Add parallel Print Page Options

Mtumiki wa Yehova

42 “Nayu mtumiki wanga, amene ndimamuchirikiza,
    amene ndamusankha, amenenso ndimakondwera naye.
Ndayika Mzimu wanga mwa Iyeyo,
    ndipo adzaweruza anthu a mitundu yonse mwachilungamo.
Iye sadzafuwula, sadzamveka mawu,
    kapena mawu ake kumveka mʼmisewu.
Bango lophwanyika sadzalithyola,
    ndipo moto wozilala sadzawuzimitsa.
Motero adzaonetsa kuti chilungamo ndicho choonadi;
    sadzafowoka kapena kukhumudwa
mpaka atakhazikitsa chilungamo pa dziko lapansi,
    ndi mpaka mayiko a mʼmbali mwa nyanja atafika poyembekezera malangizo ake.”

Yehova Mulungu
amene analenga zamlengalenga ndi kuziyalika,
    amene analenga dziko lapansi ndi zonse zimene zimabereka,
amenenso amapereka mpweya kwa anthu ake okhala mʼdzikomo,
    ndi moyo kwa onse oyendamo, akuti,
“Ine Yehova, ndakuyitana chifukwa Ine ndine wolungama;
    ndikugwira dzanja ndipo
ndidzakuteteza.
    Ndakupereka kukhala pangano langa kwa anthu
    ndi kuwunika kwa anthu a mitundu ina.
Udzatsekula maso a anthu osaona,
    udzamasula anthu a mʼndende
    ndi kutulutsa mʼndende anthu okhala mu mdima.

“Ine ndine Yehova: dzina langa ndi limenelo!
    Sindidzapereka ulemerero wanga kwa wina aliyense
    kapena matamando anga kwa mafano.
Taonani, zinthu zimene ndinalosera kale zachitikadi,
    ndipo ndikuwuzani zinthu zatsopano;
zinthuzo zisanaonekere
    Ine ndakudziwitsani.”

Nyimbo Yotamanda Yehova

10 Imbirani Yehova nyimbo yatsopano,
    mutamandeni inu okhala mʼdziko lonse lapansi,
inu amene mumayenda pa nyanja, nyanja ikokome ndi zonse zili mʼmenemo.
    Inu okhala pa zilumba tamandani Yehova.
11 Chipululu ndi mizinda yake zikweze mawu awo;
    midzi ya Akedara ikondwere.
Anthu a ku Sela ayimbe mwachimwemwe;
    afuwule kuchokera pamwamba pa mapiri.
12 Atamande Yehova
    ndipo alalike matamando ake kwa anthu apazilumba zonse.
13 Yehova adzapita ku nkhondo ngati munthu wamphamvu,
    adzawutsa ukali wake ngati munthu wankhondo;
akukuwa ndiponso akufuwula mfuwu wankhondo
    ndipo adzagonjetsa adani ake.

14 Yehova akuti, “Ndakhala ndili chete kwa nthawi yayitali,
    ndakhala ndili phee osachita kanthu.
Koma tsopano, ngati mayi pa nthawi yochira,
    ndi kubuwula ndi kupuma modukizadukiza ndipo ndili wefuwefu.
15 Ndidzawononga mapiri ndi zitunda
    ndipo ndidzawumitsa zomera zawo zonse;
ndidzasandutsa mitsinje kukhala zilumba
    ndipo ndidzawumitsa maiwe.
16 Ndidzatsogolera anthu osaona mʼmisewu imene sanayidziwe,
    ndidzawatsogolera mʼnjira zimene sanayendepo;
ndidzasandutsa mdima wa kutsogolo kwawo kuti ukhale kuwala
    ndipo ndidzasalaza malo osalala.
Zimenezi ndizo ndidzachite;
    sindidzawataya.
17 Koma onse amene amadalira mafano
    amene amanena kwa mafanowo kuti, ‘ndinu milungu yathu,’
    ndidzawachititsa manyazi kotheratu.

Aisraeli Alephera Kuphunzira

18 “Imvani, agonthi inu;
yangʼanani osaona inu, kuti muone! 19     Ali wosaona ndani, si mtumiki wanga kodi?
    Ndipo ndani ali wosamva ngati mthenga amene ndamutuma?
Kodi ndani ali wosaona ngati uja ndinachita naye pangano,
    kapena wosaona ndani ngati mtumiki wa Yehova?
20 Iwe waona zinthu zambiri, koma sunazisamale;
    makutu ako ndi otsekuka koma sumva kanthu.”
21 Chinamukomera Yehova
    chifukwa cha chilungamo chake,
    kapena lamulo lake kukhala lalikulu ndi lopambana.
22 Koma awa ndi anthu amene afunkhidwa ndi kuwalanda zinthu zawo,
    onsewa anawakola mʼmaenje
    kapena akuwabisa mʼndende.
Tsono asanduka chofunkha
    popanda wina wowapulumutsa
kapena kunena kuti,
    “Abwezeni kwawo.”

23 Kodi ndani wa inu amene adzamvetsera zimenezi
    kapena kutchera khutu ndi kumva za mʼtsogolomo?
24 Ndani anapereka Yakobo kwa ofunkha,
    ndi Israeli kwa anthu akuba?
Kodi si Yehova,
    amene ife tamuchimwirayu?
Pakuti sanathe kutsatira njira zake;
    ndipo sanamvere malangizo ake.
25 Motero anawakwiyira kwambiri,
    nawavutitsa ndi nkhondo.
Anayatsa moto ponseponse mowazungulira komabe iwo sanamvetse;
    motowo unawapsereza, koma iwo sanatengepo phunziro ayi.