Add parallel Print Page Options

53 Ndani wakhulupirira zimene tanenazi;
    kapena ndani amene Yehova wamuzindikiritsa mphamvu zake?
Iye anakula ngati mphukira pamaso pake,
    ndiponso ngati muzu mʼnthaka yowuma.
Iye analibe thupi labwino kapena nkhope yokongola yoti ife nʼkumamuchewukira,
    analibe maonekedwe woti ife nʼkumamukhumbira.
Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu,
    munthu amene moyo wake unali wamasautso, wozolowera zowawa,
ndipo anali ngati munthu amene anzake amaphimba nkhope zawo akamuona.
    Iye ananyozedwa, ndipo ife sitinamuyese kanthu.

Ndithudi, iye anamva zowawa mʼmalo mwa ife;
    ndipo anasautsidwa mʼmalo mwathu.
Koma ife tinkaganiza kuti ndi Mulungu amene akumulanga,
    kumukantha ndi kumusautsa.
Koma iye analasidwa chifukwa cha zolakwa zathu,
    ndipo anamuzunza chifukwa cha zoyipa zathu;
iye analangidwa kuti ife tikhale ndi mtendere,
    ndipo ndi mabala ake ife tinachiritsidwa.
Ife tonse, ngati nkhosa, tasochera,
    aliyense mwa ife akungodziyendera;
ndipo Yehova wamusenzetsa
    zoyipa zathu zonse.

Anthu anamuzunza ndi kumusautsa,
    koma sanayankhule kanthu.
Monga mwana wankhosa wopita naye kokamupha amachitira,
    kapena monga nkhosa imakhalira duu poyimeta,
    momwemonso iye sanatsekule pakamwa pake.
Atatha kumugwira mwankhanza ndikumuyimba mlandu, kenaka anapita naye kukamupha.
    Ndipo ndani amene analabadirako za zidzukulu zake,
poona kuti iye anachotsedwa mʼdziko la anthu amoyo?
    Ndani anaganizirapo poona kuti iye anakanthidwa chifukwa cha zolakwa za anthu anga?
Anamukonzera manda ake pamodzi ndi anthu oyipa
    ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi anthu achuma,
ngakhale kuti iye sanachite za chiwawa,
    kapena kuyankhula za chinyengo.

10 Komatu ndi Yehova amene anafuna kuti amuzunze ndi kumusautsa.
    Yehova anapereka moyo wa mtumiki wake kuti ukhale nsembe yoperekedwa chifukwa cha zolakwa.
Tsono iye adzaona zidzukulu zake ndipo adzakhala ndi moyo wautali,
    ndipo chifuniro cha Yehova chidzachitika mwa iye.
11 Atatha mazunzo a moyo wake,
    adzaona kuwala, ndipo adzakhutira.
Mwa nzeru zake mtumiki wanga wolungamayo adzalungamitsa anthu ambiri,
    popeza adzasenza zolakwa zawo.
12 Motero Ine ndidzamupatsa ulemu pamodzi ndi akuluakulu,
    adzagawana zofunkha ndi ankhondo amphamvu,
popeza anapereka moyo wake mpaka kufa,
    ndipo anamuyika mʼgulu la anthu olakwa kuti akhululukidwe.
Pakuti iye anasenza machimo a anthu ambiri,
    ndipo anawapempherera anthu olakwa.

53 Who has believed our message(A)
    and to whom has the arm(B) of the Lord been revealed?(C)
He grew up before him like a tender shoot,(D)
    and like a root(E) out of dry ground.
He had no beauty or majesty to attract us to him,
    nothing in his appearance(F) that we should desire him.
He was despised and rejected by mankind,
    a man of suffering,(G) and familiar with pain.(H)
Like one from whom people hide(I) their faces
    he was despised,(J) and we held him in low esteem.

Surely he took up our pain
    and bore our suffering,(K)
yet we considered him punished by God,(L)
    stricken by him, and afflicted.(M)
But he was pierced(N) for our transgressions,(O)
    he was crushed(P) for our iniquities;
the punishment(Q) that brought us peace(R) was on him,
    and by his wounds(S) we are healed.(T)
We all, like sheep, have gone astray,(U)
    each of us has turned to our own way;(V)
and the Lord has laid on him
    the iniquity(W) of us all.

He was oppressed(X) and afflicted,
    yet he did not open his mouth;(Y)
he was led like a lamb(Z) to the slaughter,(AA)
    and as a sheep before its shearers is silent,
    so he did not open his mouth.
By oppression[a] and judgment(AB) he was taken away.
    Yet who of his generation protested?
For he was cut off from the land of the living;(AC)
    for the transgression(AD) of my people he was punished.[b]
He was assigned a grave with the wicked,(AE)
    and with the rich(AF) in his death,
though he had done no violence,(AG)
    nor was any deceit in his mouth.(AH)

10 Yet it was the Lord’s will(AI) to crush(AJ) him and cause him to suffer,(AK)
    and though the Lord makes[c] his life an offering for sin,(AL)
he will see his offspring(AM) and prolong his days,
    and the will of the Lord will prosper(AN) in his hand.
11 After he has suffered,(AO)
    he will see the light(AP) of life[d] and be satisfied[e];
by his knowledge[f] my righteous servant(AQ) will justify(AR) many,
    and he will bear their iniquities.(AS)
12 Therefore I will give him a portion among the great,[g](AT)
    and he will divide the spoils(AU) with the strong,[h]
because he poured out his life unto death,(AV)
    and was numbered with the transgressors.(AW)
For he bore(AX) the sin of many,(AY)
    and made intercession(AZ) for the transgressors.

Footnotes

  1. Isaiah 53:8 Or From arrest
  2. Isaiah 53:8 Or generation considered / that he was cut off from the land of the living, / that he was punished for the transgression of my people?
  3. Isaiah 53:10 Hebrew though you make
  4. Isaiah 53:11 Dead Sea Scrolls (see also Septuagint); Masoretic Text does not have the light of life.
  5. Isaiah 53:11 Or (with Masoretic Text) 11 He will see the fruit of his suffering / and will be satisfied
  6. Isaiah 53:11 Or by knowledge of him
  7. Isaiah 53:12 Or many
  8. Isaiah 53:12 Or numerous