Add parallel Print Page Options

Chipulumutso kwa Anthu Ena Onse

56 Yehova akuti,

“Chitani chilungamo
    ndi zinthu zabwino,
chifukwa chipulumutso changa chili pafupi
    ndipo ndidzakuwombolani posachedwapa.
Ndi wodala munthu amene amachita zimenezi,
    munthu amene amalimbika kuzichita,
amene amasunga Sabata osaliyipitsa,
    ndipo amadziletsa kuchita zoyipa.”

Mlendo amene waphatikana ndi Yehova asanene kuti,
    “Ndithu Yehova wandichotsa pakati pa anthu ake.”
Ndipo munthu wofulidwa asanene kuti,
    “Ine ndine mtengo wowuma basi.”

Popeza Yehova akuti,

“Wofulidwa amene amasunga masabata anga,
    nachita zokomera Ine
    ndi kusunga pangano langa,
ndidzawapatsa dzina ndi mbiri yabwino
    mʼkati mwa Nyumba yanga ndi makoma ake,
    kuposa kukhala ndi ana aamuna ndi aakazi.
Ndidzawapatsa dzina labwino,
    losatha ndi losayiwalika.”
Yehova akuti, “Alendo amene amadziphatika kwa Yehova,
    motero kuti amamutumikira Iye,
amakonda dzina la Yehova,
    amamugwirira ntchito,
komanso kusunga Sabata osaliyipitsa
    ndi kusunga bwino pangano langa,
amenewa Ine ndidzawafikitsa ku phiri langa lopatulika,
    ndidzawapatsa chimwemwe mʼnyumba yanga ya mapemphero.
Zopereka zawo zopsereza ndi nsembe zawo
    ndidzazilandira pa guwa langa la nsembe.
Paja nyumba yanga idzatchedwa
    nyumba ya mapemphero ya anthu a mitundu yonse.”
Ambuye Yehova, amene amasonkhanitsa
    Aisraeli onse ali ku ukapolo akunena kuti,
“Ndidzasonkhanitsano anthu ena
    kuwonjezera amene anasonkhana kale.”

Mulungu Adzazula Anthu Oyipa

Bwerani, inu zirombo zonse zakuthengo,
    inu nonse zirombo zamʼnkhalango bwerani mudzadye!
10 Atsogoleri onse a Israeli ndi akhungu,
    onse ndi opanda nzeru;
onse ndi agalu opanda mawu,
    samatha kuwuwa:
amagona pansi nʼkumalota
    amakonda kugona tulo.
11 Ali ngati agalu amene ali ndi njala yayikulu;
    sakhuta konse.
Abusa nawonso samvetsa zinthu;
    onse amachita monga akufunira,
    aliyense amafunafuna zomupindulitsa iye mwini.
12 Aliyense amafuwulira mnzake kuti, “Bwera, tiye timwe vinyo!
    Tiyeni timwe mowa mpaka kukhuta!
Mawa lidzakhala ngati leroli,
    kapena kuposa lero lino.”

Salvation for Others

56 This is what the Lord says:

“Maintain justice(A)
    and do what is right,(B)
for my salvation(C) is close at hand
    and my righteousness(D) will soon be revealed.
Blessed(E) is the one who does this—
    the person who holds it fast,
who keeps the Sabbath(F) without desecrating it,
    and keeps their hands from doing any evil.”

Let no foreigner(G) who is bound to the Lord say,
    “The Lord will surely exclude me from his people.”(H)
And let no eunuch(I) complain,
    “I am only a dry tree.”

For this is what the Lord says:

“To the eunuchs(J) who keep my Sabbaths,
    who choose what pleases me
    and hold fast to my covenant(K)
to them I will give within my temple and its walls(L)
    a memorial(M) and a name
    better than sons and daughters;
I will give them an everlasting name(N)
    that will endure forever.(O)
And foreigners(P) who bind themselves to the Lord
    to minister(Q) to him,
to love the name(R) of the Lord,
    and to be his servants,
all who keep the Sabbath(S) without desecrating it
    and who hold fast to my covenant—
these I will bring to my holy mountain(T)
    and give them joy in my house of prayer.
Their burnt offerings and sacrifices(U)
    will be accepted on my altar;
for my house will be called
    a house of prayer for all nations.(V)(W)
The Sovereign Lord declares—
    he who gathers the exiles of Israel:
“I will gather(X) still others to them
    besides those already gathered.”

God’s Accusation Against the Wicked

Come, all you beasts of the field,(Y)
    come and devour, all you beasts of the forest!
10 Israel’s watchmen(Z) are blind,
    they all lack knowledge;(AA)
they are all mute dogs,
    they cannot bark;
they lie around and dream,
    they love to sleep.(AB)
11 They are dogs with mighty appetites;
    they never have enough.
They are shepherds(AC) who lack understanding;(AD)
    they all turn to their own way,(AE)
    they seek their own gain.(AF)
12 “Come,” each one cries, “let me get wine!(AG)
    Let us drink our fill of beer!
And tomorrow will be like today,
    or even far better.”(AH)