Add parallel Print Page Options

Phiri la Yehova

Nazi zinthu zokhudza Yuda ndi Yerusalemu, zimene Yesaya mwana wa Amozi anaziona mʼmasomphenya:

Mʼmasiku otsiriza,

phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa
    kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse,
lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse,
    ndipo mayiko onse adzathamangira kumeneko.

Anthu ambiri adzabwera ndikunena kuti,

“Tiyeni tikwere ku phiri la Yehova,
    ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo.
Iye adzatiphunzitsa njira zake,
    ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.”
Malangizo adzachokera ku Ziyoni,
    mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.
Iye adzaweruza pakati pa mayiko,
    ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu ambiri.
Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu
    ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera.
Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina,
    kapena kuphunziranso za nkhondo.

Inu nyumba ya Yakobo, bwerani,
    tiyeni tiyende mʼkuwala kwa Yehova.

Tsiku la Yehova

Inu Yehova mwawakana anthu anu,
    nyumba ya Yakobo.
Iwo adzaza ndi zamatsenga zochokera Kummawa;
    amawombeza mawula ngati Afilisti,
    ndipo amayanjana ndi anthu osapembedza Mulungu.
Dziko lawo ndi lodzaza ndi siliva ndi golide;
    ndipo chuma chawo ndi chosatha.
Dziko lawo ndi lodzaza ndi akavalo;
    ndipo magaleta awo ankhondo ngosawerengeka.
Dziko lawo ndi lodzaza ndi mafano;
    iwo amapembedza ntchito ya manja awo,
    amagwadira zomwe anapanga ndi zala zawo.
Tsono munthu aliyense adzachepetsedwa
    ndi kutsitsidwa.
    Inu Yehova musawakhululukire.

10 Lowani mʼmatanthwe,
    bisalani mʼmaenje,
kuthawa kuopsa kwa Yehova
    ndi ulemerero wa ufumu wake!
11 Kudzikuza kwa anthu kudzatha,
    ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa;
Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu pa tsiku limenelo.

12 Yehova Wamphamvuzonse wakonzeratu tsiku
    limene adzatsitse onse onyada ndi odzitama,
    ndipo adzagonjetsa
    onse amphamvu,
13 tsiku la mikungudza yonse ya ku Lebanoni, yayitali ndi yoonekera patali,
    ndiponso la mitengo yonse ya thundu ya ku Basani,
14 tsiku la mapiri onse ataliatali
    ndiponso la zitunda zonse zazitali,
15 tsiku la nsanja zonse zazitali
    ndiponso malinga onse olimba,
16 tsiku la sitima zapamadzi zonse za ku Tarisisi
    ndiponso la mabwato onse okongola.
17 Kudzikuza kwa munthu kudzatha
    ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa,
Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu tsiku limenelo,
18     ndipo mafano onse adzatheratu.

19 Anthu adzathawira mʼmapanga a matanthwe
    ndi mʼmaenje a nthaka,
kuthawa mkwiyo wa Yehova,
    ndiponso ulemerero wa ufumu wake,
    pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.
20 Tsiku limenelo anthu adzatayira
    mfuko ndi mileme
mafano awo asiliva ndi mafano awo agolide,
    amene anawapanga kuti aziwapembedza.
21 Adzathawira mʼmapanga a matanthwe
    ndiponso mʼmingʼalu ya nthaka
kuthawa mkwiyo wa Yehova
    ndiponso ulemerero wa ufumu wake,
    pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.

22 Lekani kudalira munthu,
    amene moyo wake sukhalira kutha.
Iye angathandize bwanji wina aliyense?

The Mountain of the Lord(A)

This is what Isaiah son of Amoz saw concerning Judah and Jerusalem:(B)

In the last days(C)

the mountain(D) of the Lord’s temple will be established
    as the highest of the mountains;(E)
it will be exalted(F) above the hills,
    and all nations will stream to it.(G)

Many peoples(H) will come and say,

“Come, let us go(I) up to the mountain(J) of the Lord,
    to the temple of the God of Jacob.
He will teach us his ways,
    so that we may walk in his paths.”
The law(K) will go out from Zion,
    the word of the Lord from Jerusalem.(L)
He will judge(M) between the nations
    and will settle disputes(N) for many peoples.
They will beat their swords into plowshares
    and their spears into pruning hooks.(O)
Nation will not take up sword against nation,(P)
    nor will they train for war anymore.

Come, descendants of Jacob,(Q)
    let us walk in the light(R) of the Lord.

The Day of the Lord

You, Lord, have abandoned(S) your people,
    the descendants of Jacob.(T)
They are full of superstitions from the East;
    they practice divination(U) like the Philistines(V)
    and embrace(W) pagan customs.(X)
Their land is full of silver and gold;(Y)
    there is no end to their treasures.(Z)
Their land is full of horses;(AA)
    there is no end to their chariots.(AB)
Their land is full of idols;(AC)
    they bow down(AD) to the work of their hands,(AE)
    to what their fingers(AF) have made.
So people will be brought low(AG)
    and everyone humbled(AH)
    do not forgive them.[a](AI)

10 Go into the rocks, hide(AJ) in the ground
    from the fearful presence of the Lord
    and the splendor of his majesty!(AK)
11 The eyes of the arrogant(AL) will be humbled(AM)
    and human pride(AN) brought low;(AO)
the Lord alone will be exalted(AP) in that day.(AQ)

12 The Lord Almighty has a day(AR) in store
    for all the proud(AS) and lofty,(AT)
for all that is exalted(AU)
    (and they will be humbled),(AV)
13 for all the cedars of Lebanon,(AW) tall and lofty,(AX)
    and all the oaks of Bashan,(AY)
14 for all the towering mountains
    and all the high hills,(AZ)
15 for every lofty tower(BA)
    and every fortified wall,(BB)
16 for every trading ship[b](BC)
    and every stately vessel.
17 The arrogance of man will be brought low(BD)
    and human pride humbled;(BE)
the Lord alone will be exalted in that day,(BF)
18     and the idols(BG) will totally disappear.(BH)

19 People will flee to caves(BI) in the rocks
    and to holes in the ground(BJ)
from the fearful presence(BK) of the Lord
    and the splendor of his majesty,(BL)
    when he rises to shake the earth.(BM)
20 In that day(BN) people will throw away
    to the moles and bats(BO)
their idols of silver and idols of gold,(BP)
    which they made to worship.(BQ)
21 They will flee to caverns in the rocks(BR)
    and to the overhanging crags
from the fearful presence of the Lord
    and the splendor of his majesty,(BS)
    when he rises(BT) to shake the earth.(BU)

22 Stop trusting in mere humans,(BV)
    who have but a breath(BW) in their nostrils.
    Why hold them in esteem?(BX)

Footnotes

  1. Isaiah 2:9 Or not raise them up
  2. Isaiah 2:16 Hebrew every ship of Tarshish