiriyataimu wachititsidwa manyazi ndipo wagonjetsedwa;
    linga lichititsidwa manyazi ndipo lagumulidwa.
Palibenso amene akutamanda Mowabu;
    ku Hesiboni anthu anamupanganira zoyipa:
    ‘Bwerani, tiyeni timuwonongeretu kuti asakhalenso mtundu wa anthu.’
Inunso anthu a ku Madimena, adzakukhalitsani chete;
    ankhondo adzakupirikitsani.
Tamvani mfuwu wa anthu a ku Horonaimu.
    Iwo akulira kuti, ‘Kusakazika ndi kuwonongeka kwakukulu.’
Mowabu wawonongeka;
    ana ake angʼonoangʼono akulira kwambiri.
Anthu akukwera chikweza cha ku Luhiti,
    akulira kwambiri pamene akupita.
Kulira chifukwa cha chiwonongeko kukumveka
    pa njira yotsikira ku Horonaimu.
Thawani! Dzipulumutseni;
    khalani ngati mbidzi ya mʼchipululu.
Popeza inu munkadalira ntchito zanu ndi chuma chanu,
    nanunso mudzatengedwa ukapolo,
ndipo Kemosi adzapita ku ukapolo,
    pamodzi ndi ansembe ake ndi akuluakulu ake.
Wowononga adzabwera ndi kusakaza mzinda uliwonse,
    ndipo palibe mzinda umene udzapulumuke.
Chigwa chidzasanduka bwinja
    ndipo malo athyathyathya a pamwamba pa phiri adzawonongedwa
    monga Yehova wayankhulira.
Mtsineni khutu Mowabu
    chifukwa adzasakazika;
mizinda yake idzasanduka mabwinja,
    wopanda munthu wokhalamo.

10 “Wotembereredwa munthu amene amagwira ntchito ya Yehova monyinyirika!
    Wotembereredwa munthu amene amaletsa lupanga lake kupha anthu!

11 “Mowabu wakhala pa mtendere kuyambira ubwana wake,
    ngati vinyo wokhazikika pa masese ake,
osapungulidwa kuchoka mu mtsuko wina kuthira mu mtsuko wina;
    iye sanatengedwepo ukapolo.
Nʼchifukwa chake kukoma kwake nʼkomwe kuja
    ndipo fungo lake silinasinthe.
12 Nʼchifukwa chake masiku akubwera,”
    akutero Yehova,
“pamene ndidzatuma anthu amene amakhuthula vinyo mʼmitsuko
    ndipo adzamukhutula;
adzakhuthula vinyo yense mitsuko yake
    pambuyo pake nʼkuphwanya mitsukoyo.
13 Pamenepo Mowabu adzachita manyazi ndi Kemosi,
    monga momwe Aisraeli anachitira manyazi
    ndi Beteli amene ankamukhutulira.

14 “Kodi munganene bwanji kuti, ‘Ife ndife asilikali.
    Ife ndife ngwazi, anthu amphamvu pa nkhondo?’
15 Owononga Mowabu ndi mizinda yake abwera ndipo ankhondo adzalowa mʼmidzi yake;
    anyamata ake okongola apita kukaphedwa,”
    ikutero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
16 Kugwa kwa Mowabu kuli pafupi;
    masautso ake akubwera posachedwa.
17 Mulireni kwambiri, inu nonse amene mwamuzungulira,
    inu nonse amene mumadziwa za kutchuka kwake;
nenani kuti, “Taonani momwe yathyokera ndodo yamphamvu yaufumu ija,
    taonani momwe ndodo yaulemu yathyokera!”

18 “Tsikani pa ulemerero wanu
    ndipo khalani pansi powuma,
    inu anthu okhala ku Diboni,
pakuti wowononga Mowabu
    wabwera kudzamenyana nanu,
    wasakaza mizinda yanu yotetezedwa.
19 Inu amene mumakhala ku Aroeri,
    imani mʼmbali mwa msewu ndi kumaonerera.
Funsani mwamuna amene akuthawa ndiponso mkazi amene wapulumuka,
    afunseni kuti, ‘Kodi chachitika nʼchiyani?’ ”
20 Iwo adzayankha kuti, “Mowabu wachititsidwa manyazi, pakuti wasakazika.
    Lirani mwachisoni ndipo fuwulani!
Lengezani ku mtsinje wa Arinoni
    kuti Mowabu wawonongedwa.
21 Chiweruzo chabwera ku mizinda ya ku mapiri,
    ndiyo Holoni, Yaza, Mefaati,
22     Diboni, Nebo, Beti-Dibilataimu,
23     Kiriyataimu, Beti-Gamuli, Beti-Meoni,
24     Keriyoti ndi Bozira
    ndi mizinda yonse ya Mowabu, yakutali ndi yapafupi yomwe.
25 Mphamvu za Mowabu zawonongeka;
    mkono wake wathyoka,”
            akutero Yehova.

26 “Muledzeretseni Mowabu,
    chifukwa anadzikuza powukira Yehova.
Mulekeni Mowabu avivinizike mʼmasanzi ake;
    mulekeni akhale chinthu chomachiseka.
27 Kodi suja Israeli anali kwa iwe ngati chinthu chomachiseka?
    Kodi Israeli anapezeka pakati pa akuba
kuti nthawi zonse poyankhula za iye,
    iwe uzimupukusira mutu momunyoza?
28 Inu amene mumakhala ku Mowabu,
    siyani mizinda yanu ndi kukakhala pakati pa matanthwe.
Khalani ngati nkhunda imene imamanga chisa chake
    pa khomo la phanga.

29 “Tamva za kunyada kwa Mowabu,
    kunyada kwake nʼkwakukulu.
Ndi wodzitama, wonyada ndi wodzitukumula.
    Ali ndi mtima wodzikweza.
30 Ine ndikuzidziwa ntchito zake,
            akutero Yehova.
    Ntchitozo ndi nʼzosapindulitsa kanthu.
31 Nʼchifukwa chake ndidzamulira Mowabu,
    ine ndikulira chifukwa cha anthu onse a ku Mowabu,
    ndikubuwula chifukwa cha anthu a ku Kiri Heresi.
32 Ndikukhetsa misozi chifukwa cha inu, kupambana momwe ndinalirira Yazeri.
    Inu anthu a ku Sibina muli ngati mipesa
imene nthambi zake zatambalala mpaka ku Nyanja;
    zafika mpaka ku nyanja ya Yazeri.
Wowononga wasakaza
    zipatso zake zachilimwe ndi mpesa.
33 Chimwemwe ndi chisangalalo zatha
    ku minda ya zipatso ya ku Mowabu.
Ndaletsa kuchucha kwa vinyo mopsinyira mphesa;
    palibe amene akufuwula mokondwa akamapsinya mphesa.
Ngakhale kufuwula kulipo,
    koma sikufuwula kwa chimwemwe.

34 “A ku Hesiboni ndi Eleali akulira
    ndipo mfuwu wawo ukumveka mpaka ku Yahazi,
kuchokera ku Zowari mpaka ku Horonaimu ndi ku Egilati Selisiya.
    Ngakhale madzi a ku Nimurimu aphwa.
35 Ndidzawaletsa anthu a ku Mowabu
    kupereka nsembe mʼmalo awo opembedzera
    ndi kufukiza lubani kwa milungu yawo,”
            akutero Yehova.
36 “Nʼchifukwa chake mtima wanga ukulirira Mowabu ngati chitoliro.
    Mtima wanga ukulirira anthu a ku Kiri Heresi ngati chitoliro
    chifukwa chuma chimene anachipata chatha.
37 Aliyense wameta mutu wake
    ndi ndevu zake;
manja a munthu aliyense ndi ochekacheka,
    ndipo munthu aliyense wavala chiguduli mʼchiwuno mwake.
38 Pa madenga onse a ku Mowabu
    ndiponso mʼmisewu yake
anthu akungolira,
    pakuti ndaphwanya Mowabu
    ngati mtsuko wopanda ntchito,”
            akutero Yehova.
39 “Taonani mmene waphwanyikira! Tamvani momwe akulirira!
    Taonani momwe Mowabu wachititsidwira manyazi.
Mowabu wasanduka chinthu chonyozeka,
    chinthu chochititsa mantha kwa onse amene amuzungulira.”

40 Yehova akuti,

“Mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkugwera pa Mowabu ngati chiwombankhanga
    chimene chatambalitsa mapiko ake.
41 Mizinda idzagwidwa
    ndipo malinga adzalandidwa.
Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Mowabu
    idzakhala ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.
42 Mowabu sudzakhala mtundu wa anthu
    chifukwa unadzikuza powukira Yehova.
43 Zoopsa, dzenje ndi msampha zikudikira
    inu anthu a ku Mowabu,”
            akutero Yehova.
44 “Aliyense wothawa zoopsa
    adzagwera mʼdzenje,
aliyense wotuluka mʼdzenje
    adzakodwa mu msampha.
Ndigwetsa zimenezi pa Mowabu
    pa nthawi ya chilango chake,”
            akutero Yehova.

45 “Anthu othawa nkhondo ayima pa mthunzi wa Hesiboni
    chifukwa chotopa.
Koma moto wayaka kuchokera ku Hesiboni,
    malawi a moto abuka kuchokera ku nyumba ya mfumu Sihoni.
Motowo ukuwononga mapiri a ku Mowabu,
    dziko la anthu onyada.
46 Tsoka kwa iwe Mowabu!
    Anthu opembedza Kemosi awonongeka.
Ana ako aamuna ndi aakazi
    atengedwa ukapolo.

47 “Komabe masiku akutsogolo
    ndidzabwezeranso Mowabu chuma chake,”
            akutero Yehova.

Chiweruzo cha Mowabu chathera pamenepa.

A Message About Moab(A)

48 Concerning Moab:(B)

This is what the Lord Almighty, the God of Israel, says:

“Woe to Nebo,(C) for it will be ruined.
    Kiriathaim(D) will be disgraced and captured;
    the stronghold[a] will be disgraced and shattered.
Moab will be praised(E) no more;
    in Heshbon[b](F) people will plot her downfall:
    ‘Come, let us put an end to that nation.’(G)
You, the people of Madmen,[c] will also be silenced;
    the sword will pursue you.
Cries of anguish arise from Horonaim,(H)
    cries of great havoc and destruction.
Moab will be broken;
    her little ones will cry out.[d]
They go up the hill to Luhith,(I)
    weeping bitterly as they go;
on the road down to Horonaim(J)
    anguished cries over the destruction are heard.
Flee!(K) Run for your lives;
    become like a bush[e] in the desert.(L)
Since you trust in your deeds and riches,(M)
    you too will be taken captive,
and Chemosh(N) will go into exile,(O)
    together with his priests and officials.(P)
The destroyer(Q) will come against every town,
    and not a town will escape.
The valley will be ruined
    and the plateau(R) destroyed,
    because the Lord has spoken.
Put salt(S) on Moab,
    for she will be laid waste[f];(T)
her towns will become desolate,
    with no one to live in them.

10 “A curse on anyone who is lax in doing the Lord’s work!
    A curse on anyone who keeps their sword(U) from bloodshed!(V)

11 “Moab has been at rest(W) from youth,
    like wine left on its dregs,(X)
not poured from one jar to another—
    she has not gone into exile.
So she tastes as she did,
    and her aroma is unchanged.
12 But days are coming,”
    declares the Lord,
“when I will send men who pour from pitchers,
    and they will pour her out;
they will empty her pitchers
    and smash her jars.
13 Then Moab will be ashamed(Y) of Chemosh,(Z)
    as Israel was ashamed
    when they trusted in Bethel.(AA)

14 “How can you say, ‘We are warriors,(AB)
    men valiant in battle’?
15 Moab will be destroyed and her towns invaded;
    her finest young men(AC) will go down in the slaughter,(AD)
    declares the King,(AE) whose name is the Lord Almighty.(AF)
16 “The fall of Moab is at hand;(AG)
    her calamity will come quickly.
17 Mourn for her, all who live around her,
    all who know her fame;(AH)
say, ‘How broken is the mighty scepter,(AI)
    how broken the glorious staff!’

18 “Come down from your glory
    and sit on the parched ground,(AJ)
    you inhabitants of Daughter Dibon,(AK)
for the one who destroys Moab
    will come up against you
    and ruin your fortified cities.(AL)
19 Stand by the road and watch,
    you who live in Aroer.(AM)
Ask the man fleeing and the woman escaping,
    ask them, ‘What has happened?’
20 Moab is disgraced, for she is shattered.
    Wail(AN) and cry out!
Announce by the Arnon(AO)
    that Moab is destroyed.
21 Judgment has come to the plateau(AP)
    to Holon,(AQ) Jahzah(AR) and Mephaath,(AS)
22     to Dibon,(AT) Nebo(AU) and Beth Diblathaim,
23     to Kiriathaim,(AV) Beth Gamul and Beth Meon,(AW)
24     to Kerioth(AX) and Bozrah(AY)
    to all the towns(AZ) of Moab, far and near.
25 Moab’s horn[g](BA) is cut off;
    her arm(BB) is broken,”
declares the Lord.

26 “Make her drunk,(BC)
    for she has defied(BD) the Lord.
Let Moab wallow in her vomit;(BE)
    let her be an object of ridicule.(BF)
27 Was not Israel the object of your ridicule?(BG)
    Was she caught among thieves,(BH)
that you shake your head(BI) in scorn(BJ)
    whenever you speak of her?
28 Abandon your towns and dwell among the rocks,
    you who live in Moab.
Be like a dove(BK) that makes its nest
    at the mouth of a cave.(BL)

29 “We have heard of Moab’s pride(BM)
    how great is her arrogance!—
of her insolence, her pride, her conceit
    and the haughtiness(BN) of her heart.
30 I know her insolence but it is futile,”
declares the Lord,
    “and her boasts(BO) accomplish nothing.
31 Therefore I wail(BP) over Moab,
    for all Moab I cry out,
    I moan for the people of Kir Hareseth.(BQ)
32 I weep for you, as Jazer(BR) weeps,
    you vines of Sibmah.(BS)
Your branches spread as far as the sea[h];
    they reached as far as[i] Jazer.
The destroyer has fallen
    on your ripened fruit and grapes.
33 Joy and gladness are gone
    from the orchards and fields of Moab.
I have stopped the flow of wine(BT) from the presses;
    no one treads them with shouts of joy.(BU)
Although there are shouts,
    they are not shouts of joy.

34 “The sound of their cry rises
    from Heshbon(BV) to Elealeh(BW) and Jahaz,(BX)
from Zoar(BY) as far as Horonaim(BZ) and Eglath Shelishiyah,
    for even the waters of Nimrim are dried up.(CA)
35 In Moab I will put an end
    to those who make offerings on the high places(CB)
    and burn incense(CC) to their gods,”
declares the Lord.
36 “So my heart laments(CD) for Moab like the music of a pipe;
    it laments like a pipe for the people of Kir Hareseth.(CE)
    The wealth they acquired(CF) is gone.
37 Every head is shaved(CG)
    and every beard(CH) cut off;
every hand is slashed
    and every waist is covered with sackcloth.(CI)
38 On all the roofs in Moab
    and in the public squares(CJ)
there is nothing but mourning,
    for I have broken Moab
    like a jar(CK) that no one wants,”
declares the Lord.
39 “How shattered(CL) she is! How they wail!
    How Moab turns her back in shame!
Moab has become an object of ridicule,(CM)
    an object of horror to all those around her.”

40 This is what the Lord says:

“Look! An eagle is swooping(CN) down,
    spreading its wings(CO) over Moab.
41 Kerioth[j](CP) will be captured
    and the strongholds taken.
In that day the hearts of Moab’s warriors(CQ)
    will be like the heart of a woman in labor.(CR)
42 Moab will be destroyed(CS) as a nation(CT)
    because she defied(CU) the Lord.
43 Terror(CV) and pit and snare(CW) await you,
    you people of Moab,”
declares the Lord.
44 “Whoever flees(CX) from the terror
    will fall into a pit,
whoever climbs out of the pit
    will be caught in a snare;
for I will bring on Moab
    the year(CY) of her punishment,”
declares the Lord.

45 “In the shadow of Heshbon
    the fugitives stand helpless,
for a fire has gone out from Heshbon,
    a blaze from the midst of Sihon;(CZ)
it burns the foreheads of Moab,
    the skulls(DA) of the noisy boasters.
46 Woe to you, Moab!(DB)
    The people of Chemosh are destroyed;
your sons are taken into exile
    and your daughters into captivity.

47 “Yet I will restore(DC) the fortunes of Moab
    in days to come,”
declares the Lord.

Here ends the judgment on Moab.

Footnotes

  1. Jeremiah 48:1 Or captured; / Misgab
  2. Jeremiah 48:2 The Hebrew for Heshbon sounds like the Hebrew for plot.
  3. Jeremiah 48:2 The name of the Moabite town Madmen sounds like the Hebrew for be silenced.
  4. Jeremiah 48:4 Hebrew; Septuagint / proclaim it to Zoar
  5. Jeremiah 48:6 Or like Aroer
  6. Jeremiah 48:9 Or Give wings to Moab, / for she will fly away
  7. Jeremiah 48:25 Horn here symbolizes strength.
  8. Jeremiah 48:32 Probably the Dead Sea
  9. Jeremiah 48:32 Two Hebrew manuscripts and Septuagint; most Hebrew manuscripts as far as the Sea of
  10. Jeremiah 48:41 Or The cities