Add parallel Print Page Options

Tsoka kwa Mtundu Wopanduka

30 Yehova akuti, “Tsoka kwa ana ondipandukira
    amene amachita zowakomera iwo okha osati Ine,
nachita mgwirizano wawowawo
    koma osati motsogozedwa ndi Ine.
    Choncho amanka nachimwirachimwira.
Amapita ku Igupto kukapempha thandizo
    koma osandifunsa;
amathawira kwa Farao kuti awateteze,
    ku Igupto amafuna malo opulumulira.
Koma chitetezo cha Farao chidzakhala manyazi anu,
    malo a mthunzi a ku Igupto mudzachita nawo manyazi.
Ngakhale kuti nduna zawo zili ku Zowani,
    ndipo akazembe awo afika kale ku Hanesi,
aliyense wa ku Yuda adzachita manyazi
    chifukwa cha anthu opanda nawo phindu,
amene sabweretsa thandizo kapena phindu,
    koma manyazi ndi mnyozo.”

Uthenga wonena za nyama za ku Negevi:

Akazembe akuyenda mʼdziko lovuta ndi losautsa,
    mʼmene muli mikango yayimuna ndi yayikazi,
    mphiri ndi njoka zaululu.
Iwo amasenzetsa abulu ndi ngamira chuma chawo,
    kupita nazo kwa mtundu wa anthu
umene sungawathandize.
    Amapita ku Igupto amene thandizo lake ndi lachabechabe.
Nʼchifukwa chake dzikolo ndalitcha
    Rahabe chirombo cholobodoka.

Yehova anandiwuza kuti, “Tsopano pita,
    ukalembe zimenezi mʼbuku iwo akuona
ndipo lidzakhala ngati umboni wosatha
    masiku a mʼtsogolo.
Amenewa ndi anthu owukira, onama ndi
    osafuna kumvera malangizo a Yehova.
10 Iwo amawuza alosi kuti,
    ‘Musationerenso masomphenya!’
Ndipo amanena kwa mneneri kuti,
    ‘Musatinenerenso zoona,’
mutiwuze zotikomera,
    munenere za mʼmutu mwanu.
11 Patukani pa njira ya Yehova,
    lekani kutsata njira ya Yehova;
ndipo tisamvenso mawu
    a Woyerayo uja wa Israeli!”

12 Nʼchifukwa chake Woyerayo wa Israeli akunena kuti,

“Popeza inu mwakana uthenga uwu,
    mumakhulupirira zopondereza anzanu
    ndipo mumadalira kuchita zoyipa,
13 choncho tchimo linalo lidzakhala ngati mingʼalu
    pa khoma lalitali ndi lopendama
    limene linagwa mwadzidzidzi ndi mwamsangamsanga.
14 Lidzaphwanyika ngati mbiya
    imene yanyenyekeratu,
mwakuti pakati pake sipadzapezeka phale ngakhale
    lopalira moto mʼngʼanjo
    kapena lotungira madzi mʼchitsime.”

15 Zimene Ambuye Yehova, Woyerayo wa Israeli ananena ndi izi:

“Ngati mubwerera ndi kupuma mudzapulumuka,
    ngati mukhala chete ndi kukhulupirira mudzakhala amphamvu,
    koma inu munakana zimenezi.
16 Inu mukuti, ‘Ayi ife tidzathawa,
    tidzakwera pa akavalo aliwiro.’
Zoonadi kuti mudzakwera pa akavalo aliwiro,
    koma okuthamangitsani adzakhalanso aliwiro.
17 Anthu 1,000 mwa inu adzathawa
    poona mdani mmodzi;
poona adani asanu okha
    nonsenu mudzathawa.
Otsala anu
    adzakhala ngati mbendera pa phiri,
    ndi ngati chizindikiro cha pa chulu.”

18 Komatu Yehova akufunitsitsa kuti akukomereni mtima,
    iye ali wokonzeka kuti akuchitireni chifundo.
Pakuti Yehova ndi Mulungu wachilungamo.
    Ndi odala onse amene amakhulupirira Iye!

19 Inu anthu a ku Ziyoni, amene mukhala mu Yerusalemu simudzaliranso. Mulungu adzakukomerani mtima pamene adzamva kulira kwanu kopempha thandizo! Ndipo akadzamva, adzakuyankhani. 20 Ngakhale Ambuye adzakulowetseni mʼmasautso, aphunzitsi anu sadzakhala kakasi; inu mudzawaona ndi maso anuwo. 21 Ngati mudzapatukira kumanja kapena kumanzere, mudzamva mawu kumbuyo kwanu woti, “Njira ndi iyi; yendani mʼmenemo.” 22 Pamenepo mudzawononga mafano anu okutidwa ndi siliva ndiponso zifanizo zanu zokutidwa ndi golide; mudzawataya ngati zinthu zonyansa ndipo mudzati, “Zichoke zonsezi!”

23 Yehova adzakugwetseraninso mvula pa mbewu zanu zimene mukadzale mʼnthaka, ndipo chakudya chimene mudzakolole chidzakhala chabwino ndi chochuluka. Tsiku limenelo ngʼombe zanu zidzadya msipu wochuluka. 24 Ngʼombe ndi abulu amene amalima mʼmunda adzadya chakudya chamchere, chopetedwa ndi foloko ndi fosholo. 25 Pa tsiku limene adani anu adzaphedwa ndi nsanja zawo kugwa, mitsinje ya madzi idzayenda pa phiri lililonse lalikulu ndi pa phiri lililonse lalingʼono. 26 Mwezi udzawala ngati dzuwa, ndipo kuwala kwa dzuwa kudzawonjezereka kasanu nʼkawiri, ngati kuwala kwa tsiku limodzi. Yehova adzamanga mabala a anthu ake ndi kupoletsa zilonda zimene Iye anachititsa polanga anthu ake.

27 Taonani, Yehova akubwera kuchokera kutali,
    ndipo mkwiyo wake ndiwonyeka ndi chiweruzo chake chidzakhala chopweteka.
Iye wayankhula mwaukali kwambiri,
    ndipo mawu ake ali ngati moto wonyeka.
28 Mpweya wake uli ngati mtsinje wosefukira,
    wa madzi ofika mʼkhosi.
Iye adzasefa anthu a mitundu ina ndi sefa wosakaza;
    Iye akuyika zitsulo mʼkamwa mwa anthu a mitundu ina ngati akavalo,
    kuti ziwasocheretse.
29 Ndipo inu mudzayimba
    mokondwa monga mumachitira usiku pa chikondwerero chopatulika.
Mudzasangalala
    ngati anthu oyimba zitoliro
popita ku phiri la Yehova,
    thanthwe la Israeli.
30 Anthu adzamva liwu la ulemerero la Yehova
    ndipo adzaona dzanja lake likutsika pa iwo
ndi mkwiyo woopsa, pamodzi ndi moto wonyeketsa,
    mphenzi, namondwe ndi matalala.
31 Asiriya adzaopa liwu la Yehova,
    ndipo Iye adzawakantha ndi ndodo.
32 Yehova akamadzalanga adani ake ndi ndodo,
    anthu ake adzakhala akuvina nyimbo
zoyimbira matambolini ndi azeze,
    Yehova ndiye ati adzamenyane ndi Asiriyawo.
33 Malo otenthera zinthu akonzedwa kale;
    anakonzera mfumu ya ku Asiriya.
Dzenje la motolo ndi lozama ndi lalikulu,
    ndipo muli nkhuni zambiri;
mpweya wa Yehova,
    wangati mtsinje wa sulufule,
    udzayatsa motowo pa nkhunizo.

Woe to the Obstinate Nation

30 “Woe(A) to the obstinate children,”(B)
    declares the Lord,
“to those who carry out plans that are not mine,
    forming an alliance,(C) but not by my Spirit,
    heaping sin upon sin;
who go down to Egypt(D)
    without consulting(E) me;
who look for help to Pharaoh’s protection,(F)
    to Egypt’s shade for refuge.(G)
But Pharaoh’s protection will be to your shame,
    Egypt’s shade(H) will bring you disgrace.(I)
Though they have officials in Zoan(J)
    and their envoys have arrived in Hanes,
everyone will be put to shame
    because of a people(K) useless(L) to them,
who bring neither help(M) nor advantage,
    but only shame and disgrace.(N)

A prophecy(O) concerning the animals of the Negev:(P)

Through a land of hardship and distress,(Q)
    of lions(R) and lionesses,
    of adders and darting snakes,(S)
the envoys carry their riches on donkeys’(T) backs,
    their treasures(U) on the humps of camels,
to that unprofitable nation,
    to Egypt, whose help is utterly useless.(V)
Therefore I call her
    Rahab(W) the Do-Nothing.

Go now, write it on a tablet(X) for them,
    inscribe it on a scroll,(Y)
that for the days to come
    it may be an everlasting witness.(Z)
For these are rebellious(AA) people, deceitful(AB) children,
    children unwilling to listen to the Lord’s instruction.(AC)
10 They say to the seers,(AD)
    “See no more visions(AE)!”
and to the prophets,
    “Give us no more visions of what is right!
Tell us pleasant things,(AF)
    prophesy illusions.(AG)
11 Leave this way,(AH)
    get off this path,
and stop confronting(AI) us
    with the Holy One(AJ) of Israel!”

12 Therefore this is what the Holy One(AK) of Israel says:

“Because you have rejected this message,(AL)
    relied on oppression(AM)
    and depended on deceit,
13 this sin will become for you
    like a high wall,(AN) cracked and bulging,
    that collapses(AO) suddenly,(AP) in an instant.
14 It will break in pieces like pottery,(AQ)
    shattered so mercilessly
that among its pieces not a fragment will be found
    for taking coals from a hearth
    or scooping water out of a cistern.”

15 This is what the Sovereign(AR) Lord, the Holy One(AS) of Israel, says:

“In repentance and rest(AT) is your salvation,
    in quietness and trust(AU) is your strength,
    but you would have none of it.(AV)
16 You said, ‘No, we will flee(AW) on horses.’(AX)
    Therefore you will flee!
You said, ‘We will ride off on swift horses.’
    Therefore your pursuers will be swift!
17 A thousand will flee
    at the threat of one;
at the threat of five(AY)
    you will all flee(AZ) away,
till you are left(BA)
    like a flagstaff on a mountaintop,
    like a banner(BB) on a hill.”

18 Yet the Lord longs(BC) to be gracious to you;
    therefore he will rise up to show you compassion.(BD)
For the Lord is a God of justice.(BE)
    Blessed are all who wait for him!(BF)

19 People of Zion, who live in Jerusalem, you will weep no more.(BG) How gracious he will be when you cry for help!(BH) As soon as he hears, he will answer(BI) you. 20 Although the Lord gives you the bread(BJ) of adversity and the water of affliction, your teachers(BK) will be hidden(BL) no more; with your own eyes you will see them. 21 Whether you turn to the right or to the left, your ears will hear a voice(BM) behind you, saying, “This is the way;(BN) walk in it.” 22 Then you will desecrate your idols(BO) overlaid with silver and your images covered with gold;(BP) you will throw them away like a menstrual(BQ) cloth and say to them, “Away with you!(BR)

23 He will also send you rain(BS) for the seed you sow in the ground, and the food that comes from the land will be rich(BT) and plentiful.(BU) In that day(BV) your cattle will graze in broad meadows.(BW) 24 The oxen(BX) and donkeys that work the soil will eat fodder(BY) and mash, spread out with fork(BZ) and shovel. 25 In the day of great slaughter,(CA) when the towers(CB) fall, streams of water will flow(CC) on every high mountain and every lofty hill. 26 The moon will shine like the sun,(CD) and the sunlight will be seven times brighter, like the light of seven full days, when the Lord binds up the bruises of his people and heals(CE) the wounds he inflicted.

27 See, the Name(CF) of the Lord comes from afar,
    with burning anger(CG) and dense clouds of smoke;
his lips are full of wrath,(CH)
    and his tongue is a consuming fire.(CI)
28 His breath(CJ) is like a rushing torrent,(CK)
    rising up to the neck.(CL)
He shakes the nations in the sieve(CM) of destruction;
    he places in the jaws of the peoples
    a bit(CN) that leads them astray.
29 And you will sing
    as on the night you celebrate a holy festival;(CO)
your hearts will rejoice(CP)
    as when people playing pipes(CQ) go up
to the mountain(CR) of the Lord,
    to the Rock(CS) of Israel.
30 The Lord will cause people to hear his majestic voice(CT)
    and will make them see his arm(CU) coming down
with raging anger(CV) and consuming fire,(CW)
    with cloudburst, thunderstorm(CX) and hail.(CY)
31 The voice of the Lord will shatter Assyria;(CZ)
    with his rod he will strike(DA) them down.
32 Every stroke the Lord lays on them
    with his punishing club(DB)
will be to the music of timbrels(DC) and harps,
    as he fights them in battle with the blows of his arm.(DD)
33 Topheth(DE) has long been prepared;
    it has been made ready for the king.
Its fire pit has been made deep and wide,
    with an abundance of fire and wood;
the breath(DF) of the Lord,
    like a stream of burning sulfur,(DG)
    sets it ablaze.(DH)