Add parallel Print Page Options

Za Ufumu Wamtendere wa Mesiya

11 Padzatuluka mphukira pa tsinde la Yese
    ndipo nthambi idzaphukira kuchokera ku mizu yake.
Mzimu wa Yehova udzakhala pa iye
    Mzimu wanzeru ndi wa kumvetsa zinthu,
    Mzimu wauphungu ndi wamphamvu,
    Mzimu wachidziwitso ndi wakuopa Yehova.
Ndipo kuopa Yehova ndiye chidzakhale chinthu chomukondweretsa.

Iye sadzaweruza potsata zooneka pamaso,
    kapena kugamula mlandu potsata zakumva;
koma amphawi adzawaweruza mwachilungamo,
    adzaweruza mwachilungamo mlandu wa anthu osauka a dziko lapansi.
Iye adzakantha dziko lapansi ndi mawu ake;
    atalamula Iyeyu anthu oyipa adzaphedwa.
Chilungamo chidzakhala ngati lamba wake
    ndipo kukhulupirika kudzakhala ngati chomangira mʼchiwuno mwake.

Mʼmbulu udzakhala pamodzi ndi mwana wankhosa,
    kambuku adzagona pansi pamodzi ndi mwana wambuzi,
mwana wangʼombe ndi mwana wa mkango adzadyera limodzi
    ndipo mwana wamngʼono adzaziweta.
Ngʼombe yayikazi ndi chimbalangondo zidzadya pamodzi,
    ana awo adzagona pamodzi,
    ndipo mkango udzadya udzu ngati ngʼombe.
Mwana wakhanda adzasewera pa dzenje la mamba,
    ndipo mwana wamngʼono adzapisa dzanja lake ku phanga la mphiri osalumidwa.
Sipadzakhala chilichonse chopweteka kapena chowononga
    pa phiri lopatulika la Yehova,
pakuti anthu a dziko lapansi adzadzaza ndi nzeru yotha kudziwa Yehova
    monga momwe nyanja imadzazira ndi madzi.

10 Tsiku limenelo mfumu yatsopano yochokera pa Muzu wa Yese idzakhala ngati chizindikiro kwa anthu a mitundu yonse. Mitundu ya anthu idzasonkhana kwa Iye, ndipo malo awo okhalapo adzakhala aulemerero. 11 Tsiku limenelo Ambuye adzatambasula dzanja lake kachiwiri kuti awombole anthu ake otsalira ku Asiriya, ku Igupto, ku Patirosi, Kusi, ku Elamu, ku Sinana, ku Hamati ndi pa zilumba za nyanja yamchere.

12 Adzakwezera mitundu ya anthu mbendera,
    ndipo adzasonkhanitsa otayika a ku Israeli;
Iye adzasonkhanitsa anthu obalalika a ku Yuda
    kuchokera ku mbali zonse zinayi za dziko lapansi.
13 Nsanje ya Efereimu idzatha,
    ndipo adani a Yuda adzatha;
Efereimu sadzachitira nsanje Yuda,
    ngakhale Yuda sadzamuda Efereimu.
14 Yuda ndi Efereimu adzathira nkhondo pa Afilisti mbali ya kumadzulo;
    ndipo onsewo pamodzi adzalanda zinthu za anthu a kummawa.
Adzalimbana ndi Edomu ndi Mowabu,
    ndipo Aamoni adzawagonjera.
15 Yehova adzaphwetsa
    mwendo wa nyanja ya Igupto;
adzatambasula dzanja lake ndipo adzawombetsa mphepo yotentha
    pa mtsinje wa Yufurate.
Iye adzawugawa mtsinjewo kukhala timitsinje tisanu ndi tiwiri
    kuti anthu athe kuwoloka powuma atavala nsapato.
16 Padzakhala msewu waukulu woti ayendepo anthu ake otsalira
    amene anatsalira ku Asiriya,
monga mmene panali msewu waukulu woyendapo Israeli
    pamene amachokera ku Igupto.

The Branch From Jesse

11 A shoot(A) will come up from the stump(B) of Jesse;(C)
    from his roots a Branch(D) will bear fruit.(E)
The Spirit(F) of the Lord will rest on him—
    the Spirit of wisdom(G) and of understanding,
    the Spirit of counsel and of might,(H)
    the Spirit of the knowledge and fear of the Lord
and he will delight in the fear(I) of the Lord.

He will not judge by what he sees with his eyes,(J)
    or decide by what he hears with his ears;(K)
but with righteousness(L) he will judge the needy,(M)
    with justice(N) he will give decisions for the poor(O) of the earth.
He will strike(P) the earth with the rod of his mouth;(Q)
    with the breath(R) of his lips he will slay the wicked.(S)
Righteousness will be his belt(T)
    and faithfulness(U) the sash around his waist.(V)

The wolf will live with the lamb,(W)
    the leopard will lie down with the goat,
the calf and the lion and the yearling[a] together;
    and a little child will lead them.
The cow will feed with the bear,
    their young will lie down together,
    and the lion will eat straw like the ox.(X)
The infant(Y) will play near the cobra’s den,
    and the young child will put its hand into the viper’s(Z) nest.
They will neither harm nor destroy(AA)
    on all my holy mountain,(AB)
for the earth(AC) will be filled with the knowledge(AD) of the Lord
    as the waters cover the sea.

10 In that day(AE) the Root of Jesse(AF) will stand as a banner(AG) for the peoples; the nations(AH) will rally to him,(AI) and his resting place(AJ) will be glorious.(AK) 11 In that day(AL) the Lord will reach out his hand a second time to reclaim the surviving remnant(AM) of his people from Assyria,(AN) from Lower Egypt, from Upper Egypt,(AO) from Cush,[b](AP) from Elam,(AQ) from Babylonia,[c] from Hamath(AR) and from the islands(AS) of the Mediterranean.(AT)

12 He will raise a banner(AU) for the nations
    and gather(AV) the exiles of Israel;(AW)
he will assemble the scattered people(AX) of Judah
    from the four quarters of the earth.(AY)
13 Ephraim’s jealousy will vanish,
    and Judah’s enemies[d] will be destroyed;
Ephraim will not be jealous of Judah,
    nor Judah hostile toward Ephraim.(AZ)
14 They will swoop down on the slopes of Philistia(BA) to the west;
    together they will plunder the people to the east.(BB)
They will subdue Edom(BC) and Moab,(BD)
    and the Ammonites(BE) will be subject to them.(BF)
15 The Lord will dry up(BG)
    the gulf of the Egyptian sea;
with a scorching wind(BH) he will sweep his hand(BI)
    over the Euphrates River.(BJ)
He will break it up into seven streams
    so that anyone can cross over in sandals.(BK)
16 There will be a highway(BL) for the remnant(BM) of his people
    that is left from Assyria,(BN)
as there was for Israel
    when they came up from Egypt.(BO)

Footnotes

  1. Isaiah 11:6 Hebrew; Septuagint lion will feed
  2. Isaiah 11:11 That is, the upper Nile region
  3. Isaiah 11:11 Hebrew Shinar
  4. Isaiah 11:13 Or hostility