Add parallel Print Page Options

Kudwala kwa Hezekiya

38 Nthawi imeneyo Mfumu Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Mneneri Yesaya mwana wa Amozi anapita kukamuona ndipo anati “Yehova akuti: Konza bwino nyumba yako, pakuti ukufa; suchira.”

Hezekiya anatembenuka nayangʼana kukhoma, napemphera kwa Yehova kuti, “Inu Yehova, kumbukirani momwe ndayendera pamaso panu mokhulupirika ndi modzipereka ndipo ndakhala ndikuchita zabwino pamaso panu.” Ndipo Hezekiya analira mosweka mtima.

Ndipo Yehova analamula Yesaya kuti: “Pita kwa Hezekiya ndipo ukamuwuze kuti, ‘Yehova, Mulungu wa kholo lake Davide akuti: Ndamva pemphero lako ndipo misozi yako ndayiona; ndidzakuwonjezera zaka 15 pa moyo wako. Ndipo ndidzakupulumutsa, iwe pamodzi ndi mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya, Ine ndidzawuteteza mzindawu.

“ ‘Ichi ndi chizindikiro cha Yehova kwa iwe kutsimikiza kuti Yehova adzachita zimene walonjeza: Chithunzithunzi chimene dzuwa likuchititsa pa makwerero a Ahazi ndidzachibweza mʼmbuyo makwerero khumi.’ ” Ndipo chithunzithunzi chinabwerera mʼmbuyo makwerero khumi.

Ndakatulo ya Hezekiya mfumu ya ku Yuda imene analemba atadwala ndi kuchira:

10 Ine ndinaganiza kuti
    ndidzapita ku dziko la akufa
    pamene moyo ukukoma.
11 Ndinaganiza kuti, “Sindidzaonanso Yehova,
    mʼdziko la anthu amoyo,
sindidzaonanso mtundu wa anthu
    kapena kukhala pamodzi ndi amene amakhala pa dziko lapansi lino.
12 Nyumba yanga yasasuka
    ndipo yachotsedwa.
Ngati tenti ya mʼbusa mwapindapinda moyo wanga,
    ngati munthu wowomba nsalu;
    kuyambira usana mpaka usiku mwakhala mukundisiya.
13 Ndinkalira kupempha chithandizo usiku wonse mpaka mmawa;
    koma Inu Yehova munaphwanya mafupa anga ngati mkango,
    ndipo mwakhala mukundisiya.
14 Ndinkalira ngati namzeze kapena chumba,
    ndinkabuwula ngati nkhunda yodandaula.
Maso anga anatopa nʼkuyangʼana mlengalenga.
    Inu Ambuye, ine ndili mʼmavuto bwerani mudzandithandize!”

15 Koma ine ndinganene chiyani?
    Yehova wayankhula nane, ndipo Iye ndiye wachita zimenezi.
Chifukwa cha kuwawa kwa mtima wanga,
    ine ndidzayenda modzichepetsa masiku amoyo wanga onse.
16 Ambuye, masiku anga ali mʼmanja mwanu.
    Mzimu wanga upeza moyo mwa Inu.
Munandichiritsa ndi
    kundikhalitsa ndi moyo.
17 Ndithudi, ine ndinamva zowawa zotere
    kuti ndikhale ndi moyo;
Inu munandisunga
    kuti ndisapite ku dzenje la chiwonongeko
chifukwa mwakhululukira
    machimo anga onse.
18 Pakuti akumanda sangathe kukutamandani,
    akufa sangayimbe nyimbo yokutamandani.
Iwo amene akutsikira ku dzenje
    sangakukhulupirireni.
19 Amoyo, amoyo okha ndiwo amakutamandani,
    monga mmene ndikuchitira ine lero lino;
abambo amawuza ana awo za
    kukhulupirika kwanu.

20 Yehova watipulumutsa.
    Tiyeni tiyimbe ndi zoyimbira za zingwe
masiku onse a moyo wathu
    mʼNyumba ya Yehova.

21 Yesaya anati, “Anthu atenge mʼbulu wankhunyu ndipo apake pa chithupsacho ndipo Hezekiya adzachira.”

22 Hezekiya nʼkuti atafunsa kuti, “Kodi chizindikiro chako nʼchiyani chotsimikiza kuti ndidzapita ku Nyumba ya Yehova?”

Hezekiah’s Illness(A)

38 In those days Hezekiah became ill and was at the point of death. The prophet Isaiah son of Amoz(B) went to him and said, “This is what the Lord says: Put your house in order,(C) because you are going to die; you will not recover.”(D)

Hezekiah turned his face to the wall and prayed to the Lord, “Remember, Lord, how I have walked(E) before you faithfully and with wholehearted devotion(F) and have done what is good in your eyes.(G)” And Hezekiah wept(H) bitterly.

Then the word(I) of the Lord came to Isaiah: “Go and tell Hezekiah, ‘This is what the Lord, the God of your father David,(J) says: I have heard your prayer and seen your tears;(K) I will add fifteen years(L) to your life. And I will deliver you and this city from the hand of the king of Assyria. I will defend(M) this city.

“‘This is the Lord’s sign(N) to you that the Lord will do what he has promised: I will make the shadow cast by the sun go back the ten steps it has gone down on the stairway of Ahaz.’” So the sunlight went back the ten steps it had gone down.(O)

A writing of Hezekiah king of Judah after his illness and recovery:

10 I said, “In the prime of my life(P)
    must I go through the gates of death(Q)
    and be robbed of the rest of my years?(R)
11 I said, “I will not again see the Lord himself(S)
    in the land of the living;(T)
no longer will I look on my fellow man,
    or be with those who now dwell in this world.
12 Like a shepherd’s tent(U) my house
    has been pulled down(V) and taken from me.
Like a weaver I have rolled(W) up my life,
    and he has cut me off from the loom;(X)
    day and night(Y) you made an end of me.
13 I waited patiently(Z) till dawn,
    but like a lion he broke(AA) all my bones;(AB)
    day and night(AC) you made an end of me.
14 I cried like a swift or thrush,
    I moaned like a mourning dove.(AD)
My eyes grew weak(AE) as I looked to the heavens.
    I am being threatened; Lord, come to my aid!”(AF)

15 But what can I say?(AG)
    He has spoken to me, and he himself has done this.(AH)
I will walk humbly(AI) all my years
    because of this anguish of my soul.(AJ)
16 Lord, by such things people live;
    and my spirit finds life in them too.
You restored me to health
    and let me live.(AK)
17 Surely it was for my benefit(AL)
    that I suffered such anguish.(AM)
In your love you kept me
    from the pit(AN) of destruction;
you have put all my sins(AO)
    behind your back.(AP)
18 For the grave(AQ) cannot praise you,
    death cannot sing your praise;(AR)
those who go down to the pit(AS)
    cannot hope for your faithfulness.
19 The living, the living—they praise(AT) you,
    as I am doing today;
parents tell their children(AU)
    about your faithfulness.

20 The Lord will save me,
    and we will sing(AV) with stringed instruments(AW)
all the days of our lives(AX)
    in the temple(AY) of the Lord.

21 Isaiah had said, “Prepare a poultice of figs and apply it to the boil, and he will recover.”

22 Hezekiah had asked, “What will be the sign(AZ) that I will go up to the temple of the Lord?”