Add parallel Print Page Options

Chiweruzo ndi Chipulumutso

65 “Ndinali wokonzeka kumva mapemphero a amene sankandipempha kanthu;
    ndipo ndinalola kuti anthu amene ankandifunafuna kuti andipeze.
Kwa mtundu wa anthu umene sunkapempha chithandizo kwa Ine,
    ndinati, ‘Ine ndili pano, Ine ndili pano.’
Tsiku lonse ndatambasulira manja anga
    anthu owukira aja,
amene amachita zoyipa,
    natsatira zokhumba zawo.
Ndatambasulira manja anga anthu aja amene nthawi zonse amandikwiyitsa
    mopanda manyazi.
Iwo amapereka nsembe mʼminda
    ndi kufukiza lubani pa maguwa ansembe a njerwa.
Amakatandala ku manda
    ndipo amakachezera usiku wonse kumalo obisika.
Amadya nyama ya nkhumba,
    ndipo mʼmiphika mwawo muli msunzi wa nyama yodetsedwa.
Amawuza ena kuti, ‘Khala patali usandiyandikire,
    chifukwa ungatengere kupatulika kwanga!’
Ukali wanga pa anthu otere uli ngati utsi mphuno zanga,
    ngati moto umene umayaka tsiku lonse.

“Taonani, ndatsimikiza kale mlandu ndi chilango chawo;
    sindidzakhala chete koma ndidzawalanga kwathunthu
    chifukwa cha machimo awo
ndi a makolo awo,”
    akutero Yehova.
“Chifukwa anapereka nsembe zopsereza pa mapiri
    ndi kundinyoza Ine pa zitunda zawo,
Ine ndidzawalanga kwathunthu potsata
    zimene anachita kale.”

Yehova akuti,

“Pamene madzi akanapezeka mu phava la mphesa
    ndipo anthu amati, ‘Musawononge phavalo,
    popeza madzi ena abwino akanalimobe mʼphavalo,’
Inenso chifukwa cha mtumiki wanga;
    sindidzawononga onse.
Ndidzatulutsa zidzukulu mʼbanja la Yakobo,
    ndipo a banja la Yuda adzalandira mapiri anga ngati cholowa chawo.
Anthu anga osankhidwa adzalandira zimenezi,
    ndipo atumiki anga adzakhala kumeneko.
10 Chigwa cha Saroni chidzakhala kodyetserako nkhosa,
    ndipo chigwa cha Akori chidzakhala malo opumirako ngʼombe
    kwa anthu anga ondifunafuna Ine.

11 “Koma inu amene mumasiya Yehova
    ndi kuyiwala phiri langa lopatulika,
amene munamukonzera Gadi chakudya
    ndi kuthirira Meni chakumwa,
12 ndidzakuperekani ku lupanga ngati nsembe,
    ndipo nonse mudzaphedwa;
chifukwa simunayankhe pamene ndinakuyitanani,
    ndinayankhula koma simunamvere.
Munachita zoyipa pamaso panga
    ndipo munasankha kuchita zoyipa zomwe sindikondwera nazo.”

13 Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti,

“Atumiki anga adzadya,
    koma inu mudzakhala ndi njala;
atumiki anga adzamwa,
    koma inu mudzakhala ndi ludzu;
atumiki anga adzakondwa,
    koma inu mudzakhala ndi manyazi.
14 Atumiki anga adzayimba
    mosangalala,
koma inu mudzalira kwambiri
    chifukwa chovutika mu mtima
    ndipo mudzalira mofuwula chifukwa mudzamva kuwawa mu mtima.
15 Anthu anga osankhidwa
    adzatchula dzina lanu potemberera.
Ambuye Yehova adzakuphani,
    koma atumiki ake adzawapatsa dzina lina.
16 Aliyense wopempha dalitso mʼdzikomo
    adzachita zimenezo kwa Mulungu woona;
ndipo aliyense wochita malumbiro mʼdzikomo
    adzalumbira mwa Mulungu woona.
Pakuti mavuto akale adzayiwalika
    ndipo adzachotsedwa pamaso panga.

Chilengedwe Chatsopano

17 “Taonani, ndikulenga
    mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano.
Zinthu zakale sizidzakumbukika,
    zidzayiwalika kotheratu.
18 Koma inu mukhale osangalala ndi okondwa mpaka muyaya
    chifukwa cha zimene ndikulenga,
pakuti ndikulenga Yerusalemu kukhala malo wosangalatsa
    ndipo anthu ake adzakhala achimwemwe.
19 Ine ndidzakondwa chifuwa cha Yerusalemu
    ndipo ndidzasangalala chifukwa cha anthu anga.
Kumeneko sikudzamvekanso kulira
    ndi mfuwu wodandaula.

20 “Ana sadzafa ali akhanda
    ndipo nkhalamba zonse zidzakwaniritsa zaka zawo zonse.
    Wamngʼono mwa iwo
adzafa ali ndi zaka 100.
    Amene adzalephere kufika zaka 100
adzatengedwa kukhala
    wotembereredwa.
21 Anthu adzamanga nyumba ndi kukhalamo,
    adzadzala mpesa ndipo adzadya zipatso zake.
22 Sadzamanganso nyumba anthu ena nʼkukhalamo,
    kapena kudzala ndi ena nʼkudya.
Pakuti anthu anga adzakhala ndi moyo
    wautali ngati mitengo.
Osankhidwa anga adzakondwera ndi ntchito
    ya manja awo nthawi yayitali.
23 Sadzagwira ntchito pachabe
    kapena kubereka ana kuti aone tsoka;
chifukwa adzakhala anthu odalitsidwa ndi Yehova,
    iwowo pamodzi ndi adzukulu awo omwe.
24 Ndidzawayankha ngakhale asanathe nʼkupempha komwe.
    Pamene akuyankhula kumene Ine ndidzakhala nditamva kale.
25 Mʼmbulu ndi mwana wankhosa wamkazi zidzadyera pamodzi.
    Mkango udzadya udzu monga ngʼombe,
    koma fumbi ndiye chidzakhale chakudya cha njoka.
Pa phiri langa lopatulika sipadzakhala
    chinthu chopweteka kapena chowononga,”
            akutero Yehova.