Add parallel Print Page Options

14 Yehova adzachitira chifundo Yakobo;
    adzasankhanso Israeli
    ndi kuwalola kuti akhalenso mʼdziko lawo.
Alendo adzabwera kudzakhala nawo
    ndi kudziphatika okha kukhala ngati a mʼnyumba ya Yakobo.
Anthu a mitundu ina adzaperekeza a Israeli
    ku dziko lawo.
Tsono Aisraeli adzasandutsa anthu a mitundu ina aja
    kukhala antchito awo aamuna ndi aakazi mʼdziko la Yehova.
Ndiye kuti Aisraeli adzasandutsa akapolo anthu amene kale anali ambuye awo.
    Iwo adzasandutsa akapolo anthu amene kale ankawalamulira ndi kuwazunza.

Yehova akadzakupumitsani ku zowawa ndi mavuto, ndiponso kuntchito yakalavulagaga imene ankakugwiritsani, mudzayankhula monyogodola mfumu ya Babuloni kuti,

Wopsinja uja watha!
    Ukali wake uja watha!
Yehova wathyola chikwapu cha anthu oyipa,
    Iye waphwanya ndodo ya olamulira.
Mfumu ya ku Babuloni inkakantha mitundu ya anthu mwaukali
    powamenya kosalekeza,
Iyo inkagonjetsa anthu a mitundu ina mwaukali
    ndikuwazunza kosalekeza.
Koma tsopano mayiko onse ali pa mpumulo ndi pa mtendere;
    ndipo akuyimba mokondwa.
Ngakhale mitengo ya payini ndi mikungudza ya ku Lebanoni
    ikuyimba za iwe mokondwa ndipo ikuti,
“Chigwetsedwere chako pansi,
    palibe wina anabwera kudzatigwetsa.”

Ku manda kwatekeseka
    kuti akulandire ukamabwera;
mizimu ya anthu akufa, aja amene anali atsogoleri
    a dziko lapansi, yadzutsidwa.
Onse amene anali mafumu a mitundu ya anthu
    ayimiritsidwa pa mipando yawo.
10 Onse adzayankha;
    adzanena kwa iwe kuti,
“Iwenso watheratu mphamvu ngati ife;
    Iwe wafanana ndi ife.”
11 Ulemerero wako wonse walowa mʼmanda,
    pamodzi ndi nyimbo za azeze ako;
mphutsi zayalana pogona pako
    ndipo chofunda chako ndi nyongolotsi.

12 Wagwa pansi bwanji kuchoka kumwamba,
    iwe nthanda, mwana wa mʼbandakucha!
Wagwetsedwa pansi pa dziko lapansi,
    Iwe amene unagonjetsapo mitundu ya anthu!
13 Mu mtima mwako unkanena kuti,
    “Ndidzakwera mpaka kumwamba;
ndidzakhazika mpando wanga waufumu
    pamwamba pa nyenyezi za Mulungu;
ndidzakhala pa mpando waufumu pa phiri losonkhanirako,
    pamwamba penipeni pa phiri la kumpoto.
14 Ndidzakwera pamwamba pa mitambo;
    ndidzafanana ndi Wammwambamwamba.”
15 Koma watsitsidwa mʼmanda
    pansi penipeni pa dzenje.

16 Anthu akufa adzakupenyetsetsa
    nadzamalingalira za iwe nʼkumati,
“Kodi uyu ndi munthu uja anagwedeza dziko lapansi
    ndi kunjenjemeretsa maufumu,
17 munthu amene anasandutsa dziko lonse chipululu,
    amene anagwetsa mizinda yake
    ndipo sankalola kuti anthu ogwidwa abwerere kwawo?”

18 Mafumu onse a mitundu ya anthu akugona mwaulemu
    aliyense mʼmanda akeake.
19 Koma iwe watayidwa kunja kwa manda ako,
    ngati nthambi yowola ndi yonyansa.
Mtembo wako waphimbidwa ndi anthu ophedwa;
    amene anabayidwa ndi lupanga,
    anatsikira mʼdzenje lamiyala
ngati mtembo woponderezedwa.
20     Sudzayikidwa nawo mʼmanda mwaulemu,
chifukwa unawononga dziko lako
    ndi kupha anthu ako.

Zidzukulu za anthu oyipa
    sizidzakumbukika nʼpangʼono pomwe.
21 Konzani malo woti muphere ana ake aamuna
    chifukwa cha machimo a makolo awo;
kuti angadzuke ndi kulanda dziko lapansi
    ndi kulidzaza dziko lonselo ndi mizinda yawo.

22 Yehova Wamphamvuzonse akuti,
    “Ine ndidzathira nkhondo mzinda wa Babuloni.
Ndidzachotseratu mu Babuloni dzina lake ndi onse otsaliramo.
    Ndiye kuti sipadzakhala ana kapena zidzukulu,”
            akutero Yehova.
23 “Ndidzawusandutsa mzindawo malo okhalamo anungu
    ndiponso dambo lamatope;
ndidzawusesa ndi tsache lowononga,”
    akutero Yehova Wamphamvuzonse.

Za Kulangidwa kwa Asiriya

24 Yehova Wamphamvuzonse walumbira kuti,

“Ndithudi, monga ndaganizira ndidzachitadi choncho,
    ndipo monga momwe ndatsimikizira zidzakhala momwemo ndithu.
25 Ndidzawawononga Asiriya mʼdziko langa;
    ndidzawapondereza ndi mapazi pa mapiri anga;
ndidzachotsa goli lawo pa anthu anga,
    ndipo ndidzachotsa katundu wawo pa mapewa awo.”

26 Izi ndizo ndakonza kuti zichitike pa dziko lonse lapansi,
    ndatambasula dzanja pa anthu a mitundu yonse.
27 Pakuti Yehova Wamphamvuzonse watsimikiza, ndipo ndani angamuletse?
    Dzanja lake latambasulidwa ndipo ndani angalibweze?

Za Kulangidwa kwa Afilisti

28 Uthenga uwu unabwera chaka chimene mfumu Ahazi anamwalira:

29 Musakondwere inu Afilisti nonse
    kuti Asiriya amene anali ngati ndodo yokukanthani anathedwa;
chifukwa kuchokera ku njoka yomweyi (mfumu ya Aasiriya) mudzatuluka mphiri,
    ndipo chipatso chake chidzakhala njoka yaliwiro ndiponso yaululu.
30 Osaukitsitsa adzapeza chakudya
    ndipo amphawi adzakhala mwamtendere.
Koma anthu ako ndidzawawononga ndi njala,
    ndipo njalayo idzapha ngakhale opulumuka ako.

31 Lirani kwambiri, anthu a pa chipata! Fuwulani kwambiri, anthu a mu mzinda!
    Njenjemerani ndi mantha, inu Afilisti nonse!
Mtambo wa utsi ukuchokera kumpoto,
    ndipo palibe wamantha pakati pa ankhondo ake.
32 Kodi tidzawayankha chiyani
    amithenga a ku Filisitiya?
“Yehova wakhazikitsa Ziyoni,
    ndipo mu mzinda wakewu, anthu ozunzika apeza populumukira.”

14 The Lord will have compassion(A) on Jacob;
    once again he will choose(B) Israel
    and will settle them in their own land.(C)
Foreigners(D) will join them
    and unite with the descendants of Jacob.
Nations will take them
    and bring(E) them to their own place.
And Israel will take possession of the nations(F)
    and make them male and female servants in the Lord’s land.
They will make captives(G) of their captors
    and rule over their oppressors.(H)

On the day the Lord gives you relief(I) from your suffering and turmoil(J) and from the harsh labor forced on you,(K) you will take up this taunt(L) against the king of Babylon:(M)

How the oppressor(N) has come to an end!
    How his fury[a] has ended!
The Lord has broken the rod(O) of the wicked,(P)
    the scepter(Q) of the rulers,
which in anger struck down peoples(R)
    with unceasing blows,
and in fury subdued(S) nations
    with relentless aggression.(T)
All the lands are at rest and at peace;(U)
    they break into singing.(V)
Even the junipers(W) and the cedars of Lebanon
    gloat over you and say,
“Now that you have been laid low,
    no one comes to cut us down.”(X)

The realm of the dead(Y) below is all astir
    to meet you at your coming;
it rouses the spirits of the departed(Z) to greet you—
    all those who were leaders(AA) in the world;
it makes them rise from their thrones—
    all those who were kings over the nations.(AB)
10 They will all respond,
    they will say to you,
“You also have become weak, as we are;
    you have become like us.”(AC)
11 All your pomp has been brought down to the grave,(AD)
    along with the noise of your harps;(AE)
maggots are spread out beneath you
    and worms(AF) cover you.(AG)

12 How you have fallen(AH) from heaven,
    morning star,(AI) son of the dawn!
You have been cast down to the earth,
    you who once laid low the nations!(AJ)
13 You said in your heart,
    “I will ascend(AK) to the heavens;
I will raise my throne(AL)
    above the stars of God;
I will sit enthroned on the mount of assembly,(AM)
    on the utmost heights(AN) of Mount Zaphon.[b]
14 I will ascend above the tops of the clouds;(AO)
    I will make myself like the Most High.”(AP)
15 But you are brought down(AQ) to the realm of the dead,(AR)
    to the depths(AS) of the pit.(AT)

16 Those who see you stare at you,
    they ponder your fate:(AU)
“Is this the man who shook(AV) the earth
    and made kingdoms tremble,
17 the man who made the world a wilderness,(AW)
    who overthrew(AX) its cities
    and would not let his captives go home?”(AY)

18 All the kings of the nations lie in state,
    each in his own tomb.(AZ)
19 But you are cast out(BA) of your tomb
    like a rejected branch;
you are covered with the slain,(BB)
    with those pierced by the sword,(BC)
    those who descend to the stones of the pit.(BD)
Like a corpse trampled underfoot,
20     you will not join them in burial,(BE)
for you have destroyed your land
    and killed your people.

Let the offspring(BF) of the wicked(BG)
    never be mentioned(BH) again.
21 Prepare a place to slaughter his children(BI)
    for the sins of their ancestors;(BJ)
they are not to rise to inherit the land
    and cover the earth with their cities.

22 “I will rise up(BK) against them,”
    declares the Lord Almighty.
“I will wipe out Babylon’s name(BL) and survivors,
    her offspring and descendants,(BM)
declares the Lord.
23 “I will turn her into a place for owls(BN)
    and into swampland;
I will sweep her with the broom of destruction,(BO)
    declares the Lord Almighty.(BP)

24 The Lord Almighty has sworn,(BQ)

“Surely, as I have planned,(BR) so it will be,
    and as I have purposed, so it will happen.(BS)
25 I will crush the Assyrian(BT) in my land;
    on my mountains I will trample him down.
His yoke(BU) will be taken from my people,
    and his burden removed from their shoulders.(BV)

26 This is the plan(BW) determined for the whole world;
    this is the hand(BX) stretched out over all nations.
27 For the Lord Almighty has purposed,(BY) and who can thwart him?
    His hand(BZ) is stretched out, and who can turn it back?(CA)

A Prophecy Against the Philistines

28 This prophecy(CB) came in the year(CC) King Ahaz(CD) died:

29 Do not rejoice, all you Philistines,(CE)
    that the rod that struck you is broken;
from the root of that snake will spring up a viper,(CF)
    its fruit will be a darting, venomous serpent.(CG)
30 The poorest of the poor will find pasture,
    and the needy(CH) will lie down in safety.(CI)
But your root I will destroy by famine;(CJ)
    it will slay(CK) your survivors.(CL)

31 Wail,(CM) you gate!(CN) Howl, you city!
    Melt away, all you Philistines!(CO)
A cloud of smoke comes from the north,(CP)
    and there is not a straggler in its ranks.(CQ)
32 What answer shall be given
    to the envoys(CR) of that nation?
“The Lord has established Zion,(CS)
    and in her his afflicted people will find refuge.(CT)

Footnotes

  1. Isaiah 14:4 Dead Sea Scrolls, Septuagint and Syriac; the meaning of the word in the Masoretic Text is uncertain.
  2. Isaiah 14:13 Or of the north; Zaphon was the most sacred mountain of the Canaanites.