Add parallel Print Page Options

Za Kulangidwa kwa Mowabu

15 Uthenga wonena za Mowabu:

Popeza kuti mu usiku umodzi wokha mzinda wa Ari wa ku Mowabu wawonongedwa,
    wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.
Mzinda wa Kiri wawonongedwa,
    wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.
Anthu a ku Diboni akupita ku nyumba ya milungu yawo,
    akupita ku malo awo achipembedzo kukalira;
    anthu a ku Mowabu akulirira mofuwula mzinda wa Nebo ndi wa Medeba.
Mutu uliwonse wametedwa mpala,
    ndipo ndevu zonse zametedwa.
Mʼmisewu akuvala ziguduli;
    pa madenga ndi mʼmabwalo
aliyense akulira mofuwula,
    misozi ili pupupu.
Anthu a ku Hesiboni ndi Eleali akulira mofuwula,
    mawu awo akumveka mpaka ku Yahazi.
Kotero asilikali a ku Mowabu akulira mofuwula,
    ndipo ataya mtima.

Inenso ndikulirira Mowabu;
    chifukwa othawa nkhondo ake akupita akulira ku chikweza cha Luluti mpaka ku Zowari
    ndi Egilati-Selisiya
akupita akulira ku chikweza cha Luhiti,
    Akulira mosweka mtima
pa njira yopita ku Horonaimu;
    akulira mosweka mtima chifukwa cha chiwonongeko chawo.
Madzi a ku Nimurimu aphwa
    ndipo udzu wauma;
zomera zawonongeka
    ndipo palibe chomera chobiriwira chatsala.
Kotero kuti chuma chomwe anachipeza ndi kuchisunga,
    achitenga kuti awoloke nacho chigwembe cha Misondozi.
Kulira kwawo kukumveka mʼdziko lonse la Mowabu;
    kulira kwawo kosweka mtima kukumveka
    mpaka ku Egilaimu ndi Beeri-Elimu.
Madzi a ku Dimoni afiira ndi magazi,
    komabe ndidzabweretsa zina zambiri pa Dimoni,
mkango woti udzagwire aliyense othawa mu Mowabu
    ndi aliyense wotsala mʼdzikomo.

A Prophecy Against Moab(A)

15 A prophecy(B) against Moab:(C)

Ar(D) in Moab is ruined,(E)
    destroyed in a night!
Kir(F) in Moab is ruined,
    destroyed in a night!
Dibon(G) goes up to its temple,
    to its high places(H) to weep;
    Moab wails(I) over Nebo(J) and Medeba.
Every head is shaved(K)
    and every beard cut off.(L)
In the streets they wear sackcloth;(M)
    on the roofs(N) and in the public squares(O)
they all wail,(P)
    prostrate with weeping.(Q)
Heshbon(R) and Elealeh(S) cry out,
    their voices are heard all the way to Jahaz.(T)
Therefore the armed men of Moab cry out,
    and their hearts are faint.

My heart cries out(U) over Moab;(V)
    her fugitives(W) flee as far as Zoar,(X)
    as far as Eglath Shelishiyah.
They go up the hill to Luhith,
    weeping as they go;
on the road to Horonaim(Y)
    they lament their destruction.(Z)
The waters of Nimrim are dried up(AA)
    and the grass is withered;(AB)
the vegetation is gone(AC)
    and nothing green is left.(AD)
So the wealth they have acquired(AE) and stored up
    they carry away over the Ravine of the Poplars.
Their outcry echoes along the border of Moab;
    their wailing reaches as far as Eglaim,
    their lamentation as far as Beer(AF) Elim.
The waters of Dimon[a] are full of blood,
    but I will bring still more upon Dimon[b]
a lion(AG) upon the fugitives of Moab(AH)
    and upon those who remain in the land.

Footnotes

  1. Isaiah 15:9 Dimon, a wordplay on Dibon (see verse 2), sounds like the Hebrew for blood.
  2. Isaiah 15:9 Dimon, a wordplay on Dibon (see verse 2), sounds like the Hebrew for blood.