Add parallel Print Page Options

Chipulumutso Chamuyaya cha Ziyoni

51 “Mverani Ine, inu amene mukufuna chipulumutso
    ndiponso amene mumafunafuna Yehova:
Taganizani za thanthwe kumene munasemedwa
    ndipo ku ngwenya kumene anakukumbani;
taganizani za Abrahamu, kholo lanu,
    ndi Sara, amene anakubalani.
Pamene ndinkamuyitana nʼkuti alibe mwana,
    koma ndinamudalitsa ndi kumupatsa ana ambiri.
Yehova adzatonthozadi Ziyoni,
    ndipo adzachitira chifundo mabwinja ake onse;
Dziko lake la chipululu adzalisandutsa ngati Edeni,
    malo ake owuma ngati munda wa Yehova.
Anthu adzayimba nyimbo zonditamanda
    ndi kundiyamika.

“Mverani Ine, anthu anga:
    tcherani khutu, inu mtundu wanga:
malangizo adzachokera kwa Ine;
    cholungama changa chidzawunikira anthu a mitundu yonse.
Ndili pafupi kubwera kudzawombola anthu anga.
    Ndidzabwera mofulumira ngati kuwunika kudzapulumutsa anthu anga;
    ndipo ndidzalamulira anthu a mitundu yonse.
Mayiko akutali akundiyembekezera.
    Iwo akudikira kuti ndidzawapulumutse.
Kwezani maso anu mlengalenga,
    yangʼanani pansi pa dziko;
mlengalenga udzazimirira ngati utsi,
    dziko lapansi lidzatha ngati chovala
    ndipo anthu ake adzafa ngati nsabwe.
Koma chipulumutso changa chidzakhala mpaka muyaya,
    chilungamo changa chidzakhala cha nthawi zonse.

“Mverani Ine, inu amene mukudziwa choonadi,
    anthu inu amene mukusunga malangizo anga mʼmitima yanu;
musaope kudzudzulidwa ndi anthu
    kapena kuopsezedwa akamakulalatirani.
Pakuti njenjete idzawadya ngati chovala;
    mbozi idzawadya ngati thonje.
Koma chilungamo changa chidzakhala mpaka muyaya,
    chipulumutso changa chidzakhala mpaka mibadomibado.”

Dzambatukani, dzambatukani! Valani zilimbe,
    Inu Yehova;
dzambatukani, monga munkachitira masiku amakedzana,
    monga nthawi ya mibado yakale.
Si ndinu kodi amene munaduladula Rahabe,
    amene munabaya chinjoka cha mʼnyanja chija?
10 Kodi sindinu amene munawumitsa nyanja yayikulu,
    madzi ozama kwambiri aja?
Kodi sindinu amene munapanga njira pa madzi ozama,
    kuti anthu amene munawapulumutsa awoloke powuma?
11 Anthu amene Yehova anawawombola adzabwerera
    nakafika ku Ziyoni nyimbo ili pakamwa;
    chimwemwe chamuyaya chizidzaonekera pa nkhope zawo.
Adzakhala ndi chikondwerero ndi chimwemwe,
    chisoni ndi kubuwula zidzathawa.

12 Yehova akuti, “Ndinetu amene ndimakutonthozani mtima.
    Chifukwa chiyani mukuopa munthu woti adzafa?
    Mukuopa munthu woti monga udzu sadzakhalitsa.
13 Koma inu mumayiwala Yehova Mlengi wanu,
    amene anayala za mlengalenga
    ndi kuyika maziko a dziko lapansi.
Inu nthawi zonse mumaopsezedwa
    chifukwa cha ukali wa anthu okuponderezani
    amene angofuna kukuwonongani.
Kodi uli kuti tsopano ukali wa anthu okuponderezaniwo?
14     Amʼndende adzamasulidwa posachedwa;
sadzalowa mʼmanda awo,
    kapena kusowa chakudya.
15 Pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu,
    amene ndimavundula nyanja kotero mafunde ake amakokoma.
    Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
16 Ndayika mawu anga mʼkamwa mwanu
    ndipo ndakuphimbani ndi mthunzi wa dzanja langa.
Ine ndimayika pa malo pake zinthu za mlengalenga,
    ndipo ndinayika maziko a dziko lapansi,
    ndimawuza anthu a ku Ziyoni kuti, ‘Ndinu anthu anga.’ ”

Kutha kwa Mavuto A Yerusalemu

17 Dzambatuka, dzambatuka!
    Imirira iwe Yerusalemu.
Iwe amene wamwa chikho cha mkwiyo
    chimene Yehova anakupatsa.
Iwe amene unagugudiza
    chikho chochititsa chizwezwe.
18 Mwa ana onse amene anabereka,
    panalibe ndi mmodzi yemwe anamutsogolera;
mwa ana onse amene analera,
    panalibe ndi mmodzi yemwe anamugwira dzanja.
19 Mavuto awiriwa akugwera iwe.
    Dziko lako lasakazika ndi kuwonongeka. Anthu afa ndi njala ndi lupanga.
Ndani angakumvere chisoni?
    Ndani angakutonthoze?
20 Ana ako akomoka;
    ali lambalamba pa msewu,
    ngati mphoyo yogwidwa mu ukonde.
Ukali wa Yehova
    ndi chidzudzulo chake zidzawagwera.

21 Nʼchifukwa chake imva izi iwe amene ukuvutika,
    iwe amene waledzera, koma osati ndi vinyo.
22 Ambuye Yehova wanu,
    Mulungu amene amateteza anthu ake akuti,
“Taona, ndachotsa mʼdzanja lako
    chikho chimene chimakuchititsa kudzandira;
sudzamwanso chikho
    cha ukali wanga.
23 Ndidzapereka chikhocho kwa anthu amene amakuzunza,
    amene ankakuwuza kuti,
    ‘gona pansi tikuyende pa msana.’
Ndipo msana wako anawuyesa pansi popondapo,
    ngati msewu woti ayendepo.”

Everlasting Salvation for Zion

51 “Listen(A) to me, you who pursue righteousness(B)
    and who seek(C) the Lord:
Look to the rock(D) from which you were cut
    and to the quarry from which you were hewn;
look to Abraham,(E) your father,
    and to Sarah, who gave you birth.
When I called him he was only one man,
    and I blessed him and made him many.(F)
The Lord will surely comfort(G) Zion(H)
    and will look with compassion on all her ruins;(I)
he will make her deserts like Eden,(J)
    her wastelands(K) like the garden of the Lord.
Joy and gladness(L) will be found in her,
    thanksgiving(M) and the sound of singing.

“Listen to me, my people;(N)
    hear me,(O) my nation:
Instruction(P) will go out from me;
    my justice(Q) will become a light to the nations.(R)
My righteousness draws near speedily,
    my salvation(S) is on the way,(T)
    and my arm(U) will bring justice to the nations.
The islands(V) will look to me
    and wait in hope(W) for my arm.
Lift up your eyes to the heavens,
    look at the earth beneath;
the heavens will vanish like smoke,(X)
    the earth will wear out like a garment(Y)
    and its inhabitants die like flies.
But my salvation(Z) will last forever,(AA)
    my righteousness will never fail.(AB)

“Hear me, you who know what is right,(AC)
    you people who have taken my instruction to heart:(AD)
Do not fear the reproach of mere mortals
    or be terrified by their insults.(AE)
For the moth will eat them up like a garment;(AF)
    the worm(AG) will devour them like wool.
But my righteousness will last forever,(AH)
    my salvation through all generations.”

Awake, awake,(AI) arm(AJ) of the Lord,
    clothe yourself with strength!(AK)
Awake, as in days gone by,
    as in generations of old.(AL)
Was it not you who cut Rahab(AM) to pieces,
    who pierced that monster(AN) through?
10 Was it not you who dried up the sea,(AO)
    the waters of the great deep,(AP)
who made a road in the depths of the sea(AQ)
    so that the redeemed(AR) might cross over?
11 Those the Lord has rescued(AS) will return.
    They will enter Zion with singing;(AT)
    everlasting joy will crown their heads.
Gladness and joy(AU) will overtake them,
    and sorrow and sighing will flee away.(AV)

12 “I, even I, am he who comforts(AW) you.
    Who are you that you fear(AX) mere mortals,(AY)
    human beings who are but grass,(AZ)
13 that you forget(BA) the Lord your Maker,(BB)
    who stretches out the heavens(BC)
    and who lays the foundations of the earth,
that you live in constant terror(BD) every day
    because of the wrath of the oppressor,
    who is bent on destruction?
For where is the wrath of the oppressor?(BE)
14     The cowering prisoners will soon be set free;(BF)
they will not die in their dungeon,
    nor will they lack bread.(BG)
15 For I am the Lord your God,
    who stirs up the sea(BH) so that its waves roar(BI)
    the Lord Almighty(BJ) is his name.
16 I have put my words in your mouth(BK)
    and covered you with the shadow of my hand(BL)
I who set the heavens in place,
    who laid the foundations of the earth,(BM)
    and who say to Zion, ‘You are my people.(BN)’”

The Cup of the Lord’s Wrath

17 Awake, awake!(BO)
    Rise up, Jerusalem,
you who have drunk from the hand of the Lord
    the cup(BP) of his wrath,(BQ)
you who have drained to its dregs(BR)
    the goblet that makes people stagger.(BS)
18 Among all the children(BT) she bore
    there was none to guide her;(BU)
among all the children she reared
    there was none to take her by the hand.(BV)
19 These double calamities(BW) have come upon you—
    who can comfort you?(BX)
ruin and destruction,(BY) famine(BZ) and sword(CA)
    who can[a] console you?
20 Your children have fainted;
    they lie at every street corner,(CB)
    like antelope caught in a net.(CC)
They are filled with the wrath(CD) of the Lord,
    with the rebuke(CE) of your God.

21 Therefore hear this, you afflicted(CF) one,
    made drunk,(CG) but not with wine.
22 This is what your Sovereign Lord says,
    your God, who defends(CH) his people:
“See, I have taken out of your hand
    the cup(CI) that made you stagger;
from that cup, the goblet of my wrath,
    you will never drink again.
23 I will put it into the hands of your tormentors,(CJ)
    who said to you,
    ‘Fall prostrate(CK) that we may walk(CL) on you.’
And you made your back like the ground,
    like a street to be walked on.”(CM)

Footnotes

  1. Isaiah 51:19 Dead Sea Scrolls, Septuagint, Vulgate and Syriac; Masoretic Text / how can I