Add parallel Print Page Options

Chipembedzo Chabodza Nʼchopanda Phindu

Mawu amene Yehova anayankhula kwa Yeremiya ndi awa, “Ima pa chipata cha Nyumba ya Yehova ndipo kumeneko ukalalikire uthenga uwu:

“ ‘Imvani mawu a Yehova, inu nonse anthu a ku Yuda amene mumalowa pa chipata ichi kudzapembedza Yehova. Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Konzani makhalidwe anu ndi zochita zanu, ndipo ndidzakulolani kukhala pa malo ano. Musamakhulupirire mawu anu achinyengo onena kuti, ‘Ino ndi Nyumba ya Yehova, Nyumba ya Yehova, Nyumba ya Yehova!’ Ngati mutasinthadi makhalidwe anu ndi zochita zanu, ndi kumachitirana zolungama, ngati mutaleka kuzunza mlendo, ana amasiye kapena akazi amasiye ndi kuleka kupha anthu osalakwa pa malo ano, ndipo ngati muleka kutsatira milungu ina, kuti ingakuwonongeni, Ine ndidzakulolani kukhala pa malo ano, mʼdziko limene ndinapatsa makolo anu mpaka muyaya. Koma onani, inu mukudalira mawu abodza amene alibe phindu.

“Kodi inu muziba ndi kupha, kuchita chigololo ndi kulumbira monama, kufukiza lubani kwa Baala ndi kutsatira milungu ina imene simunayidziwe, 10 ndipo kenaka nʼkubwera kudzayima pamaso panga mʼNyumba ino, Nyumba imene imadziwika ndi Dzina langa, inu nʼkumati, ‘Tapulumuka.’ Mwapulumuka kuti muzichitabe zonyansazi? 11 Kodi Nyumba ino imene imadziwika ndi Dzina langa, yasanduka phanga la anthu olanda zinthu anzawo mwachifwamba inu mukuona? Komatu ndakhala ndi kuziona zonsezi! akutero Yehova.”

12 “ ‘Pitani tsopano ku malo anga ku Silo, malo amene poyamba ankadziwika ndi Dzina langa, ndipo mukaone zimene ndinachita kumeneko chifukwa cha kuyipa kwa anthu anga Aisraeli. 13 Tsono popeza munkachita zonsezi, ngakhale Ine kukuyankhulani koma inu osamvera, kukuyitanani koma inu osayankha, 14 choncho ndidzachita pa Nyumba imene imadziwika ndi Dzina langayi, Nyumba ya Yehova imene mumayidalira, malo amene ndinapereka kwa inu ndi makolo anu, zomwe ndinachita ku Silo. 15 Ndidzakuthamangitsani pamaso panga, ngati momwe ndinachitira abale anu onse, anthu a Efereimu.’ ”

16 “Choncho iwe Yeremiya usawapempherere anthu awa ngakhale kuwapepesera kapenanso kuwapembedzera; usandidandaulire, chifukwa Ine sindidzakumvera. 17 Kodi sukuona zimene akuchita mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya ku Yerusalemu? 18 Ana akutorera nkhuni, abambo akusonkha moto, ndipo amayi akukanda ufa kuti aphike makeke oti akapereke nsembe kwa mfumukazi yazakumwamba. Iwo amathira nsembe ya zakumwa kwa milungu ina kuti andipsetse mtima. 19 Koma kodi akuvutitsa Ine? Kodi sakungodzivuta okha, ndi kudzichititsa manyazi? akutero Yehova.”

20 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Ndidzatsanulira mkwiyo wanga pa Nyumba yangayi, anthu, nyama, mitengo ndi zipatso zomwe. Mkwiyowo udzakhala ngati moto wosazimitsika.

21 “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Wonjezerani nsembe zanu zopsereza pa nsembe zanu zinazo ndipo mudye nyama yakeyo! 22 Pakuti pamene ndinatulutsa makolo anu ku Igupto ndi kuyankhula nawo, sindinawalamulire kuti azipereka nsembe zopsereza kapena nsembe zinazo, 23 koma ndinawalamula kuti: Mverani Ine, ndipo ndidzakhala Mulungu wanu ndipo inu mudzakhala anthu anga. Muzitsata zonse zimene ndakulamulirani, ndipo zinthu zidzakuyenderani bwino. 24 Koma anthuwo sanamvere kapena kulabadira; mʼmalo mwake anapitirira kusamvera ndi mitima yawo yoyipa. Iwo anabwerera mʼmbuyo mʼmalo mopita patsogolo. 25 Kuyambira tsiku limene makolo awo anachoka ku Igupto mpaka lero lino, ndakhala ndikuwatumizira atumiki anga, aneneri. 26 Koma anthuwo sanandimvere kapena kusamalira. Anawumitsa mitima yawo ndi kuchita zoyipa kuposa makolo awo.

27 “Ngakhale iwe uwawuze zonsezi koma sadzakumvera. Ngakhale uwayitane koma sadzakuyankha. 28 Nʼchifukwa chake udzawawuze kuti, ‘Uwu ndi mtundu wa anthu umene sunamvere Yehova Mulungu wake, wosalola kulangizidwa. Choonadi chatha; chazimirira pa milomo yawo.’

29 “Tsono meta tsitsi lako ndi kulitaya. Ulire kwambiri pa zitunda zopanda zomera, pakuti Yehova waukana ndi kuwusiya mʼbado umene wamukwiyitsawu.”

Chigwa cha Imfa

30 “Anthu a ku Yuda achita zoyipa pamaso panga, akutero Yehova. Ayimika mafano awo onyansa mʼnyumba imene imadziwika ndi Dzina langa ndipo ayipitsa. 31 Amanga nsanja yopembedzera Tofeti mʼChigwa cha Hinomu kuti apserezereko ana awo aamuna ndi aakazi. Zimenezi Ine sindinawalamulire ngakhale kuziganizira nʼkomwe. 32 Nʼchifukwa chake masiku akubwera, akutero Yehova, pamene anthu sadzawatchulanso malowo Tofeti kapena Chigwa cha Hinomu, koma adzawatchula Chigwa cha Imfa, chifukwa adzakwirira anthu akufa ku Tofeti mpaka osapezekanso malo owayika. 33 Ndipo mitembo ya anthu amenewa idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo zakuthengo, ndipo palibe wina amene adzazipirikitse. 34 Ndidzathetsa nyimbo zonse zachisangalalo ndi zachikondwerero mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya ku Yerusalemu. Sikudzamvekanso mawu a chikondwerero a mkwatibwi ndi mkwati pakuti dzikolo lidzasanduka chipululu.”

False Religion Worthless

This is the word that came to Jeremiah from the Lord: “Stand(A) at the gate of the Lord’s house and there proclaim this message:

“‘Hear the word of the Lord, all you people of Judah who come through these gates to worship the Lord. This is what the Lord Almighty, the God of Israel, says: Reform your ways(B) and your actions, and I will let you live(C) in this place. Do not trust(D) in deceptive(E) words and say, “This is the temple of the Lord, the temple of the Lord, the temple of the Lord!” If you really change(F) your ways and your actions and deal with each other justly,(G) if you do not oppress(H) the foreigner, the fatherless or the widow and do not shed innocent blood(I) in this place, and if you do not follow other gods(J) to your own harm, then I will let you live in this place, in the land(K) I gave your ancestors(L) for ever and ever. But look, you are trusting(M) in deceptive(N) words that are worthless.

“‘Will you steal(O) and murder,(P) commit adultery(Q) and perjury,[a](R) burn incense to Baal(S) and follow other gods(T) you have not known, 10 and then come and stand(U) before me in this house,(V) which bears my Name, and say, “We are safe”—safe to do all these detestable things?(W) 11 Has this house,(X) which bears my Name, become a den of robbers(Y) to you? But I have been watching!(Z) declares the Lord.

12 “‘Go now to the place in Shiloh(AA) where I first made a dwelling(AB) for my Name,(AC) and see what I did(AD) to it because of the wickedness of my people Israel. 13 While you were doing all these things, declares the Lord, I spoke(AE) to you again and again,(AF) but you did not listen;(AG) I called(AH) you, but you did not answer.(AI) 14 Therefore, what I did to Shiloh(AJ) I will now do to the house that bears my Name,(AK) the temple(AL) you trust in, the place I gave to you and your ancestors. 15 I will thrust you from my presence,(AM) just as I did all your fellow Israelites, the people of Ephraim.’(AN)

16 “So do not pray for this people nor offer any plea(AO) or petition for them; do not plead with me, for I will not listen(AP) to you. 17 Do you not see what they are doing in the towns of Judah and in the streets of Jerusalem? 18 The children gather wood, the fathers light the fire, and the women knead the dough and make cakes to offer to the Queen of Heaven.(AQ) They pour out drink offerings(AR) to other gods to arouse(AS) my anger. 19 But am I the one they are provoking?(AT) declares the Lord. Are they not rather harming themselves, to their own shame?(AU)

20 “‘Therefore this is what the Sovereign(AV) Lord says: My anger(AW) and my wrath will be poured(AX) out on this place—on man and beast, on the trees of the field and on the crops of your land—and it will burn and not be quenched.(AY)

21 “‘This is what the Lord Almighty, the God of Israel, says: Go ahead, add your burnt offerings to your other sacrifices(AZ) and eat(BA) the meat yourselves! 22 For when I brought your ancestors out of Egypt and spoke to them, I did not just give them commands(BB) about burnt offerings and sacrifices,(BC) 23 but I gave them this command:(BD) Obey(BE) me, and I will be your God and you will be my people.(BF) Walk in obedience to all(BG) I command you, that it may go well(BH) with you. 24 But they did not listen(BI) or pay attention;(BJ) instead, they followed the stubborn inclinations of their evil hearts.(BK) They went backward(BL) and not forward. 25 From the time your ancestors left Egypt until now, day after day, again and again(BM) I sent you my servants(BN) the prophets.(BO) 26 But they did not listen to me or pay attention.(BP) They were stiff-necked(BQ) and did more evil than their ancestors.’(BR)

27 “When you tell(BS) them all this, they will not listen(BT) to you; when you call to them, they will not answer.(BU) 28 Therefore say to them, ‘This is the nation that has not obeyed the Lord its God or responded to correction.(BV) Truth(BW) has perished; it has vanished from their lips.

29 “‘Cut off(BX) your hair and throw it away; take up a lament(BY) on the barren heights, for the Lord has rejected and abandoned(BZ) this generation that is under his wrath.

The Valley of Slaughter

30 “‘The people of Judah have done evil(CA) in my eyes, declares the Lord. They have set up their detestable idols(CB) in the house that bears my Name and have defiled(CC) it. 31 They have built the high places of Topheth(CD) in the Valley of Ben Hinnom(CE) to burn their sons and daughters(CF) in the fire—something I did not command, nor did it enter my mind.(CG) 32 So beware, the days are coming, declares the Lord, when people will no longer call it Topheth or the Valley of Ben Hinnom, but the Valley of Slaughter,(CH) for they will bury(CI) the dead in Topheth until there is no more room. 33 Then the carcasses(CJ) of this people will become food(CK) for the birds and the wild animals, and there will be no one to frighten them away.(CL) 34 I will bring an end to the sounds(CM) of joy and gladness and to the voices of bride and bridegroom(CN) in the towns of Judah and the streets of Jerusalem,(CO) for the land will become desolate.(CP)

Footnotes

  1. Jeremiah 7:9 Or and swear by false gods