Add parallel Print Page Options

Mtumiki wa Yehova

42 “Nayu mtumiki wanga, amene ndimamuchirikiza,
    amene ndamusankha, amenenso ndimakondwera naye.
Ndayika Mzimu wanga mwa Iyeyo,
    ndipo adzaweruza anthu a mitundu yonse mwachilungamo.
Iye sadzafuwula, sadzamveka mawu,
    kapena mawu ake kumveka mʼmisewu.
Bango lophwanyika sadzalithyola,
    ndipo moto wozilala sadzawuzimitsa.
Motero adzaonetsa kuti chilungamo ndicho choonadi;
    sadzafowoka kapena kukhumudwa
mpaka atakhazikitsa chilungamo pa dziko lapansi,
    ndi mpaka mayiko a mʼmbali mwa nyanja atafika poyembekezera malangizo ake.”

Yehova Mulungu
amene analenga zamlengalenga ndi kuziyalika,
    amene analenga dziko lapansi ndi zonse zimene zimabereka,
amenenso amapereka mpweya kwa anthu ake okhala mʼdzikomo,
    ndi moyo kwa onse oyendamo, akuti,
“Ine Yehova, ndakuyitana chifukwa Ine ndine wolungama;
    ndikugwira dzanja ndipo
ndidzakuteteza.
    Ndakupereka kukhala pangano langa kwa anthu
    ndi kuwunika kwa anthu a mitundu ina.
Udzatsekula maso a anthu osaona,
    udzamasula anthu a mʼndende
    ndi kutulutsa mʼndende anthu okhala mu mdima.

“Ine ndine Yehova: dzina langa ndi limenelo!
    Sindidzapereka ulemerero wanga kwa wina aliyense
    kapena matamando anga kwa mafano.
Taonani, zinthu zimene ndinalosera kale zachitikadi,
    ndipo ndikuwuzani zinthu zatsopano;
zinthuzo zisanaonekere
    Ine ndakudziwitsani.”

Nyimbo Yotamanda Yehova

10 Imbirani Yehova nyimbo yatsopano,
    mutamandeni inu okhala mʼdziko lonse lapansi,
inu amene mumayenda pa nyanja, nyanja ikokome ndi zonse zili mʼmenemo.
    Inu okhala pa zilumba tamandani Yehova.
11 Chipululu ndi mizinda yake zikweze mawu awo;
    midzi ya Akedara ikondwere.
Anthu a ku Sela ayimbe mwachimwemwe;
    afuwule kuchokera pamwamba pa mapiri.
12 Atamande Yehova
    ndipo alalike matamando ake kwa anthu apazilumba zonse.
13 Yehova adzapita ku nkhondo ngati munthu wamphamvu,
    adzawutsa ukali wake ngati munthu wankhondo;
akukuwa ndiponso akufuwula mfuwu wankhondo
    ndipo adzagonjetsa adani ake.

14 Yehova akuti, “Ndakhala ndili chete kwa nthawi yayitali,
    ndakhala ndili phee osachita kanthu.
Koma tsopano, ngati mayi pa nthawi yochira,
    ndi kubuwula ndi kupuma modukizadukiza ndipo ndili wefuwefu.
15 Ndidzawononga mapiri ndi zitunda
    ndipo ndidzawumitsa zomera zawo zonse;
ndidzasandutsa mitsinje kukhala zilumba
    ndipo ndidzawumitsa maiwe.
16 Ndidzatsogolera anthu osaona mʼmisewu imene sanayidziwe,
    ndidzawatsogolera mʼnjira zimene sanayendepo;
ndidzasandutsa mdima wa kutsogolo kwawo kuti ukhale kuwala
    ndipo ndidzasalaza malo osalala.
Zimenezi ndizo ndidzachite;
    sindidzawataya.
17 Koma onse amene amadalira mafano
    amene amanena kwa mafanowo kuti, ‘ndinu milungu yathu,’
    ndidzawachititsa manyazi kotheratu.

Aisraeli Alephera Kuphunzira

18 “Imvani, agonthi inu;
yangʼanani osaona inu, kuti muone! 19     Ali wosaona ndani, si mtumiki wanga kodi?
    Ndipo ndani ali wosamva ngati mthenga amene ndamutuma?
Kodi ndani ali wosaona ngati uja ndinachita naye pangano,
    kapena wosaona ndani ngati mtumiki wa Yehova?
20 Iwe waona zinthu zambiri, koma sunazisamale;
    makutu ako ndi otsekuka koma sumva kanthu.”
21 Chinamukomera Yehova
    chifukwa cha chilungamo chake,
    kapena lamulo lake kukhala lalikulu ndi lopambana.
22 Koma awa ndi anthu amene afunkhidwa ndi kuwalanda zinthu zawo,
    onsewa anawakola mʼmaenje
    kapena akuwabisa mʼndende.
Tsono asanduka chofunkha
    popanda wina wowapulumutsa
kapena kunena kuti,
    “Abwezeni kwawo.”

23 Kodi ndani wa inu amene adzamvetsera zimenezi
    kapena kutchera khutu ndi kumva za mʼtsogolomo?
24 Ndani anapereka Yakobo kwa ofunkha,
    ndi Israeli kwa anthu akuba?
Kodi si Yehova,
    amene ife tamuchimwirayu?
Pakuti sanathe kutsatira njira zake;
    ndipo sanamvere malangizo ake.
25 Motero anawakwiyira kwambiri,
    nawavutitsa ndi nkhondo.
Anayatsa moto ponseponse mowazungulira komabe iwo sanamvetse;
    motowo unawapsereza, koma iwo sanatengepo phunziro ayi.

The Servant of the Lord

42 “Here is my servant,(A) whom I uphold,
    my chosen one(B) in whom I delight;(C)
I will put my Spirit(D) on him,
    and he will bring justice(E) to the nations.(F)
He will not shout or cry out,(G)
    or raise his voice in the streets.
A bruised reed(H) he will not break,(I)
    and a smoldering wick he will not snuff out.(J)
In faithfulness he will bring forth justice;(K)
    he will not falter or be discouraged
till he establishes justice(L) on earth.
    In his teaching(M) the islands(N) will put their hope.”(O)

This is what God the Lord says—
the Creator of the heavens,(P) who stretches them out,
    who spreads out the earth(Q) with all that springs from it,(R)
    who gives breath(S) to its people,
    and life to those who walk on it:
“I, the Lord, have called(T) you in righteousness;(U)
    I will take hold of your hand.(V)
I will keep(W) you and will make you
    to be a covenant(X) for the people
    and a light(Y) for the Gentiles,(Z)
to open eyes that are blind,(AA)
    to free(AB) captives from prison(AC)
    and to release from the dungeon those who sit in darkness.(AD)

“I am the Lord;(AE) that is my name!(AF)
    I will not yield my glory to another(AG)
    or my praise to idols.(AH)
See, the former things(AI) have taken place,
    and new things I declare;
before they spring into being
    I announce(AJ) them to you.”

Song of Praise to the Lord

10 Sing(AK) to the Lord a new song,(AL)
    his praise(AM) from the ends of the earth,(AN)
you who go down to the sea, and all that is in it,(AO)
    you islands,(AP) and all who live in them.
11 Let the wilderness(AQ) and its towns raise their voices;
    let the settlements where Kedar(AR) lives rejoice.
Let the people of Sela(AS) sing for joy;
    let them shout from the mountaintops.(AT)
12 Let them give glory(AU) to the Lord
    and proclaim his praise(AV) in the islands.(AW)
13 The Lord will march out like a champion,(AX)
    like a warrior(AY) he will stir up his zeal;(AZ)
with a shout(BA) he will raise the battle cry
    and will triumph over his enemies.(BB)

14 “For a long time I have kept silent,(BC)
    I have been quiet and held myself back.(BD)
But now, like a woman in childbirth,
    I cry out, I gasp and pant.(BE)
15 I will lay waste(BF) the mountains(BG) and hills
    and dry up all their vegetation;
I will turn rivers into islands
    and dry up(BH) the pools.
16 I will lead(BI) the blind(BJ) by ways they have not known,
    along unfamiliar paths I will guide them;
I will turn the darkness into light(BK) before them
    and make the rough places smooth.(BL)
These are the things I will do;
    I will not forsake(BM) them.
17 But those who trust in idols,
    who say to images, ‘You are our gods,’(BN)
    will be turned back in utter shame.(BO)

Israel Blind and Deaf

18 “Hear, you deaf;(BP)
    look, you blind, and see!
19 Who is blind(BQ) but my servant,(BR)
    and deaf like the messenger(BS) I send?
Who is blind like the one in covenant(BT) with me,
    blind like the servant of the Lord?
20 You have seen many things, but you pay no attention;
    your ears are open, but you do not listen.”(BU)
21 It pleased the Lord
    for the sake(BV) of his righteousness
    to make his law(BW) great and glorious.
22 But this is a people plundered(BX) and looted,
    all of them trapped in pits(BY)
    or hidden away in prisons.(BZ)
They have become plunder,
    with no one to rescue them;(CA)
they have been made loot,
    with no one to say, “Send them back.”

23 Which of you will listen to this
    or pay close attention(CB) in time to come?
24 Who handed Jacob over to become loot,
    and Israel to the plunderers?(CC)
Was it not the Lord,(CD)
    against whom we have sinned?
For they would not follow(CE) his ways;
    they did not obey his law.(CF)
25 So he poured out on them his burning anger,(CG)
    the violence of war.
It enveloped them in flames,(CH) yet they did not understand;(CI)
    it consumed them, but they did not take it to heart.(CJ)