Add parallel Print Page Options

Za Kulangidwa kwa Mowabu

15 Uthenga wonena za Mowabu:

Popeza kuti mu usiku umodzi wokha mzinda wa Ari wa ku Mowabu wawonongedwa,
    wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.
Mzinda wa Kiri wawonongedwa,
    wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.
Anthu a ku Diboni akupita ku nyumba ya milungu yawo,
    akupita ku malo awo achipembedzo kukalira;
    anthu a ku Mowabu akulirira mofuwula mzinda wa Nebo ndi wa Medeba.
Mutu uliwonse wametedwa mpala,
    ndipo ndevu zonse zametedwa.
Mʼmisewu akuvala ziguduli;
    pa madenga ndi mʼmabwalo
aliyense akulira mofuwula,
    misozi ili pupupu.
Anthu a ku Hesiboni ndi Eleali akulira mofuwula,
    mawu awo akumveka mpaka ku Yahazi.
Kotero asilikali a ku Mowabu akulira mofuwula,
    ndipo ataya mtima.

Inenso ndikulirira Mowabu;
    chifukwa othawa nkhondo ake akupita akulira ku chikweza cha Luluti mpaka ku Zowari
    ndi Egilati-Selisiya
akupita akulira ku chikweza cha Luhiti,
    Akulira mosweka mtima
pa njira yopita ku Horonaimu;
    akulira mosweka mtima chifukwa cha chiwonongeko chawo.
Madzi a ku Nimurimu aphwa
    ndipo udzu wauma;
zomera zawonongeka
    ndipo palibe chomera chobiriwira chatsala.
Kotero kuti chuma chomwe anachipeza ndi kuchisunga,
    achitenga kuti awoloke nacho chigwembe cha Misondozi.
Kulira kwawo kukumveka mʼdziko lonse la Mowabu;
    kulira kwawo kosweka mtima kukumveka
    mpaka ku Egilaimu ndi Beeri-Elimu.
Madzi a ku Dimoni afiira ndi magazi,
    komabe ndidzabweretsa zina zambiri pa Dimoni,
mkango woti udzagwire aliyense othawa mu Mowabu
    ndi aliyense wotsala mʼdzikomo.