Add parallel Print Page Options

Kuzingidwa kwa Yerusalemu

“Thawani, inu anthu a ku Benjamini!
    Tulukani mu Yerusalemu!
Lizani lipenga ku Tekowa!
    Kwezani mbendera ku Beti-Hakeremu!
Pakuti tsoka lalikulu likubwera kuchokera kumpoto,
    ndipo chiwonongekocho nʼchachikulu.
Kodi mzinda wa Ziyoni suli ngati msipu wokongola kwambiri,
    kumene abusa amafikako ndi ziweto zawo?
Abusa ndi nkhosa zawo adzabwera kudzalimbana nawo;
    adzamanga matenti awo mowuzinga,
    ndipo aliyense adzakhazika anthu ake pamalo pake.”

Adzanena kuti, “Konzekani kuwuthira nkhondo mzindawo!
    Nyamukani, kuti tiwuthire nkhondo mzindawu masana ano.
Koma tili ndi tsoka, dzuwa lapendeka,
    ndipo zithunzithunzi za kumadzulo zikunka zitalika.
Tsono nyamukani kuti tiwuthire nkhondo mzindawu usiku uno
    ndi kuwononga malinga ake!”

Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Dulani mitengo
    ndipo mumange mitumbira yankhondo kulimbana ndi Yerusalemu.
Mzinda umenewu uyenera kulangidwa;
    wadzaza ndi kuponderezana.
Monga momwe chitsime chimatulutsira madzi
    ndi mmenenso Yerusalemu amatulutsira zoyipa zake.
Chiwawa ndi chiwonongeko ndi zomwe zimamveka mu mzindamo;
    nthenda yake ndi mabala ake ndimaziona nthawi zonse.
Iwe Yerusalemu, tengapo phunziro,
    kuopa kuti chikondi changa pa iwe chingakuchokere
ndi kusandutsa dziko lako kukhala bwinja
    mopanda munthu wokhalamo.”

Yehova Wamphamvuzonse anandiwuza kuti,

“Adani adzawakunkha ndithu anthu otsala a Israeli,
    monga momwe amachitira populula mphesa.
Tsono iwe yesetsa kupulumutsa amene ungathe
    monga mmene amachitira munthu wokolola mphesa.”

10 Kodi ndiyankhule ndi yani ndi kumuchenjeza?
    Ndinene mawu ochenjeza kwa yani kuti amve?
Makutu awo ndi otsekeka
    kotero kuti sangathe kumva.
Mawu a Yehova ndi onyansa kwa iwo;
    sasangalatsidwa nawo.
11 Koma ine ndadzazidwa ndi mkwiyo wa Yehova,
    ndipo ndatopa ndi kusunga mkwiyo wa Yehova.

Yehova anandiwuza kuti, “Tsono ndidzawutulutsira mkwiyo umenewu pa ana oyenda mʼmisewu
    ndi pa achinyamata amene asonkhana pamodzi;
pakutinso mwamuna ndi mkazi wake adzatengedwa,
    pamodzi ndi okalamba amene ali ndi zaka zochuluka.
12 Nyumba zawo adzazipereka kwa ena,
    pamodzi ndi minda yawo ndi akazi awo.
Ndidzatambasula dzanja langa kukantha
    anthu okhala mʼdzikomo,”
            akutero Yehova.
13 “Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu,
    onse ali ndi dyera lofuna kupeza phindu mwa kuba;
aneneri pamodzi ndi ansembe omwe,
    onse amachita zachinyengo.
14 Amapoletsa zilonda za anthu anga
    pamwamba pokha.
Iwo amanena kuti, ‘Mtendere, mtendere,’
    pamene palibe mtendere.
15 Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazo?
    Ayi, sachita manyazi ndi pangʼono pomwe;
    sadziwa ndi kugwetsa nkhope komwe.
Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale;
    adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalange,”
            akutero Yehova.

16 Yehova akuti,

“Imani pa mphambano ndipo mupenye;
    kumeneko ndiye kuli njira zakale,
funsani kumene kuli njira yabwino. Yendani mʼmenemo,
    ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu.
    Koma inu munati, ‘Ife sitidzayenda njira imeneyo.’
17 Ine ndinakupatsani alonda oti akuyangʼanireni
    ndipo ndinati, ‘Imvani kulira kwa lipenga!’
    koma inu munati, ‘Sitidzamvera.’
18 Nʼchifukwa chake imvani, inu anthu a mitundu ina;
    yangʼanitsitsani, inu amene mwasonkhana pano,
    chimene chidzawachitikire anthuwo.
19 Imvani, inu anthu okhala pa dziko lapansi,
ndikubweretsa masautso pa anthu awa.
    Zimenezi ndi mphotho ya ntchito zawo.
Iwowa sanamvere mawu anga
    ndipo anakana lamulo langa.
20 Kodi pali phindu lanji ngakhale mubwere ndi lubani kuchokera ku Seba,
    kapena zonunkhira zina kuchokera ku dziko lakutali?
Nsembe zanu zopsereza Ine sindidzalandira;
    nsembe zanu sizindikondweretsa.”

21 Choncho Yehova akuti,

“Ndidzayika zokhumudwitsa pamaso pa anthu awa.
    Abambo ndi ana awo aamuna onse adzapunthwa ndi kugwa;
    anansi awo ndi abwenzi awo adzawonongeka.”

22 Yehova akunena kuti,

“Taonani, gulu lankhondo likubwera
    kuchokera kumpoto;
mtundu wa anthu amphamvu wanyamuka
    kuchokera kumathero a dziko lapansi.
23 Atenga mauta ndi mikondo;
    ndi anthu ankhanza ndi opanda chifundo.
Phokoso lawo lili ngati mkokomo wa nyanja.
    Akwera pa akavalo awo
ndipo akonzekera ngati anthu ankhondo,
    kudzakuthirani nkhondo anthu a ku Ziyoni.”

24 A ku Ziyoni akuti “Ife tamva mbiri yawo,
    ndipo manja anthu alefukiratu.
Nkhawa yatigwira,
    ndipo tikumva ululu ngati mayi pa nthawi yake yochira.
25 Musapite ku minda
    kapena kuyenda mʼmisewu,
pakuti mdani ali ndi lupanga,
    ndipo ponseponse anthu akuchita mantha.
26 Inu anthu anga, valani ziguduli
    ndipo gubudukani pa phulusa;
lirani mwamphamvu
    ngati munthu wolirira mwana wake mmodzi yekha,
pakuti mwadzidzidzi wowonongayo
    adzabwera kudzatipha.

27 “Iwe Yeremiya, ndakuyika kuti ukhale choyesera zitsulo.
    Uwayese anthu anga
monga ungayesere chitsulo
    kuti uwone makhalidwe awo.
28 Onsewo ali ndi khalidwe lokanika ndi lowukira
    ndipo akunka nanena zamiseche.
Iwo ndi olimba ngati mkuwa ndi chitsulo.
    Onse amangochita zoyipa zokhazokha.
29 Moto mu mvukuto ukuyaka kwambiri;
    mtovu watha kusungunuka ndi moto.
Koma ntchito yosungunulayo sikupindula
    chifukwa zoyipa sizikuchokapo.
30 Iwo ali ngati siliva wotayidwa,
    chifukwa Yehova wawakana.”

Jerusalem Under Siege

“Flee for safety, people of Benjamin!
    Flee from Jerusalem!
Sound the trumpet(A) in Tekoa!(B)
    Raise the signal over Beth Hakkerem!(C)
For disaster looms out of the north,(D)
    even terrible destruction.
I will destroy Daughter Zion,(E)
    so beautiful and delicate.(F)
Shepherds(G) with their flocks will come against her;
    they will pitch their tents around(H) her,
    each tending his own portion.”

“Prepare for battle against her!
    Arise, let us attack at noon!(I)
But, alas, the daylight is fading,
    and the shadows of evening grow long.
So arise, let us attack at night
    and destroy her fortresses!”

This is what the Lord Almighty says:

“Cut down the trees(J)
    and build siege ramps(K) against Jerusalem.
This city must be punished;
    it is filled with oppression.(L)
As a well pours out its water,
    so she pours out her wickedness.
Violence(M) and destruction(N) resound in her;
    her sickness and wounds are ever before me.
Take warning, Jerusalem,
    or I will turn away(O) from you
and make your land desolate
    so no one can live in it.”

This is what the Lord Almighty says:

“Let them glean the remnant(P) of Israel
    as thoroughly as a vine;
pass your hand over the branches again,
    like one gathering grapes.”

10 To whom can I speak and give warning?
    Who will listen(Q) to me?
Their ears are closed[a](R)
    so they cannot hear.(S)
The word(T) of the Lord is offensive to them;
    they find no pleasure in it.
11 But I am full of the wrath(U) of the Lord,
    and I cannot hold it in.(V)

“Pour it out on the children in the street
    and on the young men(W) gathered together;
both husband and wife will be caught in it,
    and the old, those weighed down with years.(X)
12 Their houses will be turned over to others,(Y)
    together with their fields and their wives,(Z)
when I stretch out my hand(AA)
    against those who live in the land,”
declares the Lord.
13 “From the least to the greatest,
    all(AB) are greedy for gain;(AC)
prophets and priests alike,
    all practice deceit.(AD)
14 They dress the wound of my people
    as though it were not serious.
‘Peace, peace,’ they say,
    when there is no peace.(AE)
15 Are they ashamed of their detestable conduct?
    No, they have no shame at all;
    they do not even know how to blush.(AF)
So they will fall among the fallen;
    they will be brought down when I punish(AG) them,”
says the Lord.

16 This is what the Lord says:

“Stand at the crossroads and look;
    ask for the ancient paths,(AH)
ask where the good way(AI) is, and walk in it,
    and you will find rest(AJ) for your souls.
    But you said, ‘We will not walk in it.’
17 I appointed watchmen(AK) over you and said,
    ‘Listen to the sound of the trumpet!’(AL)
    But you said, ‘We will not listen.’(AM)
18 Therefore hear, you nations;
    you who are witnesses,
    observe what will happen to them.
19 Hear, you earth:(AN)
    I am bringing disaster(AO) on this people,
    the fruit of their schemes,(AP)
because they have not listened to my words(AQ)
    and have rejected my law.(AR)
20 What do I care about incense from Sheba(AS)
    or sweet calamus(AT) from a distant land?
Your burnt offerings are not acceptable;(AU)
    your sacrifices(AV) do not please me.”(AW)

21 Therefore this is what the Lord says:

“I will put obstacles before this people.
    Parents and children alike will stumble(AX) over them;
    neighbors and friends will perish.”

22 This is what the Lord says:

“Look, an army is coming
    from the land of the north;(AY)
a great nation is being stirred up
    from the ends of the earth.(AZ)
23 They are armed with bow and spear;
    they are cruel and show no mercy.(BA)
They sound like the roaring sea(BB)
    as they ride on their horses;(BC)
they come like men in battle formation
    to attack you, Daughter Zion.(BD)

24 We have heard reports about them,
    and our hands hang limp.(BE)
Anguish(BF) has gripped us,
    pain like that of a woman in labor.(BG)
25 Do not go out to the fields
    or walk on the roads,
for the enemy has a sword,
    and there is terror on every side.(BH)
26 Put on sackcloth,(BI) my people,
    and roll in ashes;(BJ)
mourn with bitter wailing(BK)
    as for an only son,(BL)
for suddenly the destroyer(BM)
    will come upon us.

27 “I have made you a tester(BN) of metals
    and my people the ore,
that you may observe
    and test their ways.
28 They are all hardened rebels,(BO)
    going about to slander.(BP)
They are bronze and iron;(BQ)
    they all act corruptly.
29 The bellows blow fiercely
    to burn away the lead with fire,
but the refining(BR) goes on in vain;
    the wicked are not purged out.
30 They are called rejected silver,(BS)
    because the Lord has rejected them.”(BT)

Footnotes

  1. Jeremiah 6:10 Hebrew uncircumcised