Add parallel Print Page Options

Ufumu Wachilungamo

32 Taonani, kudzakhala mfumu ina imene idzalamulira mwachilungamo,
    ndipo akalonga ake adzaweruza molungama.
Munthu aliyense adzakhala ngati pothawirapo mphepo
    ndi malo obisalirapo namondwe,
adzakhala ngati mitsinje ya mʼchipululu,
    ngati mthunzi wa thanthwe lalikulu la mʼdziko lowuma.

Ndipo maso a anthu openya sadzakhalanso otseka,
    ndipo makutu a anthu akumva adzamvetsetsa.
Anthu a mtima wopupuluma adzadziwa ndi kuchita zinthu mofatsa,
    ndipo anthu ovutika kuyankhula adzayankhula mosadodoma ndi momveka.
Chitsiru sichidzatchedwanso munthu waulemu wake
    ndipo munthu woyipa sadzalemekezedwa.
Pakuti munthu opusa amayankhula zauchitsiru,
    amaganiza kuchita zoyipa:
Iye amachita zoyipira Mulungu,
    ndipo amafalitsa zolakwika zokhudza Yehova;
anjala sawapatsa chakudya
    ndipo aludzu sawapatsa madzi.
Munthu woyipa njira zake ndi zoyipanso,
    iye kwake nʼkulingalira zinthu zoyipa.
Amalingalira zakuti awononge anthu aumphawi ndi mabodza ake
    ngakhale kuti waumphawiyo akuyankhula zoona.
Koma munthu wolemekezeka amalingaliranso kuchita zinthu zabwino,
    Iye amakhazikika pa zinthu zabwinozo.

Akazi a ku Yerusalemu

Khalani maso, inu akazi
    amene mukungokhala wopanda kulingalira kuti kunja kulinji
ndipo imvani mawu anga.
    Inu akazi odzitama, imvani zimene ndikunena!
10 Pakapita chaka ndi masiku pangʼono
    inu akazi amatama mudzanjenjemera;
chifukwa mitengo ya mphesa idzakanika
    ndipo zipatso sizidzaoneka.
11 Nthunthumirani inu okhala mosatekesekanu;
    ndipo njenjemerani, inu akazi omadzikhulupirira nokhanu.
Vulani zovala zanu,
    ndipo valani ziguduli mʼchiwuno mwanu.
12 Dzigugudeni pachifuwa mwachisoni chifukwa minda yachonde,
    ndi mphesa yawonongeka.
13 Mʼdziko la anthu anga
    mwamera minga ndi mkandankhuku.
Zoona, mulilire nyumba zonse zachikondwerero
    ndi mzinda uno umene unali wachisangalalo.
14 Nyumba yaufumu idzasiyidwa,
    mzinda waphokoso udzakhala wopanda anthu;
malinga ndi nsanja zidzasanduka chipululu mpaka muyaya.
    Abulu adzasangalalamo ndipo ziweto zidzapezamo msipu.
15 Yehova adzatipatsa mzimu wake,
    ndipo dziko lachipululu lidzasanduka munda wachonde,
    ndipo munda wachonde udzakhala ngati nkhalango.
16 Tsono mʼchipululu mudzakhala chiweruzo cholungama
    ndipo mʼminda yachonde mudzakhala chilungamo.
17 Mtendere udzakhala chipatso chachilungamo;
    zotsatira za chilungamo zidzakhala bata ndi kudzidalira mpaka muyaya.
18 Anthu anga adzakhala mʼmidzi yamtendere,
    mʼnyumba zodalirika,
    ndi malo osatekeseka a mpumulo.
19 Ngakhale nkhalango idzawonongedwa ndi matalala
    ndipo mzinda udzagwetsedwa mpaka pansi,
20 inutu mudzakhala odalitsika ndithu.
    Mudzadzala mbewu zanu mʼmbali mwa mtsinje uliwonse,
    ndipo ngʼombe zanu ndi abulu anu zidzadya paliponse.

The Kingdom of Righteousness

32 See, a king(A) will reign in righteousness
    and rulers will rule with justice.(B)
Each one will be like a shelter(C) from the wind
    and a refuge from the storm,(D)
like streams of water(E) in the desert(F)
    and the shadow of a great rock in a thirsty land.

Then the eyes of those who see will no longer be closed,(G)
    and the ears(H) of those who hear will listen.
The fearful heart will know and understand,(I)
    and the stammering tongue(J) will be fluent and clear.
No longer will the fool(K) be called noble
    nor the scoundrel be highly respected.
For fools speak folly,(L)
    their hearts are bent on evil:(M)
They practice ungodliness(N)
    and spread error(O) concerning the Lord;
the hungry they leave empty(P)
    and from the thirsty they withhold water.
Scoundrels use wicked methods,(Q)
    they make up evil schemes(R)
to destroy the poor with lies,
    even when the plea of the needy(S) is just.(T)
But the noble make noble plans,
    and by noble deeds(U) they stand.(V)

The Women of Jerusalem

You women(W) who are so complacent,
    rise up and listen(X) to me;
you daughters who feel secure,(Y)
    hear what I have to say!
10 In little more than a year(Z)
    you who feel secure will tremble;
the grape harvest will fail,(AA)
    and the harvest of fruit will not come.
11 Tremble,(AB) you complacent women;
    shudder, you daughters who feel secure!(AC)
Strip off your fine clothes(AD)
    and wrap yourselves in rags.(AE)
12 Beat your breasts(AF) for the pleasant fields,
    for the fruitful vines(AG)
13 and for the land of my people,
    a land overgrown with thorns and briers(AH)
yes, mourn(AI) for all houses of merriment
    and for this city of revelry.(AJ)
14 The fortress(AK) will be abandoned,
    the noisy city deserted;(AL)
citadel and watchtower(AM) will become a wasteland forever,
    the delight of donkeys,(AN) a pasture for flocks,(AO)
15 till the Spirit(AP) is poured on us from on high,
    and the desert becomes a fertile field,(AQ)
    and the fertile field seems like a forest.(AR)
16 The Lord’s justice(AS) will dwell in the desert,(AT)
    his righteousness(AU) live in the fertile field.
17 The fruit of that righteousness(AV) will be peace;(AW)
    its effect will be quietness and confidence(AX) forever.
18 My people will live in peaceful(AY) dwelling places,
    in secure homes,(AZ)
    in undisturbed places of rest.(BA)
19 Though hail(BB) flattens the forest(BC)
    and the city is leveled(BD) completely,
20 how blessed you will be,
    sowing(BE) your seed by every stream,(BF)
    and letting your cattle and donkeys range free.(BG)