Yesaya 15
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Za Kulangidwa kwa Mowabu
15 Uthenga wonena za Mowabu:
Popeza kuti mu usiku umodzi wokha mzinda wa Ari wa ku Mowabu wawonongedwa,
wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.
Mzinda wa Kiri wawonongedwa,
wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.
2 Anthu a ku Diboni akupita ku nyumba ya milungu yawo,
akupita ku malo awo achipembedzo kukalira;
anthu a ku Mowabu akulirira mofuwula mzinda wa Nebo ndi wa Medeba.
Mutu uliwonse wametedwa mpala,
ndipo ndevu zonse zametedwa.
3 Mʼmisewu akuvala ziguduli;
pa madenga ndi mʼmabwalo
aliyense akulira mofuwula,
misozi ili pupupu.
4 Anthu a ku Hesiboni ndi Eleali akulira mofuwula,
mawu awo akumveka mpaka ku Yahazi.
Kotero asilikali a ku Mowabu akulira mofuwula,
ndipo ataya mtima.
5 Inenso ndikulirira Mowabu;
chifukwa othawa nkhondo ake akupita akulira ku chikweza cha Luluti mpaka ku Zowari
ndi Egilati-Selisiya
akupita akulira ku chikweza cha Luhiti,
Akulira mosweka mtima
pa njira yopita ku Horonaimu;
akulira mosweka mtima chifukwa cha chiwonongeko chawo.
6 Madzi a ku Nimurimu aphwa
ndipo udzu wauma;
zomera zawonongeka
ndipo palibe chomera chobiriwira chatsala.
7 Kotero kuti chuma chomwe anachipeza ndi kuchisunga,
achitenga kuti awoloke nacho chigwembe cha Misondozi.
8 Kulira kwawo kukumveka mʼdziko lonse la Mowabu;
kulira kwawo kosweka mtima kukumveka
mpaka ku Egilaimu ndi Beeri-Elimu.
9 Madzi a ku Dimoni afiira ndi magazi,
komabe ndidzabweretsa zina zambiri pa Dimoni,
mkango woti udzagwire aliyense othawa mu Mowabu
ndi aliyense wotsala mʼdzikomo.
Isaiah 15
New International Version
A Prophecy Against Moab(A)
15 A prophecy(B) against Moab:(C)
Ar(D) in Moab is ruined,(E)
destroyed in a night!
Kir(F) in Moab is ruined,
destroyed in a night!
2 Dibon(G) goes up to its temple,
to its high places(H) to weep;
Moab wails(I) over Nebo(J) and Medeba.
Every head is shaved(K)
and every beard cut off.(L)
3 In the streets they wear sackcloth;(M)
on the roofs(N) and in the public squares(O)
they all wail,(P)
prostrate with weeping.(Q)
4 Heshbon(R) and Elealeh(S) cry out,
their voices are heard all the way to Jahaz.(T)
Therefore the armed men of Moab cry out,
and their hearts are faint.
5 My heart cries out(U) over Moab;(V)
her fugitives(W) flee as far as Zoar,(X)
as far as Eglath Shelishiyah.
They go up the hill to Luhith,
weeping as they go;
on the road to Horonaim(Y)
they lament their destruction.(Z)
6 The waters of Nimrim are dried up(AA)
and the grass is withered;(AB)
the vegetation is gone(AC)
and nothing green is left.(AD)
7 So the wealth they have acquired(AE) and stored up
they carry away over the Ravine of the Poplars.
8 Their outcry echoes along the border of Moab;
their wailing reaches as far as Eglaim,
their lamentation as far as Beer(AF) Elim.
9 The waters of Dimon[a] are full of blood,
but I will bring still more upon Dimon[b]—
a lion(AG) upon the fugitives of Moab(AH)
and upon those who remain in the land.
Footnotes
- Isaiah 15:9 Dimon, a wordplay on Dibon (see verse 2), sounds like the Hebrew for blood.
- Isaiah 15:9 Dimon, a wordplay on Dibon (see verse 2), sounds like the Hebrew for blood.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.