Add parallel Print Page Options

Ulemerero Wamʼtsogolo wa Ziyoni

54 “Sangalala, iwe mayi wosabala,
    iwe amene sunabalepo mwana;
imba nyimbo, ndi kufuwula mwachimwemwe,
    iwe amene sunamvepo ululu wa pobereka;
chifukwa mkazi wosiyidwa adzakhala ndi ana ambiri
    kuposa mkazi wokwatiwa,”
            akutero Yehova.
Kulitsa malo omangapo tenti yako,
    tambasula kwambiri nsalu zake,
    usaleke;
talikitsa zingwe zako,
    limbitsa zikhomo zako.
Pakuti udzasendeza malire ako kumanja ndi kumanzere;
    ndipo zidzukulu zako zidzalanda dziko la anthu a mitundu ina
    ndipo zidzakhala mʼmizinda yawo yosiyidwa.

“Usachite mantha; sadzakunyozanso.
    Usakhumudwe; sudzapeputsidwanso.
Udzayiwala za manyazi zimene zinakuchitikira nthawi ya unyamata wako
    ndipo za manyazi zimene zinakuchitikira pa nthawi ya umasiye wako sudzazikumbukanso.
Pakuti Mlengi wako ali ngati mwamuna wako,
    dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wanu;
    dzina lake ndi Mulungu wa dziko lonse lapansi.
Yehova wakuyitananso,
    uli ngati mkazi wosiyidwa ndi wodzaza ndi chisoni mu mtima,
mkazi amene anakwatiwa pa unyamata wake kenaka nʼkukanidwa,”
    akutero Mulungu wako.
“Kwa kanthawi kochepa, Ine ndinakusiya,
    koma ndidzakutenganso chifukwa ndimakukonda kwambiri.
Ndinakufulatira kwa kanthawi kochepa
    ndili wokwiya kwambiri.
Koma ndi kukoma mtima kwanga kwa muyaya,
    ndidzakuchitira chifundo,”
    akutero Yehova Mpulumutsi wako.

“Kwa ine zimenezi zili ngati mmene zinalili mʼnthawi ya Nowa.
    Monga ndinalumbira nthawi imeneyo kuti sindidzawononganso dziko lapansi ndi madzi.
Kotero tsopano ndalumbira kuti sindidzakupseraninso mtima,
    sindidzakudzudzulaninso.
10 Ngakhale mapiri atagwedezeka
    ndi zitunda kusunthidwa,
koma chikondi changa chosasinthika pa iwe sichidzatha.
    Pangano langa lamtendere silidzasintha,”
    akutero Yehova amene amakuchitira chifundo.

11 “Iwe mzinda wozunzika, wokunthidwa ndi namondwe ndiponso wopanda wokutonthoza,
    Ine ndidzakongoletsa miyala yako.
    Maziko ako ndidzamanga ndi miyala ya safiro.
12 Ndidzamanga nsanja zako zankhondo ndi miyala yokongola ya rubi.
    Ndidzamanga zipata zako ndi miyala yonyezimira ngati moto,
    ndipo linga lako lonse lidzakhala la miyala yamtengowapatali.
13 Yehova adzaphunzitsa ana ako onse,
    ndipo ana ako adzakhala ndi mtendere wochuluka.
14 Udzakhazikika mʼchilungamo chenicheni:
Sudzakhalanso wopanikizika,
    chifukwa sudzaopa kanthu kalikonse.
Sudzakhalanso ndi mantha
    chifukwa manthawo sadzafika pafupi ndi iwe.
15 Ngati wina adzakuthirani nkhondo, si ndine amene ndachititsa;
    aliyense amene adzalimbana nanu adzagonja chifukwa cha iwe.

16 “Taona, ndi Ine amene ndinalenga munthu wosula zitsulo
    amene amakoleza moto wamakala
    ndi kusula zida zoti azigwiritse ntchito.
Ndipo ndine amene ndinalenga munthu wosakaza kuti awononge;
17     palibe chida chopangidwa ndi mdani chimene chidzakupweteke,
    ndipo onse okuneneza pa mlandu udzawatsutsa.
Umu ndimo adzapezekere atumiki a Yehova.
    Chipambano chawo chichokera kwa Ine,”
            akutero Yehova.

The Future Glory of Zion

54 “Sing, barren woman,(A)
    you who never bore a child;
burst into song, shout for joy,(B)
    you who were never in labor;(C)
because more are the children(D) of the desolate(E) woman
    than of her who has a husband,(F)
says the Lord.
“Enlarge the place of your tent,(G)
    stretch your tent curtains wide,
    do not hold back;
lengthen your cords,
    strengthen your stakes.(H)
For you will spread out to the right and to the left;
    your descendants(I) will dispossess nations(J)
    and settle in their desolate(K) cities.

“Do not be afraid;(L) you will not be put to shame.(M)
    Do not fear disgrace;(N) you will not be humiliated.
You will forget the shame of your youth(O)
    and remember no more the reproach(P) of your widowhood.(Q)
For your Maker(R) is your husband(S)
    the Lord Almighty is his name—
the Holy One(T) of Israel is your Redeemer;(U)
    he is called the God of all the earth.(V)
The Lord will call you back(W)
    as if you were a wife deserted(X) and distressed in spirit—
a wife who married young,(Y)
    only to be rejected,” says your God.
“For a brief moment(Z) I abandoned(AA) you,
    but with deep compassion(AB) I will bring you back.(AC)
In a surge of anger(AD)
    I hid(AE) my face from you for a moment,
but with everlasting kindness(AF)
    I will have compassion(AG) on you,”
    says the Lord your Redeemer.(AH)

“To me this is like the days of Noah,
    when I swore that the waters of Noah would never again cover the earth.(AI)
So now I have sworn(AJ) not to be angry(AK) with you,
    never to rebuke(AL) you again.
10 Though the mountains be shaken(AM)
    and the hills be removed,
yet my unfailing love(AN) for you will not be shaken(AO)
    nor my covenant(AP) of peace(AQ) be removed,”
    says the Lord, who has compassion(AR) on you.

11 “Afflicted(AS) city, lashed by storms(AT) and not comforted,(AU)
    I will rebuild you with stones of turquoise,[a](AV)
    your foundations(AW) with lapis lazuli.(AX)
12 I will make your battlements of rubies,
    your gates(AY) of sparkling jewels,
    and all your walls of precious stones.
13 All your children will be taught by the Lord,(AZ)
    and great will be their peace.(BA)
14 In righteousness(BB) you will be established:(BC)
Tyranny(BD) will be far from you;
    you will have nothing to fear.(BE)
Terror(BF) will be far removed;
    it will not come near you.
15 If anyone does attack you, it will not be my doing;
    whoever attacks you will surrender(BG) to you.

16 “See, it is I who created the blacksmith(BH)
    who fans the coals into flame
    and forges a weapon(BI) fit for its work.
And it is I who have created the destroyer(BJ) to wreak havoc;
17     no weapon forged against you will prevail,(BK)
    and you will refute(BL) every tongue that accuses you.
This is the heritage of the servants(BM) of the Lord,
    and this is their vindication(BN) from me,”
declares the Lord.

Footnotes

  1. Isaiah 54:11 The meaning of the Hebrew for this word is uncertain.