Add parallel Print Page Options

64 Inu Yehova, bwanji mukanangongʼamba mlengalenga ndi kutsika pansi,
    kuti mapiri agwedezeke pamaso panu!
Monga momwe moto umatenthera tchire
    ndiponso kuwiritsa madzi,
tsikani kuti adani anu adziwe dzina lanu,
    ndiponso kuti mitundu ya anthu injenjemere pamaso panu.
Pakuti nthawi ina pamene munatsika munachita zinthu zoopsa zimene sitinaziyembekezere,
    ndipo mapiri anagwedezeka pamaso panu.
Chikhalire palibe ndi mmodzi yemwe anamvapo
    kapena kuona
Mulungu wina wonga Inu,
    amene amachitira zinthu zotere amene amadikira pa Iye.
Inu mumabwera kudzathandiza onse amene amakondwera pochita zolungama,
    amene amakumbukira njira zanu.
Koma Inu munakwiya,
    ife tinapitiriza kuchimwa.
    Kodi nanga tingapulumutsidwe bwanji?
Tonsefe takhala ngati anthu amene ndi odetsedwa,
    ndipo ntchito zathu zili ngati sanza za msambo;
tonse tafota ngati tsamba,
    ndipo machimo athu akutiwuluzira kutali ngati mphepo.
Palibe amene amapemphera kwa Inu
    kutekeseka kuti apemphe chithandizo kwa Inu;
pakuti mwatifulatira
    ndi kutisiya chifukwa cha machimo athu.

Komabe, Inu Yehova ndinu Atate athu.
    Ife ndife chowumba, Inu ndinu wowumba;
    ife tonse ndi ntchito ya manja anu.
Inu Yehova, musatikwiyire kopitirira muyeso
    musakumbukire machimo athu mpaka muyaya.
Chonde, mutiganizire, ife tikupempha,
    pakuti tonsefe ndi anthu anu.
10 Mizinda yanu yopatulika yasanduka chipululu;
    ngakhaletu Ziyoni wasanduka chipululu, Yerusalemu ndi wamasiye.
11 Nyumba yanu yopatulika ndi yaulemu, kumene makolo athu ankakutamandani,
    yatenthedwa ndi moto
    ndipo malo onse amene tinkawakonda asanduka bwinja.
12 Inu Yehova, zonse zachitikazi, kodi mungokhala osatithandiza?
    Kodi mudzapitirizabe kukhala chete ndi kutilangabe mopitirira muyeso?

64 [a]Oh, that you would rend the heavens(A) and come down,(B)
    that the mountains(C) would tremble before you!
As when fire sets twigs ablaze
    and causes water to boil,
come down to make your name(D) known to your enemies
    and cause the nations to quake(E) before you!
For when you did awesome(F) things that we did not expect,
    you came down, and the mountains trembled(G) before you.
Since ancient times no one has heard,
    no ear has perceived,
no eye has seen any God besides you,(H)
    who acts on behalf of those who wait for him.(I)
You come to the help of those who gladly do right,(J)
    who remember your ways.
But when we continued to sin against them,
    you were angry.(K)
    How then can we be saved?
All of us have become like one who is unclean,(L)
    and all our righteous(M) acts are like filthy rags;
we all shrivel up like a leaf,(N)
    and like the wind our sins sweep us away.(O)
No one(P) calls on your name(Q)
    or strives to lay hold of you;
for you have hidden(R) your face from us
    and have given us over(S) to[b] our sins.

Yet you, Lord, are our Father.(T)
    We are the clay, you are the potter;(U)
    we are all the work of your hand.(V)
Do not be angry(W) beyond measure, Lord;
    do not remember our sins(X) forever.
Oh, look on us, we pray,
    for we are all your people.(Y)
10 Your sacred cities(Z) have become a wasteland;
    even Zion is a wasteland, Jerusalem a desolation.(AA)
11 Our holy and glorious temple,(AB) where our ancestors praised you,
    has been burned with fire,
    and all that we treasured(AC) lies in ruins.
12 After all this, Lord, will you hold yourself back?(AD)
    Will you keep silent(AE) and punish us beyond measure?

Footnotes

  1. Isaiah 64:1 In Hebrew texts 64:1 is numbered 63:19b, and 64:2-12 is numbered 64:1-11.
  2. Isaiah 64:7 Septuagint, Syriac and Targum; Hebrew have made us melt because of