Add parallel Print Page Options

Mawu a Elifazi

15 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,

“Kodi munthu wanzeru angayankhe ndi mawu achabechabe otere,
    kapena angakhutitse mimba yake ndi mphepo yotentha yochokera kummawa?
Kodi angathe kutsutsa ndi mawu opanda pake,
    kapena kuyankhula mawu opanda phindu?
Koma iwe ukuchepetsa zoopa Mulungu
    ndipo ukutchinga zodzikhuthulira kwa Mulungu.
Tchimo lako ndiye likuyankhulitsa pakamwa pakopo;
    ndipo watengera mayankhulidwe a atambwali.
Pakamwa pakopo ndiye pakukutsutsa osati pakamwa panga;
    milomo yakoyo ikukutsutsa.

“Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa?
    Kodi unalengedwa mapiri asanalengedwe?
Kodi unali mʼgulu la alangizi a Mulungu?
    Kodi ukudziyesa wanzeru ndiwe wekha?
Kodi iwe umadziwa chiyani chimene ife sitichidziwa?
    Kodi iwe uli ndi chidziwitso chanji chimene ife tilibe?
10 Anthu a imvi ndi okalamba ali mbali yathu,
    anthu amvulazakale kupambana abambo ako.
11 Kodi mawu otonthoza mtima ochokera kwa Mulungu sakukukwanira,
    mawu oyankhula mofatsawa kwa iwe?
12 Chifukwa chiyani ukupsa mtima,
    ndipo chifukwa chiyani ukutuzula maso ako,
13 moti ukupsera mtima Mulungu
    ndi kuyankhula mawu otero pakamwa pako?

14 “Kodi munthu nʼchiyani kuti nʼkukhala woyera mtima
    kapena wobadwa mwa amayi nʼchiyani kuti nʼkukhala wolungama mtima?
15 Ngati Mulungu sakhulupirira ngakhale angelo ake,
    ngakhale zakumwamba sizoyera pamaso pake,
16 nanga kuli bwanji munthu amene ndi wonyansa ndi wa njira zokhotakhota,
    amene kuchita zoyipa kuli ngati kumwa madzi.

17 “Mvetsera kwa ine ndipo ndidzakufotokozera;
    ndilole ndikuwuze zimene ndaziona,
18 zimene anandiphunzitsa anthu anzeru,
    sanandibisire kalikonse kamene anamva kuchokera kwa makolo awo.
19 (Ndi kwa iwowa kumene dziko lino linaperekedwa
    pamene panalibe mlendo wokhala pakati pawo).
20 Munthu woyipa amavutika ndi masautso masiku onse a moyo wake,
    munthu wankhanza adzavutika zaka zake zonse.
21 Amamva mawu owopsa mʼmakutu mwake,
    pamene zonse zikuoneka ngati zili bwino, anthu achifwamba amamuthira nkhondo.
22 Iye sakhulupirira kuti angathe kupulumuka ku mdima wa imfa;
    iyeyo ndi woyenera kuphedwa.
23 Amangoyendayenda pali ponse kunka nafuna chakudya;
    amadziwa kuti tsiku la mdima lili pafupi.
24 Masautso ndi nthumanzi zimamuchititsa mantha kwambiri;
    zimamugonjetsa iye monga imachitira mfumu yokonzekera kukathira nkhondo,
25 chifukwa iye amatambasula dzanja lake kuyambana ndi Mulungu
    ndipo amadzitama yekha polimbana ndi Wamphamvuzonse.
26 Amapita mwa mwano kukalimbana naye
    atanyamula chishango chochindikala ndi cholimba.

27 “Ngakhale nkhope yake ndi yonenepa
    ndipo mʼchiwuno mwake muli mnofu wambiri,
28 munthuyo adzakhala mʼmizinda yowonongeka
    ndi mʼnyumba zosayenera kukhalamo anthu,
    nyumba zimene zikugwa ndi kuwonongeka.
29 Iye sadzalemeranso ndipo chuma chake sichidzakhalitsa,
    ngakhale minda yake sidzabala zipatso pa dziko lapansi.
30 Iyeyo sadzapulumuka mu mdimamo;
    lawi lamoto lidzawumitsa nthambi zake,
    ndipo mpweya wochokera mʼkamwa mwa Mulungu udzamusesa.
31 Asadzinyenge yekha podalira zinthu zachabechabe,
    pakuti pa mapeto pake sadzaphulapo kanthu.
32 Iye adzalandira malipiro ake nthawi yake isanakwane,
    ndipo nthambi zake sizidzaphukanso.
33 Iye adzakhala ngati mtengo wamphesa wopululidwa zipatso zake zisanapse,
    adzakhala ngati mtengo wa olivi umene wayoyola maluwa ake.
34 Pakuti anthu osapembedza Mulungu adzakhala osabala
    ndipo moto udzapsereza nyumba za onse okonda ziphuphu.
35 Iwo amalingalira zaupandu ndipo amachita zoyipa;
    mtima wawo umakonzekera zachinyengo.”

Eliphaz

15 Then Eliphaz the Temanite(A) replied:

“Would a wise person answer with empty notions
    or fill their belly with the hot east wind?(B)
Would they argue with useless words,
    with speeches that have no value?(C)
But you even undermine piety
    and hinder devotion to God.(D)
Your sin(E) prompts your mouth;(F)
    you adopt the tongue of the crafty.(G)
Your own mouth condemns you, not mine;
    your own lips testify against you.(H)

“Are you the first man ever born?(I)
    Were you brought forth before the hills?(J)
Do you listen in on God’s council?(K)
    Do you have a monopoly on wisdom?(L)
What do you know that we do not know?
    What insights do you have that we do not have?(M)
10 The gray-haired and the aged(N) are on our side,
    men even older than your father.(O)
11 Are God’s consolations(P) not enough for you,
    words(Q) spoken gently to you?(R)
12 Why has your heart(S) carried you away,
    and why do your eyes flash,
13 so that you vent your rage(T) against God
    and pour out such words(U) from your mouth?(V)

14 “What are mortals, that they could be pure,
    or those born of woman,(W) that they could be righteous?(X)
15 If God places no trust in his holy ones,(Y)
    if even the heavens are not pure in his eyes,(Z)
16 how much less mortals, who are vile and corrupt,(AA)
    who drink up evil(AB) like water!(AC)

17 “Listen to me and I will explain to you;
    let me tell you what I have seen,(AD)
18 what the wise have declared,
    hiding nothing received from their ancestors(AE)
19 (to whom alone the land(AF) was given
    when no foreigners moved among them):
20 All his days the wicked man suffers torment,(AG)
    the ruthless man through all the years stored up for him.(AH)
21 Terrifying sounds fill his ears;(AI)
    when all seems well, marauders attack him.(AJ)
22 He despairs of escaping the realm of darkness;(AK)
    he is marked for the sword.(AL)
23 He wanders about(AM) for food like a vulture;(AN)
    he knows the day of darkness(AO) is at hand.(AP)
24 Distress and anguish(AQ) fill him with terror;(AR)
    troubles overwhelm him, like a king(AS) poised to attack,
25 because he shakes his fist(AT) at God
    and vaunts himself against the Almighty,(AU)
26 defiantly charging against him
    with a thick, strong shield.(AV)

27 “Though his face is covered with fat
    and his waist bulges with flesh,(AW)
28 he will inhabit ruined towns
    and houses where no one lives,(AX)
    houses crumbling to rubble.(AY)
29 He will no longer be rich and his wealth will not endure,(AZ)
    nor will his possessions spread over the land.(BA)
30 He will not escape the darkness;(BB)
    a flame(BC) will wither his shoots,(BD)
    and the breath of God’s mouth(BE) will carry him away.(BF)
31 Let him not deceive(BG) himself by trusting what is worthless,(BH)
    for he will get nothing in return.(BI)
32 Before his time(BJ) he will wither,(BK)
    and his branches will not flourish.(BL)
33 He will be like a vine stripped of its unripe grapes,(BM)
    like an olive tree shedding its blossoms.(BN)
34 For the company of the godless(BO) will be barren,
    and fire will consume(BP) the tents of those who love bribes.(BQ)
35 They conceive trouble(BR) and give birth to evil;(BS)
    their womb fashions deceit.”