Yesaya 33
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Msautso ndi Thandizo
33 Tsoka kwa iwe, iwe wowonongawe,
amene sunawonongedwepo!
Tsoka kwa iwe, iwe mthirakuwiri,
iwe amene sunanyengedwepo!
Iwe ukadzaleka kuwononga,
udzawonongedwa,
ukadzasiya umʼthirakuwiri, adzakuwononga,
ndipo ukadzaleka kuchita zachinyengo adzakunyenga.
2 Inu Yehova, mutikomere mtima ife;
tikulakalaka Inu.
Tsiku ndi tsiku mutitchinjirize ndi mkono wanu,
ndipo mutipulumutse pa nthawi ya masautso.
3 Mukatulutsa liwu lanu longa bingu mitundu ya anthu imathawa;
pamene Inu mwadzambatuka mitundu ya anthu imabalalika.
4 Zofunkha za ku nkhondo za mitundu ina Aisraeli adzazisonkhanitsa ngati mmene limachitira dzombe.
Iwo adzalumphira zofunkhazo monga mmene limachitira dzombe.
5 Yehova wakwezeka kwambiri pakuti amakhala pamwamba pa zonse
adzadzaza Ziyoni ndi chilungamo ndi chipulumutso.
6 Iye adzakupatsani mtendere pa nthawi yanu,
adzakupatsani chipulumutso chochuluka, nzeru zambiri ndi chidziwitso chochuluka;
kuopa Yehova ngati madalitso.
7 Taonani, anthu awo amphamvu akulira mofuwula mʼmisewu;
akazembe okhazikitsa mtendere akulira kwambiri.
8 Mʼmisewu yayikulu mulibe anthu,
mʼmisewu mulibe anthu a paulendo.
Mdaniyo ndi wosasunga pangano.
Iye amanyoza mboni.
Palibe kulemekezana.
9 Dziko likulira ndipo likunka likutha.
Nkhalango ya Lebanoni ikuchita manyazi, yafota.
Chigwa cha chonde cha Saroni chasanduka chachidalala.
Masamba a mitengo ya ku Basani ndi Karimeli akuyoyoka.
10 Yehova akunena kuti, “Tsopano ndidzadzambatuka
ndipo ndidzaonetsa mphamvu zanga,
ndipo ndidzakwezedwa.
11 Zolingalira zanu nʼzachabechabe
ngati udzu wamanyowa.
Mpweya wamoto udzakupserezani.
12 Anthu a mitundu ina adzatenthedwa ngati miyala ya njereza;
ndi ngati minga yodulidwa.”
13 Inu amene muli kutali, imvani zimene ndachita;
inu amene muli pafupi, dziwani mphamvu zanga
14 Mu mzinda wa Ziyoni anthu ochimwa agwidwa ndi mantha;
anthu osapembedza Mulungu akunjenjemera:
Iwo akunena kuti, “Ndani wa ife angathe kukhala mʼmoto wonyeketsa?
Ndani wa ife angathe kukhala moto wosatha?”
15 Angathe kuti ndi amene amachita zolungama
ndi kuyankhula zoona,
amene amakana phindu lolipeza monyenga
ndipo salola manja ake kulandira ziphuphu,
amene amatseka makutu ake kuti angamve mawu opangana kupha anzawo
ndipo amatsinzina kuti angaone zoyipa.
16 Munthu wotere ndiye adzakhale pa nsanja,
kothawira kwake kudzakhala mʼmalinga a mʼmapiri.
Azidzalandira chakudya chake
ndipo madzi sadzamusowa.
17 Nthawi imeneyo maso a ana adzaona mfumu ya maonekedwe wokongola
ndi kuona dziko lotambasukira kutali.
18 Mu mtima mwanu muzidzalingalira zoopsa zinachitika kale zija:
“Ali kuti mkulu wa Asilikali uja?
Ali kuti wokhometsa misonkho uja?
Ali kuti mkulu woyangʼanira nsanja?”
19 Simudzawaonanso anthu odzikuza aja,
anthu aja achiyankhulo chosadziwika,
chachilendo ndi chosamveka.
20 Taonani Ziyoni, mzinda wa zikondwerero zachipembedzo chathu;
maso anu adzaona Yerusalemu,
mzinda wamtendere, tenti imene sidzachotsedwa,
zikhomo zake sizidzazulidwa,
kapena zingwe zake kuduka.
21 Kumeneko Yehova adzaonetsa ulemerero wake
ndipo mzindawo udzakhala kasupe wa mitsinje yayikulu.
Ngalawa za zopalasa sizidzapitamo,
sitima zapamadzi zikuluzikulu sizidzayendamo.
22 Pakuti Yehova ndi woweruza wathu,
Yehova ndiye wotilamulira,
Yehova ndiye mfumu yathu;
ndipo ndiye amene adzatipulumutse.
23 Zingwe za sitima zapamadzi za adani athu zamasuka,
sizikutha kulimbitsa mlongoti wake,
matanga ake sakutheka kutambasuka.
Ngakhale tidzagawana zofunkha zochuluka kwambiri
ndipo ngakhale olumala adzatenga zofunkhazo.
24 Palibe ndi mmodzi yemwe wokhala mʼZiyoni adzanene kuti, “Ndikudwala”
ndipo anthu onse okhala mʼmenemo machimo awo adzakhululukidwa.
Isaiah 33
New International Version
Distress and Help
33 Woe(A) to you, destroyer,
you who have not been destroyed!
Woe to you, betrayer,
you who have not been betrayed!
When you stop destroying,
you will be destroyed;(B)
when you stop betraying,
you will be betrayed.(C)
2 Lord, be gracious(D) to us;
we long for you.
Be our strength(E) every morning,
our salvation(F) in time of distress.(G)
3 At the uproar of your army,(H) the peoples flee;(I)
when you rise up,(J) the nations scatter.
4 Your plunder,(K) O nations, is harvested(L) as by young locusts;(M)
like a swarm of locusts people pounce on it.
5 The Lord is exalted,(N) for he dwells on high;(O)
he will fill Zion with his justice(P) and righteousness.(Q)
6 He will be the sure foundation for your times,
a rich store of salvation(R) and wisdom and knowledge;
the fear(S) of the Lord is the key to this treasure.[a](T)
7 Look, their brave men(U) cry aloud in the streets;
the envoys(V) of peace weep bitterly.
8 The highways are deserted,
no travelers(W) are on the roads.(X)
The treaty is broken,(Y)
its witnesses[b] are despised,
no one is respected.
9 The land dries up(Z) and wastes away,
Lebanon(AA) is ashamed and withers;(AB)
Sharon(AC) is like the Arabah,
and Bashan(AD) and Carmel(AE) drop their leaves.
10 “Now will I arise,(AF)” says the Lord.
“Now will I be exalted;(AG)
now will I be lifted up.
11 You conceive(AH) chaff,
you give birth(AI) to straw;
your breath is a fire(AJ) that consumes you.
12 The peoples will be burned to ashes;(AK)
like cut thornbushes(AL) they will be set ablaze.(AM)”
13 You who are far away,(AN) hear(AO) what I have done;
you who are near, acknowledge my power!
14 The sinners(AP) in Zion are terrified;
trembling(AQ) grips the godless:
“Who of us can dwell with the consuming fire?(AR)
Who of us can dwell with everlasting burning?”
15 Those who walk righteously(AS)
and speak what is right,(AT)
who reject gain from extortion(AU)
and keep their hands from accepting bribes,(AV)
who stop their ears against plots of murder
and shut their eyes(AW) against contemplating evil—
16 they are the ones who will dwell on the heights,(AX)
whose refuge(AY) will be the mountain fortress.(AZ)
Their bread will be supplied,
and water will not fail(BA) them.
17 Your eyes will see the king(BB) in his beauty(BC)
and view a land that stretches afar.(BD)
18 In your thoughts you will ponder the former terror:(BE)
“Where is that chief officer?
Where is the one who took the revenue?
Where is the officer in charge of the towers?(BF)”
19 You will see those arrogant people(BG) no more,
people whose speech is obscure,
whose language is strange and incomprehensible.(BH)
20 Look on Zion,(BI) the city of our festivals;
your eyes will see Jerusalem,
a peaceful abode,(BJ) a tent(BK) that will not be moved;(BL)
its stakes will never be pulled up,
nor any of its ropes broken.
21 There the Lord will be our Mighty(BM) One.
It will be like a place of broad rivers and streams.(BN)
No galley with oars will ride them,
no mighty ship(BO) will sail them.
22 For the Lord is our judge,(BP)
the Lord is our lawgiver,(BQ)
the Lord is our king;(BR)
it is he who will save(BS) us.
Footnotes
- Isaiah 33:6 Or is a treasure from him
- Isaiah 33:8 Dead Sea Scrolls; Masoretic Text / the cities
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.