Add parallel Print Page Options

Phiri la Yehova

Nazi zinthu zokhudza Yuda ndi Yerusalemu, zimene Yesaya mwana wa Amozi anaziona mʼmasomphenya:

Mʼmasiku otsiriza,

phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa
    kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse,
lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse,
    ndipo mayiko onse adzathamangira kumeneko.

Anthu ambiri adzabwera ndikunena kuti,

“Tiyeni tikwere ku phiri la Yehova,
    ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo.
Iye adzatiphunzitsa njira zake,
    ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.”
Malangizo adzachokera ku Ziyoni,
    mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.
Iye adzaweruza pakati pa mayiko,
    ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu ambiri.
Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu
    ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera.
Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina,
    kapena kuphunziranso za nkhondo.

Inu nyumba ya Yakobo, bwerani,
    tiyeni tiyende mʼkuwala kwa Yehova.

Tsiku la Yehova

Inu Yehova mwawakana anthu anu,
    nyumba ya Yakobo.
Iwo adzaza ndi zamatsenga zochokera Kummawa;
    amawombeza mawula ngati Afilisti,
    ndipo amayanjana ndi anthu osapembedza Mulungu.
Dziko lawo ndi lodzaza ndi siliva ndi golide;
    ndipo chuma chawo ndi chosatha.
Dziko lawo ndi lodzaza ndi akavalo;
    ndipo magaleta awo ankhondo ngosawerengeka.
Dziko lawo ndi lodzaza ndi mafano;
    iwo amapembedza ntchito ya manja awo,
    amagwadira zomwe anapanga ndi zala zawo.
Tsono munthu aliyense adzachepetsedwa
    ndi kutsitsidwa.
    Inu Yehova musawakhululukire.

10 Lowani mʼmatanthwe,
    bisalani mʼmaenje,
kuthawa kuopsa kwa Yehova
    ndi ulemerero wa ufumu wake!
11 Kudzikuza kwa anthu kudzatha,
    ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa;
Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu pa tsiku limenelo.

12 Yehova Wamphamvuzonse wakonzeratu tsiku
    limene adzatsitse onse onyada ndi odzitama,
    ndipo adzagonjetsa
    onse amphamvu,
13 tsiku la mikungudza yonse ya ku Lebanoni, yayitali ndi yoonekera patali,
    ndiponso la mitengo yonse ya thundu ya ku Basani,
14 tsiku la mapiri onse ataliatali
    ndiponso la zitunda zonse zazitali,
15 tsiku la nsanja zonse zazitali
    ndiponso malinga onse olimba,
16 tsiku la sitima zapamadzi zonse za ku Tarisisi
    ndiponso la mabwato onse okongola.
17 Kudzikuza kwa munthu kudzatha
    ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa,
Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu tsiku limenelo,
18     ndipo mafano onse adzatheratu.

19 Anthu adzathawira mʼmapanga a matanthwe
    ndi mʼmaenje a nthaka,
kuthawa mkwiyo wa Yehova,
    ndiponso ulemerero wa ufumu wake,
    pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.
20 Tsiku limenelo anthu adzatayira
    mfuko ndi mileme
mafano awo asiliva ndi mafano awo agolide,
    amene anawapanga kuti aziwapembedza.
21 Adzathawira mʼmapanga a matanthwe
    ndiponso mʼmingʼalu ya nthaka
kuthawa mkwiyo wa Yehova
    ndiponso ulemerero wa ufumu wake,
    pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.

22 Lekani kudalira munthu,
    amene moyo wake sukhalira kutha.
Iye angathandize bwanji wina aliyense?